< 1 Samuel 29 >

1 Cependant, les Philistins concentrèrent toutes leurs forces vers Apha, et Israël campa à Endor en Jezraël.
Afilisti anasonkhanitsa asilikali awo onse ku Afeki, ndipo Israeli anamanga misasa yawo pa chitsime cha Yezireeli.
2 Et les chefs des Philistins allaient en avant, par troupes de cent et de mille hommes; et David, suivi de ses gens, marchaient au dernier rang avec Achis.
Pamene atsogoleri a Afilisti ankatsogolera magulu awo ankhondo a miyandamiyanda, Davide ndi ankhondo ake ankayenda pambuyo pamodzi ndi Akisi.
3 Or, les chefs des Philistins dirent: Qui sont ceux-là qui nous suivent? Achis leur répondit: N'est-ce pas David le serviteur de Saül, roi d'Israël; voilà bien des jours qu'il est avec nous; la seconde année commence, et, depuis qu'il s'est attaché à moi, jusqu'à ce moment, je n'ai trouvé en lui rien à redire.
Tsono atsogoleri a Afilisti aja anafunsa kuti, “Kodi Ahebri awa akufuna chiyani?” Akisi anayankha kuti, “Uyu ndi Davide, mtumiki wa Sauli mfumu ya Israeli. Iye wakhala ndi ine kwa masiku ndithu, kapena titi zaka ndipo kuyambira tsiku limene anachoka kwa Sauli mpaka lero, ine sindinapeze cholakwa mwa iye.”
4 Les chefs des Philistins s'offensèrent de sa réponse, et ils lui dirent: Renvoie cet homme, qu'il s'en aille en la demeure où tu l'as établi; ne le laisse pas ici, et qu'il ne vienne point avec nous au combat; craignons qu'il ne nous trahisse. Comment se réconcilierait-il avec son maître, sinon avec les têtes de nos hommes?
Koma atsogoleri a ankhondo a Afilisti anamukwiyira Akisi kwambiri ndipo anati, “Mubweze munthuyu kuti abwerere ku malo amene unamupatsa. Iye asapite nafe ku nkhondo kuopa kuti angadzasanduke mdani wathu. Kodi iyeyu adzadziyanjanitsa bwanji ndi mbuye wake? Iyeyutu adzadziyanjanitsa ndi mbuye wake pakupha anthu ali panowa?
5 N'est-ce pas ce David de qui l'on chantait, en dansant: Saül les a tués par milliers, David les a tués par myriades?
Paja ameneyu ndi Davide yemwe ankamuvinira namuyimbira kuti, “‘Sauli wapha anthu 1,000 koma Davide wapha miyandamiyanda?’”
6 Achis fit donc appeler David, et il lui dit: Vive le Seigneur! tu es à mes yeux droit et bon; tu sors du camp et tu y rentres avec moi, et je n'ai découvert eu toi aucune méchanceté, depuis le jour où tu es venu me trouver, jusqu'à ce moment. Mais, aux yeux des chefs, tu n'es point bon.
Kotero Akisi anayitana Davide ndipo anamuwuza kuti, “Pali Yehova wamoyo, iwe wakhala wodalirika ndipo chikanakhala chinthu chabwino kuti uzimenya nkhondo pamodzi nane popeza chibwerere iwe kuno ine sindinapeze cholakwa chilichonse ndi iwe. Koma atsogoleri enawa ndiwo sakukufuna.
7 Ainsi, retire-toi; pars en paix; c'est le moyen de ne rien faire qui semble mal aux chefs des Philistins.
Tsono bwerera. Upite mu mtendere kuopa kuti ungachite kanthu kena koyipira atsogoleri a Afilistiwa.”
8 Et David dit à Achis: Que t'ai-je fait, et qu'as-tu à reprocher à ton serviteur, depuis le jour où je suis arrivé devant toi, jusqu'à ce moment, pour que l'on me défende de combattre les ennemis du roi mon maître?
Davide anafunsa Akisi kuti, “Kodi ndachita chiyani? Kodi mwapeza cholakwa chotani mwa ine mtumiki wanu chiyambire kukutumikirani mpaka lero? Tsono chifukwa chiyani sindingapite kukamenya nkhondo ndi adani a mbuye wanga mfumu?”
9 Achis répondit à David: A mes yeux, tu es bon; mais les chefs des Philistins ont dit: Il ne viendra pas au combat avec nous.
Akisi anayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti ndiwe wangwiro ngati mngelo wa Mulungu. Komabe atsogoleri a ankhondo a Afilisti akuti, ‘Davide asapite nafe ku nkhondo.’
10 Lève-toi donc demain de grand matin, emmène tes serviteurs; retournez au lieu où je vous ai établis, et ne laisse point entrer en ton cœur de mauvaise pensée, parce que, selon moi, tu es bon. Levez-vous pour vous mettre en route avant qu'il fasse jours et partez.
Tsono udzuke mmamawa, pamodzi ndi ankhondo ako amene unabwera nawo, ndipo unyamuke kukangocha.”
11 Et David avec ses gens se leva de grand matin; ils partirent pour garder la terre des Philistins, et ceux-ci allèrent à Jezraël pour livrer bataille.
Choncho Davide ndi anthu ake anadzuka mmamawa kubwerera ku dziko la Afilisti. Koma Afilistiwo anapita ku Yezireeli.

< 1 Samuel 29 >