< 2 Samuel 15 >

1 Il arriva ensuite qu'Absalon se fit faire des chars, il exerça des chevaux, et il eut cinquante hommes pour courir devant lui.
Patapita nthawi, Abisalomu anadzipezera galeta ndi akavalo pamodzi ndi amuna makumi asanu amene amathamanga patsogolo pake.
2 Et Absalon se levait de grand matin, il se tenait sur le chemin près de la porte, et tout homme qui était en procès, qui allait demander jugement au roi, Absalon l'appelait et lui disait: De quelle ville es-tu? A quoi l'autre répondait: Ton serviteur est de l'une des tribus d'Israël.
Iye amadzuka mmamawa ndi kuyima pa njira yopita ku chipata cha mzinda. Munthu wina aliyense akakhala ndi zodandaula zopita nazo kwa mfumu kuti akaweruze, Abisalomu amamuyitana iye ndi kumufunsa kuti, “Kodi ukuchokera ku limodzi mwa mafuko a Israeli?”
3 Et Absalon lui disait: Ta cause est bonne et claire, mais il n'y a chez le roi personne pour t'écouter.
Kenaka Abisalomu amanena kwa iye kuti, “Taona, madandawulo ako ndi abwino ndi oyenera, koma palibe woyimira mfumu woti akumvere.”
4 Et il ajoutait Que ne suis-je institué juge en cette terre; tout homme qui aurait procès ou contestation viendrait à moi, et je le jugerais?
Ndipo Abisalomu amawonjezera kunena kuti, “Ine ndikanangosankhidwa kukhala woweruza mʼdziko muno bwenzi munthu aliyense amene ali ndi madandawulo kapena milandu akubwera kwa ine ndipo ndikanaonetsetsa kuti chilungamo chachitika.”
5 Et lorsque l'homme s'approchait pour le saluer, il étendait la main, l'attirait à lui et le baisait.
Ndipo nthawi zonse amati munthu akasendera pafupi ndi kumugwandira, Abisalomu amatambalitsa dzanja lake, kumuyimiritsa munthuyo ndi kupsompsona.
6 Absalon agit de celle manière avec tous ceux d'Israël qui allaient en justice devant le roi, et il gagna le cœur de tous les hommes d'Israël.
Abisalomu amachitira izi Aisraeli onse amene amabwera kwa mfumu kuti adzaweruzidwe ndipo Abisalomuyo anagwira mtima anthu a mu Israeli.
7 Il avait quarante ans passés, et il dit à son père: Je vais partir pour Hébron, afin de m'acquitter d'un vœu que j'ai fait au Seigneur.
Patapita zaka zinayi Abisalomu anati kwa mfumu, “Loleni ndipite ku Hebroni kuti ndikakwaniritse lonjezo limene ndinachita kwa Yehova.
8 Car ton serviteur, lorsqu'il demeurait à Gedsur en Syrie, a fait ce vœu: Si le Seigneur m'accorde de rentrer à Jérusalem, je ferai un sacrifice au Seigneur.
Pamene mtumiki wanu amakhala ku Gesuri ku Aramu, anachita lonjezo ili: ‘Ngati Yehova adzandibweretsadi ku Yerusalemu, ndidzapembedza Yehovayo mu Hebroni.’”
9 Et le roi lui dit: Va en paix. Et il se leva et il alla en Hébron.
Mfumu inati kwa iye, “Pita mu mtendere” Kotero iye anapita ku Hebroni.
10 De là, Absalon envoya des émissaires parmi toutes les tribus d'Israël, disant: Quand vous entendrez sonner du cor, dites: Absalon dans Hébron est proclamé roi.
Ndipo Abisalomu anatuma amithenga ake mwamseri kwa mafuko onse a Israeli kukanena kuti, “Mukangomva kulira kwa malipenga pamenepo munene kuti, ‘Abisalomu ndiye mfumu mu Hebroni.’”
11 Absalon avait avec lui deux cents hommes, des premiers de Jérusalem qui l'avaient suivi en toute simplicité, ne sachant rien de ses projets.
Anthu 200 ochokera mu Yerusalemu anapita naye Abisalomu. Iwo anayitanidwa monga alendo ndipo anapita osadziwa chilichonse pa nkhaniyi.
12 Et pendant le sacrifice, il fit venir de Gola, sa ville, Achitophel, fils de Théconi, conseiller de David. Et il y eut une conspiration redoutable, et le peuple qui était venu auprès d'Absalon, était très nombreux.
Pamene Abisalomu amapereka nsembe, iye anayitanitsanso Ahitofele Mgiloni, mlangizi wa Davide, wa ku Gilo, kotero kuwukiraku kunakula kwambiri, ndipo anthu otsatira Abisalomu anapitirira kuchuluka.
13 Or, un homme courut l'annoncer à David, disant: Le cœur des hommes d'Israël s'est tourné vers Absalon.
Munthu wina anabweretsa uthenga ndi kudzamuwuza Davide kuti, “Mitima ya Aisraeli onse ili pa Abisalomu.”
14 Et David dit à tous les serviteurs qu'il avait avec lui en Jérusalem: Levez-vous et prenons la fuite, car il n'y a point pour nous de salut devant Absalon; hâtez-vous, de peur qu'il ne nous devance et ne nous prenne, qu'il ne nous apporte le mal, et qu'il ne passe la ville au fil de l'épée.
Ndipo Davide anati kwa akuluakulu ake amene anali mu Yerusalemu. “Bwerani! Tiyeni tithawe, mwina palibe adzapulumuke kwa Abisalomu. Tiyeni tichoke msanga, mwina iye adzabwera msanga ndi kutipitirira, nʼkuwononga ife ndi mzinda wathu ndi lupanga.”
15 Et les serviteurs du roi lui dirent: Que ta volonté du roi notre maître soit faite; voici tes serviteurs.
Akuluakulu a mfumu anamuyankha kuti, “Antchito anu ndi okonzeka kuchita chilichonse chimene mbuye wathu mfumu mukufuna kuchita.”
16 Et le roi sortit à pied, avec toute sa maison; et le roi laissa, pour garder sa demeure, dix de ses concubines.
Mfumu inanyamuka pamodzi ndi banja lake lonse. Koma iye anasiya azikazi khumi kuti azisamalira nyumba yaufumu.
17 Le roi sortit donc à pied avec tous ses serviteurs, et ils s'arrêtèrent à une maison éloignée.
Kotero mfumu inanyamuka pamodzi ndi anthu onse oyitsatira, ndipo anayima pamalo pena chapatalipo.
18 Là, tous ses serviteurs défilèrent devant lui; tout Chéléthi, tout Phéléthi; puis, ils firent halte sous les oliviers dans le désert. Tout le peuple le suivait de près ainsi que toute maison, et tous les hommes forts, au nombre de six cents combattants. Ils défilèrent devant lui comme tout Chéléthi, tout Phéléthi, et tous les Géthéens au nombre de six cents venus à pied de Geth; quand ceux ci passèrent devant le roi,
Ankhondo ake onse anayamba kuyenda pamaso pa Davide, ndipo Akereti ndi Apeleti, pamodzinso ndi Agiti okwanira 600 amene anamutsata kuchokera ku Gati, nawonso anayenda pamaso pake.
19 Il dit à Ethi le Géthéen: Pourquoi es-tu venu aussi avec nous? Va-t'en et reste chez ton roi, car tu es étranger et tu as émigré de ta contrée natale.
Mfumu inati kwa Itai Mgiti, “Nʼchifukwa chiyani iwe ukupita ndi ife? Bwerera ndipo ukakhale ndi mfumu Abisalomu. Iwe ndiwe mlendo munthu wothawa kwawo.
20 Tu ne fais que d'arriver; dois-je sitôt t'emmener avec nous? Tu changerais encore de lieux; hier tu es sorti, et aujourd'hui je te ferais venir avec nous! Pour moi, j'irai où je pourrai; va-t'en et emmène tes frères qui t'ont suivi, le Seigneur te traitera selon sa miséricorde et sa vérité.
Wangobwera dzulo lomweli, lero ndikutenge kuti uziyendayenda ndi ife, pamene ine sindikudziwa kumene ndikupita? Bwerera, ndipo tenga abale ako. Chifundo ndi kukhulupirika zikhale nawe.”
21 Or, Ethi répondit au roi: Vive le Seigneur et vive le roi mon maître! où ira mon maître, à la vie et à la mort, là sera ton serviteur.
Koma Itai anayankha mfumu kuti, “Pali Yehova wamoyo, kulikonse kumene mbuye wanga mfumu mudzakhala, kaya ndi moyo kapena imfa, mtumiki wanu adzakhala komweko.”
22 Et le roi dit à Ethi: Viens et traverse le torrent. Alors, le Géthéen Ethi, le roi, tous ses serviteurs, toute la foule qui le suivait, passèrent.
Davide anati kwa Itai, “Tiye pita nafe” Kotero Itai Mgiti anayenda pamodzi ndi anthu ake ndi mabanja amene anali naye.
23 Cependant, toute la terre pleurait en jetant les hauts cris, tout le peuple avait passé le torrent de Cédron, le roi l'avait traversé aussi. Et tous prirent le chemin qui mène au désert.
Anthu onse a madera ozungulira analira mofuwula pamene anthu onsewo amadutsa. Mfumunso inawoloka chigwa cha Kidroni, ndipo anthu onse anayenda kulowera ku chipululu.
24 A ce moment, Sadoc et avec lui tous les lévites parurent, apportant de Bélhor l'arche de l'alliance du Seigneur; ils firent arrêter l'arche de Dieu sur le mont des Oliviers, et Abiathar y monta jusqu'à ce que le peuple cessât de sortir de Jérusalem.
Zadoki anali nawonso, ndipo Alevi onse amene anali naye ananyamula Bokosi la Chipangano la Mulungu. Iwo anayika pansi Bokosi la Mulungulo ndipo Abiatara ankapereka nsembe mpaka pamene anthu onse anamaliza kutuluka mu mzinda.
25 Et le roi dit à Sadoc: Retourne à la ville avec l'arche de Dieu; si je trouve grâce devant le Seigneur, il m'y fera rentrer moi-même; il me fera revoir l'arche et sa beauté.
Kenaka mfumu inati kwa Zadoki, “Tenga Bokosi la Mulungu ubwerere nalo mu mzinda. Ngati ndidzapeza chifundo pamaso pa Yehova, adzandibweretsa kuti ndilionenso ndi malo ake okhalamo.
26 Et s'il me dit: Je ne me complais plus à être en toi; me voici, qu'il fasse de moi ce que bon lui semble.
Koma iye anati, ‘Akapanda kukondwera nane,’ chabwino, andichite chimene chimukomere.”
27 Le roi dit donc à Sadoc le prêtre: Retourne en paix à la ville avec Achimaas, ton fils, et Jonathan, fils d'Abiathar, vos deux fils vous suivront.
Mfumu inatinso kwa wansembe Zadoki, “Kodi siwe mlosi? Bwerera mu mzinda mwamtendere pamodzi ndi mwana wako Ahimaazi ndi Yonatani mwana wa Abiatara. Iwe ndi Abiatara tengani ana anu awiri.
28 Pour moi, je m'en vais en Araboth du désert, où je serai sous les armes, jusqu'à ce que vous m'ayez fait savoir quelque nouvelle.
Ine ndidzadikira powolokera Yorodani ku chipululu mpaka nditalandira mawu ochokera kwa iwe ondiwuza mmene zilili zinthu.”
29 Ainsi, Sadoc et Abiathar ramenèrent à Jérusalem l'arche de Dieu, et elle y demeura.
Kotero Zadoki ndi Abiatara ananyamula Bokosi la Mulungu lija nabwerera nalo ku Yerusalemu, ndipo anakakhala kumeneko.
30 Et David monta sur la montagne des Oliviers; en montant, il pleurait, la tête voilée; il allait pieds nus, et avec lui tout le peuple, la tête voilée, montait et pleurait.
Koma Davide anapitirira ndi kukakwera phiri la Olivi akupita nalira. Anafunda kumutu koma sanavale nsapato. Anthu onse amene anali naye anafundanso kumutu, ndipo nawonso amalira pamene amapita.
31 Or, des gens vinrent dire à David: Achitophel est au nombre des séditieux qui suivent Absalon. Et David dit: Seigneur mon Dieu, confondez les desseins d'Achitophel.
Tsono Davide anamva kuti, “Ahitofele ali pakati pa anthu owukira pamodzi ndi Abisalomu.” Choncho Davide anapemphera, “Inu Yehova, musandutse uphungu wa Ahitofele ukhale uchitsiru.”
32 David était allé jusqu'à Rhos, où il adorait le Seigneur, quand arriva devant lui Chusaï, son compagnon bien-aimé, les vêtements déchirés, la tête couverte de cendres.
Davide atafika pamwamba pa phiri pomwe anthu ankapembedzerapo Mulungu, Husai Mwariki anadzakumana naye atangʼamba mkanjo wake ndi kudzithira fumbi kumutu.
33 Et David lui dit: Si tu viens avec nous, tu seras pour moi un fardeau;
Davide anati kwa iye, “Ngati iwe upite ndi ine, udzakhala chondilemetsa.
34 Mais si tu retournes à la ville, et si tu dis à Absalon: J'ai vu passer tes frères; j'ai vu passer le roi ton père, et maintenant, ô roi! je suis ton serviteur, laisse-moi vivre; j'étais jadis, et tout à l'heure encore, serviteur de ton père, et maintenant je suis le tien; tu confondras les desseins d'Achitophel.
Koma ngati ubwerera ku mzinda ndi kukanena kwa Abisalomu kuti, ‘Inu mfumu ine ndidzakhala wantchito wanu.’ Mʼmbuyomu ndinali wantchito wa abambo anu koma tsopano ndidzakhala wantchito wanu. Ukatero udzandithandiza kulepheretsa malangizo a Ahitofele.
35 Tu auras avec toi Sadoc et Abiathar les prêtres, et toute parole que tu pourras surprendre dans la maison du roi, tu en donneras connaissance aux prêtres Sadoc et Abiathar.
Kodi ansembe, Zadoki ndi Abiatara, sakukhala nawe kumeneko? Ukawawuze zonse zimene umamva mʼnyumba yaufumu.
36 Ils ont avec eux leurs deux fils Achimaas, fils de Sadoc, et Jonathan, fils d'Abiathar; vous me ferez savoir, en me les envoyant, toute parole que vous aurez surprise.
Ana awo awiri, Ahimaazi wa Zadoki, ndi Yonatani mwana wa Abiatara ali nawo pamodzi, uzikawatuma kwa ine ndi china chilichonse chimene ukamve.”
37 Et Chusaï, le favori de David, rentra dans Jérusalem au moment où Absalon venait d'y faire son entrée.
Ndipo Husai bwenzi la Davide anafika ku Yerusalemu pamene Abisalomu amalowa mu mzinda.

< 2 Samuel 15 >