< 1 Samuel 31 >

1 Et les Philistins livrèrent bataille à Israël, et les hommes d'Israël prirent la fuite devant eux; ils furent taillés en pièces dans la montagne de Gelboé.
Tsono Afilisti anachitanso nkhondo ndi Aisraeli ndipo Aisraeli anathawa Afilistiwo, kotero kuti ambiri anaphedwa pa phiri la Gilibowa.
2 Les Philistins entourèrent Saül et ses trois fils; ils tuèrent Jonathan, Aminadab et Melchisa, fils de Saül.
Afilisti anapanikiza kwambiri Sauli ndi ana ake, ndipo anapha Yonatani, Abinadabu ndi Maliki-Suwa.
3 Et le poids de la guerre tomba sur Saül; des archers l'atteignirent, et il fut blessé au flanc.
Nkhondo inakula kwambiri mozungulira Sauli ndipo pamene anthu amauta anamupeza, anamuvulaza kwambiri.
4 Alors, Saül dit au serviteur qui portait ses armes: Tire ton épée, et perce-moi, de peur que ces incirconcis ne m'approchent, ne me percent et ne m'outragent. Le serviteur, qui portait ses armes, ne le voulut pas, car il avait grande crainte; mais Saül prit l'épée et se jeta sur la pointe.
Tsono Sauli anawuza mnyamata wake wonyamula zida zake kuti, “Solola lupanga lako undiphe kuopa kuti anthu osachita mdulidwewa angabwere kudzandizunza ine.” Koma mnyamata wonyamula zida uja anachita mantha kwambiri ndipo sanathe kutero. Choncho Sauli anatenga lupanga lake lomwe nagwerapo.
5 Le serviteur, qui portait ses armes, vit que Saül était mort; lui-même se jeta sur son épée, et il mourut avec son maître.
Mnyamata wonyamula zida zake uja ataona kuti Sauli wafa, nayenso anadzigwetsera pa lupanga lake nafa naye limodzi.
6 Ainsi Saül, ses trois fils et le serviteur qui portait ses armes, périrent ensemble ce jour-là.
Motero Sauli ndi ana ake atatu, wonyamula zida zake pamodzi ndi anthu ake onse anafera limodzi pa tsikulo.
7 Les hommes d'Israël qui étaient de l'autre côté de cette vallée, ceux des rives du Jourdain virent que l'armée était en fuite, et que Saül et ses fils étaient morts; alors ils abandonnèrent leurs villes et se cachèrent; et les Philistins survinrent, et ils prirent possession de leurs demeures.
Pamene Aisraeli amene anali tsidya lina la chigwa ndi amene anali tsidya la chigwa cha Yorodani anaona kuti gulu la ankhondo la Aisraeli lathawa komanso kuti Sauli ndi ana ake aphedwa, nawonso anathawa kusiya mizinda yawo. Ndipo Afilisti anabwera kudzakhalamo.
8 Et, le lendemain, les vainqueurs dépouillèrent les morts; ils trouvèrent Saül et ses trois fils gisant dans les montagnes de Gelboé.
Mmawa mwake, Afilisti atabwera kudzatenga zinthu za anthu ophedwa anapeza Sauli ndi ana ake atatu atafa pa phiri la Gilibowa.
9 Ils défigurèrent le roi; ils lui ôtèrent ses armes, et ils les envoyèrent aux villes d'alentour en la terre des Philistins, annonçant ces nouvelles à leurs idoles et au peuple.
Iwo anadula mutu wake ndi kumuvula zida zake zankhondo. Ndipo anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Afilisti kukafalitsa nkhani yabwinoyi kwa mafano awo ndi kwa anthu awo.
10 Ils déposèrent les armes dans le temple d'Astarté, et ils clouèrent le corps au mur de Bethsam.
Iwo anayika zida zake zankhondo mʼnyumba yopembedzera Asitoreti, ndipo thupi lake analikhomera pa khoma la mzinda wa Beti-Sani.
11 Or, ceux de Jabès-Galaad apprirent comment les Philistins avaient traité Saül.
Pamene anthu a ku Yabesi Giliyadi anamva zimene Afilisti anachitira Sauli,
12 Et tous les hommes vaillants se levèrent; ils marchèrent toute la nuit, enlevèrent des murs de Bethsam les corps de Saül et de Jonathan, et les transportèrent à Jabès, où ils les brûlèrent.
anthu awo onse olimba mtima anayenda usiku wonse kupita ku Beti-Sani. Anakachotsa mtembo wa Sauli ndi mitembo ya ana ake pa khoma la mzinda wa Beti-Sani, ndipo anabwera nayo ku Yabesi kumene anayitentha ndi moto.
13 Enfin, ils recueillirent leurs ossements; ils les inhumèrent en un champ de Jabès, et ils jeûnèrent sept jours.
Pambuyo pake anatenga mafupa awo ndi kuwakwirira pansi pa mtengo wabwemba ku Yabesi, ndipo anasala kudya masiku asanu ndi awiri.

< 1 Samuel 31 >