< 2 Rois 22 >

1 Josias avait huit ans quand il monta sur le trône, et il régna trente et un ans à Jérusalem; sa mère se nommait Jedia, fille d'Edia de Basuroth.
Yosiya anakhala mfumu ali ndi zaka zisanu ndi zitatu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 31. Amayi ake anali Yedida mwana wa Adaiya wochokera ku Bozikati.
2 Et il fit ce qui est droit aux yeux du Seigneur; il marcha dans toutes les voies de David, son aïeul; il n'en dévia ni à droite ni à gauche.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova ndipo anayenda mʼnjira zonse za Davide kholo lake, osatembenukira kumanja kapena kumanzere.
3 En la troisième année du règne de Josias, le huitième mois, le roi envoya Saphan, fils d'Ezélie, fils de Mésollam, scribe du temple du Seigneur, disant:
Mʼchaka cha 18 cha ufumu wake, Mfumu Yosiya anatuma mlembi wa nyumba ya mfumu, Safani, mwana wa Azariya, mwana wa Mesulamu, ku Nyumba ya Yehova. Iye anati,
4 Monte auprès d'Helcias le grand prêtre; compte l'argent offert par le peuple dans le temple, et recueilli par les gardiens de la porte.
“Pita kwa mkulu wa ansembe Hilikiya ndipo ukamuwuze kuti awerenge ndalama zimene anthu abwera nazo ku Nyumba ya Yehova, zimene alonda a pa khomo anasonkhanitsa kwa anthu.
5 Qu'ils remettent cet argent aux ouvriers employés dans le temple. Et l'on donna cet argent aux ouvriers du temple, pour qu'ils y fissent des réparations.
Ndalamazo azipereke kwa anthu amene asankhidwa kuti ayangʼanire ntchito ya Nyumba ya Yehova. Ndipo anthu amenewa azilipira antchito amene akukonzanso Nyumba ya Yehova,
6 On le donna aux charpentiers, aux constructeurs, aux maçons, pour acheter du bois et des pierres de taille, et consolider le temple.
amisiri a matabwa, amisiri omanga ndi amisiri a miyala. Iwo akagulenso matabwa ndi miyala yosemedwa kuti akonzere Nyumba ya Yehova.
7 Mais on ne leur demanda pas compte de l'argent qui leur fut confié, parce que les travaux furent exécutés de bonne foi.
Koma anthu amene apatsidwa ndalama zolipira antchito okonza Nyumbayo asawafunse za kagwiritsidwe ntchito ka ndalamazo, popeza ndi anthu wokhulupirika.”
8 Or, le grand prêtre Helcias dit à Saphan le scribe: J'ai trouvé dans le temple le livre de la loi. Et il lui donna le livre; puis, Saphan le lut.
Mkulu wa ansembe Hilikiya anawuza Safani, mlembiyo kuti, “Ndapeza Buku la Malamulo mʼNyumba ya Yehova.” Anapereka bukulo kwa Safani amene analiwerenga.
9 Ensuite, il entra auprès du roi dans le temple; il lui rapporta ce qui avait été fait, et il dit: Tes serviteurs ont fondu l'argent trouvé dans le temple du Seigneur, et ils l'ont remis aux ouvriers du temple.
Ndipo Safani mlembi uja, anapita nakafotokozera mfumu kuti, “Atumiki anu apereka ndalama zija zinali mʼNyumba ya Yehova kwa anthu amene akugwira ntchito ndi kuyangʼanira ntchito yokonza Nyumba ya Yehova.”
10 Et Saphan le scribe ajouta: Le prêtre Helcias m'a donné un livre. Et Saphan le lut devant le roi.
Kenaka Safani mlembiyo, anafotokozera mfumu kuti, “Wansembe Hilikiya wandipatsa buku.” Ndipo Safani analiwerenga pamaso pa mfumu.
11 Quand Josias ouït les paroles du livre de la loi, il déchira ses vêtements,
Mfumu itamva mawu a mʼBuku la Malamulo, inangʼamba zovala zake.
12 Et il donna ses ordres à Helcias le prêtre, à Achicam, fils de Saphan, à Achobor, fils de Michée, à Saphan le scribe, à Amie, serviteur du roi, et il leur dit:
Iyo inalamula wansembe Hilikiya, Ahikamu mwana wa Safani, Akibo mwana wa Mikaya, Safani mlembi uja ndi Asaiya mtumiki wa mfumu, kuti,
13 Allez au Seigneur vous enquérir de moi, de tout le peuple, de tout Juda, concernant les paroles de ce livre qu'on a trouvé; car la colère dont le Seigneur s'est enflammé contre nous est grande, parce que nos pères n'ont point écouté les paroles de ce livre pour faire selon ce qui est écrit à notre sujet.
“Pitani mukafunse Yehova mʼmalo mwanga ndi mʼmalo mwa anthu onse a mʼdziko la Yuda, za zomwe zalembedwa mʼbuku limene lapezekali. Mkwiyo wa Yehova ndi waukulu kwambiri pa ife ndipo watiyakira chifukwa makolo athu sanamvere mawu a buku ili. Iwo sanachite molingana ndi zonse zimene zalembedwa mʼmenemu zokhudza ife.”
14 Et le prêtre Helcias, Achicam, Achobor, Saphan et Asaïe, allèrent chez la prophétesse Olda, mère de Sellem, fils de Thécuan, fils d'Aras, gardien des vêtements. Elle demeurait à Jérusalem dans le quartier de Masena, et ils lui parlèrent.
Choncho Hilikiya wansembe, Ahikamu, Akibo, Safani ndi Asaiya anapita kukayankhula ndi Hulida, mneneri wamkazi, mkazi wa Salumu mwana wa Tikiva, mwana wa Harihasi, wosunga zovala zaufumu. Mneneri wamkaziyu ankakhala mu Yerusalemu, ku chigawo chachiwiri cha mzindawo.
15 Et elle leur répondit: Voici ce que dit le Seigneur Dieu d'Israël: Dites à l'homme qui vous a envoyés près de moi:
Ndipo iye anawawuza kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Kamuwuzeni munthu amene wakutumani kwa ine kuti,
16 Voici ce que dit le Seigneur: Voilà que j'apporte des maux à ce lieu et à ceux qui l'habitent, selon les paroles du livre qu'a lu le roi de Juda;
‘Ichi ndi chimene Yehova akunena: Taonani, ndidzabweretsa mavuto pa malo ano ndi pa anthu ake, molingana ndi zonse zimene zalembedwa mʼbuku limene mfumu ya Yuda yawerenga.
17 En punition de ce qu'ils m'ont abandonné, et de ce qu'ils ont encensé d'autres dieux, de sorte qu'ils m'ont irrité par toutes les œuvres de leurs mains; car ma colère est enflammée contre ce lieu, et elle ne s'éteindra pas.
Chifukwa anthuwo andisiya Ine ndi kumafukiza lubani kwa milungu ina nandikwiyitsa ndi mafano onse amene manja awo anapanga, mkwiyo wanga udzayaka pa malo ano ndipo sudzazimitsidwa.’
18 Quant au roi de Juda, qui vous a envoyés vous enquérir au Seigneur, dites-lui: Voici ce que dit le Seigneur Dieu d'Israël au sujet des paroles que tu as entendues:
Koma mfumu ya Yuda imene inakutumani kuti mudzafunse kwa Yehova kayiwuzeni kuti, ‘Ichi ndi chimene Yehova Mulungu wa Israeli akunena molingana ndi mawu amene unamva:
19 En récompense de ce que ton cœur ne s'est point endurci, de ce que devant moi tu es rentré en toi-même quand tu as ouï ce que j'ai dit contre ce lieu et contre ceux qui l'habitent, pour qu'ils soient effacés et maudits; de ce que tu as déchiré tes vêtements et pleuré en ma présence: eh bien! moi aussi j'ai entendu, dit le Seigneur.
Chifukwa unasweka mtima ndi kudzichepetsa wekha pamaso pa Yehova, pamene unamva zomwe zinayankhulidwa zotsutsana ndi malo ano ndi anthu ake, kuti adzakhala otembereredwa nasanduka bwinja, ndiponso chifukwa unangʼamba zovala ndi kulira pamaso panga, ndamva pemphero lako, akutero Yehova.
20 Il n'en sera pas ainsi: voilà que je te réunis à tes pères; tu descendras en paix dans ton sépulcre, et tes yeux ne verront aucun des maux que j'apporte en ce lieu.
Choncho taona, Ine ndidzakutenga kupita kwa makolo ako ndipo udzayikidwa mʼmanda mwako mwamtendere. Maso ako sadzaona mavuto onse amene ndidzabweretse pamalo pano.’” Ndipo anthu aja anabwerera nakafotokoza mawu amenewa kwa mfumu.

< 2 Rois 22 >