< 2 Rois 6 >

1 Et les fils des prophètes dirent à Elisée: Vois, le lieu où nous demeurons devant toi est étroit pour nous;
Ana a aneneri anati kwa Elisa, “Taonani malo amene timakhala ndi inu atichepera kwambiri.
2 Allons donc jusqu'au Jourdain, que chaque homme prenne là une solive, puis nous y construirons pour nous une maison où nous demeurerons. Et il répondit: Allez.
Tiloleni tipite ku Yorodani kumene aliyense wa ife akadule mtengo umodzi, kuti timange malo woti tizikhalamo.” Ndipo Elisa anati, “Pitani.”
3 L'un d'eux ajouta doucement: Viens avec tes serviteurs; et il reprit: J'irai.
Mmodzi wa iwo anati, “Chonde mulole kutsagana nawo atumiki anu.” Elisa anayankha kuti, “Ndipita nanu.”
4 Et il partit avec eux; ils arrivèrent au Jourdain, et ils abattirent des arbres.
Ndipo anapita nawo. Anapita ku Yorodani nayamba kudula mitengo.
5 Or, pendant que l'un d'eux coupait un tronc, le fer de sa cognée tomba dans l'eau, et il cria: Hélas! maître, la voilà perdue.
Pamene wina ankadula mtengo, nkhwangwa yake inaguluka nigwera mʼmadzi. Iye anafuwula kuti, “Mayo! Mbuye wanga! Popeza ndi yobwereka!”
6 L'homme de Dieu dit: Où est-elle tombée? L'autre lui montra la place; Elisée écorça une branche, il l'y jeta, et le fer surnagea.
Ndipo munthu wa Mulungu uja anafunsa, “Yagwera pati?” Pamene anamuonetsa malowo, Elisa anadula kamtengo nakaponya pamenepo, ndipo nkhwangwayo inayandama.
7 Et le prophète dit: Relève-le pour toi. L'autre étendit la main et le reprit.
Elisa anati, “Itenge.” Ndipo munthuyo anatambalitsa dzanja lake nayitenga.
8 Cependant, le roi de Syrie était à combattre Israël; il tint conseil avec ses serviteurs, et il dit: Je camperai en un tel lieu où l'on peut se cacher.
Tsono mfumu ya ku Aramu inali pa nkhondo ndi Israeli. Itakambirana ndi atsogoleri ake ankhondo inati, “Ndidzamanga misasa yanga pamalo akutiakuti.”
9 Et Elisée envoya au roi d'Israël, disant: Prends garde de passer en cet endroit, car le roi de Syrie y est caché.
Munthu wa Mulungu anatumiza mawu kwa mfumu ya ku Israeli kuti “Musamale podutsa malo akuti, chifukwa Aaramu akupita kumeneko.”
10 Et le roi d'Israël fit reconnaître le lieu que lui avait dit Elisée, et il s'en garda plus d'une et plus de deux fois.
Choncho mfumu ya ku Israeli inatuma anthu kumalo kumene munthu wa Mulunguyo ananena. Nthawi ndi nthawi Elisa ankachenjeza mfumu, kotero kuti ankakhala tcheru ku malo amenewo.
11 Et l'âme du roi de Syrie en fut émue; il convoqua ses serviteurs, et il leur dit: Ne me direz-vous point qui me trahit auprès du roi d'Israël?
Zimenezi zinakwiyitsa kwambiri mfumu ya ku Aramu. Mfumuyo inayitanitsa atsogoleri ake ankhondo ndipo inawafunsa kuti, “Kodi simungandiwuze munthu amene pakati pathu pano ali mbali ya mfumu ya ku Israeli?”
12 Or, l'un d'eux répondit: Cela n'est pas, ô roi mon maître, mais Elisée le prophète fait connaître au roi d'Israël les discours que tu tiens jusque dans l'alcôve de ta chambre à coucher.
Mmodzi mwa atsogoleri a ankhondowo anati, “Palibe ndi mmodzi yemwe pakati pathu, inu mbuye wanga, koma Elisa mneneri amene ali ku Israeli amawuza mfumu ya ku Israeli mawu enieni amene inu mumayankhula ku chipinda kwanu.”
13 Et il leur dit: Allez, voyez où il est, et j'enverrai des gens le prendre. Ils s'en allèrent, et ils lui firent dire: Le voici en Dothaïm.
Choncho mfumu inalamula kuti, “Pitani, kafufuzeni kumene akukhala kuti ine nditume anthu kukamugwira.” Anthuwo anabweretsa mawu oti, “Taonani, Elisa ali ku Dotani.”
14 Et il y envoya des cavaliers, des chars, une force imposante; et ses gens y arrivèrent de nuit, et ils investirent la ville.
Ndipo mfumu inatumizako magaleta ndi akavalo ndiponso gulu lankhondo lamphamvu. Anapita usiku nakawuzungulira mzindawo.
15 S'étant levé de grand matin, le serviteur d'Elisée sortit, et il vit l'armée qui entourait la ville; il vit les cavaliers, les chars, et il dit au prophète: Hélas! maître, comment ferons-nous?
Mtumiki wa munthu wa Mulungu atadzuka mmamawa ndi kutuluka panja, gulu la ankhondo pamodzi ndi akavalo ndi magaleta anali atazungulira mzindawo. Mtumikiyo anafunsa kuti, “Kalanga mbuye wanga, tidzachita chiyani?”
16 Mais son maître répondit: N'aie point de crainte; car ceux qui sont avec nous, surpassent en nombre ceux qui sont avec eux.
Mneneri anamuyankha kuti, “Usachite mantha. Amene ali mbali yathu ndi ambiri kupambana amene ali mbali yawo.”
17 Puis, le prophète pria, et dit: Seigneur, ouvrez les yeux de mon serviteur, qu'il voie. Et le Seigneur ouvrit les yeux du serviteur; il vit la montagne couverte de chevaux de feu et de chars de feu, tout autour d'Elisée.
Ndipo Elisa anapemphera kuti, “Inu Yehova tsekulani maso ake kuti aone.” Pamenepo Yehova anatsekula maso a mtumikiyo, ndipo anayangʼana naona kuti phiri lonse linali lodzaza ndi akavalo ndi magaleta a moto atazungulira Elisa.
18 Et ces chevaux et ces chars descendirent à lui; alors, il pria le Seigneur, et il dit: Frappez ce peuple d'aveuglement. Et le Seigneur les frappa d'aveuglement, selon la parole du prophète.
Pamene adaniwo ankabwera kudzalimbana naye, Elisa anapemphera kwa Yehova kuti, “Achititseni khungu anthu awa.” Kotero Yehova anawachititsa khungu monga anapemphera Elisa.
19 Elisée leur dit: Ce n'est point ici la ville, vous n'êtes pas dans le chemin. Suivez-moi, et je vous mènerai vers l'homme que vous cherchez. Et il les conduisit à Samarie.
Elisa anawawuza ankhondowo kuti, “Njira si imeneyi ndipo mzinda sumenewunso. Tsateni, ndipo ndidzakutengerani kwa munthu amene mukumufunayo.” Ndipo anawatengera ku Samariya.
20 Quand ils y furent entrés, le prophète dit: Seigneur, ouvrez-leur les yeux, qu'ils voient. Et le Seigneur leur ouvrit les yeux, et ils virent. Or, voilà qu'ils étaient au milieu de Samarie.
Atalowa mu mzinda wa Samariya, Elisa anati, “Yehova tsekulani maso a anthu awa kuti aone.” Choncho Yehova anatsekula maso awo ndipo anangoona kuti ali mʼkati mwenimweni mwa Samariya.
21 En les voyant, le roi d'Israël dit à Elisée: Faut-il frapper, père?
Mfumu ya ku Israeli itawaona, inafunsa Elisa kuti, “Abambo anga, kodi ndiwaphe? Kodi ndiwaphe?”
22 Il répondit: Ne les frappe point; frappe-t-on de l'arc ou de l'épée ceux que l'on a fait captifs? Prépare pour eux des pains et de l'eau; qu'ils mangent et boivent, pour s'en retourner ensuite auprès de leur maître.
Elisa anayankha kuti, “Musawaphe. Kodi mungaphe anthu amene munawagwira pogwiritsa ntchito lupanga ndi uta? Apatseni chakudya ndi madzi kuti adye ndi kumwa kenaka apite kwa mbuye wawo.”
23 Le roi leur fit donc grande chère, ils mangèrent et burent; après quoi, il les renvoya, et ils s'en allèrent retrouver leur maître, et les bandes de la Syrie cessèrent leurs excursions dans la terre d'Israël.
Choncho anawakonzera mphwando lalikulu, ndipo atatsiriza kudya ndi kumwa, anawatumiza kwawo ndipo anabwerera kwa mbuye wawo. Kotero magulu a ankhondo a ku Aramu analeka kuthira nkhondo dziko la Israeli.
24 Quelque temps après, Ben-Ader, roi de Syrie, réunit toute son armée, se mit en campagne, et assiégea Samarie.
Patapita nthawi, Beni-Hadadi mfumu ya Aramu anasonkhanitsa gulu lake lonse la ankhondo, napita kukazungulira mzinda wa Samariya.
25 Et il y eut une grande famine en Samarie; le siège se prolongea au point que la tête d'un âne valut cinquante sicles d'argent, et un peu de fiente de pigeon cinq sicles.
Mu mzinda wa Samariya munali njala yoopsa. Ndipo taonani, Aaramu anazungulira mzindawu kwa nthawi yayitali kotero kuti mutu wa bulu ankawugulitsa ndalama za siliva 80, ndipo magalamu 200 a zitosi za nkhunda ankawagulitsa pa mtengo wa masekeli asanu.
26 Comme le roi d'Israël passait sur les remparts, une femme cria à lui, disant: Sauve-moi, ô roi mon maître.
Pamene mfumu inkayenda pa khoma la mzindawo, mayi wina anafuwulira mfumuyo kuti, “Thandizeni mbuye wanga mfumu!”
27 Il lui dit: Si le Seigneur ne te sauve, comment pourrai-je te sauver? Ai-je rien du pressoir ou de l'aire?
Mfumu inayankha kuti, “Ngati Yehova sakuthandiza iwe, ine thandizo lako ndingalipeze kuti? Kuchokera ku malo opunthira tirigu kodi? Kuchokera kumalo opsinyira mphesa kodi?”
28 Le roi ajouta: Que t'arrive-t-il? Elle reprit: La femme que voilà m'a dit: Donne-moi ton fils, aujourd'hui nous le mangerons, et demain nous mangerons le mien.
Pamenepo mfumuyo inafunsa mayiyo kuti, “Kodi chakuvuta nʼchiyani?” Iye anayankha kuti, “Mayi uyu anandiwuza kuti, ‘Bweretsa mwana wako kuti timudye lero, ndipo mawa tidzadya mwana wangayu.’
29 Nous avons donc fait bouillir mon fils et nous l'avons mangé; puis, je lui ai dit le lendemain: Donne-moi ton fils, et aujourd'hui nous le mangerons; mais elle a caché son fils.
Choncho tinaphika mwana wanga ndi kumudya. Tsiku lotsatira lakelo ine ndinati, ‘Bweretsa mwana wako kuti timudye,’ koma iye anabisa mwana wakeyo.”
30 Lorsque le roi d'Israël eut oui les paroles de la femme, il déchira ses vêtements, il traversa le rempart, et le peuple vit le cilice sur ses chairs.
Mfumu itamva mawu a mayiyo, inangʼamba mkanjo wake. Pamene inkayenda pa khoma, anthu anayangʼana, ndipo anaona zovala zamʼkati, pakuti anavala chiguduli.
31 Et il s'écria: Que Dieu me punisse et qu'il me punisse encore, si la tête d'Elisée est encore aujourd'hui sur ses épaules.
Mfumuyo inati, “Mulungu andilange, andilange kwambiri ndikapanda kudula mutu wa Elisa mwana wa Safati lero!”
32 Or, Elisée était assis en sa demeure, et les anciens étaient assis auprès de lui. Et le roi avait envoyé contre lui un homme; avant que celui-ci arrivât, le prophète dit aux anciens: Ne savez-vous pas que le fils du meurtre a envoyé prendre ma tête? Voyez, quand son messager sera arrivé; fermez la porte et retenez-le en dedans; n'entendez-vous point derrière lui le bruit des pas de son maître?
Tsono Elisa nʼkuti atakhala mʼnyumba mwake, ndipo akuluakulu anali naye limodzi. Mfumu inatuma munthu wina kuti imutsogolere, koma asanafike, Elisa anawuza akuluakuluwo kuti, “Kodi simukuona momwe wopha munthu uja watumizira munthu wina kuti adzadule mutu wanga? Taonani mthengayo akafika, mutseke chitseko ndipo muchigwiritsitse kuti asalowe. Kodi ndikumvawo pambuyo pake si mgugu wa mbuye wake?”
33 Comme il parlait encore, le messager entra et dit: C'est le Seigneur qui fait fondre sur nous ces maux; que puis-je encore attendre, du Seigneur?
Elisa akuyankhulabe ndi anthuwo, taonani, wamthengayo anafika kwa iye. Ndipo mfumu inati, “Mavuto amenewa ndi ochokera kwa Yehova. Kodi nʼchifukwa chiyani ine ndiyenera kudikira thandizo lochokera kwa Yehova?”

< 2 Rois 6 >