< 2 Chroniques 14 >

1 Et Abias mourut, et il alla rejoindre ses pères, et on l'ensevelit en la ville de David; et Asa, son fils, régna à sa place. Sous Asa, Juda fut en paix dix années.
Tsono Abiya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide. Asa mwana wake anakhala mfumu mʼmalo mwake ndipo pa masiku ake, dziko linakhala pa mtendere kwa zaka khumi.
2 Et il fit ce qui est bon et droit devant le Seigneur son Dieu.
Asa anachita zabwino ndi zolungama pamaso pa Yehova Mulungu wake.
3 Il répudia les autels des dieux étrangers et les hauts lieux; il brisa les colonnes, il abattit les bois sacrés,
Iye anachotsa maguwa achilendo ndi malo opembedzerapo mafano, anaphwanya zipilala za miyala yachipembedzo ndi kugwetsa mafano a Asera.
4 Et il dit à Juda de chercher le Seigneur Dieu de leurs pères, et de pratiquer sa loi et ses commandements.
Asa analamula Yuda kuti afunefune Yehova Mulungu wa makolo awo ndi kumvera malamulo ndi zolamulira zake.
5 Et il détruisit, dans toutes les villes de Juda, les autels et les idoles, et paisiblement
Iye anachotsa malo opembedzera mafano ndi maguwa ofukizira lubani mu mzinda uliwonse wa mu Yuda, ndipo mu ufumu wake munali mtendere pa nthawi ya ulamuliro wake.
6 Il fortifia des places en Juda; car la terre était en paix. Il n'y eut point de guerre en ces années, parce que le Seigneur lui avait donné du repos.
Asa anamanga mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda pakuti dziko linali pa mtendere. Panalibe amene anachita naye nkhondo mʼzaka zimenezo, pakuti Yehova anamupatsa mpumulo.
7 Et il dit à Juda: Fortifions les villes, faisons-leur des murs, des tours, des portes, des verrous; nous prévaudrons sur la terre: car de même que nous avons cherché le Seigneur notre Dieu, il nous a cherchés; il nous a donné la paix tout alentour, et il nous a fait prospérer.
Iye anati kwa Yuda “Tiyeni timange mizinda iyi ndipo timange makoma ndi nsanja, zitseko ndi zotchinga. Dzikoli likanali lathu chifukwa tafuna Yehova Mulungu wathu; tinamufuna Iye ndipo watipatsa mpumulo mbali zonse.” Kotero iwo anamanga ndi kukhala pa ulemerero.
8 Or, Asa avait en la terre de Juda une force de trois cent mille hommes portant javeline et bouclier; et, en la terre de Benjamin, deux cent quatre- vingt mille archers, ou fantassins armés à la légère; tous ces hommes étaient vaillants et aguerris.
Asa anali ndi ankhondo 300,000 ochokera ku Yuda, okhala ndi zishango zikuluzikulu ndi mikondo, ndiponso ankhondo 280,000 ochokera ku Benjamini, okhala ndi zishango ndi mauta. Onsewa anali ankhondo amphamvu ndi olimba mtima.
9 Et Zara l'Ethiopien marcha contre eux avec une armée d'un million d'hommes, et trois cents chars; il s'avança jusqu'à Marèsa.
Zera wa ku Kusi anapita kukamenyana nawo ali ndi gulu lalikulu kwambiri la asilikali ndi magaleta 300 ndipo anafika mpaka ku Maresa.
10 Asa sortit à sa rencontre, et rangea son armée en bataille dans la vallée, au nord de Marèsa.
Asa anapita kukakumana naye ndipo anakhala pa mizere yawo ya nkhondo mʼchigwa cha Zefata pafupi ndi Maresa.
11 Et Asa cria au Seigneur son Dieu, et il dit: Seigneur, il ne vous est point impossible de sauver, soit avec beaucoup, soit avec peu; fortifiez-nous, Seigneur notre Dieu, car nous avons eu foi en vous, et c'est en votre nom que nous avons marché contre cette grande multitude. Seigneur notre Dieu, que l'homme ne prévaille pas contre vous.
Kenaka Asa anafuwulira Yehova Mulungu wake ndipo anati “Yehova palibe wina wofanana nanu kuti angathandize anthu opanda mphamvu pakati pa amphamvu. Tithandizeni Inu Yehova Mulungu wathu pakuti ife timadalira Inu ndipo mʼdzina lanu ife tabwera kudzalimbana ndi gulu la ankhondo lalikulu kwambiri ngati ili. Inu Yehova ndinu Mulungu wathu, musalole kuti munthu akupambaneni.”
12 Et le Seigneur frappa les Ethiopiens devant Juda, et les Ethiopiens s'enfuirent.
Yehova anakantha Akusi pamaso pa Asa ndi Ayuda. Akusi anathawa,
13 Asa et son peuple les poursuivirent jusqu'à Gedsor. Les Ethiopiens tombèrent jusqu'au dernier; car ils furent broyés devant le Seigneur et devant son armée, et les fils de Juda recueillirent d'innombrables dépouilles.
ndipo Asa ndi ankhondo ake anawathamangitsa mpaka ku Gerari. Gulu lonse lalikulu lija la Akusi linaphedwa. Sanapezeke mmodzi wamoyo pakati pawo. Iwo anakanthidwa pamaso pa Yehova ndi asilikali ake. Anthu a ku Yuda anatenga katundu wambiri olanda ku nkhondo.
14 Et ils détruisirent les bourgs autour de Gedsor; car un grand trouble, venant du Seigneur, était sur eux. Les fils de Juda pillèrent leurs villes, et ils firent un riche butin.
Iwo anawononga midzi yonse yozungulira Gerari pakuti mantha aakulu wochokera kwa Yehova anagwera anthuwo. Analanda katundu wa midzi yonse, popeza kunali katundu wambiri kumeneko.
15 Ils détruisirent les tentes des troupeaux, ils dépouillèrent les habitants de la côte, ils emmenèrent quantité de moutons et de chameaux, et ils revinrent à Jérusalem.
Anakathiranso nkhondo misasa ya anthu oweta ziweto ndipo anatenga nkhosa zambiri, mbuzi ndi ngamira. Atatero anabwerera ku Yerusalemu.

< 2 Chroniques 14 >