< 2 Rois 2 >

1 Or, dans le temps que le Seigneur ravit Elie, comme au ciel au milieu d'un tourbillon, Elie et Elisée sortirent de Galgala.
Yehova ali pafupi kutenga Eliya kupita kumwamba mu kamvuluvulu, Eliya ndi Elisa anali pa ulendo wopita ku Giligala.
2 Et Elie dit à Elisée: Reste ici, car Dieu veut que j'aille jusqu'à Béthel. Elisée répondit: Vive le Seigneur, et vive ton 'âme, je ne te quitterai pas. Ils entrèrent donc à Béthel.
Eliya anawuza Elisa kuti, “Iwe khala pano pakuti Yehova wandituma kuti ndipite ku Beteli.” Koma Elisa anati, “Pali Yehova wamoyo ndiponso pali inu nomwe, ineyo sindidzakusiyani.” Motero awiriwo anapita ku Beteli.
3 Et les fils des prophètes qui étaient à Béthel, s'approchèrent d'Elisée, et ils lui dirent: Ne sais-tu pas qu'aujourd'hui le Seigneur doit ravir ton maître au-dessus de ta tête? Il répondit Oui, je le sais, gardez le silence.
Ana a aneneri a ku Beteli anabwera kwa Elisa namufunsa kuti, “Kodi ukudziwa kuti lero Yehova akuchotsera mbuye wako?” Elisa anayankha kuti, “Inde ndikudziwa, koma musakambe zimenezi.”
4 Elie dit ensuite à Elisée: Reste ici, car Dieu veut que j'aille jusqu'à Jéricho. Et il répondit: Vive le Seigneur, et vive ton âme! je ne te quitterai pas. Ils entrèrent donc à Jéricho.
Ndipo Eliya anati kwa Elisa, “Iwe khala pano pakuti Yehova wandituma kuti ndipite ku Yeriko.” Koma Elisa anayankha kuti, “Pali Yehova wamoyo ndiponso pali inu, ineyo sindidzakusiyani.” Motero awiriwo anapita ku Yeriko.
5 Et les fils des prophètes qui étaient à Jéricho s'approchèrent d'Elisée, et ils lui dirent Ne sais-tu pas qu'aujourd'hui le Seigneur doit ravir ton maître au-dessus de ta tête? Il répondit: Oui, je le sais, gardez le silence.
Ana a aneneri amene anali ku Yeriko anapita kwa Elisa, namufunsa kuti, “Kodi ukudziwa kuti lero Yehova akuchotsera mbuye wako?” Elisa anayankha kuti, “Inde ndikudziwa, koma inu musakambe zimenezi.”
6 Elie lui dit ensuite: Reste ici, le Seigneur veut que j'aille jusqu'au Jourdain. Elisée répondit: Vive le Seigneur et vive ton âme! je ne te quitterai point. Ils marchèrent donc tous les deux.
Ndipo Eliya anati kwa Elisa, “Iwe khala pano pakuti Yehova wandituma kuti ndipite ku Yorodani.” Elisa anayankha kuti, “Pali Yehova wamoyo ndiponso pali inu nomwe, ineyo sindidzakusiyani.” Motero awiriwo anapitirira ulendo wawo.
7 Or, il y avait au loin, vis-à-vis d'eux, cinquante fils des prophètes, et ils s'arrêtèrent l'un et l'autre aux bords du fleuve.
Anthu makumi asanu mwa ana a aneneri anawatsatira nayima chapatali moyangʼanana nawo ndipo Eliya ndi Elisa anayima mʼmphepete mwa Yorodani.
8 Et Elie prit sa peau de brebis, la fit tourner, et en frappa l'eau du fleuve: et l'eau se sépara à leur droite et à leur gauche; ils passèrent tous les deux, et ils s'en furent dans le désert.
Eliya anatenga chovala chake nachipinda, napanda madzi ndi chovalacho. Madziwo anagawikana, ena kwina ena kwina, ndipo awiriwo anawoloka powuma.
9 Pendant qu'ils traversaient le Jourdain, Elie dit à Elisée: Demande ce que je ferai pour toi avant d'être ravi loin de toi. Elisée répondit: Que j'aie part à ton double esprit.
Atawoloka, Eliya anati kwa Elisa, “Ndifotokozere, ndikuchitire chiyani ndisanachotsedwe pamaso pako?” Elisa anayankha kuti, “Ndikupemphani kuti mundipatse magawo awiri a mphamvu za mzimu wanu wa uneneri.”
10 Elie reprit: Tu as demandé une chose difficile: si tu me vois quand je serai ravi d'auprès de toi, il en sera pour toi ainsi; sinon, cela ne sera pas.
Eliya anati, “Wapempha chinthu chapatali, komabe ukandiona pamene ndikuchotsedwa pamaso pako, mphamvu wapemphayi idzakhala yako, koma ukapanda kundiona sizidzachitika.”
11 Ils parlaient ainsi en marchant, et voilà qu'un char de feu et des chevaux de feu les séparèrent l'un de l'autre; puis, Elie fut ravi dans un tourbillon comme au ciel.
Akuyenda ndi kumakambirana, mwadzidzidzi galeta lamoto ndi akavalo amoto anaonekera ndi kuwasiyanitsa awiriwo, ndipo Eliya anapita kumwamba mʼkamvuluvulu.
12 Et Elisée le vit, et il cria: Père, père, char et conducteur d'Israël. Bientôt il ne le vit plus; et il saisit ses vêtements, et il les déchira en deux lambeaux.
Elisa anaona zimenezi ndipo anafuwula kuti, “Abambo anga! Abambo anga! Magaleta a Israeli ndi anthu ake okwera pa akavalo!” Ndipo Elisa sanamuonenso Eliyayo. Pamenepo Elisa anagwira zovala zake nazingʼamba pakati.
13 Ensuite, Elisée ramassa la peau de brebis qui était tombée de dessus Elie, et s'en retourna. Il s'arrêta aux bords du Jourdain.
Iye anatola chovala cha Eliya chomwe chinagwa nabwerera ndi kukayima mʼmphepete mwa Yorodani.
14 Et il prit la peau de brebis qui était tombée de dessus Elie, en frappa l'eau du fleuve, et dit: Où est maintenant le Dieu d'Elfe? Et il frappa les eaux, qui s'ouvrirent à droite et à gauche, et Elisée passa.
Ndipo Elisa anatenga chovala chomwe chinagwa kuchokera kwa Eliya napanda nacho madzi. Iye anafunsa kuti, “Ali kuti Mulungu wa Eliya?” Atapanda madzi, madziwo anagawika pakati, ena kwina ena kwina, ndipo iye anawoloka.
15 Les fils des prophètes qui étaient à Jéricho, sur la rive opposée, le virent alors arriver, et dirent: L'esprit d'Elie est resté sur Elisée. Et ils allèrent à sa rencontre, et se prosternèrent devant lui la face contre terre.
Ndipo ana a aneneri ochokera ku Yeriko atamuona anati, “Mzimu wa Eliya wakhazikika pa Elisa.” Ndipo anapita kukakumana naye nagwada ndi kuweramitsa mitu yawo pansi pamaso pake.
16 Puis, ils lui dirent: Il y a avec tes serviteurs cinquante hommes vaillants; qu'ils partent, qu'ils s'informent de ton maître; est-ce que l'Esprit du Seigneur l'a ravi, et l'a jeté dans le Jourdain ou sur l'une des montagnes, ou sur l'une des collines? Mais Elisée répondit: N'envoyez pas.
Ndipo anawuza Elisa kuti, “Ife atumiki anu tili ndi anthu amphamvu makumi asanu. Aloleni apite kuti akafunefune mbuye wanu. Mwina Mzimu wa Yehova wamutenga ndi kukamuponya ku phiri lina kapena ku chigwa china.” Elisa anayankha kuti, “Ayi, musawatume.”
17 Ils le pressèrent tant qu'il en eut honte, il dit enfin: Envoyez; en conséquence, ils firent partir cinquante hommes qui cherchèrent trois jours, et ne trouvèrent point Elie.
Koma anamukakamizabe mpaka Elisayo anachita manyazi moti sakanatha kukana. Choncho iye anati, “Atumizeni.” Ndipo anatumiza anthu makumi asanu amene anakafunafuna Eliya kwa masiku atatu koma sanamupeze.
18 Ils revinrent auprès d'Elisée, car il s'était établi à Jéricho, et il leur dit: Ne vous avais-je point dit: Ne partez pas.
Atabwerera kwa Elisa (chifukwa anali akanali ku Yeriko), iye anawawuza kuti, “Kodi sindinakuwuzeni kuti musapite?”
19 Or, les hommes de la ville dirent à Elisée: Voilà que la ville est bien située comme celles que regarde le Seigneur, mais les eaux y sont mauvaises et la terre est stérile.
Anthu a mu mzindamo anati kwa Elisa, “Mbuye wathu, taonani mzinda uno uli pamalo pabwino, monga mukuoneramu, koma madzi ake ndi oyipa, nthaka yakenso ndi yosabereka.”
20 Et Elisée dit: Prenez-moi une cruche neuve et mettez-y du sel. Ils prirent donc une cruche, et la lui apportèrent.
Iye anati, “Patseni mbale yatsopano ndipo muyikemo mchere.” Ndipo anabweretsa mbaleyo kwa iye.
21 Ensuite, Elisée alla à la source, y versa le sel, et dit: Voici ce que dit le Seigneur: J'ai assaini ces eaux; il n'y aura plus ici ni mortalité ni stérilité.
Kenaka Elisa anapita ku kasupe wa madziwo, nathiramo mchere mʼkasupemo nati, “Yehova akuti, ‘Ndachiritsa madzi awa. Madzi amenewa sadzabweretsanso imfa kapena kuchititsa kuti nthaka ikhale yosabereka.’”
22 Et les eaux sont restées saines jusqu'à nos jours, selon la parole qu'avait dite Elisée.
Kotero madziwo ndi abwino mpaka lero, molingana ndi mawu amene Elisa anayankhula.
23 De là, il monta à Béthel, et comme il marchait dans le chemin, de petits enfants sortirent de la ville, le raillèrent, et lui dirent: Monte, chauve, monte.
Kuchokera kumeneko Elisa anapita ku Beteli. Ndipo pamene ankayenda mu msewu, anyamata ena achichepere anatuluka mu mzindamo nʼkumamuseka. Iwo ankanena kuti, “Choka iwe, wachidazi! Choka iwe wachidazi”
24 Il se retourna, les vit, et les maudit au nom du Seigneur; or, voilà que deux ours s'élancèrent de la forêt, et mirent en pièces quarante-deux de ces enfants.
Iye anatembenuka nawayangʼana ndipo anawatemberera mʼdzina la Yehova. Nthawi yomweyo panatulukira zimbalangondo ziwiri kuchokera kuthengo, ndi kuphapo anyamata 42.
25 De là, il alla au mont Carmel, puis il retourna à Samarie.
Ndipo iye anapita ku phiri la Karimeli. Pochoka kumeneko anabwerera ku Samariya.

< 2 Rois 2 >