< 2 Chroniques 28 >
1 Achaz avait vingt-cinq ans lorsqu'il monta sur le trône, et il régna seize ans à Jérusalem; et il ne fit point ce qui est droit devant le Seigneur, comme David, son aïeul.
Ahazi anali ndi zaka makumi awiri pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 16. Iye sanachite zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide kholo lake.
2 Mais il marcha dans les voies des rois d'Israël, car il fit des sculptures,
Iye anayenda mʼnjira za mafumu a Israeli ndipo anawumbanso mafano a chipembedzo cha Abaala.
3 Et il sacrifia à leurs idoles dans le val de Benennom, et il fit passer ses enfants à travers la flamme; selon les abominations des peuples que le Seigneur avait exterminés devant les fils d'Israël.
Iye amapsereza nsembe ku chigwa cha Hinomu, ndipo anaperekanso ana ake aamuna ngati nsembe yopsereza kutsatira njira zonyansa za mitundu imene Yehova anayithamangitsa pamaso pa Aisraeli.
4 Et il brûla de l'encens sur les hauts lieux, et sur les terrasses des maisons, et sous les arbres touffus.
Iyeyo ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani pa malo opembedzerapo mafano, pamwamba pa mapiri ndi pansi pa mtengo uliwonse waukulu.
5 Alors le Seigneur Dieu le livra au roi de Syrie; il le frappa par ses mains, en permettant aux Syriens d'emmener à Damas une multitude de captifs; il le livra aussi au roi d'Israël, et de ses propres mains, il le frappa d'une grande plaie.
Nʼchifukwa chake Yehova Mulungu wake anamupereka mʼmanja mwa mfumu ya Aramu. Aaramu anamugonjetsa ndipo anagwira ukapolo anthu ake ambiri napita nawo ku Damasiko. Yehova anamuperekanso mʼmanja mwa mfumu ya Israeli, imene inamuzunza ndi kumuphera anthu ake ambiri.
6 Phacée, fils de Romélie, roi d'Israël, tua, en un seul jour, cent vingt mille hommes de Juda, forts et vaillants, parce qu'ils avaient abandonné le Seigneur Dieu de leurs pères.
Pa tsiku limodzi, Peka mwana wa Remaliya anapha asilikali 120,000 mu Yuda chifukwa Yuda anasiya Yehova, Mulungu wa makolo awo.
7 Et Zéchri, homme vaillant d'Ephraïm, tua Maasias, fils du roi; Esrican, son grand maître du palais, et Elcana, son lieutenant.
Zikiri msilikali wa ku Efereimu, anapha Maaseya mwana wa mfumu, Azirikamu woyangʼanira nyumba yaufumu, ndi Elikana wachiwiri kwa mfumu.
8 Et les fils d'Israël firent parmi leurs frères trois cent mille captifs: femmes, fils et filles; et ils leur enlevèrent un immense butin, et emportèrent les dépouilles à Samarie.
Aisraeli anagwira ukapolo abale awo, akazi, ana aamuna ndi ana aakazi okwanira 200,000. Iwo anafunkhanso katundu wambiri amene anapita naye ku Samariya.
9 Or, il y avait là un prophète du Seigneur nommé Obed, qui sortit à la rencontre de l'armée pendant qu'elle revenait à Samarie, et il leur dit: Voilà que la colère du Seigneur Dieu de vos pères est sur Juda; il vous les a livrés, et vous les avez massacrés avec fureur, et le bruit en est monté jusqu'au ciel.
Koma kumeneko kunali mneneri wa Yehova dzina lake Odedi, ndipo anapita kukakumana ndi gulu lankhondo pamene linabwerera ku Samariya. Iye anawawuza kuti, “Chifukwa Yehova, Mulungu wa makolo anu anakwiyira Ayuda, Iye anawapereka mʼdzanja lanu. Koma inu mwawapha mwaukali, ukali wake wofika mpaka kumwamba.
10 Et maintenant vous pensez garder comme esclaves les fils de Juda et de Jérusalem; mais ne suis-je point parmi vous pour prendre à témoin le Seigneur votre Dieu?
Ndipo tsopano mukufuna kuti amuna ndi akazi a ku Yuda ndi ku Yerusalemu akhale akapolo anu.
11 Écoutez-moi donc, et délivrez les captifs que vous avez enlevés chez vos frères; car la colère du Dieu terrible est sur vous.
Tsono mvereni! Abwezeni abale anu amene mwawagwira ukapolo, pakuti mkwiyo wa Yehova uli pa inu.”
12 Et les chefs des fils d'Ephraïm: Udie, fils de Jean; Barachias, fils de Mosolmoth; Ezéchias, fils de Sellem; et Amasias, fils d'Eldaï, s'élevèrent pareillement contre ceux qui revenaient du combat.
Tsono atsogoleri ena a ku Efereimu, Azariya mwana wa Yehohanani, Berekiya mwana wa Mesilemoti, Yehizikiya mwana wa Salumu, ndi Amasa mwana wa Hadilayi anatsutsana nawo amene ankachokera ku nkhondo kuja.
13 Et ils leur dirent: Vous n'introduirez point ici, chez nous, ces captifs; car, lorsque vous péchez contre le Seigneur, votre péché retombe sur nous; et vous entendez ajouter à vos péchés et à vos délits par ignorance, quand déjà vos fautes sont nombreuses, et quand une terrible colère du Seigneur est sur Israël?
Iwo anati, “Musabweretse akapolowo kuno, pakuti ife tidzakhala olakwa pamaso pa Yehova. Kodi mukufuna kuwonjezera pa machimo athu ndi kulakwa kwathu? Pakuti zolakwa zathu ndi zambiri kale ndipo mkwiyo wake woopsa uli pa Israeli.”
14 Et les guerriers mirent en liberté les captifs, et ils leur rendirent les dépouilles, devant les chefs de toute l'Église.
Kotero asilikali aja anawasiya akapolowo pamodzi ndi katundu amene analanda ku nkhondo pamaso pa akuluakulu ndi gulu lonse la anthu.
15 Et les hommes qui viennent d'être nominativement désignés, se levèrent, prirent soin des captifs, les vêtirent d'objets compris dans les dépouilles, les habillèrent, les chaussèrent, leur donnèrent des vivres pour manger, de l'huile pour se parfumer, firent monter les infirmes sur des ânes, les menèrent avec leurs frères jusqu'à Jéricho, ville des palmiers, et retournèrent à Samarie.
Anthu amene atchulidwa mayina aja anatenga akapolowo, ndipo kuchokera pa zolanda ku nkhondo, anawaveka onse amene anali maliseche. Anawapatsa zovala ndi nsapato, chakudya ndi chakumwa ndi mankhwala. Onse amene anali ofowoka anawakweza pa abulu. Choncho anabwera nawo kwa abale awo ku Yeriko, Mzinda wa Migwalangwa, ndipo kenaka anawabweza ku Samariya.
16 En ce temps-là, le roi Achaz envoya chez le roi assyrien demander son secours,
Pa nthawi imeneyo mfumu Ahazi inatumiza mawu kwa mfumu ya ku Asiriya kupempha chithandizo.
17 Et voici pourquoi: les Sidoniens faisaient des irruptions; ils frappaient Juda, et lui enlevaient des captifs.
Ankhondo a ku Edomu anabweranso ndi kuthira nkhondo Yuda ndi kugwira akapolo.
18 Les Philistins aussi avaient pris les armes contre les villes de la plaine, au midi de Juda, et s'étaient emparés de Bethsamys, de Galero, de Socho et de ses bourgs, de Thamna et de ses bourgs, de Gamzo et de ses bourgs, et ils s'y étaient établis.
Pamenepo nʼkuti Afilisti atathira nkhondo mizinda ya mʼmbali mwa phiri ndi ku Negevi ku Yuda. Iwo analanda mizindayo nakhala ku Beti-Semesi, Ayaloni ndi Gederoti, komanso Soko, Timna ndi Gimizo pamodzi ndi midzi yawo yozungulira.
19 Car le Seigneur avait humilié Juda, à cause du roi Achaz qui s'était détourné du Seigneur.
Yehova anapeputsa Yuda chifukwa cha mfumu Ahazi ya Israeli, pakuti analimbikitsa zoyipa ku Yuda ndipo anali munthu wosakhulupirika kwambiri pamaso pa Yehova.
20 Alors, Thelgath-Phalnasar, roi des Assyriens, intervint, mais contre lui, et il l'opprima.
Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya anabwera kwa iye, ndipo anabweretsa mavuto mʼmalo momuthandiza.
21 Et Achaz prit les richesses du temple du Seigneur, celles du palais du roi, celles des demeures des princes, et il les donna au roi assyrien; or, celui-ci n'était pas venu pour le secourir,
Ahazi anatenga zinthu zochokera mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba yaufumu ndi kwa atsogoleri ndipo anazipereka kwa mfumu ya ku Asiriya, koma zimenezo sizinamuthandize.
22 Mais pour l'écraser; cependant, le roi Achaz continua de se détourner du Seigneur, et il dit:
Pa nthawi yake yamavutoyi mfumu Ahazi inapitirira kukhalabe yosakhulupirika pamaso pa Yehova.
23 Je chercherai les dieux de Damas qui me frappent. Puis, il ajouta: Ce sont les dieux du roi de Syrie qui lui donnent de la force; je leur sacrifierai donc, et ils me protégeront. Et ils furent une cause de chute pour lui et pour Israël.
Ahazi ankapereka nsembe kwa milungu ya ku Damasiko, imene inamugonjetsa. Iye ankaganiza kuti, “Popeza milungu ya mafumu a Aaramu yawathandiza, ine ndidzapereka nsembe kwa iyo kuti indithandize.” Koma iyoyo inakhala kugwa kwake ndi kugwa kwa Aisraeli onse.
24 Achaz retira donc les vases du temple du Seigneur, il les brisa, ferma les portes du temple, et se fit des autels dans tous les carrefours de Jérusalem.
Ahazi anasonkhanitsa pamodzi zinthu zonse kuchokera mʼNyumba ya Mulungu ndipo anazitenga. Iye anatseka zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anayimika maguwa ansembe pa ngodya iliyonse ya msewu mu Yerusalemu.
25 Et il établit des hauts lieux dans toutes les villes de Juda pour que l'on y encensât des dieux étrangers; et les fils de Juda excitèrent le courroux du Seigneur Dieu de leurs pères.
Mu mzinda uliwonse wa Yuda anamangamo malo achipembedzo, operekerapo nsembe zopsereza kwa milungu ina ndipo anaputa mkwiyo wa Yehova, Mulungu wa makolo ake.
26 Le reste de ses faits et gestes, les premiers et les derniers, sont écrits au livre des Rois de Juda et d'Israël.
Zochitika zina pa ulamuliro wake ndi machitidwe ake onse, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
27 Et Achaz s'endormit avec ses pères, et il fut enseveli en la ville de David; mais on ne le transporta pas dans le sépulcre des rois d'Israël, et son fils Ezéchias régna à sa place.
Ahazi anamwalira ndipo anayikidwa mu mzinda wa Yerusalemu, koma sanamuyike mʼmanda a mafumu a Israeli. Ndipo Hezekiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.