< Amos 6 >

1 Malheur à ceux qui méprisent Sion, et qui mettent leur confiance en la montagne de Samarie! Ils ont recueilli les prémices des nations, puis ils sont entrés.
Tsoka kwa amene simukulabadira kanthu ku Ziyoni, ndiponso kwa inu amene mukukhala mwamtendere pa Phiri la Samariya, inu anthu otchuka ochokera ku mtundu wa anthu omveka, kumene Aisraeli amafikako!
2 Passez tous auprès, et voyez; et de là traversez Ématrabba, et de là descendez à Geth des Philistins; ce sont les plus puissants de tous les royaumes. Voyez si leurs frontières sont plus étendues que vos frontières.
Pitani ku mzinda wa Kaline mukawuyangʼane; mukapitenso ku Hamati-raba mzinda waukulu uja, ndipo mukatsikirenso ku Gati kwa Afilisti. Kodi mizinda imeneyi ndi yopambana maufumu anu awiriwa? Kodi dziko lawo ndi lalikulu kupambana lanu?
3 Vous qui venez pour le mauvais jour, vous qui approchez des sabbats trompeurs, et vous y attachez;
Inu simulabadirako kuti tsiku loyipa lidzafika, zochita zanu zimafulumizitsa ulamuliro wankhanza.
4 vous qui dormez sur des lits d'ivoire, et vous y étendez pour vivre avec mollesse; vous qui mangez les chevreaux de votre menu bétail, et de jeunes veaux tirés de vos troupeaux et nourris de lait;
Mumagona pa mabedi owakongoletsa ndi minyanga ya njovu, mumagona pa mipando yanu ya wofuwofu. Mumadya ana ankhosa onona ndi ana angʼombe onenepa.
5 vous qui battez des mains au son des instruments! Ils ont cru que ces choses seraient durables, et non fugitives.
Mumayimba azeze anu ndi kumangopeka nyimbo pa zingʼwenyengʼwenye ngati Davide.
6 Vous qui buvez du vin clarifié, et vous parfumez de la meilleure myrrhe, et ne souffrez nullement de l'affliction de Joseph.
Mumamwera vinyo mʼzipanda zodzaza ndipo mumadzola mafuta abwino kwambiri, koma simumva chisoni ndi kuwonongeka kwa Yosefe.
7 À cause de cela, ils passeront de la puissance des forts à la captivité, et l'on n'entendra plus le hennissement des chevaux en Éphraïm.
Nʼchifukwa chake inu mudzakhala mʼgulu la anthu oyamba kupita ku ukapolo; maphwando ndi zikondwerero zanu zidzatheratu.
8 Car le Seigneur en Lui-même a juré, disant: Puisque J'ai en abomination toute l'insolence de Jacob, j'ai pris également en haine leurs contrées, J'effacerai donc la ville avec tous ceux qui l'habitent.
Ambuye Yehova walumbira mʼdzina lake. Yehova Mulungu Wamphamvuzonse walengeza kuti, “Ndimanyansidwa ndi kunyada kwa Yakobo, ndimadana ndi nyumba zake zaufumu; Ine ndidzawupereka mzindawu pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.”
9 Et voici ce qui arrivera: Si dans une maison il y a dix hommes, ils mourront; et ceux qui y resteront cachés mourront aussi.
Ngati anthu khumi otsala adzabisala mʼnyumba imodzi, nawonso adzafa ndithu.
10 Et leurs parents les prendront, et ils se feront violence pour enlever leurs os de la maison; et l'on dira au chef de la maison: Y a-t-il encore quelqu'un avec toi? Et celui-ci répondra: Il n'y a personne; et le premier répondra: Tais-toi, garde-toi de prononcer le Nom du Seigneur.
Ndipo ngati mʼbale wake wa wina wakufayo, woyenera kusamala za maliro, adzafika kudzatulutsa mitembo mʼnyumbamo nʼkufunsa aliyense amene akubisalabe mʼnyumbamo kuti, “Kodi uli ndi wina wamoyo mʼmenemo?” Ndipo munthu wobisalayo ndi kuyankha kuti, “Ayi,” mʼbaleyo adzanena kuti, “Khala chete! Ife tisayerekeze kutchula dzina la Yehova.”
11 Car voilà que le Seigneur a donné Ses ordres; et Il frappera les grandes maisons pour ouvrir des brèches, et les petites pour y faire des crevasses.
Pakuti Yehova walamula kuti nyumba zikuluzikulu Iye adzazigamulagamula, ndipo nyumba zazingʼono zidzasanduka maduka okhaokha.
12 Les chevaux peuvent-ils courir au milieu des rochers? Peuvent-ils s'empêcher de hennir au milieu des cavales? Vous qui à la place du jugement avez mis la colère, et qui avez changé en amertume les fruits de la justice;
Kodi akavalo amathamanga pa thanthwe? Kodi wina amatipula ndi ngʼombe mʼnyanja? Koma chiweruzo cholungama mwachisandutsa kukhala zinthu zakupha ndipo chipatso cha chilungamo mwachisandutsa kukhala chowawa.
13 vous qui mettez votre joie dans le néant; vous qui dites: N'est-ce point par notre force que nous avons des fronts puissants?
Inu amene mukunyadira kuti munagonjetsa Lo Debara ndipo mukunena kuti, “Kodi sitinatenge Karinaimu ndi mphamvu zathu zokha?”
14 Maison d'Israël, J'exciterai contre vous une nation, dit le Seigneur Dieu des armées; et elle vous brisera depuis l'entrée d'Émath jusqu'au torrent du désert d'Occident.
Koma Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akulengeza kuti, “Inu nyumba ya Israeli, ndidzakudzutsirani mtundu wina wa anthu umene udzakuzunzani kuchokera ku Lebo Hamati mpaka ku Chigwa cha Araba.”

< Amos 6 >