< 2 Samuel 11 >

1 Le cours de l'année ramena le temps où les rois se mettent en campagne, et David fit partir Joab, ses serviteurs et tout Israël; ils ravagèrent la contrée des fils d'Ammon, et ils assiégèrent Rhabbath; cependant, David était resté à Jérusalem.
Nthawi ya mphukira, nthawi imene mafumu amapita ku nkhondo, Davide anatumiza Yowabu ndi ankhondo a mfumu pamodzi ndi gulu lonse lankhondo la Aisraeli. Iwo anawononga Aamoni ndi kuzungulira mzinda wa Raba. Koma Davide anatsala ku Yerusalemu.
2 Et ceci advint: sur le soir, David se leva de sa couche, et il se promena sur la plate-forme de la maison royale; et, de sa plate-forme, il vit une femme qui se baignait; or, la femme était extrêmement belle de visage.
Tsiku lina cha kumadzulo Davide anadzuka pa bedi lake ndipo ankayenda pamwamba pa nyumba yake. Ali pa dengapo anaona mkazi akusamba. Mkaziyo anali wokongola kwambiri.
3 Et David envoya, et il s'informa de la femme, et on lui dit: N'est-ce point Bersabée, fille d'Eliab, femme d'Urie l'Hettéen?
Ndipo Davide anatuma munthu wina kuti akafufuze za iye. Munthuyo anati, “Kodi uyu si Batiseba, mwana wa Eliamu, mkazi wa Uriya Mhiti?”
4 Aussitôt, David, dépêchant des messagers, la fit prendre, s'approcha d'elle, et dormit avec elle; puis, lorsqu'elle se fut purifiée de son impureté, elle retourna en sa maison.
Ndipo Davide anatumiza amithenga kwa iye kukamuyitana. Batiseba anabwera kwa Davide ndipo anagona naye. (Nʼkuti mkaziyu atayeretsedwa ku masiku ake osamba). Kenaka anabwerera ku nyumba yake.
5 La femme conçut; elle le fit savoir à David, et elle dit: Je suis enceinte.
Mkaziyo anakhala woyembekezera ndipo anatumiza mawu kwa Davide kunena kuti, “Ine ndine woyembekezera.”
6 Et David fit dire à Joab: Envoie près de moi Urie l'Hettéen, et Joab envoya Urie près de David.
Ndipo Davide anatumiza mawu awa kwa Yowabu: “Nditumizire Uriya Mhiti.” Ndipo Yowabu anamutumiza kwa Davide.
7 Urie arriva, et il entra chez le roi, et David lui demanda comment allaient Joab, et l'armée, et la guerre.
Uriya atafika kwa Davide, Davide anamufunsa za momwe analili Yowabu, za asilikali ndi momwe nkhondo inkayendera.
8 Et David dit à Urie: Va à ta maison, et lave-toi les pieds. Urie sortit donc de la demeure royale, et, derrière lui, on porta un mets de la table du roi.
Kenaka Davide anati kwa Uriya, “Pita ku nyumba yako ukapumule.” Choncho Uriya anachoka ku nyumba yaufumu, ndipo mfumuyo inatumiza mphatso kwa Uriya.
9 Mais Urie dormit devant la porte du roi, parmi les serviteurs de son maître, et il n'alla pas jusqu'à sa maison.
Koma Uriya anagona pa chipata cha nyumba yaufumu pamodzi ndi antchito onse a mbuye wake ndipo sanapite ku nyumba yake.
10 On l'alla dire à David; il sut qu'Urie n'était pas allé jusqu'à sa maison, et David dit à Urie: Ne viens-tu pas de faire un voyage? Pourquoi n'es-tu pas entré en ta demeure?
Davide atawuzidwa kuti, “Uriya sanapite ku nyumba yake.” Iye anafunsa kuti, “Kodi iwe sunachokera kutali? Nʼchifukwa chiyani sunapite ku nyumba yako?”
11 Et Urie répondit à David: L'arche, Israël et Juda demeurent sous des tentes; mon maître Joab et les serviteurs de mon maître sont campés eu plein air, et moi j'entrerais en ma maison pour manger et boire, et dormir avec ma femme! Comment ferais-je pareille chose? Vive ton âme! je ne la ferai jamais.
Uriya anayankha Davide kuti, “Bokosi la Chipangano ndi Israeli ndiponso Yuda akukhala mʼmatenti, ndipo mbuye wanga Yowabu ndi ankhondo anu mbuye wanga amanga misasa pa mtetete. Ine ndingapite bwanji ku nyumba yanga kukadya ndi kumwa ndiponso kugona ndi mkazi wanga? Pali inu wamoyo, ine sindidzachita chinthu chimenechi.”
12 Et David dit à Urie: Demeure encore avec nous aujourd'hui; demain, je te congédierai. Urie passa donc à Jérusalem cette journée là et le lendemain.
Ndipo Davide anati kwa iye, “Ukhale konkuno tsiku lina limodzi, ndipo mawa ndikulola kuti upite.” Kotero Uriya anakhala mu Yerusalemu tsiku limenelo ndi tsiku linalo.
13 Ensuite, David l'invita; il mangea, il but, il s'enivra, et il sortit sur le soir pour dormir où il s'était déjà couché, parmi les serviteurs de son maître; mais il n'entra point en sa maison.
Davide anayitana Uriya nadya ndi kumwa naye, ndipo Davide anamuledzeretsa. Koma madzulo Uriya anapita kukagona pa mphasa pamodzi ndi antchito a mbuye wake. Iye sanapite ku nyumba yake.
14 Le jour parut, et David écrivit une lettre à Joab, et il la remit à Urie.
Mmawa Davide analemba kalata kwa Yowabu ndipo anayitumiza ndi Uriya.
15 Voici ce qu'en sa lettre il disait: Conduis Urie au fort du péril, et laisse-le là seul; qu'il soit frappé et qu'il meure.
Mʼkalatayo analembamo kuti, “Uriya mumuyike patsogolo penipeni, pamene pali nkhondo yoopsa. Ndipo mumusiye yekha kuti akanthidwe ndi kufa.”
16 Et, pendant que Joab plaçait des gardes autour de la ville, il donna à Urie un poste où il savait qu'il se trouvait des hommes vaillants.
Kotero Yowabu atawuzinga mzindawo, anamuyika Uriya pamalo pamene amadziwa kuti pali asilikali amphamvu.
17 Ces hommes, en effet, firent une sortie; ils combattirent Joab; plusieurs hommes de l'armée, serviteurs de David, tombèrent, et Urie l'Hettéen fut au nombre des morts.
Ankhondo a mu mzindawo atabwera kudzamenyana ndi Yowabu, anthu ena a gulu la ankhondo la Davide anaphedwa ndipo Uriya Mhiti uja anaphedwanso.
18 Et Joab envoya rapporter à David tout ce qui venait de se passer dans ce combat.
Yowabu anatumiza wamthenga kwa Davide kukafotokoza mwatsatanetsatane za nkhondoyo.
19 Et il donna ses instructions au messager, disant: Lorsque tu auras fini de rapporter à David tout ce qui s'est passé dans le combat,
Iye anamulangiza wa mthengayo kuti, “Pamene ukatsiriza kufotokozera mfumu za ku nkhondozi,
20 Peut-être le roi se mettra-t-il en colère, et te dira-t-il: Pourquoi donc combattre si près de la ville? Ne saviez-vous pas que du haut des remparts on vous atteindrait?
mfumu ikapsa mtima, ndipo akakakufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani munapita pafupi ndi mzindawo kukamenya nkhondo? Inu simunadziwe kuti atha kukuponyerani mivi kuchokera pa khoma?
21 Qui donc a renversé Abimélech, fils de Jérobaal, fils de Ner? N'est-ce pas une femme qui lui a lancé, de la muraille, un éclat de meule dont il est mort à Thamasi? Pourquoi donc vous êtes-vous approchés du rempart? Alors, tu répondras: Urie l'Hettéen, ton serviteur, est du nombre des morts.
Kodi anapha Abimeleki mwana wa Yerubeseti ndani? Kodi mkazi sanamuponyere mphero kuchokera pa khoma? Kotero kuti anakafera ku Tebezi. Nʼchifukwa chiyani munafika pafupi ndi khoma?’ Ngati iye akafunsa zimenezi, iwe ukanene kwa iye kuti, ‘Mtumiki wanunso Uriya Mhiti wafa.’”
22 Le messager de Joab se rendit à Jérusalem, et, selon l'ordre de Joab, il fit au roi le rapport de tout ce qui était arrivé à la guerre.
Mthengayo ananyamuka, ndipo atafika anamuwuza Davide zonse zimene Yowabu anamutuma kuti akanene.
23 Le messager répondit à David: Parce que ceux de la ville ont prévalu sur nous; ils ont fait une sortie dans la campagne; puis, nous les avons repoussés jusqu'aux portes de la ville.
Mthengayo anati kwa Davide, “Anthuwo anatiposa mphamvu ndipo anabwera kudzalimbana nafe poyera, koma ife tinawabwezera ku chipata cha mzindawo.
24 Alors, des archers ont tiré du haut des remparts sur tes serviteurs; plusieurs des serviteurs du roi ont péri; ton serviteur Urie l'Hettéen est du nombre des morts.
Ndipo anthu oponya mivi anatiponyera kuchokera pa khoma, anthu ena a mfumu afa. Kuwonjezera apo, mtumiki wanu Uriya Mhiti wafanso.”
25 Et David dit au messager: Voici ce que tu diras à Joab: Ne t'afflige pas de cet événement; le glaive dévore tantôt celui-ci, tantôt celui-là; fortifie tes postes autour de la ville, enlève-la, et t'en rends maître.
Davide anamuwuza mthengayo kuti, “Ukanene izi kwa Yowabu: ‘Zimenezi zisakukhumudwitse; lupanga limapha wina nthawi zinanso wina. Limbikitsa nkhondo pa mzindawo ndipo uwuwononge!’ Ukanene zimenezi pomulimbikitsa Yowabu.”
26 Et la femme d'Urie apprit que son mari était mort, et elle pleura sur son mari.
Mkazi wa Uriya atamva kuti mwamuna wake wafa, analira maliro.
27 Le temps du deuil écoulé, David envoya près d'elle, la fit venir en sa demeure, et la prit pour femme; elle lui enfanta un fils. Mais l'action que David avait commise était mauvaise aux yeux du Seigneur.
Nthawi yolira maliro itatha, Davide anamubweretsa ku nyumba yake, ndipo anakhala mkazi wake nabala mwana wamwamuna. Koma Yehova sanakondwe ndi zimene Davide anachitazo.

< 2 Samuel 11 >