< Daniel 5 >

1 Le roi Baltasar offrit un magnifique repas à ses grands au nombre de mille, et devant les mille convives il y avait du vin.
Tsiku lina mfumu Belisazara anakonza phwando lalikulu la akalonga ake 1,000 ndipo anamwa vinyo pamodzi ndi iwo.
2 Et Balthasar buvait, et dans l'ivresse du vin il dit que l'on apportât les vases d'or et d'argent enlevés par Nabuchodonosor son père au temple de Jérusalem, et que le roi et ses grands, ses concubines et ses femmes, bussent dans ces vases.
Pamene Belisazara ankamwa vinyo, analamula kuti ziwiya zagolide ndi zasiliva zimene Nebukadinezara abambo ake anakatenga mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu zikatengedwe kuti mfumu ndi akalonga ake, akazi ake ndi azikazi amweremo.
3 Et l'on apporta les vases d'or et d'argent que l'on avait rapportés du temple de Jérusalem, et le roi et ses grands, ses concubines et ses femmes burent dans ces vases.
Choncho anabweretsa ziwiya zagolide zimene anazitenga mʼNyumba ya Mulungu; ndipo mfumu ndi akalonga ake, akazi ake ndi azikazi ake anamweramo.
4 Ils burent du vin, et ils louèrent leurs dieux d'or et d'argent, d'airain, de fer, de pierre et de bois.
Akumwa vinyo, anatamanda milungu yagolide ndi siliva, yamkuwa, chitsulo, yamtengo ndi mwala.
5 Au même instant apparurent des doigts d'homme, et ils écrivirent devant le luminaire sur l'enduit du mur du palais du roi, et le roi suivait du regard le mouvement des phalanges de la main qui écrivait.
Mwadzidzidzi zala za dzanja la munthu zinaonekera ndi kulemba pa khoma, pafupi ndi choyikapo nyale mʼnyumba yaufumu. Mfumu inapenyetsetsa dzanjalo pamene limalemba.
6 Alors le roi changea de visage, et ses pensées le troublèrent, et la ceinture de ses reins se dénoua, ses genoux s'entre-choquèrent.
Nkhope yake inasandulika ndipo inachita mantha, nkhongono zii, mawondo gwedegwede.
7 Et le roi, criant de toute sa force, ordonna d'amener les mages, les Chaldéens et les sorciers. Et il dit aux sages de Babylone: Celui qui lira ce qui est écrit, et qui m'en fera connaître l'interprétation, sera revêtu de pourpre, et il aura autour du cou un collier d'or, et dans mon royaume il commandera le troisième après moi.
Mfumu inafuwula kuyitana owombeza, alawuli ndi amawula kuti abwere. Ndipo anawawuza anthu anzeru a ku Babuloni kuti, “Aliyense amene awerenge malembawa ndi kundiwuza tanthauzo lake adzavekedwa chovala cha pepo ndi mkanda wa golide udzavekedwa mʼkhosi mwake, ndipo adzakhala wolamulira wachitatu mu ufumuwu.”
8 Et tous les sages du roi s'avancèrent, et ils ne purent lire ce qui était écrit ni en donner au roi l'interprétation.
Pamenepo anzeru onse a mfumu anabwera, koma sanakwanitse kuwerenga malembawo kapena kumutanthauzira mfumu.
9 Et le roi Baltasar fut troublé, et il changea de visage, et ses grands furent troublés comme lui.
Choncho mfumu Belisazara anachita mantha koposa ndipo nkhope yake inapitirira kusinthika. Akalonga ake anathedwa nzeru.
10 Et la reine entra dans la salle du festin, et elle dit: Roi, vis à jamais, que tes pensées ne se troublent pas, et ne change pas de visage!
Mfumukazi, pakumva mawu a mfumu ndi akalonga ake, analowa mʼchipinda cha phwando ndipo anati, “Mfumu mukhale ndi moyo wautali! Musavutike! Nkhope yanu isasinthike!
11 Il est dans ton royaume un homme en qui est l'Esprit de Dieu; et du temps de ton père la vigilance et la sagesse furent trouvées en lui, et le roi Nabuchodonosor ton père le fit chef des devins, des mages, des Chaldéens et des sorciers,
Pali munthu wina mu ufumu wanu uno amene mwa iye muli mzimu wa milungu yoyera. Pa nthawi ya ulamuliro wa abambo anu iye anapezeka kuti ali ndi chidziwitso, luntha ndi nzeru zonga za milungu. Mfumu Nebukadinezara, abambo anu, Ine ndikukuwuzani anamusankha iye kukhala mkulu wa amatsenga, owombeza, alawuli ndi amawula.
12 Parce que l'esprit était supérieur en lui, et que la prudence et la sagesse étaient en lui pour interpréter les songes, pour répondre aux questions difficiles, pour dénouer les choses inextricables; c'est Daniel, et ton père l'appelait Baltasar; maintenant donc, qu'on l'appelle, et il te fera connaître son interprétation.
Munthu ameneyu dzina lake ndi Danieli, koma mfumu inamutcha Belitesezara ndipo ali ndi nzeru zapadera, ndi wodziwa ndi kuzindikira zinthu, ndiponso luso lakutanthauzira maloto, kufotokozera miyambi ndi kuthetsa mavuto osautsa. Muyitaneni Danieli, ndipo adzakuwuzani chomwe mawuwa akutanthauza.”
13 Alors Daniel fut introduit devant le roi, et le roi dit à Daniel: Es-tu Daniel, l'un des fils des captifs de la Judée qu'a transportés mon père?
Choncho anabwera naye Danieli pamaso pa mfumu ndipo inati kwa iye, “Kodi ndiwe Danieli, mmodzi mwa akapolo omwe abambo anga mfumu anabwera nawo kuchoka ku Yuda?
14 J'ai oui dire que l'Esprit de Dieu est en toi, et que la vigilance, l'intelligence et une sagesse supérieure ont été trouvées en toi.
Ndamva kuti mzimu wa milungu uli mwa iwe ndi kuti uli ndi chidziwitso, luntha ndi nzeru zapadera.
15 Or maintenant les sages, les mages, les sorciers sont venus devant moi, pour lire cette écriture, et m'en faire connaître l'interprétation; et ils n'ont pu me rien dire.
Anzeru ndi owombeza anabwera pamaso panga kuti awerenge zolembedwazi ndi kundiwuza tanthauzo lake koma sanakwanitse kundifotokozera.
16 Et moi, j'ai appris que tu peux interpréter les jugements; si donc tu peux lire cette écriture et me l'interpréter, tu seras revêtu de pourpre, tu auras un collier d'or autour du cou, et tu commanderas dans mon royaume, le troisième après moi.
Tsopano ndamva kuti iwe ukhoza kupereka matanthauzo ndi kuthetsa mavuto. Ngati ungawerenge zolembedwazi ndi kundiwuza tanthauzo lake, udzavekedwa chovala cha pepo ndi kuyikidwa mkanda wa golide mʼkhosi mwako, ndipo udzakhala wolamulira wachitatu mu ufumu uno.”
17 Et Daniel dit en présence du roi: Que tes présents te restent, donne à un autre les dons de ton palais; pour moi, je te lirai ce qui est écrit, et je t'en ferai connaître l'interprétation.
Pamenepo Danieli anayankha mfumu kuti, “Inu musunge mphatso zanuzo kwa inu nokha ndipo mupereke mphothoyo kwa wina aliyense. Komabe ine ndi kuwerengerani malembawa mfumu; ndikukuwuzani tanthauzo lake.
18 Roi, le Dieu très-haut a donné à Nabuchodonosor ton père la royauté et la magnificence, les honneurs et la gloire.
“Inu mfumu, Mulungu Wammwambamwamba anapatsa abambo anu Nebukadinezara mphamvu ndi ukulu ndi ulemerero ndi ufumu.
19 Et devant la grandeur que Dieu lui avait donnée, les peuples, les tribus, les hommes de toutes langues étaient tremblants et pleins de crainte devant son visage; ceux d'entre eux qu'il voulait tuer, il les tuait; ceux qu'il voulait frapper, il les frappait; ceux qu'il voulait glorifier, il les glorifiait; et ceux qu'il voulait humilier, il les humiliait.
Chifukwa cha udindo waukulu umene anapatsidwanso, anthu onse ndi mitundu ndi anthu aziyankhulo zosiyanasiyana ankanjenjemera ndikumuopa iye. Amene mfumu inafuna anawaphadi; amene inafuna kuwasunga, inawasunga; amene inafuna kuwakweza, inawakweza; ndipo amene inafuna kuwatsitsa, inawatsitsa.
20 Et quand son cœur se fut élevé, et que son esprit se fut endurci dans son orgueil, il fut précipité du trône, et ses honneurs lui furent enlevés.
Koma pamene inayamba kudzitama ndi kuwumitsa mtima wake ndi kuyamba kunyada, inachotsedwa pa mpando wake waufumu ndi kulandidwa ulemerero wake.
21 Et il fut chassé loin des hommes, et un cœur lui fut donné comme aux bêtes, et sa demeure fut parmi les ânes sauvages; on lui donna sa part de fourrage comme à un bœuf, et son corps fut baigné par la rosée du ciel, jusqu'à ce qu'il eût reconnu que le Dieu très-haut est le maître du royaume des hommes, et qu'il le donne à qui bon lui semble.
Iyo inachotsedwa pakati pa anthu ndi kupatsidwa mtima ngati wa nyama; inakhala pamodzi ndi abulu akutchire ndi kudya udzu ngati ngʼombe; ndipo thupi lake linanyowa ndi mame akumwamba, mpaka pamene anavomereza kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye wolamulira maufumu a anthu ndipo amawupereka kwa aliyense amene Iye wafuna.
22 Et toi donc, son fils Baltasar, tu n'as pas non plus humilié ton cœur devant Dieu: ne sais-tu point toutes ces choses?
“Koma inu mwana wake, Belisazara, simunadzichepetse, ngakhale kuti mumadziwa zonsezi.
23 Tu t'es enorgueilli contre le Seigneur Dieu du ciel, et l'on a apporté devant toi les vases de son temple; et toi et tes grands, tes concubines et tes femmes, vous avez bu du vin dans ces vases; et tu as loué les dieux d'or et d'argent, d'airain, de fer, de pierre et de bois, qui ne voient, n'entendent ni ne comprennent; et le Dieu qui tient en sa main ton souffle et toutes tes voies, tu ne l'as point glorifié.
Mʼmalo mwake, mwadzikweza nokha kutsutsana ndi Ambuye wakumwamba. Inu mwatenga ziwiya za mʼNyumba mwake, ndipo inu ndi akalonga anu, akazi anu ndi azikazi anu mwamwera vinyo mu zimenezi. Inu munatamanda milungu yasiliva ndi golide, yamkuwa, chitsulo, mtengo ndi mwala, imene singaone kapena kumva kapena kuzindikira. Koma simunamupatse ulemu Mulungu amene asunga mʼmanja mwake moyo wanu ndi njira zanu zonse.
24 C'est pourquoi il a envoyé de devant lui les doigts de cette main, et lui a ordonné de tracer cette inscription.
Choncho Iye watumiza dzanja limene lalemba mawu amenewa.
25 Or, cette inscription, la voici: Mané, Thécel, Pharès.
“Mawu amene analembedwa ndi awa: MENE, MENE, TEKELI, PARASINI.
26 Et voici l'interprétation de ces paroles: Mané, Dieu a mesuré ton règne, et en a marqué la fin.
“Zimene mawuwa akutanthauza ndi izi:
27 Thécel, ta royauté a été placée sur la balance, et elle a été trouvée trop légère.
Tekeli: Inu mwayesedwa pa sikelo ndipo mwapezeka kuti mukuperewera.
28 Pharès, ton royaume a été divisé, et donné aux Mèdes et aux Perses.
Parasini: Ufumu wanu wagawidwa ndi kupatsidwa kwa Amedi ndi Aperezi.”
29 Et Baltasar donna ses ordres: et l'on revêtit Daniel de pourpre, et on lui mit autour du cou un collier d'or, et le roi lui-même le proclama le troisième chef du royaume.
Mwa lamulo la Belisazara, Danieli anavekedwa chovala cha pepo, mkanda wagolide unayikidwa mʼkhosi mwake, ndipo analengeza kuti anali wachitatu mu ulamuliro mu ufumuwo.
30 Et cette même nuit fut tué Baltasar, le roi chaldéen.
Usiku womwewo Belisazara, mfumu ya anthu a ku Babuloni, inaphedwa,
31 Et le Mède Darius reçut le gouvernement de son royaume, à l'âge de soixante-deux ans.
ndipo Dariyo Mmedi analanda ufumuwo ali ndi zaka 62.

< Daniel 5 >