< 2 Samuel 4 >

1 Quand Isboseth, fils de Saül, apprit qu'Abner, fils de Ner, était mort à Hébron, ses bras en furent énervés, et tous les hommes d'Israël défaillirent.
Isiboseti mwana wa Sauli atamva kuti Abineri waphedwa ku Hebroni, anataya mtima ndipo Aisraeli onse anachita mantha kwambiri.
2 Or, il y avait deux chefs des troupes d'Isboseth, fils de Saül: l'un se nommait Baana, et l'autre Rhéchab; ils étaient fils de Rhemmon, de Bèroth de la tribu de Benjamin; car Bèroth était comptée parmi les villes de Benjamin.
Koma Isiboseti anali ndi anthu akuluakulu awiri amene ankatsogolera magulu a ankhondo. Mmodzi mwa iwo dzina lake linali Baana ndipo mnzakeyo anali Rekabu. Iwo anali ana a Rimoni wa banja la Beeroti wa fuko la Benjamini Beeroti. Iwo ankatengedwa ngati mbali imodzi ya Benjamini,
3 Ceux de Bèroth ont depuis émigré à Géthalin, où, de nos jours encore, ils sont colons.
chifukwa anthu a ku Beeroti anathawira ku Gitaimu ndipo akhala ali kumeneko ngati alendo mpaka lero lino.
4 Il restait de Jonathan, fils de Saül, un fils de cinq ans, infirme des pieds; car, lorsqu'on vint de Jezraël annoncer que Saül et Jonathan étaient morts, la nourrice de cet enfant le prit dans ses bras et s'enfuit. En se hâtant de l'éloigner, elle le laissa tomber, et il resta boiteux; il se nommait Miphiboseth.
(Yonatani mwana wa Sauli anali ndi mwana wamwamuna amene anali wolumala mapazi ake onse awiri. Iye anali ndi zaka zisanu pamene nkhani ya Sauli ndi Yonatani inamveka kuchokera ku Yezireeli. Amene amamulera anamunyamula ndi kuthawa naye, koma pamene amachita zinthu mofulumira mwanayo anagwa ndipo analumala. Dzina lake linali Mefiboseti).
5 Et les fils de Rhemmon le Bérothéen, Rhéchab et Baana partirent; et, par la grande chaleur du jour, ils entrèrent chez Isboseth, comme il dormait sur un lit de repos, à l'heure de midi.
Choncho Rekabu ndi Baana ana a Rimoni wa ku Beeroti ananyamuka kupita ku nyumba ya Isi-Boseti, ndipo anafika nthawi ya masana kukutentha pamene iye amapumula.
6 Le gardien de la porte avait vanné du froment, sa tête s'était affaissée, et il s'était endormi; Rhéchab et Baana poussèrent donc plus avant.
Iwo analowa mʼchipinda chamʼkati ngati kuti amakatenga tirigu, ndipo anamulasa mʼmimba. Kenaka Rekabu ndi mʼbale wake Baana anathawa.
7 Ils pénètrent dans la maison où Isboseth dormait sur son lit de repos, en sa chambre à coucher; ils le frappent, le tuent, lui tranchent la tête, qu'ils emportent, et marchent toute la nuit du côté de l'occident.
Iwo analowa mʼnyumbamo iye akugona pa bedi mʼchipinda chake. Atamulasa ndi kumupha, anadula mutu wake nʼkuwutenga, nayenda usiku wonse mʼnjira yopita ku Araba.
8 Et ils portèrent à David, en Hébron, la tète d'Isboseth, et ils dirent au roi: Voici la tête d'Isboseth, fils de Saül, ton ennemi, qui te cherchait pour te faire périr; le Seigneur a achevé aujourd'hui de venger, de Saül et de sa race, le seigneur roi.
Iwo anabweretsa mutu wa Isi-Boseti kwa Davide ku Hebroni ndipo anati kwa mfumu, “Nawu mutu wa Isiboseti mwana wa Sauli, mdani wanu, amene anafuna kukuphani. Lero lino Yehova wabwezera mbuye wanga mfumu adani anu, Sauli ndi ana ake.”
9 Et David répondit à Rhéchab et à Baana son frère, fils de Rhemmon le Bérothéen, et il leur dit: Vive le Seigneur! le sauveur de mon âme en toutes ses afflictions,
Davide anayankha Rekabu ndi mʼbale wake Baana, ana a Rimoni wa ku Beeroti kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene wandipulumutsa ku mavuto anga onse,
10 Celui qui est venu m'annoncer la mort de Saül, et qui croyait m'apporter une bonne nouvelle, je l'ai saisi et l'ai fait mourir en Sécelac, où il s'attendait à recevoir une récompense.
pamene munthu wina anandiwuza kuti, ‘Sauli wafa’ ndipo ankaganiza kuti wabweretsa nkhani yabwino, ine ndinamugwira ndi kumupha ku Zikilagi. Iyi inali mphotho imene ndinapereka kwa iyeyo chifukwa cha uthenga wake!
11 Et maintenant, de méchants hommes ont tué un homme juste, dans sa maison, sur sa couche. Certes, je vous demanderai compte du sang que votre main a versé, et je vous effacerai de la terre.
Nanji pamene anthu oyipa apha munthu wosalakwa ali mʼnyumba mwake ndiponso pa bedi lake! Kodi ine ndingaleke kukulangani ndi kukuchotsani pa dziko lapansi pano?”
12 David donna donc ses ordres à ses serviteurs, et ils les tuèrent; puis, ils leurs coupèrent les mains et les pieds, et les pendirent vers la fontaine d'Hébron, et ils inhumèrent la tête d'Isboseth dans le sépulcre d'Abner, fils de Ner.
Kotero Davide analamulira ankhondo ake, ndipo anawapha. Iwo anawadula manja ndi mapazi ndi kupachika matupi awo pa dziwe la ku Hebroni. Koma anatenga mutu wa Isi-Boseti nawuyika mʼmanda a Abineri ku Hebroni.

< 2 Samuel 4 >