< 2 Chroniques 12 >

1 Or, quand Roboam eut organisé son royaume et s'y fut affermi, il abandonna les commandements du Seigneur, et tout le peuple suivit son exemple.
Rehobowamu atakhazikika monga mfumu nakhaladi wamphamvu, iyeyo pamodzi ndi Aisraeli onse anasiya malamulo a Yehova.
2 Et la cinquième année de son règne, parce qu'il avait péché contre le Seigneur, Susacim (Sésac), roi d'Égypte, marcha contre Jérusalem,
Chifukwa anakhala osakhulupirika pamaso pa Yehova, Sisaki mfumu ya dziko la Igupto inathira nkhondo Yerusalemu mʼchaka chachisanu cha mfumu Rehobowamu.
3 Avec douze cents chars, soixante mille chevaux et une multitude innombrable des Libyens, de Troglodytes et d'Ethiopiens.
Sisakiyo anabwera ndi magaleta 1,200 ndi anthu okwera akavalo 60,000 ndiponso asilikali osawerengeka ochokera ku Libiya, Suki ndi Kusi amene anabwera naye kuchokera ku Igupto.
4 Et ils s'emparèrent de toutes les forteresses de Juda, et ils arrivèrent devant Jérusalem,
Iye analanda mizinda yotetezedwa ya Yuda ndipo anafika mpaka ku Yerusalemu.
5 Et Samaïas le prophète alla trouver Roboam et les princes de Juda, qui s'étaient réunis à Jérusalem par crainte de Susacim, et il leur dit: Voici que dit le Seigneur: Vous m'avez abandonné, et moi je vous abandonnerai pour vous livrer à Susacim.
Ndipo mneneri Semaya anabwera kwa Rehobowamu ndi kwa atsogoleri a Yuda amene anasonkhana mu Yerusalemu chifukwa cha Sisaki ndipo iye anawawuza kuti, “Yehova akuti, ‘Inu mwandisiya, choncho Inenso ndakusiyani ndi kukuperekani kwa Sisaki.’”
6 Et le roi et les chefs de Juda eurent honte, et ils dirent: Le Seigneur est juste.
Atsogoleri a Israeli pamodzi ndi mfumu anadzichepetsa nati, “Yehova ndi wolungama.”
7 Quand le Seigneur vit qu'ils s'étaient repentis, la parole du Seigneur vint à Samaïas, disant: Ils se sont repentis, je ne les détruirai pas; je leur accorderai comme une ombre de salut, et ma colère ne tombera pas sur Jérusalem.
Yehova ataona kuti adzichepetsa, anayankhula ndi Semaya kuti, “Pakuti adzichepetsa, Ine sindiwawononga koma posachedwapa ndiwapulumutsa. Sinditsanulira ukali wanga pa Yerusalemu kudzera mwa Sisaki.
8 Ils seront asservis, et ils connaîtront la différence de ma servitude avec la servitude des rois de la terre.
Komabe iwo adzakhala pansi pa ulamuliro wake, kuti aphunzire kudziwa kusiyanitsa pakati pa kutumikira Ine ndi kutumikira mafumu a mayiko ena.”
9 Et Susacim, roi d'Égypte, marcha contre Jérusalem; il prit tous les trésors du temple du Seigneur, et tous les trésors du palais du roi, il prit tout; il prit aussi les boucliers d'or qu'avait faits Salomon.
Sisaki mfumu ya dziko la Igupto atathira nkhondo Yerusalemu, iye anatenga chuma cha mʼNyumba ya Yehova ndi chuma cha mʼnyumba yaufumu. Iye anatenga zinthu zonse kuphatikizapo zishango zagolide zimene Solomoni anapanga.
10 (Le roi Roboam les remplaça par des boucliers d'airain). Et le roi Susacim mit au-dessus de lui des capitaines de ses gardes surveillant la porte du palais.
Ndipo mfumu inapereka zishango zamkuwa kwa oyangʼanira mʼmalo mwake ndipo iwo anazipereka kwa oyangʼanira alonda amene amayangʼanira pa chipata cha nyumba yaufumu.
11 Et lorsque le roi entrait dans le temple du Seigneur, les gardes y entraient aussi, et avec les coureurs ceux qui allaient à la rencontre des coureurs.
Nthawi ina iliyonse imene mfumu ikupita ku Nyumba ya Yehova, alonda amapita nayo atanyamula zishango, ndipo kenaka amakazibwezera ku chipinda cha alonda.
12 Mais parce qu'il s'était repenti, le Seigneur détourna de lui sa colère, et il ne fut pas entièrement détruit; car il y avait encore en Juda de bonnes pensées.
Pakuti mfumu Rehobowamu inadzichepetsa, mkwiyo wa Yehova unamuchokera, sanawonongedweretu. Kunena zoona, munali zinthu zina zabwino mu Yuda.
13 Et le roi Roboam se raffermit en Jérusalem et il régna; il avait quarante et un ans quand il monta sur le trône, et il régna dix-sept ans à Jérusalem dans la ville que, parmi toutes les tribus d'Israël, le Seigneur s'était choisie pour que son nom y fût invoqué; sa mère, nommée Noomma, était Ammonite.
Mfumu Rehobowamu anayika maziko a ufumu wake mwamphamvu mu Yerusalemu ndipo anapitirira kukhala mfumu. Iye anali ndi zaka 41 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira zaka 17 mu Yerusalemu, mzinda wa Yehova umene anasankha pakati pa mafuko a Aisraeli mmene Yehova anakhazikikamo. Dzina la amayi ake linali Naama, amene anali Mwamoni.
14 Et il fit le mal parce qu'il ne dirigea pas son cœur à la recherche de Dieu.
Rehobowamu anachita zoyipa chifuwa mtima wake sunafunefune Yehova.
15 Quant aux discours de Roboam, les premiers et les derniers, et à ses actions, ne sont-ils pas écrits dans les Récits de Samaïas le prophète, et d'Addo le voyant? Roboam fut toujours en guerre avec Jéroboam.
Ntchito za Rehobowamu, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri la mneneri Semaya ndi mlosi Ido amene amalemba mbiri? Panali nkhondo yosatha pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu.
16 Et Roboam alla rejoindre ses pères, et il fut enseveli dans la ville de David; et Abias, son fils, régna à sa place.
Rehobowamu anamwalira, ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide. Ndipo mwana wake Abiya analowa ufumu mʼmalo wake.

< 2 Chroniques 12 >