< 2 Rois 13 >

1 En la vingt-troisième année du règne de Joas, fils d'Ochozias, roi de Juda, Joachaz, fils de Jéhu, commença en Samarie un règne qui dura dix-sept ans.
Mʼchaka cha 23 cha ufumu wa Yowasi mwana wa Ahaziya mfumu ya Yuda, Yehowahazi, mwana wa Yehu anakhala mfumu ya Israeli mu Samariya, ndipo analamulira zaka 17.
2 Et il fit le mal aux 'yeux du Seigneur; il marcha dans les péchés où Jéroboam, fils de Nabat, avait fait tomber les fils d'Israël, et il ne s'en retira point.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova potsatira machimo a Yeroboamu mwana Nebati amene anachimwitsa nawo Israeli ndipo iye sanawaleke machimowo.
3 Et le Seigneur se courrouça contre Israël; il les livra aux mains d'Azaël, roi de Syrie, et aux mains d'Ader, fils d'Azaël, tant que ces rois vécurent.
Ndipo Yehova anakwiyira Aisraeli nawayika pansi pa ulamuliro wa Hazaeli mfumu ya Siriya ndi Beni-Hadadi mwana wa Hazaeli masiku awo onse.
4 Mais Joachaz implora le Seigneur, et le Seigneur l'écouta, parce qu'il vit l'affliction d'Israël; car le roi de Syrie l'affligeait.
Tsono Yehowahazi anapempha Yehova kuti amuchitire chifundo ndipo Yehova anamva pempho lake chifukwa anaona momwe mfumu ya Aramu inkapsinjira Aisraeli.
5 Et le Seigneur sauva Israël; le peuple fut affranchi du joug des Syriens, et les fils d'Israël furent tranquilles en leurs demeures comme autrefois.
Yehova anapatsa Aisraeli munthu woti awapulumutse ndipo anapulumuka mʼdzanja la Aramu. Choncho Aisraeli anakhala mʼnyumba zawo monga ankachitira kale.
6 Cependant, ils ne se retirèrent point des péchés où la maison de Jéroboam avait lait tomber Israël; ils marchèrent dans ces péchés, et laissèrent debout le bois sacré en Samarie.
Komabe Aisraeli sanaleke kuchita machimo a nyumba ya Yeroboamu, amene anachimwitsa nawo Israeli. Iwo anapitirira kuchita machimowo. Ndiponso fano la Asera linakhalabe ku Samariya.
7 Or, Joachaz n'avait plus d'armée, sauf cinquante cavaliers, dix chars et dix mille piétons, parce que le roi de Syrie avait détruit ses troupes, et les avait broyées comme la poussière que l'on foule aux pieds.
Yehowahazi sanatsale ndi ankhondo ambiri koma 50 okha okwera pa akavalo, magaleta khumi ndi asilikali oyenda pansi 10,000.
8 Quant au reste de l'histoire de Joachaz, aux actions qu'il fit en sa puissance, ne sont-ils pas écrits au livre des Faits et gestes des rois d'Israël.
Ntchito zina za Yehowahazi ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
9 Et Joachaz s'endormit avec ses pères; on l'ensevelit en Samarie, et Joas, son fils, régna à sa place.
Yehowahazi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Samariya. Ndipo Yowasi mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
10 En la trente-septième année du règne de Joas, roi de Juda, Joas, fils de Joachaz, roi d'Israël, commença en Samarie un règne qui dura seize ans.
Mʼchaka cha 37 cha Yowasi mfumu ya Yuda, Yehowahazi anakhala mfumu ya Israeli mu Samariya, ndipo analamulira zaka 16.
11 Et il fit le mal aux yeux du Seigneur, et il ne se retira point des péchés où Jéroboam avait fait tomber Israël; il marcha dans ces péchés.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo sanaleke kuchita tchimo la Yeroboamu mwana wa Nebati limene anachimwitsa nalo Israeli.
12 Quant au reste de l'histoire de Joas, roi d'Israël, et à ses combats avec Amasias, roi de Juda, ne sont-ils pas écrits au livre des Faits et gestes des rois d'Israël?
Ntchito zina za Yowasi ndi zonse zimene anachita, kuphatikizapo nkhondo yake ndi Amaziya mfumu ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
13 Et Joas s'endormit avec ses pères; il avait assis sur son trône Jéroboam, et il fut enseveli en Samarie avec les rois d'Israël.
Yowasi anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake ndipo Yeroboamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake. Yowasi anayikidwa mʼmanda mu Samariya pamodzi ndi mafumu a Israeli.
14 Et Elisée tomba malade, de la maladie dont il mourut; Joas, roi d'Israël, l'alla trouver; il pleura devant lui, et il dit: Père, père, char et conducteur d'Israël.
Tsono Elisa anadwala matenda amene anafa nawo. Yowasi mfumu ya Israeli inapita kukamuona ndipo inamulirira. Iye polira ankanena kuti, “Abambo anga! Abambo anga! Magaleta a Israeli ndi okwerapo ake a Israeli!”
15 Elisée lui dit: Prends un arc et une flèche; il prit donc un arc et une flèche.
Elisa anamuwuza kuti, “Tenga uta ndi mivi.” Ndipo anaterodi.
16 Puis, le prophète dit au roi: Place ta main sur l'arc. Joas y plaça la main, et Elisée imposa ses mains sur les mains du roi.
Elisa anawuza mfumu ya Israeli kuti, “Tenga uta mʼdzanja lako.” Pamene anatenga utawo, Elisa anayika manja ake pa manja a mfumuyo.
17 Ensuite, il dit: Ouvre la fenêtre du côté de l'orient. Le roi ouvrit, et Elisée lui dit: Lance le trait. Il le lança, et le prophète dit: Trait de salut du Seigneur, trait de salut contre la Syrie; tu triompheras de la Syrie en Aphec, jusqu'à ce que tu l'aies consumée.
Elisa anamuwuza kuti, “Tsekula zenera.” Ndipo anatsekuladi. Elisa anati, “Ponya muviwo!” Ndipo anaponyadi. Elisa anati, “Muvi wa chigonjetso cha Yehova, muvi wogonjetsera Aaramu! Iwe udzawawononga kwathunthu Aaramu ku Afeki.”
18 Elisée lui dit encore: Prends l'arc et les flèches. Le roi les prit, et le prophète dit au roi: Frappe la terre. Et le roi frappa trois fois; puis, il s'arrêta.
Kenaka Elisa anati, “Tenga mivi.” Ndipo mfumu inatenga miviyo. Iye anati, “Lasa pansi.” Mfumu inalasa pansi miviyo katatu nʼkuleka.
19 L'homme de Dieu s'en affligea sur lui, et il dit: Si tu avais frappé cinq ou six fois, tu aurais frappé la Syrie jusqu'à ce que tu l'eusses consumée. Maintenant, tu ne remporteras sur elle que trois victoires.
Munthu wa Mulungu anapsera mtima mfumuyo ndipo anati, “Ukanalasa pansi kasanu kapena kasanu nʼkamodzi. Pamenepo ukanatha kuwagonjetsa Aaramu ndi kuwawononga kwathunthu. Koma tsopano udzawagonjetsa katatu kokha.”
20 Et le prophète mourut, et on l'ensevelit; et des maraudeurs de Moab, au commencement de cette année, vinrent dans la terre promise.
Elisa anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda. Tsono magulu a ankhondo a Amowabu ankabwera kudzalowa ndi kudzathira nkhondo dzikolo nthawi ya dzinja.
21 Or, ceci advint: pendant qu'on ensevelissait Elisée, on vit le corps d'un maraudeur; on le jeta dans la fosse du prophète; il y roula, il toucha les ossements d'Elisée, il ressuscita et il se leva sur ses pieds.
Tsiku lina Aisraeli ena akukayika maliro mʼmanda, mwadzidzidzi anaona gulu lankhondo ndipo munthu womwalirayo anamuponyera mʼmanda a Elisa. Pamene mtembowo unakhudza mafupa a Elisa, munthu wakufayo anatsitsimuka nayimirira.
22 Azaël avait grandement affligé le peuple tout le temps de la vie de Joachaz.
Hazaeli mfumu ya Aramu inazunza Aisraeli nthawi yonse ya ulamuliro wa Yehowahazi.
23 Mais le Seigneur eut pitié et compassion des fils d'Israël; il les regarda favorablement, à cause de son alliance avec Abraham, Isaac et Jacob; et le Seigneur ne voulut pas les détruire, il ne les rejeta pas de devant sa face.
Koma Yehova anawachitira chifundo Aisraeliwo ndi kukhudzika ndi zomwe zinkawachitikira chifukwa cha pangano lake ndi Abrahamu, Isake ndi Yakobo. Mpaka lero lino Iye sanafune kuwawononga kapena kuwachotsa pamaso pake.
24 Et Azaël mourut, et son fils Ader régna après lui.
Hazaeli mfumu ya Aramu inamwalira ndipo mwana wake Beni-Hadadi analowa ufumu mʼmalo mwake.
25 Alors, Joas, fils de Joachaz, se remit en campagne, et il prit à Ader les villes que son père avait prises à Joachaz. Joas remporta trois victoires, et il reprit les villes d'Israël.
Pamenepo Yowasi mwana wa Yehowahazi analandanso kwa Beni-Hadadi mwana wa Hazaeli mizinda yonse imene iye analanda Yehowahazi abambo ake. Yehowasi anagonjetsa Beni-Hadadi katatu ndipo anatenganso mizinda ya Israeli.

< 2 Rois 13 >