< Daniel 11 >

1 Je suis celui qui, en la première année du règne de Cyrus, se tint près de lui pour le fortifier et l'affermir.
Ndipo chaka choyamba cha Dariyo Mmedi ine Mikayeli ndinabwera kumuthandiza ndi kumuteteza Gabrieli.
2 Et maintenant je te ferai connaître la vérité: trois rois règneront encore sur la Perse; le quatrième prospèrera et les surpassera tous en richesses; et lorsqu'il sera en possession de ses richesses, il fera la guerre à tous les royaumes des Hellènes.
“Ndipo tsopano ndikuwuza zoona: Mafumu ena atatu adzalamulira ku Peresiya, ndipo kenaka padzadzuka mfumu yachinayi imene idzakhala yolemera kwambiri kuposa onsewo. Popeza kuti idzakhala ndi mphamvu chifukwa cha chuma chake, idzadzutsa onse kuti alimbane ndi ufumu wa Grisi.
3 Et un roi puissant s'élèvera, et il sera maître d'un grand empire, et il fera ce qu'il voudra.
Kenaka mfumu yamphamvu idzafika imene idzalamulira ndi ufumu waukulu ndi kuchita zimene ifuna.
4 Et, au moment où son empire sera affermi, il sera brisé et partagé aux quatre vents du ciel; et il ne passera point à ses descendants, et il ne gardera point sa puissance selon ses désirs; car sa royauté lui sera arrachée; puis elle passera à d'autres après lui.
Koma ufumu wake ukadzafika pachimake, udzawonongedwa ndi kugawidwa mʼzigawo zinayi. Ufumuwo sudzaperekedwa kwa zidzukulu zake, ndipo olowa mʼmalo mwake sadzakhala ndi mphamvu monga anali nazo, chifukwa ufumu wake udzazulidwa ndi kuperekedwa kwa ena.
5 Et le roi du midi se fortifiera; mais l'un de ces princes prévaudra contre lui, et il dominera sur un grand royaume.
“Mfumu ya kummwera idzakhala yamphamvu, koma mmodzi mwa akalonga ake adzakhala ndi mphamvu kuposa iyo; adzalamulira ufumu wake waukulu kwambiri.
6 Et quelques années après ils s'uniront; et la fille du roi du midi ira trouver le roi de l'aquilon pour faire alliance avec lui; mais elle ne retirera pas de là un bras puissant; et la race du vainqueur ne se maintiendra pas; et elle-même sera livrée avec ceux qui la conduisaient, et la jeune fille, et celui qui la fortifiait en ces temps.
Patapita zaka zingapo, mfumu ya kummwera ndi mfumu ya kumpoto adzachita pangano. Mwana wamkazi wa mfumu ya kummwera adzapita nakakwatiwa ndi mfumu ya kumpoto pokhazikitsa pangano la mtendere, koma ulamuliro wake pamodzi ndi wa mwana wake sudzakhalitsa. Mʼmasiku amenewo iye, mwamuna wake, mwana wake ndi atumiki ake, onse adzaperekedwa kwa adani.
7 Mais un rejeton de la fleur de sa racine s'élèvera bientôt après; et il s'avancera à la tête d'une armée, et il entrera dans les forteresses du roi de l'aquilon; il combattra contre elles, et il s'en rendra maître.
“Mmodzi wochokera ku banja la mkaziyo adzadzuka nadzalamulira mʼmalo mwake. Iye adzamenyana ndi ankhondo a mfumu ya kumpoto ndi kulowa mʼmalo ake otetezedwa; adzachita nawo nkhondo ndi kupambana.
8 Et il transportera en Égypte, avec les captifs, leurs dieux et leurs statues de fonte et leurs objets précieux d'argent et d'or; et lui-même subsistera plus longtemps que le roi de l'aquilon.
Iye adzalandanso milungu yawo, mafano awo achitsulo, ndi ziwiya zawo zamtengowapatali zasiliva ndi golide ndi kubwerera nazo ku Igupto. Adzaleka osayithira nkhondo mfumu ya kumpoto kwa zaka zingapo.
9 Celui-ci à son tour entrera dans le royaume du roi du midi, puis il retournera en sa propre terre.
Kenaka mfumu ya kumpoto idzathira nkhondo dziko la mfumu ya kummwera koma idzalephera ndi kubwerera kwawo.
10 Et ses fils parmi maintes nations rassembleront une grande multitude; et l'un d'eux se mettra en campagne; et en sa marche il s'avancera comme un torrent débordé; il passera, il campera et rassemblera, ses forces pour le combat.
Ana ake adzakonzekera nkhondo ndi kusonkhanitsa gulu lankhondo lalikulu, limene lidzathira nkhondo mfumu yakummwera ngati chigumula mpaka kumalo ake otetezedwa.
11 Et le roi du midi s'effarouchera, et il s'avancera pour combattre le roi de l'aquilon; et il lèvera une grande armée, et une grande multitude d'ennemis lui sera livrée.
“Kenaka mfumu yakummwera idzatuluka mokwiya ndi kumenya nkhondo ndi mfumu yakumpoto, imene idzasonkhanitsa gulu lalikulu la nkhondo, koma idzayigonjetsa.
12 Et il prendra captive cette multitude, et son cœur s'enorgueillira, et il massacrera des myriades d'ennemis; mais il n'en sera pas plus puissant.
Gulu la nkhondoli likadzagwidwa, mfumu yakummwera idzayamba kudzikuza ndipo idzapha anthu miyandamiyanda, koma kupambanaku sikudzapitirira.
13 Car le roi de l'aquilon reviendra, et il conduira des troupes en plus grand nombre que la première fois; et à la fin des temps et des années une armée envahissante arrivera avec une grande force et de grands approvisionnements.
Popeza mfumu ya kumpoto idzasonkhanitsa gulu lina lankhondo, lochulukirapo kuposa loyamba; ndipo patapita zaka zingapo idzabwera ndi chigulu chachikulu cha nkhondo chokonzekeratu ndi zida.
14 Et en ce temps-là plusieurs se soulèveront contre le roi du midi, et des fils de ton peuple s'élèveront comme un fléau pour accomplir une vision; mais ils manqueront de force.
“Nthawi imeneyo ambiri adzawukira mfumu ya kummwera. Anthu achisokonezo pakati panu nawonso adzawukira pokwaniritsa masomphenya, koma sadzapambana.
15 Car le roi de l'aquilon s'avancera; il élèvera des terrasses; il prendra des villes fortes; et les bras du roi du midi soutiendront le choc, et ses troupes d'élite se lèveront; mais ils ne seront pas de force à résister.
Kenaka mfumu ya kumpoto idzafika ndikuzinga mzinda powunda nthumbira za nkhondo ndipo idzagonjetsa mzinda wotetezedwa. Gulu lankhondo la kummwera lidzasowa mphamvu; ngakhale akatswiri awo ankhondo sadzakhala ndi mphamvu zogonjetsera ankhondo a kumpoto.
16 Et le roi de l'aquilon, après l'avoir ainsi envahi, fera tout ce qu'il voudra, et nul ne tiendra devant lui. Et il s'arrêtera en la terre de Sabé; et il la détruira de sa main.
Mfumu ya kumpoto idzachita zofuna zake; palibe aliyense adzayigonjetse. Idzakhazikitsa ulamuliro wake mu Dziko Lokongola. Zonse zidzakhala mu ulamuliro wa mfumu yakumpoto ija.
17 Et il tournera son visage pour entrer en forces dans le royaume du midi, et toutes choses prospèreront devant lui; il donnera au roi ennemi une fille des femmes pour le perdre; mais il n'y réussira point, et elle ne sera pas à lui.
Idzafika ndi mphamvu za ufumu wake wonse ndipo idzayesa kuchita pangano la mtendere ndi mfumu ya kummwera. Ndipo idzamupatsa mwana wake wamkazi kuti amukwatire ndi cholinga cholanda ufumu, koma zolinga zake sizidzatheka kapena kumuthandiza.
18 Alors il tournera son visage contre les îles, et il en prendra plusieurs; et il arrêtera d'abord les princes de son opprobre; mais son opprobre retombera sur lui.
Kenaka idzatembenukira ku mayiko a mʼmbali mwa nyanja ndi kulanda mizinda yambiri, koma mtsogoleri wina wa nkhondo adzathetsa kudzikuza kwakeko ndipo adzabwezera chipongwecho kwa iye.
19 Et il retournera son visage vers la force de sa terre; mais il sera affaibli, et il tombera, et on ne le retrouvera plus.
Zikadzatha izi, mfumu idzabwerera ku malo otetezedwa a dziko la kwawo koma idzapunthwa ndi kugwa osapezekanso.
20 Et de sa racine s'élèvera un rejeton qui sera comme un plant sur le trône qu'il occupait avec gloire. Et en ces jours-là il sera encore brisé, mais non en face, non dans un combat.
“Mfumu imene idzatenga malo ake idzatumiza wokhometsa msonkho kuti chuma cha ufumu wake chichuluke. Komabe mʼzaka zochepa mfumuyo idzawonongedwa osati mu mkwiyo kapena ku nkhondo.
21 Un autre prendra sa place, qui sera méprisé; on ne lui aura point accordé les honneurs de la royauté; mais il viendra avec ruse, et à force d'artifices il se rendra maître du royaume,
“Mʼmalo mwake mudzalowa munthu wonyozeka amene si wa banja laufumu. Iye adzabwera pamene anthu akuganiza kuti ali pa mtendere, ndipo adzalanda ufumuwo mwa chinyengo.
22 Et les bras de son adversaire seront énervés devant sa face; ils seront brisés, ainsi que le chef de l'alliance.
Kenaka adzagonetsa gulu lalikulu lankhondo kuphatikizapo Mkulu wa Ansembe wapangano.
23 Et après leur traité, il trompera encore celui-ci; il s'avancera, et prévaudra sur lui avec un petit nombre de troupes.
Atatha kuchita naye pangano, iye adzachita monyenga, ndipo ngakhale adzakhale ndi anthu ochepa adzakhalabe ndi mphamvu.
24 Il viendra en des régions paisibles et opulentes; et il fera ce que n'ont fait ni ses pères ni les pères de ses pères; il emportera leur butin, leurs dépouilles, leurs richesses, et il concevra de mauvais desseins contre l'Égypte; mais cela n'aura qu'un temps.
Mwadzidzidzi, iye adzazithira nkhondo zigawo zolemera kwambiri ndipo adzachita zimene makolo ake ngakhale agogo ake sanachitepo. Iye adzagawira zolanda, zofunkha ndi chuma kwa omutsatira. Adzachita chiwembu cholanda mizinda yotetezedwa koma kwa kanthawi kochepa.
25 Et sa force et son cœur s'élèveront avec une grande force contre le roi du midi; et le roi du midi soutiendra aussi la guerre avec une force très grande et très redoutable; mais ses armées ne tiendront pas, parce que de mauvais desseins auront été formés contre lui.
“Mfumu ya kumpoto idzalimba mtima, ndipo idzasonkhanitsa gulu lalikulu la ankhondo kuti lithire nkhondo mfumu yakummwera. Mfumu yakummwera ndi gulu lake lankhondo lalikulu ndi lamphamvu idzathirana nkhondo ndi mfumu yakumpoto koma sidzapambana chifukwa cha ziwembu zimene adzamukonzera.
26 On mangera avec lui; puis on le brisera, et son ennemi engloutira ses armées, et les morts tomberont en foule.
Amene amadya chakudya ndi mfumu adzamuukira; gulu lake lankhondo lidzagonjetsedwa, ndipo ambiri adzafera ku nkhondo.
27 Et les deux rois, le cœur plein de perversité, assis à la même table, se diront des mensonges; mais cela ne réussira pas, parce que leur fin arrivera au temps marqué.
Mafumu awiriwa mitima yawo idzalinga ku zoyipa. Azidzanamizana ali pa tebulo limodzi, koma zolinga zawo sizidzatheka chifukwa nthawi idzakhala isanakwane.
28 Et le roi de l'aquilon retournera en sa terre avec de grandes richesses; et son cœur sera opposé à l'alliance sainte, et il fera de grandes choses, et il rentrera dans son royaume.
Mfumu ya kumpoto idzabwerera ku dziko la kwawo ndi chuma chambiri, koma mtima wake udzafunitsitsa pangano lopatulika. Idzawononga panganolo ndipo kenaka idzabwerera ku dziko lake.
29 Il reviendra au temps marqué, et marchera contre le midi; mais cette dernière invasion ne sera pas comme la première.
“Patapita nthawi mfumu ya kumpoto idzabwereranso kummwera koma sidzapambana monga inachitira kale.
30 Les Citians, sortis de leurs pays, marcheront contre lui; et par eux il sera abaissé, et il battra en retraite; il s'irritera contre l'alliance sainte, et agira contre elle; puis il se remettra en campagne, et s'entendra avec ceux qui auront abandonné l'alliance sainte.
Sitima zapamadzi zochokera ku mayiko a ku madzulo zidzalimbana naye, ndipo adzataya mtima. Kenaka idzabwerera mopsa mtima ndi kudzalimbana ndi chipembedzo cha anthu opatulika. Idzabwerera ndi kuchitira chifundo amene sadzasunga pangano loyera.
31 Et des rejetons de lui s'élèveront, et ils profaneront le sanctuaire de la Toute-Puissance, et ils feront cesser le sacrifice perpétuel, et ils le remplaceront par l'abomination de la désolation.
“Ankhondo ake adzayipitsa linga la Nyumba ya Mulungu ndipo adzathetsa nsembe za tsiku ndi tsiku. Kenaka adzakhazikitsa chonyansa chimene chabweretsa chiwonongeko.
32 Et les impies feront alliance entre eux pour faire le mal; mais un peuple connaissant son Dieu prévaudra et agira vaillamment.
Ndi mawu oshashalika mfumuyo idzakopa amene anaphwanya pangano, koma anthu amene amadziwa Mulungu wawo adzalimbika ndipo adzayikana mfumuyo kwathunthu.
33 Et les sages du peuple comprendront beaucoup de choses; toutefois ils seront affaiblis par le glaive, par le feu, par la captivité, et par un pillage qui durera bien des jours.
“Amene ndi anzeru adzalangiza ambiri. Koma patapita kanthawi adzaphedwa ndi lupanga kapena kutenthedwa, kapena kugwidwa kapena kulandidwa katundu.
34 Et dans leur détresse ils recevront un faible secours; mais plusieurs se joindront à eux avec des vues perfides,
Pa nthawi yozunzikayi ena adzawathandiza pangʼono, koma ambiri othandizawo adzakhala achinyengo.
35 Et parmi les sages quelques-uns auront beaucoup à souffrir pour être purifiés, élus et manifestés aux derniers jours; car ces choses doivent s'accomplir au temps marqué.
Ena mwa anzeruwo adzaphedwa ndi cholinga chakuti ayengedwe, otsala mwa iwo ayeretsedwe ndi kukhala wopanda banga kufikira nthawi yomaliza, popeza idzafika ndithu nthawi imene Mulungu wayika.
36 Et le roi fera selon sa volonté; il s'élèvera, et il se glorifiera contre toute divinité, et il parlera un langage superbe, et il prospèrera jusqu'à ce que la colère de Dieu s'accomplisse; car cela doit finir ainsi.
“Mfumu ya kumpoto idzachita zimene ikufuna. Idzadzikweza ndi kudziyesa yopambana mulungu aliyense ndipo idzanenera za mwano Mulungu wa milungu. Iyo idzapambana mpaka nthawi yoti Mulungu ayilange mwa mkwiyo itakwana popeza chimene chatsimikizika chiyenera kuchitika.
37 Et il ne reconnaîtra aucun des dieux de ses pères; il sera épris des femmes, et ne reconnaîtra aucun dieu; car il se croira plus grand qu'eux tous.
Mfumuyo idzanyoza milungu ya makolo ake ndiponso mulungu wokondedwa ndi akazi, sidzachitiranso ulemu mulungu aliyense, koma idzadzikweza yokha pamwamba pa onse.
38 Et il honorera le dieu Maozim en son temple, et il le glorifiera en lui offrant de l'or, de l'argent, des pierres précieuses et des choses de prix, ce dieu que ses pères ne connaissaient pas.
Mʼmalo mwa onsewo, idzachitira ulemu mulungu wachitetezo; mulungu wosadziwika ndi makolo ake. Iyo idzapereka kwa mulunguyo golide ndi siliva, ndi miyala yokongola, ndiponso mphatso za pamwamba kwambiri.
39 Et il donnera place dans les forteresses de refuge à un dieu étranger; il multipliera ses honneurs; il lui assujettira beaucoup d'hommes, et il partagera la terre pour en faire des présents.
Anthu opembedza mulungu wachilendo adzakhala ngati linga lake. Idzalemekeza iwowa kwambiri, ndipo idzawayika kuti alamulire anthu ambiri. Idzawagawira dziko ngati malipiro awo.
40 Et au temps marqué il sera aux prises avec le roi du midi; et le roi de l'aquilon conduira contre lui une multitude de chars, de cavaliers, de vaisseaux, et il envahira sa terre, et il la traversera, et il la foulera aux pieds.
“Pa nthawi yomaliza mfumu yakummwera idzachita nkhondo ndi mfumu yakumpoto. Koma mfumu yakumpotoyi idzayikantha ndi magaleta ndi akavalo ndi sitima zapamadzi zambiri ngati mphepo yamkokomo. Idzalowa mʼmayiko ambiri ndikuwakokolola onse ngati madzi osefukira.
41 Et il entrera dans la terre de Sébaïm, et beaucoup succomberont. Et voici ceux qui échapperont à sa main: Édom, Moab et la principauté des fils d'Ammon.
Idzalowanso mʼDziko Lokongola ndipo anthu ambiri adzaphedwa. Koma Edomu, Mowabu ndi olamulira a Amoni adzapulumuka.
42 Et il étendra son bras sur la terre de Palestine, et l'Égypte ne sera pas sauvée.
Idzathira nkhondo mayiko ambiri ndipo ngakhale Igupto sadzapulumuka.
43 Et il se rendra maître des lieux où sont cachés l'or et l'argent et tout ce qu'il y a de précieux en Égypte, en Libye et en Éthiopie, et dans leurs forteresses.
Idzalanda chuma cha golide, siliva, ndi zonse za mtengowapatali za ku Igupto, ndiponso anthu a ku Libiya ndi Akusi adzagonja kwa iwo.
44 Puis des rumeurs, des nouvelles pressantes, de l'orient et du nord, le troubleront; et il viendra plein de colère pour exterminer beaucoup d'ennemis.
Koma uthenga wochokera kummawa ndi kumpoto udzayiopsa, ndipo idzapita ndi ukali kukawononga ndi kutheratu anthu ambiri.
45 Et il dressera les tentes de son palais entre les mers, sur la montagne sainte de Sébaïn, et il y viendra jusqu'à sa fin, et nul ne pourra le sauver.
Mfumuyo idzayimika matenti ake aufumu, pakati pa nyanja ndi phiri lokongola. Komabe mapeto ake mfumuyo idzaphedwa, ndipo palibe amene adzayithandize.”

< Daniel 11 >