< 2 Rois 12 >

1 Joas monta sur le trône la septième année du règne de Jéhu; il régna quarante ans à Jérusalem; le nom de sa mère était Sabia de Bersabée.
Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri cha Yehu, Yowasi anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka makumi anayi. Amayi ake anali Zibiya wa ku Beeriseba.
2 Et Joas fit ce qui était droit devant le Seigneur tant que le prêtre Joïada vécut pour l'éclairer.
Yowasi anachita zolungama pamaso pa Yehova masiku onse amene wansembe Yehoyada ankamulangiza.
3 Seulement, aucun des autels des hauts lieux ne fut déplacé; le peuple y fit encore des sacrifices et y brûla de l'encens.
Komabe sanachotse malo opembedzerapo mafano ndipo anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani ku malo opembedzerako mafanowo.
4 Or, Joas dit aux prêtres: Que les prêtres prennent tout l'argent des choses saintes, entrant dans le temple du Seigneur, et provenant soit des évaluations, soit des dons que chacun fait au gré de son cœur.
Yowasi anati kwa ansembe, “Tolerani ndalama zonse zimene zimaperekedwa monga chopereka chopatulika ku Nyumba ya Yehova, ndalama zonse zamsonkho wa munthu aliyense, ndalama zomwe munthu amapereka akalonjeza ndiponso ndalama zimene munthu amapereka mwaufulu ku Nyumba ya Yehova.
5 Que les prêtres le prennent, chacun selon son rang, et qu'ils l'emploient aux réparations du temple partout où ils en trouveront à faire.
Wansembe aliyense alandire ndalamazo kuchokera kwa abwenzi ake, ndipo zigwiritsidwe ntchito yokonzera chilichonse chimene chipezeke kuti ndi chowonongeka mʼnyumbayo.”
6 En la vingt-troisième année du règne de Joas, le temple n'était pas encore entièrement réparé.
Koma pofika chaka cha 23 cha ufumu wa Yowasi, ansembewo anali asanakonze nyumbayo.
7 Alors, le roi Joas fit venir le prêtre Joïada et les autres prêtres, et il leur dit: Pourquoi le temple n'est-il pas réparé? Désormais, ne prenez plus d'argent selon votre rang; donnez-le pour réparer le temple.
Choncho Mfumu Yowasi inayitanitsa wansembe Yehoyada ndi ansembe ena ndipo inafunsa kuti, “Chifukwa chiyani simukukonza malo owonongeka a mʼnyumbayi? Musasungenso ndalama zina zochokera kwa abwenzi anu, koma muzipereke kuti akonzere nyumbayi.”
8 Et les prêtres consentirent à ne plus recevoir d'argent du peuple, pourvu qu'ils ne fussent plus chargés des réparations du temple.
Ansembe anavomera kuti salandiranso ndalama kuchokera kwa anthu ndipo kuti sindiwo amene ati akonzenso nyumbayo.
9 Et Joad le prêtre prit une cassette; il en troua le couvercle, et il le mit près de l'autel, en la demeure d'un homme appartenant au temple du Seigneur. Puis, les prêtres, gardiens de la porte, y versèrent tout l'argent trouvé dans la maison du Seigneur.
Koma wansembe Yehoyada anatenga bokosi ndipo anabowola chivundikiro chake. Anayika bokosilo pambali pa guwa lansembe, kudzanja lamanja la aliyense amene akulowa mʼNyumba ya Yehovayo. Ansembe amene ankalondera pa khomopo ankaponya mʼbokosi ndalama zonse zimene ankabwera nazo ku nyumba ya Yehova.
10 Lorsqu'ils virent qu'il y avait beaucoup d'argent dans la cassette, le scribe du roi et le grand prêtre lièrent et comptèrent l'argent trouvé dans le temple du Seigneur.
Nthawi zonse akaona kuti mʼbokosimo muli ndalama zambiri, mlembi wa mfumu ndi mkulu wa ansembe ankabwera ndipo ankawerenga ndalama zomwe anthu ankabwera nazo ku Nyumba ya Yehova ndi kuziyika mʼmatumba.
11 Puis, il remirent l'argent qu'on avait recueilli entre les mains de ceux qui exécutaient les travaux signalés par les surveillants du temple du Seigneur; ils en donnèrent aussi aux charpentiers et aux constructeurs employés au temple,
Ankati akadziwa kuti ndalamazo zilipo zingati, ankazipereka kwa anthu amene ankayangʼanira ntchito yokonza nyumbayo. Ndalamazo ankalipira anthu amene ankagwira ntchito yokonza Nyumba ya Yehova, amisiri a matabwa ndi amisiri omanga nyumba,
12 Ainsi qu'aux maçons et aux tailleurs de pierre, afin qu'ils achetassent des bois et des pierres de taille pour consolider le temple, jusqu'à ce que l'on eût dépensé tout ce que l'on avait reçu, pour les réparations du temple.
amisiri a miyala ndiponso anthu ophwanya miyala. Iwo ankagula matabwa ndi miyala yosema yokonzera Nyumba ya Yehova ndipo ankalipira zinthu zonse zofunika pokonzanso nyumbayo.
13 Mais on ne devait rien prendre de l'argent offert dans le temple du Seigneur, pour fabriquer les portes d'argent, les clous, les fioles, les trompettes, les vases d'or et les vases d'argent;
Koma ndalama zomwe anthu ankabwera nazo ku nyumbayo sanagulire siliva wopangira mabeseni, zozimitsira nyale, mbale zowazira magazi, malipenga kapena ziwiya zina zilizonse zagolide kapena zasiliva za ku Nyumba ya Yehova.
14 Parce qu'on devait le donner à ceux qui faisaient les réparations; et ceux-ci l'employèrent à consolider le temple du Seigneur.
Ndalamazi anazipereka kwa anthu antchito amene anazigwiritsa ntchito yokonzera nyumbayo.
15 Et l'on ne demanda pas de comptes aux hommes à qui l'argent fut donné, pour qu'ils le remissent aux ouvriers chargés des travaux, parce que les réparations furent exécutées de bonne foi.
Koma sanawafunse kuti afotokoze kagwiritsidwe ntchito ka ndalama zolipira amene ankagwira ntchito, chifukwa anthuwo ankagwira ntchitoyo mokhulupirika kwambiri.
16 L'argent dû pour les péchés, l'argent dû pour les omissions, tout ce qu'on apporta dans le temple alla aux prêtres.
Ndalama zomwe zinkaperekedwa pa nsembe yopepesera machimo ndi nsembe yoperekedwa chifukwa cha tchimo sanabwere nazo ku Nyumba ya Yehova pakuti zinali za ansembe.
17 En ce temps-là, Azaël, roi de Syrie, sortit pour combattre Geth, et il s'en empara; puis, il se retourna pour marcher sur Jérusalem.
Pa nthawi imeneyo, Hazaeli, mfumu ya Aramu anapita kukathira nkhondo mzinda wa Gati nawulanda. Kenaka Hazaeli anatembenuka kupita kukathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu.
18 Mais Joas, roi de Juda, prit toutes les offrandes consacrées par Josaphat, par Joram et par Ochozias, ses pères, rois de Juda; il prit ses propres offrandes et tout l'or qui se trouva, soit dans le temple du Seigneur, soit dans le palais du roi; puis, il envoya tout à Azaël, roi de Syrie; et celui-ci s'éloigna de Jérusalem.
Koma Yowasi mfumu ya Yuda anatenga zinthu zonse zopatulika zomwe anazipatula Yehosafati, Yehoramu, ndi Ahaziya abambo ake, mafumu a Yuda ndi mphatso zonse zomwe iye mwini anazipereka: golide yense amene anapezeka mʼnyumba yosungiramo chuma cha mʼnyumba ya Yehova ndi zomwe zinali mʼnyumba ya mfumu, nazipereka kwa Hazaeli mfumu ya Aramu. Pamenepo iye anachoka ku Yerusalemuko.
19 Quant au reste de l'histoire de Joas, n'est-il pas écrit au livre des Faits et gestes des rois de Juda?
Ndipo ntchito zina za Yowasi ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
20 Et ses serviteurs se révoltèrent; ils tramèrent un complot, et ils frappèrent Joas en la maison de Mello qui est à Sella.
Akuluakulu ake anamuchitira chiwembu ndi kumupha ku Beti Milo, pa njira yotsikira ku Silo.
21 Jézirchar, fils de Jémuath, et Jézébuth, fils de Somer, ses serviteurs, le frappèrent, et il mourut; on l'ensevelit auprès de ses pères en la ville de David; et son fils Amasias régna à sa place.
Yozakara mwana wa Simeati ndi Yehozabadi mwana wa Someri atumiki ake anamukantha nafa. Ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Amaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Rois 12 >