< Amos 5 >

1 Écoutez cette parole du Seigneur que j'ai recueillie à votre sujet, écoutez cette plainte: la maison d'Israël est tombée, jamais elle ne se relèvera.
Israeli, imva mawu awa, nyimbo ya maliro imene ndikuyimba za iweyo:
2 La vierge d'Israël est tombée sur la terre, nul ne pourra la remettre debout.
“Namwali Israeli wagwa, moti sadzadzukanso, wasiyidwa mʼdziko lake lomwe, popanda woti ndi kumudzutsa.”
3 À cause de cela, le Seigneur Dieu dit ces choses: La ville d'où sortaient mille hommes, il en sera laissé cent; celle d'où sortaient cent hommes, il en sera laissé dix en la maison d'Israël.
Ambuye Yehova akuti, “Mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 1,000 amphamvu udzatsala ndi anthu 100 okha; mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 100 amphamvu udzatsala ndi anthu khumi okha basi.”
4 C'est pourquoi, voici ce que dit le Seigneur à la maison d'Israël: Cherchez-Moi, et vous vivrez;
Zimene Yehova akunena kwa nyumba ya Israeli ndi izi: “Mundifunefune kuti mukhale ndi moyo;
5 mais ne cherchez point Béthel, et n'allez point en Galgala, et ne dépassez point le puits du serment; car Galgala sera emmenée captive, et Béthel sera comme n'étant plus.
musafunefune Beteli, musapite ku Giligala, musapite ku Beeriseba. Pakuti Giligala adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, ndipo Beteli adzawonongekeratu.”
6 Cherchez le Seigneur et vivez, de peur que la maison de Joseph ne brûle comme un feu, et ne vous dévore; car nul ne sera là pour éteindre l'incendie en la maison d'Israël.
Funani Yehova kuti mukhale ndi moyo, mukapanda kutero Iye adzatentha nyumba ya Yosefe ngati moto; motowo udzawononga, ndipo sipadzakhala wina wozimitsa motowo ku Beteli.
7 Celui qui juge du haut des cieux, a de même établi la justice sur la terre.
Inu amene mumasandutsa chiweruzo cholungama kukhala chowawa ndi kunyoza chilungamo.
8 Celui qui a créé toutes choses les change à Son gré: Il change les ténèbres en matin; Il change le jour en nuit sombre; c'est Lui qui appelle l'eau de la mer, qui la répand sur la surface de la terre; le Seigneur est Son Nom
(Iye amene analenga nyenyezi za Nsangwe ndi Akamwiniatsatana, amene amasandutsa mdima kuti ukhale mmawa ndi kudetsa usana kuti ukhale usiku, amene amayitana madzi a mʼnyanja ndi kuwathira pa dziko lapansi, Yehova ndiye dzina lake.
9 Lui qui amène la ruine contre la force, et déchaîne la misère contre le lieu fortifié.
Iyeyo amabweretsa chiwonongeko modzidzimutsa pa anthu amphamvu ndi kuwononga mizinda yotetezedwa),
10 Ils ont haï l'homme qui les réprimandait devant leurs portes, et ils ont eu en abomination la parole sainte.
inu mumadana ndi amene amadzudzula mʼbwalo la milandu ndi kunyoza amene amanena zoona.
11 À cause de cela, et en punition de ce que vous avez frappé du poing les pauvres, et de ce que vous avez accepté d'eux de beaux présents, bâtissez des maisons de pierres de taille, et vous ne les habiterez pas; plantez des vignes excellentes, et vous n'en boirez pas le vin;
Mumapondereza munthu wosauka ndi kumukakamiza kuti akupatseni tirigu. Nʼchifukwa chake, ngakhale mwamanga nyumba zamiyala yosema, inuyo simudzakhalamo. Ngakhale mwalima minda yabwino ya mphesa, inu simudzamwa vinyo wake.
12 car Je connais vos nombreuses impiétés, et vos péchés sont grands; vous foulez aux pieds la justice; pour juger, vous prenez des présents; et vous vous détournez des pauvres devant les portes de la ville.
Pakuti Ine ndikudziwa kuchuluka kwa zolakwa zanu ndi kukula kwa machimo anu. Inu mumapondereza anthu olungama ndi kulandira ziphuphu ndipo anthu osauka simuwaweruza mwachilungamo mʼmabwalo anu amilandu.
13 C'est pourquoi l'homme intelligent, en ces temps-là, gardera le silence; car c'est le temps de la perversité.
Nʼchifukwa chake pa nthawi yotere munthu wanzeru sayankhulapo kanthu, popeza ndi nthawi yoyipa.
14 Cherchez le bien et non le mal, afin que vous viviez; et, de cette manière, le Seigneur Dieu tout-puissant sera avec vous. Comme vous avez dit:
Muyike mtima wanu pa zabwino osati pa zoyipa, kuti mukhale ndi moyo. Mukatero Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzakhala nanu, monga mmene mumanenera kuti ali nanu.
15 Nous avons haï le mal, et nous aimons le bien; faites revivre la justice devant les portes de la ville, afin que le Seigneur Dieu tout-puissant ait pitié des restes de Joseph.
Mudane ndi zoyipa, mukonde zabwino; mukhazikitse chiweruzo cholungama mʼmabwalo anu amilandu. Mwina mwake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzachitira chifundo anthu otsala a mʼbanja la Yosefe.
16 À cause de cela, voici ce que dit le Seigneur Dieu tout-puissant: On se frappera la poitrine sur toutes les places; et dans toutes les rues on criera: Malheur! malheur! On appellera le laboureur à ce deuil et à cette plainte, pour qu'il se joigne à ceux qui savent se lamenter.
Choncho izi ndi zimene Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, akunena: “Mʼmisewu monse mudzakhala kulira mofuwula, ndi kulira chifukwa cha kuwawa kwa masautso kudzakhala paliponse. Adzayitana alimi kuti adzalire, ndipo anthu odziwa maliridwe anthetemya adzalira mofuwula.
17 Et sur toutes les voies on se frappera la poitrine, parce que Je viendrai au milieu de vous, dit le Seigneur.
Mʼminda yonse ya mpesa mudzakhala kulira kokhakokha, pakuti Ine ndidzadutsa pakati panu,” akutero Yehova.
18 Malheur à ceux qui désirent le jour du Seigneur. Et pourquoi ce jour-là est-il pour vous le jour du Seigneur? C'est que ce jour est ténèbres, et non lumière.
Tsoka kwa inu amene mumalakalaka tsiku la Yehova! Chifukwa chiyani mumalakalaka tsiku la Yehova? Tsikulo kudzakhala mdima osati kuwala.
19 Vous serez comme un homme qui s'enfuit en voyant un lion, puis aussitôt rencontre une ourse; et qui, si il bondit jusqu'à sa demeure, s'il appuie sa main contre le mur, est mordu par un serpent.
Lidzakhala ngati tsiku limene munthu pothawa mkango amakumana ndi chimbalangondo, ngati pamene munthu walowa mʼnyumba, natsamira dzanja lake pa khoma ndipo njoka nʼkuluma.
20 Le jour du Seigneur n'est-il pas ténèbres, et non lumière? Ce jour n'est- il pas obscurité sans la moindre lueur?
Kodi tsiku la Yehova silidzakhala mdima osati kuwala, mdima wandiweyani, popanda powala pena paliponse?
21 Je hais, Je répudie vos fêtes; Je ne puis souffrir l'odeur de vos victimes en vos solennités.
“Ndimadana nawo masiku anu achikondwerero ndipo ndimawanyoza; sindikondwera nayo misonkhano yanu.
22 Si donc vous M'offrez des holocaustes et des sacrifices, Je ne les agréerais pas; Je n'aurai point égard à vos hosties pacifiques.
Ngakhale mupereke nsembe zopsereza ndi nsembe zachakudya, Ine sindidzazilandira. Ngakhale mupereke nsembe zabwino zachiyanjano, Ine sindidzaziyangʼana nʼkomwe.
23 Éloignez de Moi les bruit de vos cantiques, Je n'écouterai pas le son de vos harpes.
Musandisokose nazo nyimbo zanu! Sindidzamvetsera kulira kwa azeze anu.
24 Et Mon jugement roulera comme une pluie violente, et Ma justice comme un torrent où l'on ne peut naviguer.
Koma chiweruzo cholungama chiyende ngati madzi, chilungamo ngati mtsinje wosaphwa!
25 Maison d'Israël, ne M'avez-vous pas offert des sacrifices et des victimes durant quarante ans dans le désert?
“Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?
26 Vous avez élevé le tabernacle de Moloch, et l'étoile de votre dieu Raiphan, et leurs images que vous aviez fabriqués.
Inu mwanyamula kachisi wa mfumu yanu, ndi nyenyezi ija Kaiwani, mulungu wanu, mafano amene munadzipangira.
27 Et Je vous ferai émigrer au delà de Damas, dit le Seigneur; le Dieu tout- puissant est Son Nom.
Nʼchifukwa chake Ine ndidzakupititsani ku ukapolo, kutali kupitirira ku Damasiko,” akutero Yehova, amene dzina lake ndi Mulungu Wamphamvuzonse.

< Amos 5 >