< 2 Samuel 21 >

1 Et du temps de David, il y eut une famine qui dura trois années consécutives. David questionna le Seigneur, et le Seigneur dit: Sur Saül et sur sa maison pèse une iniquité qui demande encore de son sang, parce qu'il a mis à mort les Gabaonites.
Pa nthawi ya ulamuliro wa Davide kunali njala kwa zaka zitatu zotsatana. Kotero Davide anapemphera kwa Yehova. Yehova anati, “Izi zachitika chifukwa chakuti Sauli ndi banja lake akanali ndi mlandu wakupha Agibiyoni.”
2 Le roi David appela les Gabaonites, et il s'entretint avec eux. Or, les Gabaonites ne sont point fils d'Israël, mais un débris des Amorrhéens, et les fils d'Israël leur avaient prêté serment; malgré cela, Saül entreprit de les exterminer, dans son zèle pour les fils d'Israël et de Juda.
Mfumu inayitanitsa Agibiyoni ndipo inayankhula nawo. (Tsono Agibiyoni sanali Aisraeli, koma otsala mwa Aamori. Aisraeli analumbira kuwasiya ndi moyo, koma Sauli chifukwa cha chikondi cha pa Israeli ndi Yuda, anafuna kuwawonongeratu).
3 David dit donc aux Gabaonites: Que puis-je faire pour vous? comment pourrai-je vous apaiser afin que vous bénissiez l'héritage du Seigneur?
Davide anafunsa Agibiyoni kuti, “Kodi ine ndikuchitireni chiyani? Ndipepese bwanji kuti inu mudalitse cholowa cha Yehova?”
4 Et les Gabaonites répondirent: Entre nous et entre Saül et sa famille, il n'est question ni d'argent, ni d'or, et nul en Israël ne doit, à cause de nous, mourir. Et David reprit: Que voulez-vous dire? Parlez, je le ferai pour vous.
Agibiyoni anamuyankha kuti, “Ife tilibe ufulu woti nʼkulamula Sauli ndi banja lake kuti atipatse siliva kapena golide, tilibenso ufulu woti nʼkupha wina aliyense mu Israeli.” Davide anafunsa, “Mukufuna ine ndikuchitireni chiyani?”
5 Et ils dirent au roi: L'homme qui a tourné contre nous ses forces, qui nous a traqués, qui a conçu le vain projet de nous exterminer, nous voulons l'effacer de sorte qu'il ne reste rien de lui, sur tout le territoire d'Israël.
Iwo anayankha mfumu kuti, “Tsono za munthu amene anatiwononga ndi kukonza chiwembu choti titheretu ndi kukhala wopanda malo mu Israeli,
6 Livre-nous sept de ses fils, afin qu'en Gabaon, ville de Saül, nous les exposions au soleil pour le Seigneur; sept fils de Saül, choisis pour le Seigneur. Et le roi dit: Je vous les livrerai.
mutipatse adzukulu ake aamuna asanu ndi awiri kuti tiwaphe ndi kuwapereka pamaso pa Yehova ku Gibeya wa Sauli, wosankhidwa wa Yehova.” Choncho mfumu inati, “Ine ndidzakupatsani.”
7 Le roi épargna Miphiboseth, fils de Jonathan, fils de Saül, à cause du serment du Seigneur que s'étaient mutuellement prêté Jonathan et David.
Koma mfumu inasunga Mefiboseti mwana wa Yonatani, mwana wa Sauli, chifukwa cha kulumbira kumene mfumu Davide ndi Yonatani mwana wa Sauli anachita pamaso pa Yehova.
8 Mais il prit les deux fils de Respha, fille d'Ais, qu'elle avait eus de Saül: Hermoni et Miphiboseth, et les cinq fils de Michol, fille de Saül, qu'elle avait eus d'Esdriel, fils de Berzelli, le Moülathite.
Ndipo mfumu inatenga Arimoni ndi Mefiboseti, ana aamuna awiri a Rizipa, mwana wamkazi wa Ayiwa, amene anaberekera Sauli pamodzi ndi ana asanu a Merabi mwana wamkazi wa Sauli, amene anabereka Adirieli mwana wa Barizilai Mmeholati.
9 Et il les remit aux Gabaonites, qui les exposèrent au soleil, sur la montagne, devant le Seigneur, et tous les sept succombèrent ensemble. Ils moururent dans les premiers jours de la moisson, comme on commençait à couper les orges.
Iye anawapereka kwa anthu a ku Gibiyoni, amene anawapha nawayika pa phiri la Yehova. Onse asanu ndi awiri anafera limodzi. Iwo anaphedwa masiku oyamba kukolola barele.
10 Et Respha, fille d'Aïa, prit un cilice, et, au commencement de la moisson des orges, elle se plaça près de la roche; elle y demeura jusqu'à ce que l'eau du ciel tombât sur les morts, et elle ne laissa pas les oiseaux du ciel se poser sur eux, pendant le jour, ni les bêtes fauves des champs les atteindre, pendant la nuit.
Rizipa mwana wamkazi wa Ayiwa anatenga chiguduli ndi kudziyalira pa mwala (pamene panali mitemboyo). Kuyambira nthawi yoyamba kukolola mpaka pamene mvula inayambanso kugwa, iye sanalole kuti mbalame zikhudze mitemboyo masana kapena nyama zakuthengo usiku.
11 On alla dire à David ce que faisait Respha, fille d'Aïa, concubine de Saül; puis, on détacha les cadavres; et Dan, fils de Joa, de la race des géants, les prit.
Davide atawuzidwa zimene Rizipa mwana wamkazi wa Ayiwa, mzikazi wa Sauli anachita,
12 Après cela, David partit, et il reprit les ossements de Saül et ceux de Jonathan, aux hommes de Jabès-Galaad qui les avaient dérobés dans les rues de Bethsam, où les Philistins les avaient cloués, le jour de leur victoire sur Saül en Gelboé.
anapita kukatenga mafupa a Sauli ndi mwana wake Yonatani kwa anthu a ku Yabesi Giliyadi (iwo anawatenga mwamseri kuchoka pabwalo la ku Beti-Sani, kumene Afilisti anawapachika atapha Sauli ku Gilibowa).
13 Et il rapporta de cette ville les ossements de Saül et ceux de Jonathan, et il recueillit les ossements des sept exposés au soleil.
Davide anakatenga mafupa a Sauli ndi mwana wake Yonatani kumeneko ndiponso mafupa otayidwa a amene anaphedwa nawasonkhanitsa pamodzi.
14 Et l'on ensevelit tous ces ossements, en Benjamin, sur les flancs de la montagne, dans le sépulcre de Cis, père de Saül; on exécuta tout ce que David avait prescrit, et après cela Dieu exauça les vœux de la terre.
Iwo anayika mafupa a Sauli ndi mwana wake Yonatani mʼmanda a Kisi abambo ake a Sauli ku Zera mʼdziko la Benjamini, ndipo anachita zonse zimene mfumu inalamula. Atachita zimenezi, Mulungu anayankha pemphero lopempherera dzikolo.
15 Ensuite, la guerre s'alluma encore entre les Philistins et Israël. David se mit en campagne avec ses serviteurs; dans une bataille contre les Philistins, lui-même sortit des rangs, et de l'autre côté,
Nthawi inanso panali nkhondo pakati pa Afilisti ndi Aisraeli, Davide anapita ndi ankhondo ake kukamenyana ndi Afilisti ndipo iye anatopa kwambiri.
16 Jesbi, de la race des géants. Celui-ci portait une javeline dont la pointe pesait trois cents sicles d'airain; à sa ceinture pendait une massue, et il pensait tuer David.
Ndipo Isibi-Benobi, mmodzi mwa zidzukulu za Rafa, amene mkondo wake unkalemera makilogalamu atatu ndi theka ndipo analinso ndi lupanga latsopano, anati adzapha Davide.
17 Mais Abessa vint au secours du roi; il frappa le Philistin et il le tua. Alors, les hommes de David jurèrent et dirent: Tu ne viendras plus à la guerre avec nous, de peur que tu n'éteignes la lampe d'Israël.
Koma Abisai mwana wa Zeruya anabwera kudzapulumutsa Davide. Iye anamukantha Mfilisitiyo ndi kumupha. Pamenepo asilikali a Davide analumbira kwa iye kuti, “Inu simudzapita nafenso ku nkhondo, kuti nyale ya Israeli isadzazimitsidwe.”
18 Après cela, il y eut encore un combat près de Geth avec les Philistins. Alors, Sebocha, d'Astaroth, tua Seph, de la race des géants.
Patapita nthawi, panali nkhondo ina ndi Afilisti ku Gobu. Pa nthawi imeneyo Sibekai Mhusati anapha Safu, mmodzi mwa zidzukulu za Arefai.
19 Puis, il y eut une bataille à Rhom avec les Philistins, et Eléanan, fils d'Ariorgim de Bethléem, tua Goliath le Géthéen, qui portait une javeline dont le bois ressemblait au mât d'un tisserand.
Pa nkhondo inanso ndi Afilisti ku Gobu, Elihanani mwana wa Yaare-Oregimu wa ku Betelehemu anapha Goliati Mgiti, amene anali ndi mkondo ngati ndodo yowombera nsalu.
20 Il y eut encore un combat à Geth. Et il y avait un homme de grande taille, ayant six doigts à chaque main et six doigts à chaque pied, en tout vingt-quatre doigts. Et il était aussi de la race des géants.
Pa nkhondo inanso imene inachitika ku Gati panali munthu wina wamtali kwambiri wa zala zisanu ndi chimodzi mʼmanja ndi mʼmapazi ndipo zonse pamodzi zinalipo 24. Iyenso anali chidzukulu cha Rafa.
21 Et il défiait Israël; il fut tué par Jonathan, fils de Sémeï, frère de David.
Pamene iye ankanyoza Aisraeli, Yonatani mwana wa Simea, mʼbale wake wa Davide anamupha.
22 Tous les quatre étaient issus des géants, et ils étaient nés à Geth dans la famille de Rhapha, et ils tombèrent sous les coups de David ou de ses serviteurs.
Anthu anayi amenewa anali zidzukulu za Rafa ku Gati, ndipo onse anaphedwa ndi Davide ndi ankhondo ake.

< 2 Samuel 21 >