< 2 Rois 1 >

1 Après la mort d'Achab, Moab se souleva contre Israël.
Atamwalira Ahabu, Mowabu anawukira Israeli.
2 Et Ochozias tomba à travers le treillis de sa chambre haute, en Samarie; il en fut malade; et il fit partir des messagers auxquels il dit: Allez demander à Baal-Mouche, dieu d'Accaron, si je survivrai à cette maladie? Ils partirent, et ils le questionnèrent pour leur roi.
Ndipo Ahaziya anagwa kuchokera pa khonde la chipinda chake chammwamba ku Samariya, ndipo anavulala kwambiri. Choncho iye anatuma amithenga nawawuza kuti, “Pitani mukafunse kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, ngati ndichire matendawa.”
3 Or, un ange du Seigneur appelant Elie le Thesbite, dit: Lève-toi, va à la rencontre des messagers d'Ochozias, roi de Samarie, et lu leur diras: Est-ce qu'il n'y a point de Dieu en Israël, que vous allez interroger Baal-Mouche, dieu d'Accaron? Il n'en sera pas ainsi.
Koma mngelo wa Yehova anawuza Eliya wa ku Tisibe kuti, “Nyamuka, pita ukakumane ndi amithenga a mfumu ya ku Samariya ndipo ukawafunse kuti, ‘Kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake inu mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni?’
4 Voici ce que dit le Seigneur: La couche sur laquelle tu es monté, tu n'en descendras plus; car assurément tu mourras. Elie partit donc, et il leur dit ces paroles.
Tsono Yehova akuti, ‘Iweyo sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’” Ndipo Eliya ananyamuka.
5 Et les messagers retournèrent auprès de leur maître, qui leur dit: Pourquoi êtes-vous revenus?
Amithenga aja atabwerera kwa mfumu, mfumuyo inawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwabwerera?”
6 Ils répondirent: Un homme est venu à notre rencontre, il nous a dit: Retournez auprès du roi qui vous a envoyés, et dites-lui: Voici ce que dit le Seigneur: Est-ce qu'il n'y a point de Dieu en Israël, que tu vas consulter Baal-Mouche, le dieu d'Accaron? Il n'en sera point ainsi. La couche sur laquelle tu es montée, tu n'en descendras plus, car tu mourras.
Iwo anayankha kuti, “Munthu wina anabwera kudzakumana nafe, ndipo anatiwuza kuti, bwererani kwa mfumu imene inakutumani ndipo mukayiwuze kuti, ‘Yehova akuti, kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni? Tsono sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’”
7 Ainsi, après leur retour, ils rapportèrent au roi les paroles d'Elie, et le roi leur dit: Comment est l'homme qui a été à votre rencontre, et qui vous a dit ces paroles?
Mfumu inafunsa amithengawo kuti, “Kodi munthu amene anabwera kudzakumana nanuyo ndi kukuwuzani zimenezi amaoneka bwanji?”
8 Ils reprirent: C'est un homme velu, qui est vêtu d'une peau de brebis. Et le roi s'écria: C'est Elie le Thesbite.
Iwo anayankha kuti, “Munthuyo anavala zovala zaubweya ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake.” Mfumu inati, “Munthu ameneyo ndi Eliya wa ku Tisibe.”
9 Puis, il envoya vers lui un chef de cinquante hommes; le chef partit avec sa troupe, et il vit Elie assis sur la cime de la montagne, et il lui dit: Descends, homme de Dieu, le roi te demande.
Pamenepo mfumu inatuma mtsogoleri wa ankhondo ndi anthu ake makumi asanu kwa Eliya. Mtsogoleriyo anapita kwa Eliya, amene anali atakhala pamwamba pa phiri, ndipo anati, “Munthu wa Mulungu, mfumu ikuti, ‘Tsikani!’”
10 Or, Elle répondit: Si je suis un homme de Dieu, le feu du ciel va tomber et dévorer toi et tes cinquante hommes. Aussitôt, le feu du ciel tomba et dévora le chef avec sa troupe.
Eliya anayankha mtsogoleriyo kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu makumi asanu akowo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
11 Le roi lui envoya une seconde fois un chef et ses cinquante hommes. Et le chef dit à Elie: Homme de Dieu: Voici ce que dit le roi: Descends au plus vite.
Zitachitika izi, mfumu inatumanso mtsogoleri wina pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleriyo anati kwa Eliya, “Munthu wa Mulungu, zimene mfumu ikunena ndi izi, ‘Tsikani msangamsanga!’”
12 Le prophète répondit: Si je suis un homme de Dieu, le feu du ciel va tomber et dévorer toi et tes cinquante hommes. Aussitôt, le feu du ciel tomba, et dévora le chef avec sa troupe.
Eliya anayankha kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu ako makumi asanuwo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
13 Et le roi envoya encore un chef et ses cinquante hommes; et ce troisième chef partit, se mit à genoux devant Elie, le pria, et lui dit: Homme de Dieu, que ma vie et celle de ces cinquante hommes, tes serviteurs, ne soient pas sans prix à tes yeux.
Ndipo mfumu inatumanso mtsogoleri wachitatu pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleri wachitatuyu anakwera pa phiripo ndi kugwada pamaso pa Eliya. Iye anayankhula mopemba kuti, “Munthu wa Mulungu, chonde musandiwononge ineyo pamodzi ndi atumiki makumi asanu anuwa!
14 Le feu du ciel est tombé et a dévoré déjà deux chefs de cinquante hommes; maintenant donc, que ma vie ne soit pas sans prix à tes yeux.
Taonani, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kupsereza atsogoleri awiri pamodzi ndi anthu awo onse. Koma tsopano musawononge moyo wanga!”
15 Or, l'ange du Seigneur dit au prophète: Descends avec lui, ne crains rien d'eux. Et le prophète se leva, et il se rendit avec eux au-devant du roi.
Mngelo wa Yehova anati kwa Eliya, “Pita naye, usamuope.” Choncho Eliya ananyamuka natsika naye limodzi kupita kwa mfumu.
16 Et il lui dit: Voici ce que dit le Seigneur: Pourquoi as-tu envoyé des messagers consulter Baal-Mouche, dieu d'Accaron? Ce ne sera point ainsi: la couche sur laquelle tu es monté, tu n'en descendras plus, car tu mourras.
Eliya anawuza mfumu kuti, “Yehova akuti, ‘Chifukwa chiyani munatumiza amithenga kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, kukafunsa ngati muti muchire? Kodi mu Israeli mulibe Mulungu woti nʼkukuyankhani funso lanu? Choncho, popeza mwachita izi, simudzadzuka pamene mwagonapo; mudzafa ndithu.’”
17 Il mourut, en effet, selon la parole du Seigneur que le prophète lui avait dite.
Motero Ahaziya anafadi, monga mwa mawu a Yehova amene Eliya anayankhula. Tsono popeza Ahaziya analibe mwana, Yoramu analowa ufumu mʼmalo mwake mʼchaka chachiwiri cha Yehoramu mwana wa Yehosafati mfumu ya ku Yuda.
18 Quant au reste de l'histoire d'Ochozias, n'est-il pas écrit au livre des faits et gestes des rois d'Israël?
Ntchito zina zonse zimene Ahaziya anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?

< 2 Rois 1 >