< Amos 8 >
1 Ceci est la vision que m'a envoyé le Seigneur Dieu; voilà un vase d'oiseleur à la glu.
Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: dengu la zipatso zakupsa.
2 Et le Seigneur me dit: Que vois-tu, Amos? et je dis: Un vase d'oiseleur à la glu; et le Seigneur me dit: La fin de Mon peuple d'Israël est arrivée; Je ne continuerai plus de Me montrer à lui.
Iye anandifunsa kuti, “Amosi nʼchiyani ukuona?” Ine ndinayankha kuti, “Dengu la zipatso zakupsa.” Ndipo Yehova anati kwa ine, “Nthawi yachimaliziro yawakwanira anthu anga Aisraeli; sindidzawakhululukiranso.
3 Et en ce jour-là les lambris du temple pousseront des cris de douleur, dit le Seigneur. Une multitude d'hommes tomberont en tous lieux; et J'étendrai sur eux le silence.
“Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akulengeza kuti, “Nyimbo za mʼNyumba ya Mulungu zidzasanduka kulira kofuwula. Mitembo ya anthu idzachuluka, ndipo adzayiponya ponseponse! Kudzangoti zii!”
4 Écoutez donc ces choses, vous qui le matin opprimez l'indigent, et qui foulez aux pieds les pauvres de la terre,
Imvani izi, inu amene mumapondereza anthu osowa ndipo simulabadira anthu osauka a mʼdzikomu.
5 disant: Quand donc le mois sera-t-il écoulé pour que nous vendions? Quand finira le sabbat pour que nous ouvrions nos greniers, que nous fassions petite mesure, que nous augmentions les poids et faussions le balance;
Mumanena kuti, “Kodi chikondwerero cha mwezi watsopano chidzatha liti kuti tigulitse zinthu? Ndipo tsiku la Sabata litha liti kuti tigulitse tirigu, kuti tichepetse miyeso, kukweza mitengo kuti tibere anthu ndi miyeso ya chinyengo,
6 pour que nous achetions le pauvre à prix d'argent; l'indigent pour des sandales, et que nous trafiquions sur toutes les denrées?
tigule osauka ndi ndalama zasiliva ndi osowa powapatsa nsapato, tigulitse ngakhale mungu wa tirigu?”
7 Le Seigneur fait serment de punir l'orgueil de Jacob: Nulle de vos œuvres, en Ma victoire, ne sera oubliée.
Yehova amene Yakobo amamunyadira, walumbira kuti: Ine sindidzayiwala chilichonse chimene anachita.
8 Et n'est-ce pas à cause de ces choses que la terre sera troublée, que tous ceux qui l'habitent seront dans la douleur; et que la destruction montera comme le fleuve d'Égypte, et descendra comme lui?
“Kodi dziko silidzagwedezeka chifukwa cha zimenezi, ndi onse okhala mʼmenemo kulira mwachisoni? Dziko lonse lidzavunduka ngati mtsinje wa Nailo; lidzagwedezeka kenaka nʼkukhala bata ngati mtsinje wa ku Igupto.
9 En ce jour-là ceci arrivera, dit le Seigneur Maître: Le soleil se couchera à Midi, et sur la terre, la lumière fera place aux ténèbres,
“Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akunena kuti, “Ndidzadetsa dzuwa masana ndi kugwetsa mdima pa dziko lapansi dzuwa likuswa mtengo.
10 et Je changerai vos fêtes en deuil, et tous vos cantiques en lamentations; et je ceindrai vos reins de cilices, et toute tête deviendra chauve; et Israël pleurera, comme on pleure un bien-aimé, et ceux qui l'accompagneront souffriront comme en un jour de douleurs.
Maphwando anu achipembedzo ndidzawasandutsa kulira kwa chisoni ndipo kuyimba kwanu konse ndidzakusandutsa maliro. Ndidzakuvekani chiguduli nonsenu ndi kumeta mipala mitu yanu. Nthawi imeneyo idzakhala ngati yolira mwana wamwamuna mmodzi yekhayo, ndipo tsikulo lidzakhala lowawa mpaka kutha kwake.
11 Voilà que ces jours arrivent, dit le Seigneur, et J'enverrai la famine sur la terre, non la disette de pain et d'eau, mais la soif d'entendre la parole du Seigneur.
“Nthawi ikubwera,” Ambuye Yehova akunena kuti, “Ndidzagwetsa njala mʼdziko lonse; osati njala ya chakudya kapena ludzu la madzi, koma njala yofuna kumva mawu a Yehova.
12 Et d'une mer à l'autre les hommes seront agités, et du nord au levant ils courront, cherchant la parole du Seigneur, et ils ne la trouveront pas.
Anthu azidzangoyendayenda kuchoka ku nyanja ina kupita ku nyanja ina. Azidzangoyendayenda kuchoka kumpoto kupita kummawa, kufunafuna mawu a Yehova, koma sadzawapeza.
13 En ce jour-là, les vierges les plus belles et les jeunes hommes tomberont de soif.
“Tsiku limenelo “anamwali okongola ndi anyamata amphamvu adzakomoka ndi ludzu.
14 Ceux qui jurent par la propitiation de Samarie, et disent: Vive ton Dieu, Dan! vive ton Dieu, Bersabée! ceux-là tomberont et ne se relèveront plus.
Onse amene amalumbira pa tchimo la Samariya, kapena kumanena kuti, ‘Iwe Dani, pali mulungu wako wamoyo,’ kapena, ‘Pali mulungu wamoyo wa ku Beeriseba.’ Iwowo adzagwa ndipo sadzadzukanso.”