< 2 Chroniques 6 >
1 Et Salomon s'écria: Le Seigneur avait dit qu'il habiterait dans le nuage.
Pamenepo Solomoni anati, “Yehova anati adzakhala mʼmitambo yakuda;
2 Et moi, Seigneur, j'ai construit à votre saint nom un temple, préparé pour vous abriter à jamais.
ine ndakumangirani Nyumba yokongola kwambiri, malo woti muzikhalamo mpaka muyaya.”
3 Puis, le roi se retourna, et il bénit toute l'Église d'Israël, et toute l'Église d'Israël était debout.
Aisraeli onse ali chiyimire pomwepo, mfumu inatembenuka ndi kuwadalitsa.
4 Et il ajouta: Béni soit le Seigneur Dieu d'Israël, qui, de sa bouche, a parlé, concernant David, mon père; et qui, de ses mains, a rempli ses promesses; il avait dit:
Ndipo inati, “Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli amene wachita ndi dzanja lake zimene analonjeza ndi pakamwa pake kwa Davide abambo anga. Pakuti Iye anati,
5 Depuis le jour où j'ai tiré mon peuple de l'Égypte, je n'avais point choisi de ville, parmi toutes les tribus d'Israël, pour qu'on bâtit un temple ou résidât mon nom; je n'avais point fait choix d'un homme qui fût le chef de mon peuple Israël.
‘Kuyambira tsiku limene ndinatulutsa anthu anga ku Igupto, sindinasankhe mzinda wina uliwonse pa fuko lina lililonse la Aisraeli kuti kumeneko andimangire Nyumba kuti ndizikhalamo kapena munthu wina aliyense kuti akhale mtsogoleri wa Aisraeli anthu anga.
6 Depuis, j'ai choisi Jérusalem pour que mon nom y réside, et j'ai choisi David pour qu'il soit sur mon peuple Israël.
Koma tsopano ndasankha Yerusalemu kuti Dzina langa likhale kumeneko ndiponso ndasankha Davide kuti alamulire anthu anga Aisraeli.’
7 Or, mon père avait en son cœur la pensée de bâtir un temple au nom du Seigneur Dieu d'Israël.
“Abambo anga Davide anali ndi maganizo mu mtima mwawo oti amangire Nyumba Yehova Mulungu wa Israeli.
8 Et le Seigneur dit à David, mon père: La pensée est venue en ton cœur de bâtir un temple à mon nom; il est bon qu'elle soit venue à ton cœur.
Koma Yehova ananena kwa abambo anga Davide kuti, ‘Popeza zinali mu mtima mwako kumangira Nyumba dzina langa, unachita bwino kukhala ndi maganizo amenewa mu mtima mwakomo.
9 Néanmoins, tu ne bâtiras point ce temple: c'est le fils issu de tes entrailles qui le bâtira à mon nom.
Komatu si iwe amene udzamanga Nyumba ya Mulungu koma mwana wako, mwana amene iwe udzabereke. Iyeyo ndiye amene adzandimangire Nyumba.’
10 Le Seigneur a relevé la parole qu'il avait dite; j'ai été suscité à la place de David, mon père, et je me suis assis sur le trône d'Israël, comme l'avait dit le Seigneur, et j'ai bâti un temple au nom du Seigneur Dieu d'Israël.
“Yehova wasunga zimene analonjeza. Ine ndalowa mʼmalo mwa abambo anga Davide, ndipo tsopano ndili pa mpando waufumu wa Israeli, monga momwe Yehova analonjezera, ndipo ndamangira nyumba Dzina la Yehova Mulungu wa Israeli.
11 Et j'ai placé l'arche qui renferme l'alliance que le Seigneur a faite avec Israël.
Mʼmenemo ndayikamo Bokosi la Chipangano, mmene muli pangano la Yehova limene anapangana ndi ana a Israeli.”
12 Ensuite, Salomon se tint devant l'autel du Seigneur et devant toute l'Église d'Israël, et il étendit les mains;
Pamenepo Solomoni anayimirira patsogolo pa guwa lansembe la Yehova patsogolo pa gulu lonse la Aisraeli ndipo anakweza manja ake.
13 Car il avait fait un piédestal d'airain qu'il avait placé au milieu du parvis du grand prêtre; ce piédestal avait cinq coudées de long, sur cinq de large, et trois de haut; or, le roi y était monté, et il se mit à genoux devant toute l'Église d'Israël, et il étendit les mains vers le ciel,
Iyeyo anali atapanga nsanja yamkuwa, kutalika kwake kunali mamita awiri, mulifupi mwake munali mamita awiri, msinkhu wake unali mita imodzi ndi theka ndipo nsanjayo anayimika pakati pa bwalo lakunja. Iye anayimirira pa nsanjapo nagwada pamaso pa gulu lonse la Aisraeli ndipo anakweza manja ake kumwamba.
14 Et il dit: Seigneur Dieu d'Israël, il n'est point au ciel et sur la terre de Dieu tel que vous, gardant alliance et miséricorde pour vos serviteurs qui marchent de toute leur âme devant vous.
Iye anati, “Inu Yehova, Mulungu wa Israeli, palibe Mulungu wofanana nanu kumwamba kapena pa dziko. Inu amene mumasunga pangano ndi kuonetsa chikondi chosasinthika kwa atumiki anu amene amayenda pamaso panu ndi mtima wawo wonse.
15 Ce que vous avez réservé à votre serviteur David, ce que vous lui avez promis, ce que vous lui avez dit de votre bouche, vous l'avez exécuté de vos mains, comme il se voit aujourd'hui.
Inu mwasunga lonjezo lanu kwa abambo anga Davide, mtumiki wanu. Inde zimene munalonjeza ndi pakamwa panu, mwazikwaniritsa ndi manja anu monga mmene tikuonera lero lino.
16 Maintenant, Seigneur Dieu d'Israël, gardez pour votre serviteur David, mon père, cette parole que vous lui avez dite: il ne manquera jamais d'hommes de ton sang pour être assis sur le trône d'Israël, devant ma face, pourvu que tes enfants observent leurs voies, et qu'ils marchent, à mes yeux, comme toi-même as marché.
“Ndipo tsopano, Inu Yehova Mulungu wa Israeli, sungani zimene munalonjeza kwa abambo anga Davide, mtumiki wanu pamene munati, ‘Sudzasowa munthu wokhala pamaso panga pa mpando waufumu wa Israeli, ngati ana ako adzasamalira mayendedwe awo ndi kusunga malamulo anga monga iwe wachitira.’
17 Maintenant, Seigneur Dieu d'Israël, que votre promesse à David, mon père, votre serviteur, soit confirmée.
Ndipo tsopano Inu Yehova, Mulungu wa Israeli, lolani kuti mawu anu akwaniritsidwe amene munalonjeza mtumiki wanu Davide.
18 Est-il donc croyable que Dieu réside sur la terre parmi les hommes? Si le ciel et le ciel des cieux ne peuvent vous contenir, comment ce temple, que j'ai bâti à votre nom, vous contiendrait-il?
“Kodi Mulungu angakhaledi pa dziko lapansi ndi munthu? Mlengalenga ngakhale kumwamba kwenikweni sikungakukwaneni. Nanga kuli bwanji ndi Nyumba iyi imene ndamanga!
19 O Seigneur Dieu d'Israël, considérez la demande et la prière de votre serviteur, pour exaucer la demande et la prière que fait aujourd'hui devant vous votre serviteur.
Koma Inu Yehova, Mulungu wanga, imvani pemphero ndi pembedzero la mtumiki wanu. Imvani kulira ndi pemphero la mtumiki wanu limene ndikupempha pamaso panu.
20 Que vos yeux soient ouverts nuit et jour sur ce temple, sur ce lieu dont vous avez dit que votre nom y serait invoqué; accueillez la prière que vous fait en ce lieu votre serviteur.
Maso anu azikhala otsekuka kuyangʼana Nyumba ino usana ndi usiku, malo ano amene Inu munati mudzayikamo Dzina lanu, imvani pemphero la mtumiki wanu limene akupemphera pa malo ano.
21 Oui, vous écouterez la prière de votre serviteur et de votre peuple Israël, toutes les fois qu'ils prieront dans ce lieu; vous les entendrez du lieu que vous habitez au ciel, et vous les exaucerez, et vous leur serez propice.
Imvani mapembedzero a mtumiki wanu ndi a anthu anu Aisraeli pamene akupemphera akuyangʼana malo ano. Imvani kumwambako, malo anu amene mumakhala; ndipo mukamva muzitikhululukira.
22 Si un homme a péché contre son prochain, et que celui-ci prête serment contre lui et qu'il lui défère le serment, et que le premier vienne jurer dans ce temple devant votre autel,
“Munthu akalakwira mnzake, nawuzidwa kuti alumbire, akabwera kudzalumbira patsogolo pa guwa lansembe la Nyumba ino,
23 Vous l'entendrez du haut du ciel, et vous agirez, et vous jugerez vos serviteurs, pour rétribuer l'inique et faire retomber ses mauvaises voies sur sa tête; pour justifier le juste et le rétribuer selon son équité.
imvani kumwambako ndi kuchitapo kanthu. Weruzani atumiki anuwo, wochimwa mugamule kuti ndi wolakwa ndipo alangidwe chifukwa cha zimene wachita. Wosachimwa mugamule kuti wosalakwa, ndipo muonetse kusalakwa kwakeko.
24 Et si votre peuple Israël est frappé par son ennemi; s'ils ont péché contre vous, et qu'ils se convertissent, qu'ils rendent hommage à votre nom, qu'ils prient et supplient devant vous en ce temple;
“Anthu anu Aisraeli akagonja kwa adani awo chifukwa akuchimwirani ndipo akatembenukira kwa Inu ndi kuvomereza Dzina lanu, kupemphera ndi kupembedzera pamaso panu mʼNyumba ino,
25 Vous les entendrez du haut du ciel, et vous serez miséricordieux pour les péchés de votre peuple Israël, et vous les ramènerez dans la terre que vous avez donnée à eux et à leurs pères.
pamenepo imvani kumwambako ndi kukhululukira tchimo la anthu anu Aisraeli ndi kuwabweretsa ku dziko limene munawapatsa iwo ndi makolo awo.
26 Lorsque vous aurez fermé le ciel et qu'il n'y aura plus de pluie, parce qu'ils auront péché contre vous, ils prieront en ce lieu, et ils rendront gloire à votre nom, et ils feront pénitence de leurs péchés, après que vous les aurez humiliés.
“Pamene kumwamba kwatsekeka ndipo mvula sikugwa chifukwa anthu anu akuchimwirani, ndipo pamene apemphera akuyangʼana malo ano ndi kuvomereza Dzina lanu ndi kutembenuka kuchoka ku machimo awo chifukwa inu mwawalanga,
27 Et vous les entendrez du haut du ciel, et vous serez miséricordieux pour les péchés de vos serviteurs et de votre peuple Israël; car vous leur aurez montré la bonne voie qu'ils doivent suivre, et vous accorderez de la pluie à la terre que vous avez donnée en héritage à votre peuple.
pamenepo imvani kumwambako ndipo muwakhululukire atumiki anu, anthu anu Aisraeli. Aphunzitseni makhalidwe oyenera, ndipo gwetsani mvula mʼdziko limene munapereka kwa anthu anu monga cholowa chawo.
28 Lorsqu'il y aura en la terre: famine, mortalité, vents pestilentiels, jaunisse, sauterelles; lorsqu'un ennemi aura opprimé votre peuple devant ses villes; dans toutes nos plaies et nos peines,
“Pamene mʼdziko mwagwa njala kapena mliri, chinoni kapena chiwawu, dzombe kapena kapuchi, kapena pamene adani azungulira mzinda wawo wina uliwonse, kaya mavuto kapena matenda abwera,
29 Toute prière, toute supplication, que vous feront dans ce temple, les mains étendues, soit un homme, soit le peuple entier d'Israël, vous l'exaucerez. Si quelqu'un reconnaît sa faute et sa plaie,
ndipo wina aliyense mwa Aisraeli akapemphera kapena kukudandaulirani, aliyense wa iwo akadziwa masautso ake ndi ululu wake, ndi kukweza manja awo kuloza Nyumba ino,
30 Vous l'écouterez du haut du ciel, du lieu où est votre demeure; vous serez miséricordieux, et vous rétribuerez chacun selon sa voie, selon ce que vous aurez vu dans son cœur, car vous seul connaissez le cœur des fils des hommes.
pamenepo imvani kumwambako, malo anu wokhalamo. Khululukani ndipo muchitire aliyense molingana ndi zonse zimene anachita popeza Inu mumadziwa mtima wake, (pakuti ndinu nokha amene mumadziwa mitima ya anthu),
31 Ainsi, auront-ils crainte de toutes vos voies, tout le temps qu'ils vivront en la terre que vous avez donnée à nos pères.
motero iwo adzakuopani ndipo adzayenda mʼnjira zanu masiku onse amene adzakhale mʼdziko limene munalipereka kwa makolo athu.
32 Et tout étranger qui n'est point de votre peuple Israël, et qui viendra d'une contrée lointaine, à cause de votre grand nom, de votre forte main et de votre bras tout-puissant, entrera aussi et priera dans ce temple.
“Ndipo kunena za mlendo amene si mmodzi wa anthu anu Aisraeli, koma wabwera kuchokera ku dziko lakutali chifukwa cha dzina lanu lotchukali, ndiponso za dzanja lanu lamphamvu ndi lochita zazikulu, kudzapemphera akuyangʼana Nyumba ino,
33 Et vous l'entendrez du haut du ciel, du lieu où est votre demeure; vous agirez selon la prière de l'étranger qui vous aura invoqué, afin que tous les peuples connaissent votre nom, et qu'ils aient crainte de vous, comme le peuple d'Israël, et qu'ils sachent que votre nom est invoqué dans ce temple que j'ai bâti.
pamenepo imvani kumwambako, malo anu okhalamo, ndipo muchite zonse zimene mlendoyo akukupemphani, kotero kuti anthu onse a dziko lapansi adziwe dzina lanu ndi kukuopani monga amachitira anthu anu Aisraeli, ndipo adziwe kuti nyumba ino imene ndakumangirani imadziwika ndi dzina lanu.
34 Si votre peuple va en guerre contre ses ennemis, en suivant la voie où vous l'aurez envoyé, et s'il invoque le nom du Seigneur, tourné vers la ville que vous vous êtes choisie, et vers le temple que j'ai bâti à votre nom,
“Anthu akapita ku nkhondo kukamenyana ndi adani awo, kulikonse kumene mungawatume, ndipo akapemphera moyangʼana mzinda uno umene mwausankha ndi Nyumba yanu imene ndakumangirani,
35 Vous entendrez du haut du ciel sa demande et sa prière, et vous rendrez sur lui votre jugement.
pamenepo imvani kumwamba pemphero lawo ndi kupempha kwawo ndipo muwapulumutse.
36 Ils pècheront contre vous, car il n'est point d'homme qui ne pèche; vous les frapperez, vous les livrerez à des ennemis qui les emmèneront captifs en leur terre voisine ou lointaine.
“Pamene achimwira inu, pakuti palibe amene sachimwa, ndipo inu mwawakwiyira ndi kuwapereka kwa adani awo, amene awatenga ukapolo ku dziko lawo lakutali kapena pafupi.
37 Et en la terre où ils auront été transportés, ils convertiront leurs cœurs, et ils se repentiront, et ils prieront dans leur captivité, disant: Nous avons péché, nous avons été déréglés et iniques.
Ngati asintha mitima yawo ku dziko limene ali akapolo ndi kulapa ndi kukudandaulirani inu mʼdziko la ukapolo wawo ndi kunena kuti, ‘Ife tachimwa, tachita zolakwa ndipo tachita moyipa kwambiri.’
38 Et ils reviendront à vous de tout leur cœur, de toute leur âme, en la contrée de ceux qui les auront pris, et où ils seront retenus captifs, et ils vous prieront, tournés vers la terre que vous avez donnée à leurs pères, vers la ville que vous vous êtes choisie, vers ce temple que j'ai bâti au nom du Seigneur.
Ndipo ngati atembenukira kwa inu ndi mtima ndi moyo wawo wonse mʼdziko lawo la ukapolo kumene anatengedwako ndi kupemphera moyangʼana dziko limene inu munalipereka kwa makolo awo, moyangʼana Nyumba yanu imene ndakumangirani;
39 Et vous entendrez du haut du ciel, du lieu de votre demeure, leur demande et leur prière; vous les jugerez, et vous serez miséricordieux envers ce peuple qui aura péché contre vous.
pamenepo imvani kumwamba, malo anu okhala, pemphero lawo ndi kudandaula kwawo, ndipo muwapulumutse. Ndipo mukhululukire anthu anu, amene akuchimwirani.
40 Et maintenant, Seigneur, ouvrez les yeux, prêtez une oreille attentive à la prière que je fais en ce temple.
“Tsono Inu Mulungu wanga, tsekulani maso anu ndi makutu anu kuti mumve mapemphero ochitikira pa malo ano.
41 Levez-vous, ô Seigneur mon Dieu, pour entrer dans ce lieu de repos avec l'arche de votre force; que vos prêtres se revêtent du salut, et que vos enfants se réjouissent de vos biens.
“Tsopano dzukani Inu Yehova Mulungu, ndipo bwerani ku malo anu ampumulo,
42 Seigneur Dieu, ne vous détournez pas de votre christ; souvenez-vous de votre miséricorde envers David, votre serviteur.
Inu Yehova Mulungu musamukane wodzozedwa wanu.