< Amos 2 >

1 Voici ce que dit le Seigneur: Ce n'est point à cause des triples et quadruples impiétés de Moab que Je le prendrai en aversion, c'est parce qu'il a brûlé les os du roi de l'Idumée, jusqu'à les réduire en poudre.
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Mowabu akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatentha mafupa a mfumu ya ku Edomu, mpaka kuwasandutsa phulusa,
2 Et Je lancerai la flamme sur Moab; et elle dévorera les fondations de ses villes, et Moab périra dans l'impuissance, au milieu des cris et au son des trompettes.
Ine ndidzatumiza moto pa Mowabu, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Keriyoti. Mowabu adzafera pakati pa nkhondo yoopsa, mʼkati mwa mfuwu wa nkhondo ndi kuliza malipenga.
3 Et Je détruira son juge, et J'exterminerai ses princes avec lui, dit le Seigneur.
Ndidzawononga wolamulira wake ndi kupha akuluakulu onse amene ali pamodzi ndi iye,” akutero Yehova.
4 Voici ce que dit le Seigneur: Ce n'est point à cause des triples et quadruples impiétés des fils de Juda que Je les prendrai en aversion, c'est parce qu'ils ont répudié la loi du Seigneur, et qu'ils n'ont point gardé les commandements, et que les vaines idoles qu'ils avaient fabriquées et qu'avaient suivies leurs pères les ont eux-mêmes égarés.
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Yuda akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza iwo akana lamulo la Yehova ndipo sanasunge malangizo ake, popeza asocheretsedwa ndi milungu yabodza, milungu imene makolo awo ankayitsatira,
5 Et Je lancerai la flamme sur Juda, et elle dévorera les fondations de Jérusalem.
Ine ndidzatumiza moto pa Yuda, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu.”
6 Voici ce que dit le Seigneur: Ce n'est point à cause des triples et quadruples impiétés d'Israël que Je le prendrai en aversion; c'est parce qu'il a livré le juste à prix d'argent, et le pauvre pour des sandales
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Israeli akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Iwo amagulitsa anthu olungama ndi siliva, ndi osauka ndi nsapato.
7 que l'on traîne dans la poussière des chemins; c'est parce qu'ils ont frappé du poing la tête de l'indigent, qu'ils ont fait dévier le faible, et que le fils et le père ont eu la même concubine, afin de profaner le Nom de leur Dieu,
Amapondereza anthu osauka ngati akuponda fumbi, ndipo sawaweruza mwachilungamo anthu oponderezedwa. Abambo ndi mwana wawo amagonana ndi mtsikana mmodzi yemweyo, ndipo potero amanyozetsa dzina langa loyera.
8 et parce que, liant avec des cordes leurs manteaux, ils en ont voilé l'autel, et bu le vin des calomnies, dans le temple de leur Dieu.
Anthuwo amakagonana mʼmbali mwa guwa lililonse la nsembe pa zovala zimene anatenga ngati chikole. Mʼnyumba ya mulungu wawo amamweramo vinyo amene analipiritsa anthu pa milandu.
9 Cependant c'est Moi qui ai, devant leur face, chassé l'Amorrhéen d'où il était; sa taille était celle du cèdre, sa force celle du chêne; et J'ai desséché ses fruits au-dessus de la terre, et ses racines au-dessous.
“Ine ndinawononga Aamori pamaso pawo, ngakhale iwo anali anthu ataliatali ngati mikungudza ndiponso amphamvu ngati mitengo ya thundu. Ndinawononga zipatso zawo ndiponso mizu yawo.
10 Et vous, Je vous ai ramenés de la terre d'Égypte, et Je vous ai conduits çà et là dans le désert, pendant quarante ans, pour vous donner ensuite en héritage la terre des Amorrhéens.
“Ine ndinakutulutsani ku Igupto, ndipo ndinakutsogolerani mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kudzakupatsani dziko la Aamori.
11 Et J'ai pris de vos fils pour en faire des prophètes, et de vos jeunes enfants pour Me les consacrer; tout cela n'est-il pas vrai, fils d'Israël? dit le Seigneur.
Ine ndinawutsanso ena mwa ana ako kuti akhale aneneri, ndi ena mwa anyamata ako kuti akhale anaziri. Kodi si choncho, inu Aisraeli?” akutero Yehova.
12 Et vous faites boire du vin aux Nazaréens, et vous donnez des ordres aux prophètes, disant: Ne prophétisez pas!
“Koma inu munawamwetsa vinyo anaziri aja, ndipo munalamula aneneri kuti asanenere.
13 Et, à cause de cela, voilà que Je vais rouler sur vous, comme un chariot rempli de paille.
“Tsono Ine ndidzakupsinjani monga imapsinjikira ngolo imene yadzaza ndi tirigu.
14 Et il n'y aura pas de fuite pour le coureur, et le fort ne pourra se prévaloir de sa force, et le guerrier ne sauvera pas sa vie;
Munthu waliwiro sadzatha kuthawa, munthu wamphamvu sadzakhalanso ndi nyonga, wankhondo sadzapulumutsa moyo wake.
15 et l'archer ne résistera pas, et l'homme aux pieds légers ne saura s'échapper, et le cavalier ne sauvera pas sa vie.
Munthu wa uta sadzalimbika, msilikali wothamanga kwambiri sadzapulumuka, ndipo wokwera pa akavalo sadzapulumutsa moyo wake.
16 Et le fort ne mettra plus son cœur en ses forces; et, nu, il s'enfuira en ce jour, dit le Seigneur.
Ngakhale asilikali olimba mtima kwambiri adzathawa ali maliseche pa tsikulo,” akutero Yehova.

< Amos 2 >