< 2 Chroniques 24 >

1 Joas avait sept ans quand il monta sur le trône, et il régna quarante ans à Jérusalem; sa mère s'appelait Sable de Bersabée.
Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka makumi anayi. Dzina la amayi ake linali Zibiya wa ku Beeriseba.
2 Et Joas fit ce qui est droit aux yeux du Seigneur, tant que Joad vécut.
Yowasi anachita zolungama pamaso pa Yehova nthawi yonse ya moyo wa wansembe Yehoyada.
3 Joad lui fit épouser deux femmes, et il engendra des fils et des filles.
Yehoyada anamupezera iye akazi awiri, ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi.
4 Après cela, la pensée de restaurer le temple entra dans le cœur de Joas.
Patapita nthawi Yowasi anatsimikiza zokonzanso Nyumba ya Yehova.
5 Il réunit donc les prêtres et les lévites, et il leur dit: Allez dans toutes les villes de Juda, et recueillez de tout Israël de l'argent pour réparer, d'année en année, le temple du Seigneur; hâtez-vous de partir. Mais les lévites ne se hâtèrent pas.
Iye anayitanitsa pamodzi ansembe ndi Alevi ndipo anawawuza kuti, “Pitani ku mizinda ya Yuda ndi kukasonkhetsa ndalama za pa chaka kwa Aisraeli onse zokonzera Nyumba ya Mulungu wanu. Chitani zimenezi tsopano.” Koma Alevi sanachite zimenezi mwachangu.
6 Et le roi Joas appela Joad leur chef, et il lui dit: Pourquoi n'as-tu point veillé à ce que les lévites apportassent de Juda et de Jérusalem ce qu'a réglé Moïse l'homme de Dieu, quand il eut rassemblé Israël au sujet du tabernacle du témoignage?
Choncho mfumu inayitanitsa Yehoyada, mkulu wa ansembe ndipo inati kwa iye, “Kodi nʼchifukwa chiyani simunawuze Alevi kuti asonkhetse ndalama ku Yuda ndi Yerusalemu, msonkho umene anakhazikitsa Mose mtumiki wa Yehova ndiponso gulu lonse la Aisraeli mu tenti yaumboni?”
7 Car Athalie était pleine d'iniquité, et ses fils ont ébranlé le temple de Dieu; ils ont employé pour Baal les choses saintes du temple du Seigneur.
Ana a mkazi woyipa, Ataliya, anathyola chitseko cha Nyumba ya Mulungu ndipo anagwiritsa ntchito zinthu zopatulika popembedza Baala.
8 Et le roi ajouta: Que l'on fasse une cassette, et qu'on la place extérieurement à la porte principale du temple,
Mfumu italamulira, bokosi linapangidwa ndipo linayikidwa panja pa chipata cha Nyumba ya Yehova.
9 Et que l'on proclame en Juda et à Jérusalem que chacun ait à apporter pour le Seigneur ce que Moïse, serviteur de Dieu, a dit dans le désert concernant Israël.
Ndipo analengeza kwa anthu a mu Yuda ndi mu Yerusalemu kuti abweretse kwa Yehova msonkho umene Mose mtumiki wa Mulungu analamulira Aisraeli mʼchipululu.
10 Alors, tous les chefs donnèrent, tout le peuple donna; chacun apporta son offrande et la jeta dans la cassette, jusqu'à ce qu'elle fût remplie.
Akuluakulu onse ndi anthu onse anabweretsa zopereka zawo mokondwera ndipo anaziponya mʼbokosi mpaka linadzaza.
11 Or, quand les lévites virent que l'argent abondait, ils portèrent la cassette devant les intendants du roi; le scribe du roi avec l'intendant du grand prêtre vinrent, et ils vidèrent la cassette; puis, ils la remirent à sa place. Ils firent de même chaque jour, et ils recueillirent beaucoup d'argent,
Nthawi ina iliyonse imene Alevi abweretsa bokosilo kwa akuluakulu a mfumu ndipo akaona kuti muli ndalama zambiri, mlembi waufumu ndi nduna yayikulu ya mkulu wa ansembe amabwera ndi kuchotsa ndalama mʼbokosi muja ndipo amalitenga kukaliyika pamalo pake. Iwo amachita izi nthawi ndi nthawi ndipo anapeza ndalama zambiri.
12 Que le roi et Joad donnèrent aux conducteurs des travaux du temple; ceux-ci engagèrent des tailleurs de pierre et des charpentiers, et des hommes habiles à forger le fer et l'airain, pour restaurer le temple.
Mfumu pamodzi ndi Yehoyada anapereka ndalamazo kwa anthu oyangʼanira ntchito ku Nyumba ya Yehova. Analemba ntchito amisiri a miyala ndi a matabwa kuti akonzenso Nyumba ya Yehova. Analembanso ntchito amisiri a zitsulo ndi mkuwa kuti akonze Nyumba ya Mulungu.
13 Et les travailleurs se mirent à l'œuvre, qui prospéra entre leurs mains; ils rétablirent le temple du Seigneur jusqu'aux fondations, et ils le consolidèrent.
Anthu amene ankagwira ntchito anali odziwa bwino, ndipo ntchitoyo inagwiridwa bwino ndi manja awo. Iwo anamanganso Nyumba ya Mulungu motsatira mapangidwe ake oyamba ndipo anayilimbitsa.
14 Quand ils eurent achevé, ils rapportèrent au roi et à Joad le reste de l'argent, et l'on fit des vases pour le temple du Seigneur, des ustensiles pour le service des holocaustes, des encensoirs d'or et d'argent. Enfin, on offrit des holocaustes perpétuels, tant que vécut Joad.
Atamaliza, iwo anabweretsa ndalama zotsala kwa mfumu ndi Yehoyada, ndipo anazigwiritsira ntchito popangira zida za mʼNyumba ya Yehova: ziwiya zogwiritsa ntchito potumikira ndi popereka nsembe zopsereza, komanso mbale ndi ziwiya zagolide ndi siliva. Nthawi yonse ya moyo wa Yehoyada, nsembe zopsereza zinkaperekedwa mosalekeza mʼNyumba ya Yehova.
15 Et Joad devint vieux, et plein de jours, et il mourut âgé de cent trente ans.
Tsono Yehoyada anakalamba ndipo anali ndi zaka zambiri. Pambuyo pake iye anamwalira ali ndi zaka 130.
16 On l'ensevelit en la ville de David avec les rois, parce qu'il avait été bon envers Israël, envers Dieu et envers son temple.
Iyeyo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu mu mzinda wa Davide chifukwa cha zabwino zimene anachita mu Israeli, kuchitira Mulungu ndi Nyumba yake.
17 Et après sa mort les princes de Juda entrèrent auprès de Joas, et ils se prosternèrent devant lui, et il leur prêta l'oreille.
Atamwalira Yehoyada, akuluakulu a Yuda anabwera kudzapereka ulemu kwa mfumu, ndipo mfumu inawamvera.
18 Et ils abandonnèrent le temple du Seigneur Dieu de nos pères, et ils servirent Astarté et les idoles; or, en ce jour-là, il y eut une colère du Seigneur contre Juda et contre Jérusalem.
Iwo anasiya Nyumba ya Yehova, Mulungu wa makolo awo ndipo anapembedza Asera ndi mafano. Chifukwa cha kulakwa kwawo, mkwiyo wa Yehova unabwera pa Yuda ndi Yerusalemu.
19 Il leur envoya des prophètes pour les ramener à lui; mais, ils ne les écoutèrent pas; il leur signifia sa volonté; mais, ils n'obéirent pas.
Ngakhale Yehova anatumiza aneneri kwa anthuwo kuti awabweze kwa Iye, ngakhale aneneri ananenera mowatsutsa, anthuwo sanamvere.
20 Alors l'Esprit de Dieu vint sur Zacharie, fils de Joad, le prêtre, et il se plaça devant le peuple, et il s'écria: Voici ce que dit le Seigneur: Pourquoi transgressez-vous les commandements du Seigneur? Vous ne prospèrerez pas, car vous avez abandonné le Seigneur, et il vous abandonnera.
Kenaka Mzimu wa Mulungu unabwera pa Zekariya mwana wa wansembe Yehoyada. Iye anayimirira pamaso pa anthu ndipo anati, “Zimene Mulungu akunena ndi Izi: ‘Chifukwa chiyani simukumvera Malamulo a Yehova? Simudzapindula. Chifukwa mwasiya Yehova, Iyenso wakusiyani.’”
21 Mais, ils se jetèrent sur lui, et, par l'ordre du roi Joas, ils le lapidèrent dans le parvis du temple du Seigneur.
Koma anthuwo anamuchitira chiwembu molamulidwa ndi mfumu ndipo anamugenda miyala ndi kumupha mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
22 Ainsi, Joas oublia les bienfaits de Joad, et il fit lapider son fils. Celui-ci dit en mourant: Que le Seigneur voie et juge.
Mfumu Yowasi sinakumbukire zabwino zimene Yehoyada abambo ake a Zekariya anamuchitira, koma anapha mwana wake. Pamene amafa, iye ananena kuti, “Yehova aone zimenezi ndipo abwezere chilango.”
23 Et après que l'année eut fini son cours, l'armée syrienne marcha contre Joas; elle attaqua Juda et Jérusalem; elle extermina, au milieu du peuple, tous les princes, et elle envoya leurs dépouilles au roi de Damas.
Pakutha kwa chaka, gulu lankhondo la Aramu linadzamenyana ndi Yowasi. Linalowa mu Yuda ndi mu Yerusalemu ndi kupha atsogoleri onse a anthu. Zonse zimene analanda anazitumiza kwa mfumu ya ku Damasiko.
24 Elle était venue peu nombreuse; mais Dieu lui avait livré une grande armée, parce que les fils de Juda avaient abandonné le Dieu de leurs pères, et que le Seigneur avait prononcé l'arrêt de Joas.
Ngakhale kuti gulu lankhondo la Aramu linabwera ndi anthu ochepa okha, Yehova anapereka mʼmanja mwawo gulu lalikulu lankhondo. Chifukwa Yuda anasiya Yehova Mulungu wa makolo awo, chiweruzo chinachitika pa Yowasi.
25 Et après que les Syriens se furent éloignés de celui-ci, lorsqu'ils l'eurent laissé aux prises avec des maux cruels, ses serviteurs eux-mêmes portèrent la main sur lui pour le punir d'avoir versé le sang du fils de Joad le prêtre; ils le tuèrent sur sa couche, et il mourut; et on l'ensevelit dans la ville de David, mais non dans le sépulcre des rois.
Pamene Aaramu amachoka, anasiya Yowasi atavulazidwa kwambiri. Akuluakulu ake anamuchitira chiwembu chifukwa anapha mwana wa wansembe Yehoyada, ndipo anamupha ali pa bedi pake. Choncho anafa ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide, koma osati manda a mafumu.
26 Et ceux qui l'avaient assailli étaient Zabed, fils de Samaath l'Ammonite, et Jozabed, fils de Samareth le Moabite,
Iwo amene anamuchitira chiwembu anali Zabadi mwana wa Simeati, mkazi wa ku Amoni, ndi Yehozabadi mwana wa Simiriti, mkazi wa ku Mowabu.
27 Et tous les fils de ce dernier, car il y en avait cinq, qui se joignirent à lui. Le reste est écrit aux Récits des rois; et Amasias, fils de Joas, régna à sa place.
Za ana ake aamuna, uneneri wonena za iye, mbiri ya kumanganso Nyumba ya Mulungu, zalembedwa mʼbuku lofotokoza za mafumu. Ndipo Amaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Chroniques 24 >