< 2 Samuel 2 >

1 Après cela, David consulta le Seigneur, disant: Irai-je en l'une des villes de Juda? Et le Seigneur lui répondit: Va. Et David demanda: Où irai- je? A Hébron, reprit le Seigneur.
Patapita nthawi, Davide anafunsa Yehova kuti, “Kodi ndipite ku umodzi mwa mizinda ya Yuda?” Yehova anayankha kuti, “Pita.” Davide anafunsanso kuti, “Kodi ndipite kuti?” Yehova anayankha kuti, “Ku Hebroni.”
2 Et David partit pour Hébron, avec ses deux femmes Achinoam la Jezraélite et Abigaïl, femme de Nabal du Carmel,
Choncho Davide anapita kumeneko ndi akazi ake awiri, Ahinoamu wa ku Yezireeli ndi Abigayeli mkazi wamasiye uja wa Nabala wa ku Karimeli.
3 Et avec ses hommes, chacun emmenant sa famille; ainsi, ils habitèrent les villes d'Hébron.
Davide anatenganso anthu amene anali nawo aliyense ndi banja lake, ndipo anakakhala ku midzi ya ku Hebroni.
4 Alors, des hommes de la Judée vinrent, et ils sacrèrent David pour qu'il régnât sur la tribu de Juda; ces hommes lui apprirent que ceux de Jabès-Galaad avaient inhumé Saül.
Kenaka amuna a ku Yuda anabwera ku Hebroni ndipo kumeneko anadzoza Davide kukhala mfumu ya fuko la Yuda. Davide atawuzidwa kuti anthu a ku Yabesi Giliyadi ndi amene anayika mʼmanda Sauli,
5 Et David envoya des messagers aux chefs de Jabès-Galaad, et il leur dit: Bénis soyez-vous par le Seigneur, parce que vous avez été miséricordieux envers votre maître, envers Saül l'oint du Seigneur, et que vous l'avez inhumé, lui et son fils Jonathan.
iye anatuma amithenga kwa anthu a ku Yabesi Giliyadi kuti akayankhule nawo kuti, “Yehova akudalitseni poonetsa kukoma mtima kwanu kwa Sauli mbuye wanu pomuyika mʼmanda.
6 Que le Seigneur vous traite selon sa miséricorde et sa vérité; pour moi, j'en userai bien avec vous, parce que vous avez bien agi.
Tsopano Yehova akuonetseni kukoma mtima ndi kukhulupirika kwake ndipo inenso ndidzakukomerani mtima chifukwa munachita zimenezi.
7 Et maintenant que vos mains soient fortes; soyez vaillants vous-mêmes; car votre maître Saül n'est plus, et la maison de Juda m'a sacré, afin que je règne sur elle.
Tsopano khalani amphamvu ndi olimba mtima, pakuti Sauli mbuye wanu wafa, ndipo fuko la Yuda landidzoza kukhala mfumu yawo.”
8 Mais, Abner, fils de Ner, général de Saül, prit Isboseth, fils de Saül, et il l'emmena du camp de Manaam,
Pa nthawi imeneyi Abineri mwana wa Neri, wolamulira ankhondo a Sauli, anatenga Isi-Boseti mwana wa Sauli ndi kubwera naye ku Mahanaimu.
9 Et il le fit reconnaître roi par la contrée de Galaad, par Thasiri, par Jezraël, par Ephrahn, par Benjamin, par tout Israël.
Iye anamuyika kuti akhale mfumu yoyangʼanira Giliyadi, Asuri ndi Yezireeli, pamodzi ndi Efereimu, Benjamini ndi Israeli yense.
10 Isboseth, fils de Saül, avait quarante ans lorsqu'il devint roi d'Israël; il régna deux ans, hormis sur la maison de Juda, qui obéissait à David.
Isi-Boseti mwana wa Sauli anali wa zaka makumi anayi pamene anakhala mfumu ya Israeli ndipo analamulira zaka ziwiri. Koma fuko la Yuda linatsatira Davide.
11 Et David régna à Hébron sur la maison de Juda, sept ans et demi.
Davide anakhala mfumu ku Hebroni akulamulira fuko la Yuda, kwa zaka zisanu ndi chimodzi ndi miyezi isanu ndi umodzi.
12 Cependant, Abner, fils de Ner, et les serviteurs d'Isboseth, fils de Saül, s'en allèrent de Manaam en Gabaon.
Abineri mwana wa Neri, pamodzi ndi ankhondo a Isi-Boseti mwana wa Sauli, anachoka ku Mahanaimu ndi kupita ku Gibiyoni.
13 De son côté, Joab, fils de Sarvia, avec la troupe de David, sortit d'Hébron, et il arriva en même temps qu'eux vers la fontaine de Gabaon; ils campèrent les uns en deçà, les autres au delà de la fontaine.
Yowabu mwana wa Zeruya pamodzi ndi ankhondo a Davide anapita ndi kukakumana nawo ku dziwe la ku Gibiyoni. Gulu lina linakhala mbali ina ya dziwelo pamene gulu lina linakhala mbali inayo.
14 Et Abner dit à Joab: Que ces jeunes gens se lèvent et qu'ils viennent jouer devant nous; à quoi Joab répondit: Qu'ils se lèvent.
Kenaka Abineri anati kwa Yowabu, “Tiye tibweretse ena mwa anyamata athu kuti amenyane patsogolo pathupa.” Yowabu anayankha, “Chabwino, amenyane.”
15 Et douze des serviteurs d'Isboseth, fils de Saül, tous de la tribu de Benjamin, se portèrent à la rencontre de douze serviteurs de David.
Kotero anayimirira ndipo anawawerenga: anyamata khumi ndi awiri a fuko la Benjamini ndi Isi-Boseti mwana wa Sauli ndiponso anyamata khumi ndi awiri a Davide.
16 Et chacun saisit d'une main la tête de celui qui lui faisait face, puis, de l'autre main, il lui enfonça dans le flanc son épée, et ils tombèrent tous en même temps. Et l'on appela ce lieu qui est en Gabaon, le Champ des Traîtres.
Tsono aliyense anagwira mutu wa mnzake namubaya mnzakeyo mʼnthiti ndi mpeni ndipo onse anagwera pansi limodzi. Kotero malo amenewo ku Gibiyoni amatchedwa Helikati Hazurimu.
17 Ce jour-là, il y eut une terrible bataille; Abner et les hommes d'Israël échouèrent devant les serviteurs de David.
Tsiku limeneli nkhondo yake inali yoopsa kwambiri, ndipo Abineri ndi ankhondo a Israeli anagonjetsedwa ndi ankhondo a Davide.
18 Il se trouvait là trois fils de Sarvia, Joab, Abessa et Asaël; or, Asaël avait les pieds légers comme un daim libre dans les champs.
Ana atatu aamuna a Zeruya, Yowabu, Abisai ndi Asaheli anali komweko. Koma Asaheli anali waliwiro ngati insa.
19 Et Asaël se lança à la poursuite d'Abner; il s'attacha à ses pas, sans s'écarter à droite ni à gauche.
Iye anathamangitsa Abineri ndipo sanakhotere kumanja kapena kumanzere pamene amamutsatira.
20 Abner regardant derrière lui, s'écria: N'es-tu pas Asaël? l'autre reprit: Je le suis.
Abineri anayangʼana mʼmbuyo ndipo anafunsa, “Kodi ndiwe Asaheli?” Iye anayankha kuti, “Ndine.”
21 Abner lui dit: Détourne-toi à droite ou à gauche, attaque l'un des jeunes serviteurs, et prends pour toi ses armes. Mais Asaël refusa de s'écarter ni à droite ni à guiche.
Ndipo Abineri anati kwa iye, “Khotera kumanja kapena kumanzere: tsatira mmodzi mwa anyamatawa ndipo umulande zida zake.” Koma Asaheli sanasiye kumuthamangitsa.
22 Abner continua de lui parler, disant: Éloigne-toi donc de moi, de peur que d'un coup je ne t'étende à terre; comment alors oserais-je lever les yeux devant Joab?
Abineri anamuchenjezanso Asaheli, “Siya kuthamangitsa ine! Kodi ndikukanthe chifukwa chiyani? Kodi ndikaonana naye bwanji mʼbale wako Yowabu?”
23 Où en veux-tu venir? Retourne vers Joab, ton frère. Mais il ne voulut pas s'éloigner, et Abner le frappa du bas de sa javeline au ventre, la pointe ressortit par les reins. Asaël tomba, et il mourut en s'affaissant sur lui-même; tous ceux qui arrivèrent au lieu où il était mort s'arrêtèrent autour de lui.
Koma iye anakana kuleka kumuthamangitsa. Choncho Abineri anabaya Asaheli mʼmimba ndi msonga ya mkondo wake ndipo mkondowo unatulukira mbali ina. Iye anagwa ndi kufera pamalo pomwepo. Ndipo munthu aliyense amayima akafika pamalo pamene anagwera ndi kufa.
24 Et Joab et Abessa s'élancèrent à la poursuite d'Abner; le soleil se couchait alors; et ils allèrent jusqu'à la colline d'Amma, qui est en face d'Haï, où monte le chemin du désert de Gabaon.
Koma Yowabu ndi Abisai anathamangitsa Abineri, ndipo dzuwa likulowa, anafika ku phiri la Ama, pafupi ndi Giya pa njira yopita ku chipululu cha ku Gibiyoni.
25 Mais les fils de Benjamin, s'étant ralliés auprès de la troupe d'Abner, ne formaient plus qu'un seul corps; ils se rangèrent sur la crête d'une colline.
Pamenepo anthu a fuko la Benjamini anasonkhana kudzathandiza Abineri. Iwo anapanga gulu ndipo anayima pamwamba pa phiri.
26 Et Abner appela Joab, et il lui dit: Est-ce que l'épée dévorera sans relâche? Ne sais-tu pas qu'elle peut devenir amère à la fin? Qu'attends-tu donc pour ordonner aux tiens de ne plus poursuivre nos frères?
Abineri anayitana Yowabu, “Kodi tipitirize kumenyana mpaka kalekale? Kodi sukuzindikira kuti mathero ake kudzakhala kuwawidwa mitima? Kodi udzawaletsa liti ankhondo ako kuthamangitsa abale awo?”
27 Et Joab répondit: Vive le Seigneur! si tu n'avais parlé, aucun des nôtres qui, depuis le matin, poursuivent leurs frères, ne se fût arrêté.
Yowabu anayankha kuti, “Pali Yehova wamoyo, ukanapanda kuyankhula, ankhondo anga akanapitiriza kuthamangitsa abale awo mpaka mmawa.”
28 Et Joab sonna de la trompette, et toute l'armée s'arrêta; elle ne poursuivit plus Israël, et le combat finit.
Chomwecho Yowabu analiza lipenga, ndipo ankhondo onse anayima. Iwo analeka kuthamangitsa Aisraeli kapena kumenyana nawo.
29 Partis le soir même, Abner et ses hommes marchèrent toute la nuit; ils traversèrent le Jourdain, le côtoyèrent et rentrèrent dans leur camp.
Usiku wonsewo Abineri ndi ankhondo ake anayenda kudutsa Araba. Iwo anawoloka Yorodani, napitirira mpaka kudutsa dera lonse la Bitironi ndipo anafika ku Mahanaimu.
30 Joab revint sur ses pas, laissant partir Abner; il rassembla tout le peuple, et il vit que des serviteurs de David, il manquait dix-neuf hommes outre Asaël.
Choncho Yowabu anabwerera kuchokera kothamangitsa Abineri ndipo anasonkhanitsa ankhondo ake onse. Kupatula Asaheli, panali ankhondo khumi ndi anayi a Davide amene anasowa.
31 Et les serviteurs de David avaient tué trois cent soixante des fils de Benjamin, qui accompagnaient Abner.
Koma ankhondo a Davide anapha ankhondo a fuko la Benjamini 360 amene anali ndi Abineri.
32 Et ils emportèrent le corps d'Asaël pour l'ensevelir à Bethléem, dans le sépulcre de son père; Joab et ses hommes marchèrent aussi toute la nuit; le jour paraissait quand ils arrivèrent à Hébron.
Iwo anatenga Asaheli ndi kukamuyika mʼmanda a abambo ake ku Betelehemu. Ndipo Yowabu ndi ankhondo ake anayenda usiku wonse ndi kufika ku Hebroni kukucha.

< 2 Samuel 2 >