< 2 Chroniques 19 >

1 Et Josaphat, roi de Juda, revint en son palais à Jérusalem.
Yehosafati, mfumu ya Yuda itabwerera mwamtendere ku nyumba yake yaufumu ku Yerusalemu,
2 Et le prophète Jéhu, fils d'Anani, sortit à sa rencontre, et il lui dit Roi Josaphat, n'as-tu pas porté secours à un impie, et donné ton amitié à un ennemi du Seigneur? A cause de cela, la colère du Seigneur a été excitée contre toi.
mlosi Yehu, mwana wa Hanani, anatuluka kukakumana naye ndipo anati kwa mfumu, “Kodi nʼkoyenera kuthandiza oyipa ndi kukonda iwo amene amadana ndi Yehova? Chifukwa cha zimenezi mkwiyo wa Yehova uli pa inu.
3 Cependant, il s'est trouvé du bon en toi; car tu as détruit les bois sacrés en la terre de Juda, et, d'un cœur droit, tu as cherché Dieu.
Komabe, muli zinthu zina zabwino mwa inu, pakuti inu mwachotsa mʼdziko muno mafano a Asera ndipo mwakhazikitsa mtima wanu pa kufunafuna Mulungu.”
4 Et Josaphat résida en Jérusalem; il en sortit encore une fois pour visiter le peuple depuis Bersabée jusqu'aux montagnes d'Ephraïm, et il les ramena au Seigneur Dieu de leurs pères.
Yehosafati anakakhala ku Yerusalemu, ndipo amayenda pakati pa anthu kuchokera ku Beeriseba mpaka ku dziko lamapiri la Efereimu ndipo anawatembenuzira kwa Yehova, Mulungu wa makolo awo.
5 Et il institua des juges dans toutes les places fortes de Juda: un par ville.
Iye anasankha oweruza mʼdzikomo, mu mzinda uliwonse wotetezedwa wa Yuda.
6 Et il dit aux juges: Soyez attentifs à ce que vous faites; car vous ne jugez pas pour l'homme, mais pour le Seigneur, et les paroles du jugement sont avec vous.
Ndipo anawawuza kuti, “Muganize bwino zimene mukuchita, chifukwa simukuweruza mʼmalo mwa munthu koma Yehova, amene ali nanu pamene mukupereka chiweruzo.
7 Que la crainte du Seigneur soit donc en vous; veillez et agissez; car, avec le Seigneur notre Dieu, il n'est point d'iniquité; il n'y a point à considérer la personne, ni à recevoir des présents.
Tsopano kuopsa kwa Yehova kukhale pa inu. Muweruze mosamala, pakuti ndi Yehova Mulungu wathu palibe kupotoza chilungamo kapena kukondera kapenanso kulandira ziphuphu.”
8 Et Josaphat institua en Jérusalem des prêtres, des lévites et des chefs de familles d'Israël, pour juger les choses du Seigneur et les habitants de la ville.
Mu Yerusalemu, Yehosafati anasankha Alevi ena, ansembe ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli kuti aziyangʼanira Malamulo a Yehova ndi kuweruza milandu. Ndipo iwo amakhala mu Yerusalemu.
9 Et il leur donna ses ordres, disant: Vous ferez votre devoir avec la crainte de Dieu, en la plénitude et en la sincérité de votre cœur.
Iye anawalamula kuti, “Inu mutumikire mokhulupirika ndi mtima wanu wonse moopa Yehova.
10 Quels que soient ceux de vos frères qui, de leurs villes, viendront à vous en justice, soit pour une décision entre le sang et le sang, soit pour une application des commandements et des préceptes, déterminez bien pour eux le droit et la sentence; et ils ne pècheront pas envers le Seigneur, et il n'y aura point de colère, ni contre vos frères, ni contre vous. Faites ainsi, et vous ne pècherez pas.
Pa mlandu uliwonse wobwera kwa inu kuchokera kwa abale anu amene amakhala mʼmizinda, mlandu wokhetsa magazi kapena mlandu wosamvera malamulo kapena malangizo kapena ziphunzitso zina, inu muziwachenjeza kuti asachimwire Yehova pakuti mukapanda kutero mkwiyo wake udzakhala pa inu ndi abale anu. Chitani zimenezi ndipo simudzachimwa.
11 Et Ananias le prêtre sera votre chef en ce qui concernera le Seigneur; Zabdias, fils d'Ismaël, prince de la maison de Juda, sera votre chef en ce qui concernera le roi, et vous aurez avec vous des scribes et des lévites; fortifiez-vous, et faites, et le Seigneur sera avec les bons.
“Amariya, mkulu wa ansembe adzakhala wokuyangʼanirani pa zonse zokhudza Yehova, ndipo Zebadiya mwana wa Ismaeli, mtsogoleri wa fuko la Yuda, adzakhala wokuyangʼanirani pa zonse zokhudza mfumu ndipo Alevi adzatumikira ngati okuyangʼanirani. Muchite molimba mtima ndipo Yehova akhale ndi iwo amene adzachita bwino.”

< 2 Chroniques 19 >