< 2 Chroniques 11 >

1 Roboam rentra donc à Jérusalem; puis, il réunit Juda et Benjamin, cent quatre-vingt mille jeunes gens allant à la guerre, afin de combattre Israël, et de recouvrer la royauté pour Roboam.
Rehobowamu atafika ku Yerusalemu anasonkhanitsa asilikali 180,000 a fuko la Yuda ndi Benjamini kuti akachite nkhondo ndi Israeli, kuti abwezeretse ufumu kwa Rehobowamu.
2 Mais, la parole du Seigneur vint à Samaïas, homme de Dieu; disant:
Koma Yehova anayankhula ndi munthu wa Mulungu Semaya kuti,
3 Parle à Roboam, fils de Salomon, à tout Juda et à Benjamin, dis-leur:
“Kawuze Rehobowamu mwana wa Solomoni mfumu ya Yuda ndi Aisraeli onse ali mu Yuda ndi Benjamini kuti,
4 Voici ce que dit le Seigneur: Ne partez pas, ne combattez point vos frères les fils d'Israël, retournez chacun en votre demeure, car cette chose est de moi. Ils obéirent à la parole du Seigneur, et, selon son ordre, ils renoncèrent à marcher contre Jéroboam.
‘Yehova akuti: Musapite kukamenyana ndi abale anu. Pitani kwanu, aliyense wa inu, pakuti izi ndikuchita ndine.’” Choncho anamvera mawu a Yehova ndi kubwerera osapita kukamenyana ndi Yeroboamu.
5 Et Roboam habita Jérusalem, et il bâtit des places fortes en Judée.
Rehobowamu amakhala mu Yerusalemu ndipo anamanga mizinda ya chitetezo iyi mu Yuda:
6 Il bâtit encore Bethléem, Etan, Thécoé,
Betelehemu, Etamu, Tekowa,
7 Bethsura, Sochoth, Odollam,
Beti Zuri, Soko, Adulamu,
8 Geth, Marisan, Ziph,
Gati, Maresa, Zifi,
9 Adoraï, Lachis, Azéca,
Adoraimu, Lakisi, Azeka,
10 Saraa, Aïlon et Hébron, qui appartient à Juda et à Benjamin; toutes villes qu'il entoura de remparts.
Zora, Ayaloni ndi Hebroni. Iyi ndiye inali mizinda yotetezedwa ya Yuda ndi Benjamini.
11 Et il les fortifia, et leur donna des chefs auxquels il assigna des vivres, de l'huile et du vin,
Iye anakhwimitsa chitetezo cha mizindayi ndipo anayikamo atsogoleri a ankhondo, pamodzi ndi chakudya, mafuta a olivi ndi vinyo.
12 Et il approvisionna chacune d'elles de lances et de boucliers, et il en multiplia les défenses; et il eut à lui Juda et Benjamin.
Mʼmizinda yonse anayikamo zishango zikuluzikulu ndi mikondo, ndipo anachititsa kuti mizindayo ikhale yamphamvu. Choncho iye amalamulira Yuda ndi Benjamini.
13 Cependant, les prêtres et les lévites qui étaient en tout Israël, se rassemblaient auprès de lui de tous les points du territoire.
Ansembe ndi Alevi a mʼmadera onse a Israeli anakhala mbali ya Rehobowamu.
14 Car, ils abandonnèrent leurs villes de résidence, et ils se rendirent en Juda et à Jérusalem, parce que Jéroboam et ses fils leur avaient ôté le service du Seigneur.
Alevi anasiya malo awo owetera ziweto ndi katundu wawo, ndi kubwera ku Yuda ndi ku Yerusalemu chifukwa Yeroboamu ndi ana ake anawakana kukhala ansembe a Yehova.
15 Et Jéroboam avait institué pour lui des prêtres des hauts lieux qui sacrifiaient aux idoles, aux choses vaines, aux veaux d'or, qu'avaient faits Jéroboam.
Ndipo iye anasankha ansembe akeake a pa malo opatulika ndi a mafano a mbuzi ndi mwana wangʼombe amene anapanga.
16 Et il avait chassé des tribus d'Israël ceux qui dévouaient leur cœur à chercher le Seigneur Dieu d'Israël; et ils vinrent à Jérusalem pour sacrifier au Seigneur Dieu de leurs pères.
Anthu ochokera fuko lililonse la Israeli amene anatsimikiza mitima yawo kufunafuna Yehova Mulungu wa Israeli, ankapitabe ku Yerusalemu kukapereka nsembe kwa Yehova, Mulungu wa makolo awo.
17 Et ils affermirent le royaume de Juda, et Roboam, fils de Salomon, en fut fortifié pendant trois ans, parce qu'il marcha trois ans dans les voies de David et de Salomon.
Iwo analimbikitsa ufumu wa Yuda, ndipo anathandiza Rehobowamu mwana wa Solomoni kwa zaka zitatu. Pa nthawi imeneyi iye amatsatira zochita za Davide ndi Solomoni.
18 Roboam prit pour femmes Moolath, fille de Jerimuth, fils de David; et Abigaïl, fille d'Eliab, fils de Jessé.
Rehobowamu anakwatira Mahalati, amene abambo ake anali Yerimoti, mwana wa Davide, ndipo amayi ake anali Abihaili, mwana wa Eliabu, mwana wa Yese.
19 Celle-ci lui enfanta des fils: Jéhu, Samoria et Zaam.
Mkaziyo anamubereka ana aamuna awa: Yeusi, Semariya ndi Zahamu.
20 Après cela, il épousa Maacha, fille d'Absalon, et elle lui enfanta Abias, Jetthi, Zéza et Salémoth.
Kenaka anakwatira Maaka, mwana wamkazi wa Abisalomu, amene anamubereka Abiya, Atai, Ziza ndi Selomiti.
21 Or, Roboam aima Maacha, fille d'Absalon, plus que toutes ses femmes et ses concubines, car il avait dix-huit femmes et soixante concubines; il eut d'elles vingt-huit fils et soixante filles.
Rehobowamu ankamukonda Maaka mwana wa Abisalomu kuposa aliyense mwa akazi ake ndi azikazi. Iye anali ndi akazi 18, azikazi 60, ana aamuna 28 ndi ana aakazi 60.
22 Et il fit Adias, fils de Maacha, chef de tous ses frères, car il avait dessein de lui laisser le trône.
Rehobowamu anasankha Abiya mwana wa Maaka kuti akhale mtsogoleri pa abale ake, ndi cholinga choti adzakhale mfumu.
23 Et il le fortifia plus que tous ses autres fils dispersés sur tout le territoire de Juda et de Benjamin, dans les villes entourées de remparts où Roboam maintenait abondance de vivres, et où il leur fit épouser beaucoup de femmes.
Iye anachita mwanzeru, pomwaza ena mwa ana ake ku madera onse a Yuda ndi Benjamini, ndi ku mizinda yonse yotetezedwa. Iye anawapatsa zinthu zambiri ndiponso anawafunira akazi ambiri.

< 2 Chroniques 11 >