< 2 Rois 14 >

1 En la seconde année de Joas, fils de Joachaz, roi d'Israël, commença le règne d'Amasias, fils de Joas, roi de Juda.
Mʼchaka chachiwiri cha Yehowasi mwana wa Yowahazi mfumu ya Israeli, Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
2 Il avait alors vingt-cinq ans, et il en régna vingt-neuf en Jérusalem; le nom de sa mère était Joadim de Jérusalem.
Iye anali ndi zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 29. Amayi ake anali Yehoyadini wa ku Yerusalemu.
3 Et il fit ce qui était droit aux yeux du Seigneur, mais non pas comme David, son aïeul. Il fit tout ce qu'avait fait Joas, son père.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, koma osafanana ndi zomwe anachita Davide kholo lake. Iye anatsatira zochita zonse za Yowasi abambo ake.
4 Il ne détruisit point les hauts lieux; le peuple offrit encore des sacrifices, et brûla de l'encens sur les hauts lieux.
Komabe sanachotse malo opembedzerapo mafano. Anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
5 Quand la royauté fut affermie dans ses mains, il tua ceux de ses serviteurs qui avaient frappé son père.
Atakhazikika mu ufumu wake, Amaziya anapha atumiki ake amene anapha abambo ake, mfumu ija.
6 Mais il ne fit pas périr les fils des meurtriers, se conformant à ce qui est écrit au livre de la loi de Moïse, et à l'ordonnance du Seigneur, disant: Les pères ne seront pas mis à mort à cause des fils, et les fils ne seront pas mis à mort à cause des pères; chacun mourra pour son péché.
Komatu iye sanaphe ana a anthu amene anapha abambo ake potsatira zomwe zinalembedwa mʼbuku la Malamulo a Mose. Mʼmenemo Yehova analamula kuti, “Makolo asaphedwe chifukwa cha ana awo, ndipo ana asaphedwe chifukwa cha makolo awo, koma aliyense ayenera kufa chifukwa cha zolakwa zake.”
7 Ensuite, il tailla en pièces, dans la vallée des Sels, dix mille hommes de l'Idumée; et il prit, en cette guerre, le rocher auquel il donna le nom de Jéthoël, nom qui lui est resté jusqu'à nos jours.
Iye ndiye amene anapha Aedomu 10,000 mʼchigwa cha Mchere nalanda mzinda wa Sela pa nkhondo ndipo anawutcha Yokiteeli, dzina lake ndi lomwelo mpaka lero lino.
8 Alors, Amasias envoya des messagers à Joas, fils de Joachaz, fils de Jéhu, roi d'Israël, disant: Viens, que nous nous voyions face à face.
Tsono Amaziya anatuma amithenga kwa Yehowasi mwana wa Yehowahazi, mwana wa Yehu mfumu ya Israeli ndi kumuopseza kuti, “Bwera tidzaonane maso ndi maso.”
9 Mais Joas, roi d'Israël, fit répondre au roi de Juda: Le chardon du Liban envoya des gens au cèdre pour lui dire: Donne ta fille à mon fils pour femme; et les bêtes fauves du champ voisin passèrent, et elles foulèrent aux pieds le chardon.
Koma Yehowasi mfumu ya Israeli anabweza mawu kwa Amaziya mfumu ya Yuda kuti, “Mtengo wa minga wa ku Lebanoni unatumiza uthenga kwa mkungudza wa ku Lebanoni. ‘Patse mwana wako wamkazi kuti ndimukwatire.’ Kenaka chirombo cha ku Lebanoni chinabwera ndi kupondaponda mtengo wa mingawo.
10 Tu as battu l'Iduméen, et ton cœur s'est exalté; glorifie-toi tranquillement en ta demeure; à quoi bon me cherches-tu querelle pour ta perte? Tu tomberas, et avec toi Juda.
Inde iwe wagonjetsa Edomu ndipo tsopano wayamba kudzikuza. Dzitamandire chifukwa cha kupambana kwako, koma khala kwanu konko! Nʼchifukwa chiyani ukuyamba dala mavuto amene adzakuwononga pamodzi ndi Yuda?”
11 Amasias ne l'écouta point; et Joas, roi d'Israël, partit, et ils se virent face à face à Bethsamys en Juda.
Koma Amaziya sanamvere zimenezi. Choncho Yehowasi mfumu ya Israeli anakamuthira nkhondo. Yehowasi ndi Amaziya anakumana maso ndi maso ku Beti-Semesi mʼdziko la Yuda.
12 Mais Juda tomba devant Israël, et chacun s'enfuit en sa demeure.
Israeli anagonjetsa Yuda ndipo munthu aliyense anathawira kwawo.
13 Et Joas, roi d'Israël, fit prisonnier, à Bethsamys, Amasias, fils de Joas, fils d'Ochozias; il entra à Jérusalem, et il abattit le rempart depuis la porte d'Ephraïm jusqu'à la porte de l'angle, sur une longueur de quatre cents coudées.
Yehowasi mfumu ya Israeli anagwira Amaziya mfumu ya Yuda, mwana wa Yowasi, mwana wa Ahaziya ku Beti-Semesi. Ndipo anapita ku Yerusalemu nakagwetsa khoma la Yerusalemu kuyambira ku Chipata cha Efereimu mpaka ku Chipata Chapangodya, gawo lotalika mamita 180.
14 Il prit l'argent et l'or, et tous les ornements qu'il trouva soit dans le temple du Seigneur, soit dans le palais du roi; il se fit donner des otages, et il retourna en Samarie.
Iye anatenga golide ndi siliva yense pamodzi ndi ziwiya zonse zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndi zimene zinali mosungira chuma cha nyumba ya mfumu. Iye anagwiranso anthu nabwerera ku Samariya.
15 Quant au reste de l'histoire de Joas, et à ses combats avec Amasias, ne sont-ils pas écrits au livre des Faits et gestes des rois d'Israël?
Ntchito zina za Yehowasi ndi zonse zimene anachita, kuwonjezera za nkhondo yake ndi Amaziya mfumu ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
16 Et Joas s'endormit avec ses pères; il fut enseveli à Samarie avec les rois d'Israël, et Jéroboam, son fils, régna à sa place.
Yehowasi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Samariya pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo mwana wake Yeroboamu analowa ufumu mʼmalo mwake.
17 Amasias, fils de Joas, roi de Jérusalem, vécut encore quinze ans après la mort de Joas, fils de Joachaz, roi d'Israël.
Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anakhala zaka khumi ndi zisanu atamwalira Yehowasi mwana wa Yehowahazi mfumu ya Israeli.
18 Quant au reste de l'histoire d'Amasias, n'est-il pas écrit au livre des Faits et gestes des rois de Juda?
Ntchito zina za Amaziya, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
19 Et il y eut un complot contre lui en Jérusalem; il se réfugia à Lachis, où les conjurés le poursuivirent, et ils le tuèrent dans cette ville.
Anthu anapangana zomuchita chiwembu mu Yerusalemu ndipo Amaziya anathawira ku Lakisi, koma anatumiza anthu ku Lakisiko nakamuphera komweko.
20 Puis, ils l'enlevèrent sur un char, et il fut enseveli à Jérusalem auprès de ses pères, dans la ville de David.
Anabwera naye ku pa kavalo ku Yerusalemu ndi kumuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide.
21 Et tout le peuple de Juda fit choix d'Azarias, alors âgé de seize ans, et ils le proclamèrent roi à la place d'Amasias son père.
Ndipo anthu onse a ku Yuda anatenga Azariya, amene anali ndi zaka 16 namulonga ufumu mʼmalo mwa abambo ake Amaziya.
22 Ce fut lui qui bâtit Elath, après l'avoir reprise pour Juda, lorsque le roi eut été déposé auprès de ses pères.
Azariya anamanga mzinda wa Elati ndi kuwubwezeretsa ku Yuda, Amaziya atamwalira.
23 En la quinzième année du règne d'Amasias, fils de Joas, roi de Juda, Jéroboam, fils de Joas, roi d'Israël, commença un règne qui dura quarante et un ans.
Mʼchaka cha khumi ndi chisanu cha Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda, Yeroboamu mwana wa Yehowasi mfumu ya Israeli analowa ufumu ku Samariya ndipo analamulira za 41.
24 Et il fit le mal devant le Seigneur; il ne se retira pas des péchés où Jéroboam, fils de Nabat, avait fait tomber Israël.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo sanasiye machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
25 Ce fut lui qui rétablit les limites d'Israël, depuis l'entrée d'Emath jusqu'à la mer d'Araba, selon la parole que le Seigneur Dieu d'Israël avait fait connaître par son serviteur le prophète Jonas, fils d'Amatbi, de Gethchopher;
Iye ndi amene anabwezeretsanso malire a Israeli kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku Nyanja ya Araba, molingana ndi zimene ananena Yehova Mulungu wa Israeli, kudzera mwa mtumiki wake Yona mwana wa Amitai, mneneri wochokera ku Gati-Heferi.
26 Parce que le Seigneur avait vu l'abaissement bien triste d'Israël, son petit nombre, son asservissement, son indigence et son isolement; car il n'était personne qui secourût Israël.
Pakuti Yehova anaona masautso a Israeli amene anali owawa kwambiri, panalibe kapolo kapena mfulu ngakhale wina aliyense amene akanathandiza Israeli.
27 Et le Seigneur dit qu'il ne voulait pas effacer sous les cieux la race d'Israël; mais il la sauva par les mains de Jéroboam, fils de Joas.
Pakuti Yehova anali asananene zofafaniza ufumu wa Israeli pa dziko lapansi, Iye anawapulumutsa kudzera mʼdzanja la Yeroboamu mwana wa Yowasi.
28 Quant au reste de l'histoire de Jéroboam, et aux actions qu'il fit en sa puissance, et aux combats qui rendirent Damas et Emath de Juda à Israël, ne sont-ils pas écrits au livre des Faits et gestes des rois d'Israël?
Ntchito zina za Yeroboamu ndi zonse zimene anachita, za kupambana kwake pa nkhondo, za mmene anagonjetsera Damasiko ndi Hamati, imene inali mizinda ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
29 Et Jéroboam s'endormit avec ses pères, avec les rois d'Israël, et Zacharias, son fils, régna à sa place.
Yeroboamu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo Zekariya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Rois 14 >