< 2 Chroniques 20 >
1 Après cela, les fils de Moab, les fils d'Ammon, et, avec eux, des Minéens, se mirent en campagne pour attaquer Josaphat.
Zitatha izi, Amowabu ndi Aamoni pamodzi ndi Ameuni ena anabwera kudzachita nkhondo ndi Yehosafati.
2 Et des gens vinrent et ils l'apprirent au roi, disant: Une grande multitude est venue contre toi des bords de la mer, du côté de la Syrie, et la voici en Asasan-Thamar (la même qu'Engaddi).
Anthu ena anabwera kudzamuwuza Yehosafati kuti, “Gulu lalikulu kwambiri lankhondo likubwera kudzachita nanu nkhondo lochokera ku Edomu, ku mbali ina ya Nyanja. Gululi lafika kale ku Hazazoni Tamara” (ndiye kuti Eni-Gedi).
3 Et Josaphat eut crainte, et il s'appliqua à chercher le Seigneur, et il proclama un jeûne dans tout Juda.
Ndi mantha, Yehosafati anaganiza zofunsira kwa Yehova, ndipo analengeza kuti Ayuda onse asale zakudya.
4 Et Juda se rassembla pour chercher le Seigneur; et, de toutes les villes de Juda, on vint pour chercher le Seigneur.
Anthu a ku Yuda anabwera pamodzi kudzafuna thandizo kwa Yehova, ndipo anabweradi kuchokera ku mzinda uliwonse wa mu Yuda kudzafunafuna Yehova.
5 Et Josaphat, avec toute l'Église de Juda en Jérusalem, se tint debout dans le temple du Seigneur devant le parvis neuf.
Yehosafati anayimirira pakati pa msonkhano wa Yuda ndi Yerusalemu, pa Nyumba ya Yehova patsogolo pa bwalo latsopano
6 Et il dit: Seigneur Dieu de mes pères, n'êtes-vous point Dieu dans le ciel au-dessus de nous? N'êtes-vous pas le Seigneur de tous les royaumes des nations? N'est-ce pas en vos mains que réside la force du pouvoir? Est-il quelqu'un qui puisse vous résister?
ndipo anati: “Inu Yehova, Mulungu wa makolo athu, kodi Inu sindinu Mulungu amene muli kumwamba? Inu mumalamulira maufumu onse a mitundu ya anthu. Mphamvu ndi nyonga zili mʼmanja mwanu, ndipo palibe amene angalimbane nanu.
7 N'êtes-vous pas le Seigneur dont le bras a exterminé les habitants de cette terre, devant les fils d'Israël, votre peuple? Ne l'avez-vous point donnée pour toujours à la race d'Abraham, votre bien-aimé?
Inu Mulungu wathu, kodi simunathamangitse nzika za dziko lino pamaso pa anthu anu Aisraeli ndipo munalipereka kwa zidzukulu za Abrahamu bwenzi lanu kwamuyaya?
8 Elle y demeure; elle y a bâti un lieu saint à votre nom, disant
Iwo akhala mʼdzikolo ndipo anamangira Dzina lanu malo opatulika, nʼkumati,
9 Si le mal, le glaive, la vengeance, la mort, la famine, viennent sur nous, nous nous tiendrons devant le temple et devant vous, ô Seigneur, parce que votre nom est sur le temple, et, dans notre affliction, nous crierons à vous, et vous nous entendrez, et vous nous sauverez.
‘Ngati tsoka litigwera kaya ndi lupanga lachiweruzo, kapena mliri, kapenanso njala, ife tidzayima pamaso panu patsogolo pa Nyumba ya Mulungu ino imene imatchedwa ndi Dzina lanu ndipo tidzalirira kwa inu mʼmasautso athu, ndipo Inu mudzatimvera ndi kutipulumutsa.’
10 Et maintenant, voilà que les fils d'Ammon, et Moab et ceux de la montagne de Seïr, chez qui vous n'avez point permis à Israël de passer, à sa sortie d'Égypte (car il s'est détourné de leurs territoires, et ne les a point exterminés),
“Koma tsopano pano pali anthu ochokera ku Amoni, Mowabu ndi Phiri la Seiri amene dziko lawo Inu simunawalole Aisraeli kuti alithire nkhondo pamene amabwera kuchokera ku Igupto. Kotero anatembenuka ndi kuwaleka ndipo sanawawononge.
11 Voilà qu'ils nous attaquent pour entrer dans l'héritage que vous nous avez donné, et pour nous en bannir.
Taonani, mmene akutibwezera ife pobwera kudzatithamangitsa mʼdziko limene inu munatipatsa ngati cholowa chathu.
12 Seigneur notre Dieu, ne les jugerez-vous pas? Car nous n'avons pas la force de résister à l'immense multitude qui marche contre nous, et nous ne savons que leur faire, sinon de tourner nos yeux vers vous.
Inu Mulungu wathu, kodi simuwaweruza? Pakuti ife tilibe mphamvu zolimbana ndi gulu lalikulu lankhondo limene likutithira nkhondoli. Ife sitikudziwa choti tichite, koma maso athu ali pa Inu.”
13 Or, tout Juda était là devant le Seigneur, avec leurs enfants et leurs femmes.
Anthu onse a Yuda, pamodzi ndi akazi awo ndi ana ndi makanda, anayima chilili pamaso pa Yehova.
14 Et, dans l'Église, l'Esprit du Seigneur descendit sur Oziel, fils de Zacharie, des fils de Bandias, des fils d'Elihel, fils du lévite Matthanias, des fils d'Asaph.
Ndipo Mzimu wa Yehova unabwera pa Yahazieli mwana wa Zekariya, mwana wa Benaya, mwana wa Yeiyeli, mwana wa Mataniya Mlevi, chidzukulu cha Asafu, atayimirira mu msonkhano.
15 Et il dit: Écoutez, ô Juda, et vous habitants de Jérusalem, et toi, roi Josaphat: voici ce que vous dit le Seigneur: N'ayez point de crainte, ne tremblez pas devant cette multitude immense; car ce combat n'est point de vous, mais de Dieu.
Iye anati, “Tamverani mfumu Yehosafati ndi onse amene amakhala mu Yuda ndi Yerusalemu! Zimene Yehova akunena kwa inu ndi izi: ‘Musaope kapena kutaya mtima chifukwa cha gulu lalikulu lankhondo ili. Pakuti nkhondoyi si yanu, koma ya Mulungu.
16 Marchez demain contre elle; ils monteront le coteau d'Assis, et vous les trouverez à l'extrémité du torrent qui traverse le désert de Jerihel.
Mawa mupite mukamenyane nawo. Adzakhala akubwera mokweza kudzera Njira ya Zizi, ndipo mukawapeza kumapeto kwa chigwa cha ku chipululu cha Yeruweli.
17 Ce n'est point à vous de les combattre; comprenez cela, et voyez comme le Seigneur, ô Juda et Jérusalem, opèrera votre salut. N'ayez point de crainte, n'hésitez pas à marcher demain à leur rencontre: le Seigneur est avec vous.
Sikudzafunika kuti Inu mumenyane nawo pa nkhondo imeneyi. Inu mukhale pa malo anu; imani molimba ndipo onani chipulumutso chimene Yehova adzakupatsani, Inu Yuda ndi Yerusalemu. Musaope, musataye mtima. Pitani kuti mukakumane nawo mawa, ndipo Yehova adzakhala nanu.’”
18 Et Josaphat, et tout Juda et les habitants de Jérusalem s'étant prosternés la face contre terre tombèrent devant le Seigneur pour l'adorer.
Yehosafati anaweramitsa nkhope yake ndi kugunda pansi, ndiponso anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anagwa pansi ndi kulambira Yehova.
19 Puis, les lévites des fils de Caath et des fils de Coré se levèrent pour chanter à haute voix les louanges du Seigneur Dieu d'Israël.
Kenaka Alevi ena ochokera ku mabanja a Kohati ndi Kora anayimirira ndipo anatamanda Yehova Mulungu wa Israeli ndi mawu ofuwula kwambiri.
20 Et le peuple se leva dès l'aurore, et ils sortirent dans le désert de Thécoé; et, pendant qu'ils sortaient, Josaphat, se tenant immobile, cria, et dit: Écoutez-moi, Juda, et vous, habitants de Jérusalem, mettez votre confiance dans le Seigneur notre Dieu, et il se confiera en vous; mettez votre confiance dans son prophète, et vous prospérerez.
Mmamawa, ananyamuka kupita ku chipululu cha Tekowa. Akunyamuka, Yehosafati anayimirira ndipo anati, “Tandimverani ine anthu a Yuda ndi Yerusalemu! Khalani ndi chikhulupiriro mwa Yehova Mulungu wanu ndipo mudzatchinjirizidwa, khalani ndi chikhulupiriro mwa aneneri ake ndipo mudzapambana.”
21 Ensuite, il tint conseil avec le peuple; puis, il plaça en tête de l'armée, comme elle sortait, des chantres harpistes pour célébrer et louer les choses saintes, et ils disaient: Rendez gloire au Seigneur, car sa miséricorde est éternelle.
Atafunsira kwa anthu, Yehosafati anasankha anthu oti ayimbire Yehova ndi kumutamanda chifukwa cha ulemerero wa chiyero chake pamene amapita ali patsogolo pa gulu la ankhondo, akunena kuti: “Yamikani Yehova pakuti chikondi chake ndi chosatha.”
22 Et, au moment où ils commençaient à chanter ses louanges, le Seigneur excita la guerre entre les fils d'Ammon et Moab, d'une part, et ceux de la montagne de Seïr, d'autre part; ils avaient tous marché sur Israël, et ils se tournèrent les uns contre les autres.
Atangoyamba kuyimba ndi kutamanda, Yehova anapereka mʼmanja mwawo anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu ndiponso a ku Phiri la Seiri amene amalimbana ndi Yuda, ndipo anagonjetsedwa.
23 Les fils d'Ammon et Moab se levèrent pour exterminer ceux de la montagne de Seïr, et, quand ils les eurent broyés, ils s'attaquèrent mutuellement, de sorte qu'ils se détruisirent.
Anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu anawukira anthu ochokera ku Phiri la Seiri, ndipo anawawononga ndi kuwatheratu. Atatsiriza kuwapha anthu ochokera ku Seiri anamenyana wina ndi mnzake mpaka kuwonongana.
24 Lors donc que Juda arriva sur la hauteur d'où l'on découvre le désert, il regarda et il vit cette multitude, et voilà qu'ils étaient tous tombés morts, et gisant à terre, pas un ne s'était échappé.
Anthu a ku Yuda atafika pa malo oyangʼanana ndi chipululu ndi kuona kumene kunali gulu lalikulu lankhondo, iwo anangoona mitembo yokhayokha itagona pansi ndipo palibe amene anathawa.
25 Et Josaphat avec tout son peuple descendit pour recueillir les dépouilles; ils trouvèrent quantité de bétail, des bagages, des couvertures et des choses précieuses; ils les prirent et ils mirent trois jours à recueillir le butin, tant il y en avait.
Choncho Yehosafati ndi anthu ake anapita kukafunkha, ndipo pakati pawo anapeza katundu wambiri ndi zovala ndiponso zinthu zina zamtengowapatali kuposa zomwe akanatha kunyamula. Kunali katundu wambiri kotero kuti zinawatengera masiku atatu kuti amutenge.
26 Le quatrième jour, ils reprirent leurs rangs dans le val de la bénédiction; car, en ce lieu, ils bénirent le Seigneur; à cause de cela cette vallée est appelée encore de nos jours la Vallée de la Bénédiction.
Tsiku lachinayi anasonkhana ku chigwa cha Beraka kumene anatamanda Yehova. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa chigwa cha Beraka mpaka lero.
27 Et tout Juda, Josaphat à sa tête, revint à Jérusalem avec une grande allégresse, car le Seigneur les avait comblés de joie aux dépens de leurs ennemis.
Tsono motsogozedwa ndi Yehosafati, anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anabwerera ku Yerusalemu mokondwera pakuti Yehova anawagonjetsera adani awo.
28 Et ils entrèrent à Jérusalem au son des harpes et des cithares, auxquelles se joignirent les trompettes quand ils arrivèrent au temple du Seigneur.
Iwo analowa mu Yerusalemu ndipo anapita ku Nyumba ya Mulungu akuyimba azeze, apangwe ndi malipenga.
29 Et il y eut un grand trouble venant du Seigneur, parmi tous les royaumes de la terre, quand ils surent que le Seigneur avait combattu les ennemis d'Israël.
Kuopsa kwa Mulungu kunali pa maufumu onse a mayiko amene anamva mmene Yehova anamenyera adani a Aisraeli.
30 Ainsi le royaume de Josaphat fut en paix; car le Seigneur, alentour, apaisa tout.
Ndipo ufumu wa Yehosafati unali pa mtendere pakuti Mulungu wake anamupatsa mpumulo ku mbali zonse.
31 Et Josaphat régna en Jérusalem; il avait trente-cinq ans lorsqu'il monta sur le trône, et son règne dura vingt-cinq ans. Sa mère s'appelait Azuba, fille de Sali.
Choncho Yehosafati analamulira Yuda. Iye anali wa zaka 35 pamene anakhala mfumu ya Yuda ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 25. Dzina la amayi ake linali Azuba mwana wa Sili.
32 Et il marcha dans les voies d'Asa, son père, et il ne s'en détourna pas, et il fit ce qui est droit aux yeux du Seigneur.
Iye ankayenda mʼnjira za Asa abambo ake ndipo sanapatuke pa zimenezi pakuti anachita zolungama pamaso pa Yehova.
33 Cependant, les hauts lieux subsistèrent encore, et le peuple ne dirigea pas encore son cœur vers le Seigneur Dieu de ses pères.
Komabe malo opembedzerapo mafano sanachotsedwe ndipo anthu sanaperekebe mitima yawo kwa Mulungu wa makolo awo.
34 Le reste des actes de Josaphat, des premiers et des derniers, est compris dans les récits de Jéhu, fils d'Anani, qui écrivit le livre des Rois d'Israël.
Zochitika zina zokhudza ufumu wa Yehosafati, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la Yehu mwana wa Hanani, zomwe zikupezeka mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
35 Après cela, Josaphat, roi de Juda, fit alliance avec Ochozias, roi d'Israël, et il pécha,
Zitapita izi, Yehosafati mfumu ya Yuda inachita mgwirizano ndi Ahaziya mfumu ya Israeli, amene anachita zoyipa kwambiri.
36 En agissant et en marchant avec lui pour construire une flotte qui partit d'Asion-Gaber, allant à Tharsis.
Iye anagwirizana ndi Ahaziya kuti apange sitima zapamadzi zochitira malonda. Atazipanga zimenezi ku Ezioni-Geberi,
37 Alors, Eliézer, fils de Dodia de Marine, prophétisa contre Josaphat, disant: Parce que tu t'es lié avec Ochosias, le Seigneur a détruit ton ouvrage; il a brisé ta flotte, et elle n'a pu aller jusqu'à Tharsis.
Eliezara mwana wa Dodavahu wa ku Maresa ananenera motsutsana ndi Yehosafati ndipo anati, “Chifukwa chakuti wachita mgwirizano ndi Ahaziya, Yehova adzawononga zimene mwapangazo!” Sitima za pamadzizo zinawonongeka ndipo sizinapite nʼkomwe kumene zimakachita malonda.