< Deutéronome 18 >

1 La tribu entière de Lévi, prêtres et lévites, n'aura ni part ni héritage en Israël; ils vivront des oblations au Seigneur, selon leurs services.
Ansembe Achilevi amene ndi fuko lonse la Alevi, asapatsidwe malo kapena cholowa pakati pa Aisraeli. Iwowa azidzadya zoperekedwa kwa Yehova ngati nsembe, popeza zimenezo ndiye cholowa chawo.
2 Ils n'auront point d'héritage parmi leurs frères; le Seigneur seul est leur héritage, comme il le leur a dit.
Iwowa sadzakhala ndi cholowa pakati pa abale awo pakuti Yehova ndiye cholowa chawo monga anawalonjezera.
3 Et voici la loi pour les prêtres, concernant les offrandes du peuple et les sacrifices des veaux ou des brebis: tu donneras au prêtre l'épaule, les joues et la poitrine,
Anthu amene abwera kudzapereka nsembe ya ngʼombe kapena nkhosa, azipereka kwa wansembe gawo lake motere: mwendo wakutsogolo, nyama yamʼmasaya ndi zamʼkati.
4 Et les prémices de ton blé, de ton vin, de ton huile; tu lui donneras aussi les prémices des rejetons de tes menus troupeaux,
Muziwapatsa zamasika zoyamba za tirigu wanu, vinyo watsopano ndi mafuta, ndi ubweya woyamba pometa nkhosa zanu,
5 Parce que le Seigneur l'a choisi, entre toutes les tribus, pour qu'il se tienne devant le Seigneur Dieu, pour qu'il exerce le sacerdoce, pour que lui et ses fils bénissent en son nom le peuple d'Israël.
pakuti Yehova Mulungu wanu wawasankha iwowa ndi ana awo pakati pa mafuko anu onse kuti aziyimirira ndi kutumikira mʼdzina la Yehova nthawi zonse.
6 Lorsque le lévite, de l'une des villes qu'il habite, partira au gré de son désir, et viendra au lieu qu'aura choisi le Seigneur,
Ngati Mlevi asuntha achoka ku mzinda wake ndi kupita kumalo kwina kumene Yehova wasankha mu Israeli momwemo ndi mtima wake wonse,
7 Il servira, au nom du Seigneur son Dieu, comme tous ses frères les lévites qui se tiendront en ce lieu devant le Seigneur.
kumeneko akhoza kukatumikirako mʼdzina la Yehova Mulungu wake monga Alevi anzake onse amene akutumikira pamaso pa Yehova.
8 Il mangera la portion qui lui est assignée indépendamment de la vente de ce qui lui revient dans sa famille.
Iye ayenera kulandira zogawana zawo mofanana ndi anzakewo ngakhale kuti iye anagulitsa kale cholowa cha pa banja pawo.
9 Lorsque tu seras entré en la terre que le Seigneur ton Dieu te donne, tu n'apprendras pas à imiter les abominations des Gentils.
Mukafika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, musakaphunzire makhalidwe onyansa a anthu a mʼdzikolo.
10 Il ne se trouvera parmi vous personne qui, pour purifier son fils ou sa fille, les fasse passer par le feu; qui use de la divination, qui prédise, qui prenne les augures.
Pasapezeke pakati panu munthu wootcha pa moto mwana wake wamwamuna kapena wamkazi ngati nsembe. Asapezekenso pakati panu munthu wowombeza kapena wochita mawula, wolosera, wochita za ufiti,
11 Tu ne chercheras pas à charmer par des incantations magiques, à devenir sorcier ni interprète des prodiges, à interroger les morts.
wolodza, kapena woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ndi kumafunsira nzeru kwa anthu akufawo.
12 Car quiconque fait ces choses est une abomination pour le Seigneur ton Dieu; c'est à cause de ces abominations que le Seigneur exterminera les Gentils devant ta face.
Aliyense wochita zinthu zotere ndi wonyansa pamaso pa Yehova, ndipo chifukwa cha zonyansa zimenezi Yehova adzakupirikitsirani mitundu ya anthu imeneyi.
13 Tu seras parfait devant le Seigneur ton Dieu.
Muzikhala angwiro pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
14 Car les nations dont tu vas prendre l'héritage, écoutent les devins et ceux qui prédisent l'avenir, et tu es instruit autrement par le Seigneur ton Dieu.
Mitundu ya anthu imene mudzayipirikitseyo imamvera anyanga kapena owombeza mawula. Koma inu Yehova Mulungu wanu sanakuvomerezeni kutero.
15 Le Seigneur ton Dieu suscitera parmi tes frères un prophète semblable à moi; c'est lui que vous écouterez,
Yehova Mulungu wanu adzawutsa pakati pa abale anu mneneri ngati ine. Muyenera kumumvera ameneyo.
16 Parce que, en Horeb, tu en as fait la demande au Seigneur ton Dieu, le jour de l'Eglise; tu as dit: Que nous ne continuions plus d'entendre la voix du Seigneur notre Dieu, que nous ne voyions plus ce grand feu, de peur que nous ne mourions.
Pakuti izi ndi zimene munapempha kwa Yehova Mulungu wanu ku Horebu pa tsiku la msonkhano lija pamene munati, “Ife tisamvenso mawu a Yehova Mulungu wathu kapena kuona moto woopsawu, kuopa kuti tingafe.”
17 Et le Seigneur m'a dit: ils ont bien parlé.
Yehova anati kwa ine, “Zimene akunenazi ndi zabwino.
18 Je susciterai pour eux, parmi leurs frères, un prophète semblable à toi; et je mettrai mes paroles dans sa bouche, et il leur parlera selon ce que je lui prescrirai.
Ndidzawawutsira mneneri ngati iwe pakati pa abale awo ndipo ndidzayika mawu anga mʼkamwa mwake ndipo adzawawuza chilichonse chimene ndidzamulamula.
19 Et je tirerai vengeance de tout homme qui n'écoutera pas ce que ce prophète lui aura dit en mon nom.
Ine mwini ndidzaweruza aliyense amene sadzamvera mawu anga amene mneneriyo adzayankhula mʼdzina langa.
20 Tout autre prophète qui sera assez impie pour dire en mon nom une parole que je ne lui aurai point commandé de dire, ou qui parlera au nom d'autres dieux, ce prophète sera mis à mort.
Koma mneneri wonena zinthu mʼdzina langa ndisanamulamulire kutero, kapena mneneri wonenera mʼdzina la milungu ina, ayenera kuphedwa.”
21 Et si tu dis en ton cœur: Comment discernerons-nous la parole que le Seigneur n'aura pas dite?
Mwina mukhoza kumadzifunsa kuti, “Kodi tingadziwe bwanji kuti uthengawu sanayankhule ndi Yehova?”
22 Tout ce qu'aura dit ce prophète au nom du Seigneur et qui n'arrivera pas, qui ne se réalisera pas, n'aura point été dit par le Seigneur. Ce prophète aura parlé dans son impiété: vous ne le recevrez pas.
Ngati zimene mneneriyo wanenera mʼdzina la Yehova sizinachitike kapena kukwaniritsidwa, ndiye kuti umenewo si uthenga umene Yehova wayankhula. Mneneri ameneyo amangoyankhula za mʼmutu mwake ndiye musadzidzimuke naye.

< Deutéronome 18 >