< 2 Samuel 17 >

1 Et Achitophel dit à Absalon: Je vais choisir douze mille hommes, et je partirai, et je poursuivrai David cette nuit.
Ahitofele anati kwa Abisalomu, “Mundilole ndisankhe asilikali 12,000, ndinyamuke usiku womwe uno kuti ndithamangire Davide.
2 Il sera fatigué, énervé, quand je l'attaquerai et le remplirai de trouble; tout le peuple qui l'entoure fuira, et je frapperai le roi dès qu'il sera seul.
Ndipo ndikamuthira nkhondo atatopa ndiponso atataya mtima. Ndikamuchititsa mantha ndipo anthu onse amene ali naye akathawa. Ine ndikakantha mfumu yokhayo,
3 Ensuite, je te ramènerai tout le peuple, et il te reviendra comme revient une épouse auprès de son mari; puisque tu n'en veux qu'à la vie d'un seul homme, tout le peuple sera en paix.
ndipo anthu onse ndidzabwera nawo kwa inu, ngati mkwati amene akubwerera kwa mwamuna wake. Imfa ya munthu mmodzi yekha idzakhalitsa anthu onse pa mtendere.”
4 Le conseil parut excellent à Absalon et à tous les anciens d'Israël.
Malangizo awa anaoneka abwino kwa Abisalomu ndi kwa akuluakulu onse a Israeli.
5 Et Absalon dit: Appelez Chusaï d'Arach; sachons ce que celui-là aussi pourra nous dire.
Koma Abisalomu anati, “Muyitanenso Husai Mwariki kuti timve zimene iye adzanena.”
6 Chusaï entra donc auprès d'Absalon, et Absalon lui dit: Voici comme a parlé Achitophel; ferons-nous ce qu'il a conseillé? Si ce n'est pas ton avis, parle à ton tour.
Husai atabwera kwa iye, Abisalomu anati, “Ahitofele wapereka malangizo ake. Kodi tichite zimene wanena? Ngati sichoncho, tiwuze maganizo ako.”
7 Pour cette fois, répondit Chusaï, le conseil d'Achitophel n'est pas bon.
Husai anayankha Abisalomu kuti, “Malangizo amene Ahitofele wapereka si abwino pa nthawi ino.
8 Et Chusaï ajouta: Tu connais ton père et ses hommes; ils sont très vaillants, et leur âme est pleine d'amertume. Ils ressemblent à l'ours à qui, dans les champs, on a enlevé ses petits, ou au sanglier hérissé de la plaine; ton père est un guerrier, et il ne laisse pas son armée prendre de repos.
Inu mukudziwa bwino abambo anu ali ndi ankhondo awo. Iwo ndi anthu ankhondo komanso ndi woopsa ngati chimbalangondo chimene chalandidwa ana ake. Kuwonjezera apa abambo anu ndi katswiri wa nkhondo. Iwo sanagone pamodzi ndi asilikali awo.
9 Maintenant, il est à couvert dans les montagnes ou dans quelque autre lieu, et vous ne l'aurez pas plutôt assailli qu'un bruit se répandra, et que l'on dira: Il y a eu un massacre de ceux qui suivent Absalon.
Onani, ngakhale tsopano lino abisala mʼphanga lina ku malo ena ake. Ngati iwo atayamba kuthira nkhondo asilikali anu, aliyense amene adzamve zimenezi adzati, ‘Gulu lalikulu lankhondo lotsatira Abisalomu laphedwa.’
10 Et même le fils de la vaillance, dont le cœur est comme le cœur du lion, défaillira; car tout Israël sait que ton père est un homme vaillant, et qu'il est entouré de fils vaillants.
Tsono ngakhale msilikali wolimba mtima kwambiri, amene mtima wake uli ngati wa mkango, adzagwidwa ndi mantha aakulu pakuti Aisraeli akudziwa kuti abambo anu ndi ankhondo ndipo kuti iwo amene ali nawo ndi anthu olimba mtima.
11 C'est pourquoi voici ce que je préfère de beaucoup: rassemble auprès de toi tout Israël, depuis Dan jusqu'à Bersabée, aussi nombreux que le sable du rivage de la mer; et mets-toi en campagne au milieu de, cette multitude.
“Kotero ine ndikukulangizani kuti: Aisraeli onse, kuchokera ku Dani mpaka ku Beeriseba; ochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja, asonkhane kwa inu ndipo muwatsogolera kupita ku nkhondo.
12 Alors, nous marcherons contre lui en l'un des lieux où nous pensons le trouver; nous tomberons sur lui à l'improviste, comme la rosée tombe sur la terre, et nous n'épargnerons ni lui ni un seul des hommes qui l'accompagnent.
Ndipo ife tidzapita kukamuthira nkhondo kulikonse kumene tikamupeze, ndipo ife tikamuthira nkhondo ngati mame pa nthaka. Palibe amene adzakhale wamoyo kaya iye kapena ankhondo ake.
13 Et s'il s'est réfugié avec ses gens en quelque ville, tout Israël apportera des câbles devant cette ville, et nous en entraînerons les débris jusqu'au torrent, afin qu'il n'en reste pas une pierre.
Iye akakathawira mu mzinda, Aisraeli onse adzabweretsa zingwe ku mzindawo, ndipo ife tidzawugwetsera ku chigwa mpaka sipadzapezeka ngakhale kachidutswa.”
14 Absalon et tout Israël s'écrièrent: Le conseil de Chusaï d'Arach vaut mieux que le conseil d'Achitophel. Et le Seigneur voulut que le sage dessein d'Achitophel fût confondu, afin que le Seigneur fit tomber sur Absalon toute sorte de maux.
Abisalomu ndi ankhondo ena onse a Israeli anati, “Malangizo a Husai Mwariki ndi abwino kuposa a Ahitofele.” Pakuti Yehova anatsimikiza kutsutsa malangizo onse abwino a Ahitofele ndi cholinga choti zimuvute Abisalomu.
15 Et Chusaï d'Arach dit aux prêtres Sadoc et Abiathar: Voilà ce qu'avait conseillé Achitophel à Absalon et aux anciens du peuple; voilà ce que je leur ai conseillé.
Husai anawuza ansembe Zadoki ndi Abiatara kuti, “Ahitofele analangiza Abisalomu ndi akuluakulu a Israeli zakuti, koma ine ndawalangiza kuchita zakutizakuti.
16 Maintenant, faites-le rapidement savoir à David; qu'on lui dise: Ne passe pas la nuit à Araboth dans le désert; hâte-toi de traverser le Jourdain, de peur que le roi et tous les siens ne périssent.
Tsopano tumizani wamthenga msangamsanga kuti akamuwuze Davide kuti, ‘Musakagone powolokera Yorodani ku chipululu koma mukawoloke. Mukapanda kutero, mfumu ndi anthu onse amene ali naye adzaphedwa.’”
17 Or, Jonathan et Achimaas étaient restés vers la fontaine de Rhogel; une servante y courut et leur transmit le message; eux-mêmes partirent pour le porter au roi David; car il n'était pas possible qu'on les eût vus entrer dans Jérusalem.
Yonatani ndi Ahimaazi amakhala ku Eni Rogeli. Tsono wantchito wamkazi ndiye amapita kukawawuza ndipo iwo amayenera kupita kukamuwuza mfumu Davide, pakuti iwowo sankayenera kuonekera polowa mu mzinda.
18 Mais un jeune serviteur les vit en marche, et il l'alla rapporter à Absalon. Cependant, ils s'étaient hâtés, et ils étaient déjà dans la maison d'un homme de Bahurim, qui avait dans sa cour une citerne, où ils descendirent.
Koma mnyamata wina anawaona ndipo anakawuza Abisalomu. Kotero anthu awiriwo anachoka mofulumira ndipo anapita ku nyumba ya munthu wina ku Bahurimu. Iye anali ndi chitsime ku mpanda kwake ndipo iwo analowamo.
19 Alors, la femme de cet homme étendit une couverture sur l'orifice de la citerne; elle y mit sécher du blé, et la chose ne fut point découverte.
Mkazi wake anatenga chophimba ndipo anachiyika pamwamba pa chitsimecho nawazapo tirigu. Palibe amene anadziwa chilichonse za izi.
20 Les serviteurs d'Absalon vinrent dans la maison vers la femme, et ils lui dirent Où sont Achimaas et Jonathan? Elle répondit: Ils ont passé un peu au delà du torrent. Et les serviteurs cherchèrent; et, ne les ayant pas trouvés, ils retournèrent à Jérusalem.
Anthu a Abisalomu atafika kwa mkaziyo pa nyumbapo anafunsa kuti, “Kodi Ahimaazi ndi Yonatani ali kuti?” Mkaziyo anawayankha kuti, “Awoloka mtsinje.” Anthuwo anafunafuna koma sanapeze munthu, kotero anabwerera ku Yerusalemu.
21 Lorsqu'ils se furent éloignés, les deux jeunes gens sortirent de leur citerne, s'en allèrent, et dirent tout à David; puis, ils ajoutèrent: Hâte- toi de traverser le fleuve, car voici le conseil qu'a donné contre toi Achitophel.
Anthu aja atapita, awiriwo anatuluka mʼchitsimemo ndipo anapita kukawuza mfumu Davide nati kwa iye, “Nyamukani, muwoloke mtsinje msangamsanga. Ahitofele wapereka malangizo akutiakuti kutsutsana nanu.”
22 David se leva, ainsi que tout le peuple qui l'accompagnait; ils passèrent le Jourdain jusqu'au lever de l'aurore, et il n'y eut pas un seul des siens qui restât en deçà du fleuve.
Kotero Davide ndi anthu onse amene anali nawo ananyamuka ndi kuwoloka Yorodani. Pofika mmamawa, panalibe munthu amene anatsala asanawoloke Yorodani!
23 Quand Achitophel vit que son conseil n'était pas suivi, il bâta son ânesse, retourna en sa demeure dans sa ville, donna des instructions à sa famille, se pendit, et mourut; on l'ensevelit dans le sépulcre de son père.
Ahitofele ataona kuti malangizo ake sanatsatidwe, iye anakwera bulu wake napita ku mzinda wa kwawo ku nyumba yake. Iye anakonza mʼnyumba mwakemo ndi kudzimangirira. Kotero anafa nayikidwa mʼmanda a abambo ake.
24 Cependant, David passa en Manaïm, et Absalon franchit à son tour le Jourdain avec tout Israël.
Davide anapita ku Mahanaimu, ndipo Abisalomu anawoloka Yorodani pamodzi ndi ankhondo ena onse a Israeli.
25 Et Absalon mit à la tête de l'armée, à la place de Joab, Amessaï, fils d'un homme qui se nommait Jéther le Jezraélite; celui-ci l'avait eu d'Abigail, fille de Naas, sœur de Sarvia, mère de Joab.
Abisalomu anasankha Amasa kukhala mkulu wa ankhondo mʼmalo mwa Yowabu. Amasa anali mwana wa munthu wotchedwa Itira Mwisraeli amene anakwatira Abigayeli mwana wa Nahasi mlongo wake wa Zeruya, amayi ake a Yowabu.
26 Or, tout Israël et Absalon campèrent en la terre de Galaad.
Aisraeli ndi Abisalomu anamanga zithando mʼdziko la Giliyadi.
27 Lorsque David était arrivé en Manaïm, Uesbi, fils de Naas, de Rhabbath, ville des fils d'Aramon, Machis, fils d'Amiel de Ladabar, et Berzelli le Galaadite, de Rhogellim,
Davide atafika ku Mahanaimu, Sobi mwana wa Nahasi wochokera ku Raba ku dziko la Amoni ndi Makiri mwana wa Amieli wochokera ku Lodebara, ndi Barizilai Mgiliyadi wochokera ku Rogelimu
28 Lui apportèrent dix tapis laineux des deux côtés, dix marmites, des vases d'argile, du froment, de l'orge, de la pâte, de la farine, des fèves, des lentilles,
anabweretsa zofunda, mabeseni ndi miphika. Iwo anabweretsanso kwa Davide ndi anthu ake zakudya izi: tirigu ndi barele, ufa ndi tirigu wokazinga, nyemba ndi mphodza,
29 Du miel, du beurre, des moutons et du fromage de vache; ils offrirent tout cela à David et au peuple qui l'accompagnait; car ils s'étaient dit: Ce peuple a faim, il est exténué et il souffre de la soif dans le désert.
uchi ndi chambiko, nkhosa ndi mafuta olimba a mkaka wangʼombe. Pakuti anati, “Anthuwa ali ndi njala ndipo atopa, alinso ndi ludzu muno mʼchipululu.”

< 2 Samuel 17 >