< 1 Samuel 8 >

1 Et Samuel devint vieux, et il institua ses fils juges d'Israël.
Samueli atakalamba anasankha ana ake kuti akhale oweruza Aisraeli.
2 Voici les noms de ces fils: le premier-né s'appelait Joël, le second Abia; ils jugeaient en Bersabée.
Mwana wake woyamba anali Yoweli, wachiwiri anali Abiya, ndipo ankaweruza ku Beeriseba.
3 Mais ses fils ne marchèrent pas en ses voies; ils en furent détournés par l'intérêt; ils acceptèrent des présents et ils firent dévier la justice.
Koma ana akewo sanatengere makhalidwe ake abwino. Iwo ankapotokera ku zoyipa namatsata phindu mwachinyengo. Ankalandira ziphuphu ndi kumaweruza mwachinyengo.
4 En conséquence, les fils d'Israël se rassemblèrent; ils allèrent trouver Samuel en Armathem,
Tsono akuluakulu onse a Israeli anasonkhana pamodzi ndipo anabwera kwa Samueli ku Rama.
5 Et ils lui dirent: Écoute, tu es devenu vieux, et tes fils ne marchent pas en tes voies; donne-nous donc un roi comme en ont les autres nations, afin qu'il nous juge.
Iwo anati kwa iye “Taonani, inu mwakula tsopano ndipo ana anu sakutsata makhalidwe anu abwino. Tsono mutipatse mfumu kuti izitilamulira, monga momwe ikuchitira mitundu ina yonseyi.”
6 Cette parole parut mauvaise à Samuel, lorsqu'ils dirent: Donne-nous un roi, afin qu'il nous juge; et Samuel pria le Seigneur.
Koma mawu oti, “Mutipatse mfumu kuti izitilamulira,” sanakondweretse Samueli. Choncho anapemphera kwa Yehova.
7 Or, le Seigneur dit à Samuel: Écoute la voix du peuple, fais comme ils te diront; ce n'est point toi, c'est moi qu'ils ont méprisé et dont ils ne veulent pas pour régner sur eux.
Yehova anamuyankha nati, “Mvera zonse zimene anthuwa akukuwuza. Si ndiwe amene akumukana, koma akukana Ine kuti ndikhale mfumu yawo.
8 C'est ce qu'ils ont toujours fait à mon égard depuis le jour où je les ai tirés de l'Égypte jusqu'à ce moment: ils m'ont abandonné, et ils ont servi d'autres dieux; ils te traitent de même maintenant.
Kuyambira tsiku limene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto mpaka lero zochita zawo zakhala zondikana Ine nʼkumatumikira milungu ina. Tsopano akukukananso iwe.
9 Obéis donc à leur voix; seulement prends-les à témoin, et prends-les à témoin pour leur faire connaître les droits du roi qui règnera sur eux.
Tsono amvere zimene akunena, koma uwachenjeze kwambiri ndipo uwawuzitse za khalidwe la mfumu imene idzawalamulire.”
10 Et Samuel répéta toutes les paroles du Seigneur au peuple qui lui demandait un roi.
Samueli anawawuza anthu amene amamupempha mfumu aja mawu onse a Yehova.
11 Il leur dit: Voici quels seront les droits du roi qui régnera sur vous: Il prendra vos fils, et il les placera sur ses chars de guerre ou parmi ses cavaliers; il les fera courir devant ses chars.
Iye anati, “Zimene mfumu imene idzakulamulireniyo idzachite ndi izi: Izidzatenga ana anu aamuna kuti akhale ankhondo ake; ena pa magaleta ake, ena pa akavalo ake ndipo ena othamanga patsogolo pa magaleta akewo.
12 Il s'en fera des centeniers et des chefs de mille hommes; il leur fera faire sa moisson et sa vendange; il leur fera fabriquer des armes de guerre, et les pièces diverses de ses chariots.
Ena adzawayika kukhala olamulira asilikali 1,000, ena olamulira asilikali makumi asanu, ndi ena otipula minda yake, ndi kukolola ndiponso ena adzakhala osula zida zankhondo ndi zida za magaleta ake.
13 Il prendra vos filles pour préparer ses parfums, cuire son pain, et faire sa cuisine.
Iyo idzatenga ana anu akazi kuti akhale oyenga mafuta onunkhira, ophika chakudya ndi kupanga buledi.
14 Il prendra vos champs, vos vignes, vos meilleurs oliviers, pour les donner à ses serviteurs.
Idzatenga minda yanu yabwino ya mpesa ndi ya mitengo ya olivi ndipo adzayipereka kwa antchito ake.
15 Il prendra la dîme de vos grains et de votre vendange, pour la donner à ses eunuques et à ses esclaves.
Idzatenga gawo lakhumi la tirigu wanu ndi mphesa zanu ndi kupereka kwa nduna zake ndi akapitawo ake.
16 Il prendra vos serviteurs, vos servantes, vos bœufs et vos ânes; il prendra la dîme de tous les fruits de vos travaux.
Mfumuyo idzatenga antchito anu aamuna ndi aakazi. Idzatenganso ngʼombe zanu zabwino ndi abulu anu nʼkumazingwiritsa ntchito.
17 Il prendra la dîme de votre bétail, et vous serez ses esclaves.
Iyo idzatenga gawo lakhumi la zoweta zanu, ndipo inu eni mudzakhala akapolo ake.
18 Et, ce jour-là, vous crierez à cause du roi que vous vous serez choisi; et, ce jour-là, le Seigneur ne vous écoutera point, parce que c'est vous-mêmes qui aurez voulu ce roi pour vous.
Nthawi imeneyo ikadzafika inu mudzalira momvetsa chisoni chifukwa cha mfumu imene mwadzisankhira, koma Yehova sadzakuyankhani.”
19 Mais le peuple ne voulut pas écouter Samuel, et il dit: Nullement, mais nous aurons un roi,
Koma anthu anakana kumumvera Samueli. Iwo anati, “Ayi! Ife tikufuna mfumu yotilamulira.
20 Nous serons comme toutes les nations; notre roi nous jugera, il marchera à notre tête et il dirigera nos guerres.
Kotero ifenso tidzakhala ngati mayiko ena. Mfumu yathu idzatiweruza ndiponso idzatuluka nafe kutitsogolera kukamenya nkhondo.”
21 Et Samuel écouta tous les discours du peuple, et il les transmit au Seigneur.
Samueli atamva zonse zimene anthuwo ananena, iye anakazifotokozanso kwa Yehova.
22 Et le Seigneur dit à Samuel: Obéis-leur, et donne-leur un roi. Alors, Samuel dit aux fils d'Israël: Que chacun s'en retourne en sa ville.
Yehova anamuyankha nati, “Amvere zimene akunena ndipo apatse mfumu.” Ndipo Samueli anati kwa Aisraeli aja, “Bwererani aliyense kwawo.”

< 1 Samuel 8 >