< 2 Chroniques 25 >

1 Amasias avait vingt-cinq ans lorsqu'il monta sur le trône, et il régna vingt-neuf ans à Jérusalem; sa mère s'appelait Joadan de Jérusalem.
Amaziya anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 29. Dzina la amayi ake linali Yehoyadini wa ku Yerusalemu.
2 Et il fit ce qui est droit devant' Dieu, mais non avec plénitude de cœur.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, koma osati ndi mtima wonse.
3 Lorsqu'il eut affermi sa royauté, il fit mettre à mort les serviteurs qui avaient tué le roi, son père.
Pamene mphamvu zonse zaufumu zinali mʼmanja mwake, iye anapha akuluakulu amene anapha abambo ake, mfumu ija.
4 Mais il ne fit pas périr leurs fils, se conformant à l'alliance de la loi du Seigneur. Car il est écrit, et tel est le commandement de Dieu: Les pères ne mourront pas à cause de leurs enfants, et les fils ne mourront pas à cause de leurs pères; mais chacun portera la peine de son péché.
Komabe iye sanaphe ana awo koma anatsatira zolembedwa mʼbuku la Mose, mʼmene Yehova analamula kuti, “Makolo sadzaphedwa chifukwa cha ana awo kapena ana kuphedwa chifukwa cha makolo awo. Aliyense adzafera machimo ake.”
5 Ensuite, Amasias assembla la maison de Juda, et il les mit par familles paternelles sous des chefs de mille hommes et des centeniers, en Juda et en Jérusalem; il fit le dénombrement du peuple depuis vingt ans et au-dessus, et il trouva trois cent mille hommes capables de faire la guerre, sachant manier la javeline et le bouclier.
Amaziya anasonkhanitsa anthu a ku Yuda ndipo anawapatsa zochita molingana ndi mabanja awo kukhala anthu olamulira 1,000, ndi olamulira 100 pa Ayuda onse ndi Benjamini. Ndipo iye anawerenga amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo napeza kuti analipo amuna 300,000 okonzeka kugwira ntchito ya usilikali, okhoza kugwiritsa ntchito mkondo ndi chishango.
6 Il enrôla de plus cent mille hommes d'Israël, vaillants et robustes, au prix de cent talents d'argent.
Iye analembanso ntchito anthu odziwa nkhondo 100,000 ochokera ku Israeli pa mtengo wa makilogalamu 3,400 a siliva.
7 Mais un homme de Dieu vint le trouver, disant: Roi, n'emmène pas avec toi les troupes d'Israël, car le Seigneur n'est point avec Israël, ni avec aucun des fils d'Ephraïm.
Koma munthu wa Mulungu anabwera kwa iye ndipo anati, “Inu mfumu, asilikali awa ochokera ku Israeli asapite ndi inu, pakuti Yehova sali ndi Israeli kapena ndi aliyense wa anthu a Efereimu.
8 Si tu les prends pour te renforcer, le Seigneur te mettra en fuite devant tes ennemis; car il appartient au Seigneur de renforcer une armée ou de la mettre en fuites.
Ngakhale mupite ndi kuchita nkhondo molimba mtima, Mulungu adzakugonjetsani pamaso pa adani anu, pakuti Mulungu ali ndi mphamvu yothandiza kapena kugonjetsa.”
9 Alors, Amasias dit à l'homme de Dieu: Que deviendront les cent talents d'argent que j'ai donnés aux troupes d'Israël? Et l'homme de Dieu répondit: Il ne tient qu'au Seigneur de t'en rendre beaucoup plus.
Amaziya anafunsa munthu wa Mulungu kuti, “Koma nanga za makilogalamu aja a siliva amene ndapereka kwa asilikali a Israeli?” Munthu wa Mulungu anayankha kuti, “Yehova atha kukupatsani zambiri kuposa zimenezo.”
10 Et Amasias éloigna l'armée qui était venue près de lui d'Ephraïm, pour que chacun retournât en sa demeure. Et ils se courroucèrent vivement contre Juda, et ils s'en allèrent chez eux la colère dans l'âme.
Choncho Amaziya anachotsa asilikali amene anabwera kwa iye kuchokera ku Efereimu ndipo anawatumiza kwawo. Iwo anakwiyira anthu a ku Yuda ndipo anapita kwawo atapsa mtima kwambiri.
11 Et Amasias se fortifia, et il prit son peuple, et il alla dans le val des Sels, et il tailla en pièces dix mille des fils de Seïr.
Ndipo Amaziya analimba mtima ndipo anatsogolera gulu lake lankhondo ku Chigwa cha Mchere, kumene anapha anthu 10,000 a ku Seiri.
12 Et les fils de Juda firent, en outre, dix mille prisonniers; ils les transportèrent sur la cime du précipice, et ils les jetèrent au bas des rochers, et ces hommes furent déchirés.
Gulu la ankhondo la Yuda linagwiranso anthu amoyo 10,000, napita nawo pamwamba pa thanthwe ndipo anawaponya pansi kotero kuti onse ananyenyeka.
13 Et les hommes de l'armée qu'Amasias avait congédiés, pour qu'ils n'allassent pas en guerre avec lui, attaquèrent les villes de Juda, depuis Samarie jusqu'à Béthoron, et ils y tuèrent trois mille hommes, et ils y firent un riche butin.
Pa nthawi imeneyi asilikali amene Amaziya anawabweza ndipo sanawalole kuti achite nawo nkhondo, anakathira nkhondo mizinda ya Yuda kuyambira ku Samariya mpaka ku Beti-Horoni. Iwo anapha anthu 3,000 ndipo anafunkha katundu wambiri.
14 Or, après qu'Amasias revint ayant vaincu l'Idumée, il en rapporta les dieux des fils de Séir, et il les tint pour des dieux véritables, et il se prosterna devant eux, et il leur fit des sacrifices.
Amaziya atabwerera kuja anakapha Aedomu, anabweretsa milungu ya anthu a ku Seiri. Ndipo anayika kuti ikhale milungu yake, ankayipembedza ndi kupereka nsembe zopsereza.
15 Et la colère du Seigneur s'enflamma centre Amasias, et il lui envoya le prophète, qui lui dit: Pourquoi as-tu cherché les dieux d'un peuple qu'ils n'ont pu délivrer de tes mains?
Yehova anakwiyira Amaziya, ndipo anamutumizira mneneri amene anati, “Nʼchifukwa chiyani mukupembedza milungu ya anthu awa, imene sinathe kupulumutsa anthu ake mʼdzanja lanu?”
16 Et, pendant que le prophète parlait encore, Amasias dit: Est-ce que je t'ai fait conseiller du roi? Contiens-toi, si tu ne veux être fustigé. Et le prophète garda le silence, et il se dit: Je sais que le Seigneur a résolu de te détruire, parce que tu as fais cette chose, et que tu refuses d'écouter mes conseils.
Iye ali kuyankhula, mfumu inati, “Kodi ife takusankha iwe kuti ukhale mlangizi wa mfumu? Khala chete! Ufuna kuphedweranji?” Choncho mneneriyo analeka koma anati, “Ine ndikudziwa kuti Mulungu watsimikiza kukuwonongani chifukwa mwachita izi ndipo simunamvere uphungu wanga.”
17 Ensuite, Amasias, roi de Juda, délibéra, et il envoya dire à Joas, fils de Joachaz, fils de Jéhu, roi d'Israël: Viens, que nous nous voyions face à face.
Amaziya mfumu ya ku Yuda, atafunsa alangizi ake, anatumiza mawu awa kwa Yowasi mwana wa Yehowahazi mwana wa Yehu, mfumu ya Israeli: “Bwera udzakumane nane maso ndi maso.”
18 Et Joas, roi d'Israël, envoya dire à Amasias: Le chardon du Liban envoya dire au cèdre du Liban: Donne en mariage ta fille à mon fils; mais voilà que les bêtes fauves des campagnes, qui sont dans le Liban, allaient venir, et les bêtes fauves vinrent, et elles foulèrent aux pieds le chardon.
Koma Yowasi mfumu ya Israeli inayankha Amaziya mfumu ya Yuda kuti, “Nthawi ina kamtengo kaminga ka ku Lebanoni kanatumiza mawu kwa mkungudza wa ku Lebanoni kuti, ‘Pereka mwana wako wamkazi kwa mwana wanga kuti amukwatire!’ Koma chirombo cha ku Lebanoni chinabwera ndi kupondaponda mtengo wa minga uja.
19 Or, tu as dit: Voilà que j'ai vaincu l'Idumée. Et ton cœur impérieux s'est enorgueilli; reste donc en repos dans ta maison; car, pourquoi te mettre aux prises avec le malheur? Tu tomberas, et Juda avec toi.
Iwe ukuti wagonjetsa Edomu, ndipo tsopano ukudzikuza ndi kudzitamandira, koma khala kwanu komweko! Nʼchifukwa chiyani ukufuna mavuto ndi kudzichititsa kuti ugwe pamodzinso ndi Yuda?”
20 Mais Amasias ne l'écouta pas, car le Seigneur avait dessein de le livrer aux mains de Joas, parce qu'il avait cherché les dieux d'Edom.
Komabe Amaziya sanamvere pakuti ndi Mulungu amene anakonzeratu kuti awapereke kwa Yehowasi, chifukwa iwo amapembedza milungu ya ku Edomu.
21 Joas, roi d'Israël, partit donc, et les deux rois se virent l'un l'autre à Bethsamys en Judée.
Kotero Yowasi mfumu ya Israeli inakamuthira nkhondo. Iye ndi Amaziya anayangʼanana maso ndi maso ku Beti-Semesi ku Yuda.
22 Et Juda tourna le dos devant Israël, et chacun s'enfuit en sa demeure.
Yuda anagonjetsedwa ndi Israeli ndipo munthu aliyense anathawira kwawo.
23 Et Joas fit Amasias prisonnier, et il le ramena à Jérusalem; et il abattit un pan des remparts, long de quatre cents coudées, depuis la porte d'Ephraïm jusqu'à la porte de l'angle.
Yehowahazi mfumu ya Israeli inagwira Amaziya mfumu ya Yuda, mwana wa Yowasi, mwana wa Ahaziya ku Beti-Semesi. Yehowasi anabwera naye ku Yerusalemu ndipo anagwetsa khoma la Yerusalemu kuyambira pa Chipata cha Efereimu mpaka ku Chipata Chapangodya, khoma lotalika mamita 180.
24 Et il prit l'argent, l'or, tous les ornements qu'il trouva dans le temple du Seigneur, ce qui provenait d'Abdedom, les trésors du palais du roi, des otages, et il retourna dans Samarie.
Iye anatenga golide ndi siliva yense ndi zida zonse zimene zimapezeka mʼNyumba ya Mulungu zimene ankazisamalira Obedi-Edomu, pamodzinso ndi chuma cha mʼnyumba yaufumu ndipo anatenga anthu ngati chikole.
25 Amasias, fils de Joas, roi de Juda, vécut encore quinze ans après la mort de Joas, fils de Joachaz, roi d'Israël.
Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anakhala ndi moyo kwa zaka khumi ndi zisanu atamwalira Yehowasi mwana wa Yehowahazi mfumu ya Israeli.
26 Les restes des actes d'Amasias, les premiers et les derniers, ne sont-ils pas écrits au livre des Rois de Juda?
Ntchito zina za mfumu Amaziya, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli?
27 Dans le temps où Amasias s'était éloigné du Seigneur, un complot éclata contre lui, et il s'enfuit de Jérusalem à Lachis; mais les révoltés envoyèrent à sa poursuite, et, en cette ville, ils le tuèrent.
Kuyambira nthawi imene Amaziya analeka kutsatira Yehova anthu anamukonzera chiwembu mu Yerusalemu ndipo anathawira ku Lakisi, koma adaniwo anatumiza anthu ku Lakisiko ndipo anamupha komweko.
28 Et ils l'enlevèrent sur un char, et ils l'ensevelirent auprès de ses pères dans la ville de David.
Iwo anabwera naye ali pa kavalo ndipo anayikidwa mʼmanda ndi makolo ake mu mzinda wa Yuda.

< 2 Chroniques 25 >