< Daniel 2 >

1 En la seconde année de son règne, Nabuchodonosor eut un songe, et son esprit en fut saisi de stupeur, et le sommeil s'éloigna de lui.
Chaka chachiwiri cha ulamuliro wake, Nebukadinezara analota maloto; anavutika mu mtima mwake ndipo analephera kugona.
2 Et le roi ordonna de convoquer les devins et les mages, les sorciers et les Chaldéens, pour interpréter le songe qu'il avait eu. Ils vinrent donc, et ils comparurent devant le roi.
Tsono mfumu inayitana amatsenga, owombeza, amawula ndi oyangʼana nyenyezi kuti amufotokozere zomwe analota. Pamene iwo analowa ndi kuyima pamaso pa mfumu,
3 Et le roi leur dit: J'ai eu un songe, et mon esprit en a été frappé de stupeur au point de ne rien connaître à ce songe.
mfumuyo inawawuza kuti, “Ndalota loto lomwe likundisautsa ndipo ndikufuna kudziwa tanthauzo lake.”
4 Et les Chaldéens dirent au roi en langue syriaque: Ô roi, vis à jamais, dis ton songe à tes serviteurs, et nous t'en donnerons l'interprétation.
Pamenepa alawuli anati kwa mfumu mʼChiaramu, “Mukhale ndi moyo wautali mfumu! Tiwuzeni ife atumiki anu zimene mwalota, ndipo tidzakuwuzani tanthauzo lake.”
5 Le roi répondit aux Chaldéens: Les paroles se sont éloignées de moi; si vous ne me faites connaître le songe et son interprétation, vous serez mis à mort, et vos maisons seront pillées.
Mfumu inayankha alawuliwo kuti, “Zimene ndatsimikiza kuchita ndi izi: Ngati inu simundifotokozera zimene ndalota ndi tanthauzo lake, mudzadulidwa nthulinthuli ndipo nyumba zanu ndidzazisandutsa bwinja.
6 Mais si vous me faites connaître le songe et son interprétation, vous recevrez de moi des dons, des présents et de grands honneurs; seulement faites-moi connaître mon songe et son interprétation.
Koma ngati mundiwuza zimene ndalota ndi tanthauzo lake, ndidzakupatsani mphatso ndi mphotho ndi ulemu waukulu. Choncho mundiwuze zimene ndalota ndi tanthauzo lake.”
7 Ils répondirent une seconde fois, et dirent: Que le roi dise à ses serviteurs quel songe il a eu, et nous lui en ferons connaître l'interprétation.
Iwo anayankhanso kachiwiri kuti, “Mfumu iwuze atumiki ake chimene yalota, ndipo ife tidzatanthauzira.”
8 Et le roi reprit, et dit: En vérité, je sais, moi, que vous voulez gagner du temps, parce que vous voyez que les paroles du songe se sont éloignées de moi.
Ndipo mfumu inayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti mukungozengereza kufuna kutaya nthawi chabe chifukwa mukuzindikira kuti izi ndi zimene ndatsimikiza kuchita.
9 Si donc vous ne me dites pas mon songe, je sais que vous êtes convenus entre vous de me dire des paroles fausses et altérées, jusqu'à ce que le temps se soit écoulé. Dites-moi mon songe, et alors je saurai que vous m'en ferez connaître aussi l'interprétation.
Ngati simundiwuza zimene ndalota, chilango chake ndi chimodzi. Inu mwagwirizana kuti mundiwuze ine bodza ndi chinyengo ndi kuyembekeza kuti ine ndisintha. Tsono mundiwuze zimene ndalota, ndipo ine ndidzadziwa kuti mukhoza kunditanthauzira.”
10 Les Chaldéens répondirent devant le roi, et ils dirent: Il n'est point d'homme sur la terre qui puisse faire connaître cette parole au roi, de même qu'il n'est point de grand roi ni de prince qui fasse pareille question à un devin, ou mage, ou Chaldéen.
Alawuli anayankha mfumu kuti, “Palibe munthu pa dziko lapansi amene akhoza kuchita chimene mfumu ikufunsa! Palibe mfumu, kaya yayikulu kapena yamphamvu bwanji imene inafunsapo amatsenga, owombeza kapena alawuli aliwonse zimenezi.
11 Car la parole sur laquelle le roi nous questionne est grave, et nul autre que nous ne pourra la découvrir au roi, sinon des dieux dont la demeure n'est pas en la chair.
Zimene mfumu yafunsa ndi zapatali. Palibe wina amene angathe kuwulula izi kwa mfumu kupatula milungu, ndipo sikhala pakati pa anthu.”
12 Alors le roi, plein de fureur et d'indignation, ordonna que l'on mît à mort tous les sages de Babylone.
Zimenezi zinapsetsa mtima mfumu ndipo inakwiya kwambiri kotero inalamula kuti anzeru onse a ku Babuloni aphedwe.
13 Et sa sentence s'exécuta, et les sages furent mis à mort, et on chercha Daniel et ses amis pour les tuer aussi.
Choncho lamulo linaperekedwa kuti anthu anzeru aphedwe, ndipo anatuma anthu kukafunafuna Danieli ndi anzake kuti iwonso aphedwe.
14 Alors Daniel parla avec réflexion et sagesse à Arioch, chef des cuisines du roi, qui était sorti pour mettre à mort les sages de Babylone.
Danieli anayankhula mwanzeru ndi mwaulemu kwa Ariyoki, mkulu wa asilikali olondera mfumu amene anatumidwa kukapha anthu anzeru a ku Babuloni.
15 Ministre du roi, lui dit-il, à quel sujet cet ordre impitoyable est-il sorti de la bouche du roi? Et Arioch fit connaître l'affaire à Daniel.
Danieli anafunsa Ariyoki kapitawo wa mfumu kuti, “Chifukwa chiyani mfumu yapereka lamulo lankhanza lotere?” Kenaka Ariyoki anafotokoza nkhaniyi kwa Danieli.
16 Et Daniel demanda au roi de lui accorder du temps, promettant de lui faire connaître l'interprétation du songe.
Danieli anapita mofulumira kwa mfumu ndipo anamupempha kuti amupatse nthawi kuti amuwuze zimene walota ndi tanthauzo lake.
17 Et Daniel rentra dans sa maison, et il raconta l'affaire à Ananias, Misaël, Azarias, ses amis.
Kenaka Danieli anabwerera ku nyumba kwake ndi kukafotokozera anzake aja zimenezi: Hananiya, Misaeli ndi Azariya.
18 Et ils implorèrent les miséricordes du Dieu du ciel sur ce mystère, afin que ni Daniel ni ses amis ne périssent avec le reste des sages de Babylone.
Danieli anadandaulira anzake kuti apemphe kwa Mulungu wakumwamba kuti awachitire chifundo ndi kumuwululira chinsinsi, kuti iye ndi anzakewo asanyongedwe pamodzi ndi anzeru ena onse a ku Babuloni.
19 Alors à Daniel, en une vision nocturne, le mystère fut révélé, et il bénit le Dieu du ciel,
Usiku Yehova anamuwululira Danieli chinsinsi chija mʼmasomphenya. Pamenepo Danieli anatamanda Mulungu wakumwamba,
20 Disant: Que le nom du Seigneur soit béni, maintenant et dans tous les siècles, parce que toute sagesse et toute intelligence lui appartiennent.
ndipo anati: “Litamandike dzina la Mulungu ku nthawi za nthawi; nzeru ndi mphamvu zonse ndi zake.
21 C'est lui qui change les heures et les temps, lui qui place et déplace les rois, lui qui donne la sagesse aux sages, et la prudence aux prudents.
Amasintha nthawi ndi nyengo; amakweza mafumu ndipo amawatsitsanso. Amapatsa nzeru kwa anzeru ndi chidziwitso kwa ozindikira zinthu.
22 C'est lui qui révèle les choses profondes et cachées, lui qui sait ce qui est dans les ténèbres; et la lumière est avec lui.
Amavumbulutsa zinthu zozama ndi zobisika; amadziwa zimene zili mu mdima, ndipo kuwunika kumakhala ndi Iye.
23 Vous donc, Dieu de mes pères, je vous rends hommage et je vous loue, parce que vous m'avez donné la force et la sagesse, que vous m'avez appris ce que nous vous avons demandé, et que vous m'avez révélé la vision du roi.
Ndikuyamika ndi kutamanda Inu Mulungu wa makolo anga: mwandipatsa nzeru ndi mphamvu, mwandiwululira zomwe tinakupemphani, mwatiwululira maloto a mfumu.”
24 Et Daniel alla trouver Arioch, que le roi avait chargé de mettre à mort les sages de Babylone, et il lui dit: N'exécute pas les sages de Babylone; mais introduis-moi en présence du roi, et je donnerai au roi l'interprétation du songe qu'il a eu.
Motero Danieli anapita kwa Ariyoki, amene mfumu inamusankha kuti akaphe anthu anzeru a ku Babuloni, ndipo anati kwa iye, “Musaphe anthu anzeru a ku Babuloni. Ndiperekezeni kwa mfumu, ndipo ndidzayimasulira maloto ake.”
25 Aussitôt Arioch s'empressa d'introduire Daniel en présence du roi, et il lui dit: J'ai trouvé un homme des fils des captifs de la Judée, qui donnera au roi l'interprétation du songe.
Ariyoki anapita naye Danieli kwa mfumu nthawi yomweyo ndipo anati, “Ndapeza munthu pakati pa akapolo ochokera ku Yuda amene akhoza kuwuza mfumu zimene maloto ake akutanthauza.”
26 Et le roi prit la parole, et il dit à Daniel, que l'on nommait Baltasar: Pourras-tu me faire connaître le songe que j'ai eu et son interprétation?
Mfumu inafunsa Danieli (wotchedwanso Belitesezara) kuti, “Kodi ukhoza kundiwuza zomwe ine ndinaona mʼmaloto anga ndi tanthauzo lake?”
27 Et Daniel répondit devant le roi, disant: Le mystère que le roi me demande, il n'appartient ni aux juges, ni aux mages, ni aux devins, ni aux augures, de le révéler au roi.
Danieli anayankha kuti, “Palibe munthu wanzeru, wowombeza, wamatsenga kapena wamawula amene akhoza kufotokozera mfumu chinsinsi chimene mwafuna kudziwa,
28 Mais c'est Dieu qui, dans le ciel, révèle tous les mystères, et qui a fait connaître au roi Nabuchodonosor ce qui doit arriver dans les derniers jours. Ton songe et les visions de ta tête sur ta couche, les voici:
koma kuli Mulungu kumwamba amene amawulula zinsinsi. Iye waonetsera mfumu Nebukadinezara zimene zidzachitika mʼmasiku akutsogolo. Maloto ndi masomphenya anu amene munawaona mukugona pa bedi lanu ndi awa:
29 Ô roi, tes pensées sur ta couche s'étaient portées sur ce qui doit arriver après le moment présent; et Celui qui révèle les mystères t'a fait connaître ce qui doit arriver
“Mukugona pa bedi, inu Mfumu, maganizo anakufikirani a zinthu zakutsogolo, ndipo Yehova wowulula zinsinsi anakuonetserani zimene zidzachitika.
30 Et c'est à moi qu'il a révélé ce mystère, non à cause de la sagesse qui est en moi, ni dans les autres vivants; mais afin que je te découvre, ô roi, l'interprétation de ton songe, et que tu connaisses les pensées de ton cœur.
Koma chinsinsi ichi chavumbulutsidwa kwa ine, si chifukwa chakuti ndili ndi nzeru zochuluka kuposa anthu ena onse, koma kuti mfumu mudziwe tanthauzo la maloto anu ndi kuti muzindikire maganizo amene anali mu mtima mwanu.
31 Toi donc, ô roi, tu regardais; et voilà qu'une statue se tint debout devant ta face; cette statue était grande, et son aspect terrible.
“Inu mfumu, munaona chinthu chowumba chachikulu chimene chinayima pamaso panu. Chowumbachi chinali chonyezimira mʼmaonekedwe.
32 C'était une statue dont la tête était d'or pur, les mains, la poitrine et les bras d'argent, le ventre et les cuisses d'airain;
Mutu wa chowumbacho unali wagolide wabwino kwambiri. Chifuwa ndi manja ake zinali zasiliva. Mimba ndi ntchafu zake zinali zamkuwa.
33 Les jambes de fer, et les pieds partie de fer, partie d'argile.
Miyendo yake inali yachitsulo, mapazi ake anali achitsulo chosakaniza ndi dongo.
34 Tu regardais, quand une pierre détachée de la montagne, sans qu'une main la poussât, vint frapper la statue à ses pieds de fer et d'argile, et à la fin elle les broya.
Inu mukuona, mwala unagamuka, koma osati ndi manja a munthu. Unagwera fanolo pa mapazi ake achitsulo chosakaniza ndi dongo aja ndi kuwaphwanya.
35 Alors furent broyés à la fois l'argile, le fer, l'airain, l'argent et l'or, et ils devinrent comme la poudre qui l'été s'élève au-dessus d'une aire; et un souffle violent les emporta, et l'on n'en trouva plus la place. Et la pierre qui avait frappé la statue devint une grande montagne, et elle couvrit toute la terre.
Tsono chitsulo, dongo, mkuwa, siliva ndi golide zonse zinaphwanyika pamodzi ndikukhala tizidutswa towuluka ndi mphepo ngati mungu wa mowombera tirigu nthawi ya chilimwe. Zonse zinawuluka ndi mphepo osasiyako chilichonse. Koma mwala umene unagwera pa chowumba chija unasanduka phiri lalikulu ndi kudzaza dziko lonse lapansi.
36 Voilà ton songe, et nous allons en dire l'interprétation devant le roi.
“Maloto aja ndi amenewa; tidzafotokoza tanthauzo lake kwa mfumu.
37 Ô roi, tu es le roi des rois, à qui le Dieu du ciel a donné un empire puissant, fort et glorieux,
Inu mfumu, ndinu mfumu ya mafumu. Mulungu wakumwamba wakupatsani ufumu, ulamuliro ndi mphamvu ndi ulemerero;
38 En tout lieu où demeurent les fils des hommes; toi à qui il a soumis les bêtes fauves des champs, et les oiseaux du ciel, et les poissons de la mer; toi qu'il a établi maître de toutes choses, tu es la tête d'or.
Iye anayika mʼmanja mwanu anthu ndi nyama zakuthengo ndi mbalame zamlengalenga. Kulikonse kumene zikhala, iye anakuyikani wolamulira wa zonse. Inu ndinu mutu wagolidewo.
39 Et le royaume qui s'élèvera après toi sera moindre que le tien; puis viendra un troisième royaume, qui sera d'airain, et qui commandera à toute la terre.
“Pambuyo pa inu, ufumu wina udzadzuka, wochepa mphamvu poyerekeza ndi wanuwu. Padzabweranso ufumu wachitatu, wamkuwa, udzalamulira dziko lonse lapansi.
40 Puis viendra un quatrième royaume qui sera fort comme le fer: de même que le fer broie et dompte toutes choses, il broiera et domptera toutes choses.
Pomaliza, padzakhala ufumu wachinayi, wolimba ngati chitsulo popeza chitsulo chimaphwanya ndi kutikita chilichonse. Ndipo monga chitsulo chimaphwanya zinthu ndikuteketeratu, choncho udzawononga ndi kuphwanya maufumu ena onse.
41 Et comme tu as vu les pieds et les doigts partie de fer, et partie d'argile, ce royaume sera divisé, et il sera détaché de ses racines de fer, comme tu as vu le fer mêlé à l'argile.
Ndipo monga munaonera kuti mapazi ndi zala zake zinali za chitsulo chosakaniza ndi dongo, choncho uwu udzakhala ufumu wogawikana; komabe udzakhala ndi mphamvu zina zachitsulo zotikita.
42 Et les doigts des pieds étant partie de fer, partie d'argile, une part de ce royaume sera forte, une autre sera broyée.
Monga zala zinali za chitsulo chosakaniza ndi dongo, choncho ufumu uwu udzakhala pangʼono wolimba ndi pangʼono wofowoka.
43 Et de même que tu as vu le fer confondu avec l'argile, de même il y aura des mélanges dans la race des hommes; mais ce ne sera pas un tout parfaitement uni, pas plus qu'il n'y a d'alliage entre l'argile et le fer.
Ndipo monga munaona chitsulo chosakanizidwa ndi dongo, choncho anthu adzakhala wosakanizana ndipo sadzagwirizana, monga muja chitsulo sichingasakanizike ndi dongo.
44 Et du temps de ces rois le Dieu du ciel suscitera un royaume qui ne périra point dans les siècles; et jamais son royaume ne sera subjugué par un autre peuple; et son royaume nivellera et vannera tous les royaumes, et il se maintiendra durant tous les siècles;
“Pa nthawi ya mafumu amenewo, Mulungu wakumwamba adzakhazikitsa ufumu umene sudzawonongedwa, kapenanso kuperekedwa kwa anthu ena. Udzawononga maufumu onse aja ndi kuwatheratu, koma iwo wokha udzakhalapobe mpaka muyaya.
45 Comme tu as vu la pierre se détacher de la montagne, sans qu'une main la poussât, et broyer l'argile, le fer, l'airain, l'argent et l'or. C'est ainsi que le grand Dieu a fait connaître au roi ce qui doit arriver après ces temps. Et véritable est le songe, et l'interprétation digne de foi.
Limeneli ndilo tanthauzo la masomphenya a mwala umene unagamuka pa phiri, koma osati ndi manja a anthu; mwala umene unaphwanya chitsulo, mkuwa, dongo, siliva ndi golide mʼtizidutswa. “Mulungu wamkulu wakuonetsani mfumu chimene chidzachitika kutsogolo. Malotowo ndi woona ndipo tanthauzo lake ndi lodalirika.”
46 Alors le roi Nabuchodonosor tomba la face contre terre, et il adora Daniel, et il ordonna qu'on lui offrît des oblations et de l'encens.
Pamenepo mfumu Nebukadinezara inadzigwetsa chafufumimba pamaso pa Danieli ndi kumupatsa ulemu. Ndipo inalamula kuti anthu onse amuthirire Danieli nsembe ndi kumufukizira lubani.
47 Et le roi, prenant la parole, dit à Daniel: En vérité, votre Dieu seul est le Dieu des dieux et le Seigneur des rois; c'est lui qui révèle les mystères; car tu n'aurais pu révéler celui-ci.
Mfumu inati kwa Danieli, “Zoonadi, Mulungu wako ndi Mulungu wa milungu ndi Ambuye wa mafumu ndi wowulula zinsinsi, pakuti iwe wathadi kuwulula chinsinsi ichi.”
48 Et le roi glorifia Daniel; il lui fit de grands et magnifiques présents, et il le mit à la tête de toute la province de Babylone, et il l'institua chef des satrapes et de tous les sages de Babylone.
Ndipo mfumu inamukweza Danieli ndi kumupatsa mphatso zambiri. Anamuyika kuti akhale wolamulira chigawo chonse cha Babuloni ndi kutinso akhale woyangʼanira anthu ake onse anzeru.
49 Et sur la demande de Daniel le roi chargea de toutes les affaires de la province de Babylone Sidrach, Misach et Abdénago, et Daniel resta dans le palais du roi.
Komanso, monga mwa pempho la Danieli, mfumu inayika Sadirake, Mesaki ndi Abedenego, kuti akhale oyangʼanira chigawo cha Babuloni, pamene Danieliyo ankakhazikika mʼbwalo la mfumu.

< Daniel 2 >