< 2 Chroniques 30 >

1 Et Ézéchias envoya en tout Israël et en Juda, et il écrivit des lettres à Ephraïm et à Manassé, pour qu'ils vinssent au temple du Seigneur à Jérusalem, faire la Pâque du Seigneur Dieu d'Israël.
Hezekiya anatumiza uthenga mʼdziko lonse la Israeli ndi ku Yuda ndiponso analemba makalata ku Efereimu ndi Manase, oyitana anthu kuti abwere ku Nyumba ya Yehova ku Yerusalemu kudzakondwerera Paska wa Yehova, Mulungu wa Israeli.
2 Et le roi, et les princes et toute l'Église de Jérusalem, résolurent de faire la Pâque le second mois.
Mfumu ndi akuluakulu ake pamodzi ndi anthu onse a mu Yerusalemu anagwirizana kuti akondwerere Paska pa mwezi wachiwiri.
3 Car ils ne la pouvaient faire en ce moment, parce qu'il n'y avait point assez de prêtres consacrés, et que tout le peuple n'était point réuni à Jérusalem.
Iwo sanathe kukondwerera pa nthawi yake chifukwa si ansembe ambiri amene anadziyeretsa ndiponso anthu anali asanasonkhane mu Yerusalemu.
4 Et cette décision fut agréable au roi et à toute l'Église.
Chikonzerochi chinaoneka kuti chinali chabwino kwa mfumu pamodzi ndi anthu onse.
5 Ils ordonnèrent aussi que l'on proclamât en tout Israël, depuis Bersabée jusqu'à Dan, que l'on eût à venir pour faire la Pâque du Seigneur Dieu à Jérusalem; car la multitude ne l'avait jamais faite comme le prescrit l'Écriture.
Iwo anagwirizana zoti alengeze mu Israeli monse kuyambira ku Beeriseba mpaka ku Dani, kuyitana anthu kuti abwere ku Yerusalemu ndi kudzakondwerera Paska wa Yehova, Mulungu wa Israeli. Si ambiri amene ankachita chikondwererochi monga momwe kunalembedwera.
6 Les courriers, avec les lettres du roi et des princes, parcoururent tout Juda et tout Israël, selon l'ordre d'Ézéchias, et ils dirent: Fils d'Israël, revenez au Seigneur Dieu d'Abraham, d'Isaac et d'Israël; ramenez ceux de vous qui survivent et qui ont échappé aux mains du roi d'Assyrie.
Molamulidwa ndi mfumu, amithenga anapita mu Israeli yense ndi Yuda ndi makalata ochokera kwa mfumu ndi kwa akuluakulu ake, olembedwa kuti, “Aisraeli bwererani kwa Yehova, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Israeli, kuti abwerere kwa inu amene mwatsala, amene mwapulumuka mʼdzanja la mafumu a ku Asiriya.
7 Ne soyez pas comme vos pères et vos frères; ils se sont séparés du Seigneur Dieu de leurs pères, et le Seigneur les a livrés à la dévastation, comme vous avez vu.
Musakhale ngati makolo anu ndi abale anu, amene anali osakhulupirika kwa Yehova Mulungu wa makolo awo kotero kuti anawachititsa kuti akhale chinthu chochititsa mantha, monga mukuoneramu.
8 Maintenant donc, n'endurcissez point vos cœurs comme vos pères; glorifiez le Seigneur votre Dieu, entrez dans le lieu saint qu'il a consacré pour toujours; servez le Seigneur votre Dieu, et il détournera de vous sa terrible colère.
Musawumitse khosi monga anachitira makolo anu, Gonjerani Yehova. Bwerani ku malo opatulika, amene anawapatula kwamuyaya. Tumikirani Yehova Mulungu wanu kuti mkwiyo wake ukuchokereni.
9 Car, lorsque vous serez revenus au Seigneur, vos frères et vos enfants trouveront miséricorde chez ceux qui les ont emmenés captifs, et Dieu vous les ramènera en cette terre; car le Seigneur notre Dieu est miséricordieux et compatissant, et il ne détournera point de vous sa face, si nous retournons à lui.
Ngati inu mubwerera kwa Yehova, pamenepo abale anu ndi ana anu adzachitiridwa chifundo ndi amene anawagwira ukapolo ndipo adzabwereranso ku dziko lino pakuti Yehova, Mulungu wanu ndi wokoma mtima ndi wachifundo. Iye sadzakufulatirani ngati inuyo mubwerera kwa Iye.”
10 Et les courriers passèrent de ville en ville, dans les montagnes d'Ephraïm et de Manassé, jusqu'à Zabulon, et ils furent un sujet de risée et de raillerie.
Amithenga aja anapita mzinda ndi mzinda wa ku Efereimu ndi Manase mpaka ku Zebuloni, koma anthu anawanyoza ndi kuwachita chipongwe.
11 Toutefois, des hommes d'Aser, de Manassé et de Zabulon, rentrèrent en eux-mêmes, et vinrent à Jérusalem en Juda.
Komabe anthu ena a ku Aseri, Manase ndi Zebuloni anadzichepetsa ndipo anapita ku Yerusalemu.
12 Car la main du Seigneur excita leur cœur à partir et à suivre les ordres du roi et des princes, selon la parole du Seigneur.
Dzanja la Mulungu linalinso pa anthu a ku Yuda, kuwapatsa mtima umodzi wochita zimene mfumu ndi akuluakulu ake analamula potsata mawu a Yehova.
13 Une grande multitude se réunit donc à Jérusalem pour faire la fête des azymes le second mois; l'Église fut très-nombreuse.
Gulu lalikulu la anthu linasonkhana mu Yerusalemu kudzachita chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti pa mwezi wachiwiri.
14 Et ils se levèrent, et ils abattirent dans Jérusalem tous les autels où l'on brûlait de l'encens pour les faux dieux; ils les enlevèrent et les jetèrent dans le torrent de Cédron.
Anachotsa mu Yerusalemu maguwa ofukizira lubani ndipo anakawaponya mʼchigwa cha Kidroni.
15 Et ils immolèrent la pâque le quatorzième jour de la seconde lune, et les prêtres et les lévites, s'étant repentis et purifiés, offrirent des holocaustes dans le temple du Seigneur.
Iwo anapha mwana wankhosa wa Paska pa tsiku la 14 la mwezi wachiwiri. Ansembe ndi Alevi anachita manyazi ndipo anadziyeretsa ndi kubweretsa nsembe zopsereza ku Nyumba ya Yehova.
16 Et chacun se tint à son rang, selon leur ordonnance et selon les commandements de Moïse, homme de Dieu; les prêtres reçurent le sang des mains des lévites.
Ndipo anakhala mʼmalo awo a nthawi zonse potsatira zolembedwa mʼmalamulo a Mose munthu wa Mulungu. Ansembe anawaza magazi amene anawapatsa Alevi.
17 Car la plus grande partie de l'Église ne s'était point encore sanctifiée, et les lévites étaient prêts à immoler la pâque pour tous ceux qui n'avaient pu se sanctifier au Seigneur.
Popeza ambiri mʼgululo anali asanadziyeretse, Alevi anapha ana ankhosa a Paska a iwo amene, mwa mwambo, anali osayeretsedwa ndipo sakanatha kupereka ana ankhosa awo kwa Yehova.
18 Parmi le peuple d'Ephraïm, de Manassé, d'Issachar, de Zabulon, le plus grand nombre ne s'était pas purifié; mais ils mangèrent la pâque contrairement à l'Écriture; à cause de cela, Ezéchias fit pour eux cette prière, disant: Que le Seigneur, dans sa bonté, soit propice
Ngakhale kuti ambiri mwa anthu ochokera ku Efereimu, Manase, Isakara ndi Zebuloni sanadziyeretse okha, komabe anadya Paska motsutsana ndi zimene zinalembedwa. Koma Hezekiya anawapempherera, kunena kuti, “Yehova wabwino, khululukirani aliyense
19 A tous les cœurs qui cherchent avec droiture le Seigneur Dieu de leurs pères, quoiqu'ils n'aient point la pureté que veulent les choses saintes.
amene wayika mtima wake kufunafuna Yehova, Mulungu wa makolo ake, ngakhale ali wosayeretsedwa molingana ndi malamulo a malo opatulika.”
20 Et le Seigneur exauça Ezéchias, et il guérit tout le peuple.
Ndipo Yehova anamvera Hezekiya ndipo anachiritsa anthuwo.
21 Et les fils d'Israël, qui se trouvaient à Jérusalem, firent la fête des Azymes sept jours, en grande allégresse, célébrant chaque jour le Seigneur; et les prêtres et les lévites accompagnaient leurs chants avec les instruments consacrés.
Aisraeli amene anali mu Yerusalemu anachita chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti kwa masiku asanu ndi awiri akusangalala kwambiri, pamene Alevi ndi ansembe amayimbira Yehova tsiku lililonse, akuyimbira zida zamatamando za Yehova.
22 Et Ezéchias parla au cœur des lévites et de tous ceux qui comprenaient le mieux le Seigneur, et ils firent la fête des Azymes sept jours, sacrifiant l'hostie pacifique, et rendant gloire au Seigneur Dieu de leurs pères.
Hezekiya anayankhula molimbikitsa Alevi onse amene anaonetsa kumvetsa bwino za kutumikira Yehova. Kwa masiku asanu ndi awiri anadya gawo lawo ndi kupereka nsembe zachiyanjano ndi kutamanda Yehova, Mulungu wa makolo awo.
23 Et l'Église résolut de fêter une seconde fois sept jours, et ils les fêtèrent avec joie.
Ndipo msonkhano wonse unagwirizana zopitiriza chikondwerero kwa masiku ena asanu ndi awiri. Kotero kwa masiku ena asanu ndi awiri anachita chikondwererocho mosangalala.
24 Car Ezéchias offrit à Juda et à l'Église mille bœufs et sept mille brebis, et les princes amenèrent, pour le peuple, mille bœufs et dix mille brebis, et il y eut une multitude de prêtres qui furent sanctifiés.
Hezekiya mfumu ya Yuda anapereka ngʼombe zamphongo 1,000 ndi nkhosa ndi mbuzi 7,000 ku msonkhanoko ndipo akuluakulu ake anapereka ngʼombe zamphongo 1,000, nkhosa ndi mbuzi 10,000. Ansembe ambiri anadziyeretsa.
25 Et toute l'Église était pénétrée de joie: prêtres, lévites, Église de Juda, peuple réuni à Jérusalem, prosélytes venus de la terre d'Israël, étrangers habitant Juda.
Gulu lonse la ku Yuda linasangalala, pamodzi ndi ansembe ndi Alevi ndi onse amene anasonkhana ochokera ku Israeli, kuphatikizanso alendo amene anachokera ku Israeli ndi amene amakhala ku Yuda.
26 Et l'allégresse fut grande en Jérusalem; on n'y avait point vu pareille fête depuis les jours de Salomon et de David.
Munali chikondwerero chachikulu mu Yerusalemu, pakuti kuyambira masiku a Solomoni mwana wa Davide mfumu ya Israeli sizinachitikepo zotere mu Yerusalemu.
27 Et les prêtres et les lévites se levèrent, et ils bénirent le peuple, et leur voix fut entendue, et leur prière monta jusqu'aux saintes demeures de Dieu dans le ciel.
Ansembe ndi Alevi anayimirira kudalitsa anthu, ndipo Mulungu anawamvera pakuti pemphero lawo linafika kumwamba, malo ake oyera.

< 2 Chroniques 30 >