< 1 Samuel 21 >
1 David se rendit à Nomba chez le prêtre Abimélech; Abimélech, étonné de sa venue, lui dit: Pourquoi es-tu seul, et n'y a-t-il personne avec toi?
Davide anapita ku Nobi kwa wansembe Ahimeleki. Ahimelekiyo ankanjenjemera pamene ankamuchingamira, ndipo anafunsa kuti, “Muli nokha chifukwa chiyani? Chifukwa chiyani mulibe wokuperekezani?”
2 David dit au prêtre: Le roi aujourd'hui m'a donné ce commandement: Que nul ne sache l'affaire pour laquelle je t'envoie, et dont je te charge. J'ai donc convoqué mes serviteurs au lieu dit la Foi de Dieu (Phellani-Maimoni).
Davide anayankha Ahimeleki kuti, “Mfumu yandituma zinthu zina ndipo yandiwuza kuti, ‘Munthu aliyense asadziwe za zimene ndakutumazo.’ Kunena za anthu anga, ndawawuza kuti tikakumane pamalo pena pake.
3 Maintenant, as-tu sous la main cinq pains? Donne-moi ce que tu pourras trouver.
Kodi muli ndi chakudya? Patseniko malofu a buledi asanu, kapena chilichonse muli nacho.”
4 Le prêtre répondit à David, et il lui dit: Je n'ai point sous la main de pains profanes, je n'ai que des pains consacrés; si tes gens se sont au moins abstenus de femmes, ils en peuvent manger.
Koma wansembeyo anamuyankha Davide kuti, “Ine ndilibe buledi wamba woti ndikupatseni. Koma pali buledi wachipembedzo yekha. Ngati anthu amene muli nawo sanagone ndi akazi awo mukhoza kudya.”
5 David reprit: Quant aux femmes, depuis trois jours, nous nous en sommes abstenus; lorsque je suis parti, tous mes hommes ont été purifiés; mais la route elle-même les souille; c'est pourquoi nous nous purifions aujourd'hui en lavant nos vêtements.
Davide anayankha kuti, “Kunena zoona sitinakhudzane ndi mkazi monga timachitira nthawi zonse tikakhala pa ulendo. Anthu anga salola kudziyipitsa ndi mkazi ngakhale pa ulendo wamba. Nanji lero tili pa ulendo woterewu!”
6 Alors, Abimélech le prêtre lui donna les pains de proposition; car il n'y avait là d'autres pains que ceux qu'on venait d'ôter de devant la face du Seigneur, pour les remplacer par des pains chauds, le jour même où David les prit.
Choncho wansembe uja anamupatsa buledi wachipembedzo popeza kunalibeko buledi wina aliyense koma yekhayo amene amaperekedwa kwa Yehova. Uyu ndi amene anachotsedwa tsiku limenelo kuti ayikepo wina wotentha.
7 Or, il se trouvait là un serviteur de Saül, retenu devant le Seigneur; il se nommait Doeg le Syrien, et il faisait paître les mulets de Saül.
Koma tsiku limenelo mmodzi wa antchito a Sauli anali pomwepo kudikirira kuti achite mwambo wa chipembedzo mʼnyumba ya Mulungu. Munthuyu dzina lake anali Doegi Mwedomu, munthu wamphamvu pakati pa abusa a Sauli.
8 Et David dit à Abimélech: Vois si tu as ici sous la main quelque javeline ou quelque épée; car je n'ai pris ni mon glaive ni aucune arme, tant l'affaire du roi exigeait de précipitation.
Davide anafunsa Ahimeleki kuti, “Kodi muli ndi mkondo kapena lupanga pano? Ine sindinatenge lupanga langa kapena chida china chilichonse chifukwa zimene andituma amfumu ndi zamsangamsanga.”
9 Et le prêtre dit: Voici l'épée de Goliath le Philistin, que tu as vaincu dans le vallon d'Ela; elle est enveloppée dans un manteau; si tu la veux, tu peux l'emporter; hormis cette arme, il n'en est aucune ici. A quoi David répondit: Donne-la-moi; elle n'a pas sa pareille.
Wansembeyo anayankha kuti, “Kuno kuli lupanga la Goliati Mfilisiti uja amene unamupha mʼchigwa cha Ela, lakulungidwa mʼnsalu paseli pa Efodi. Ngati mufuna kulitenga, tengani popeza kuno kulibe lina koma lokhalo.” Davide anati, “Palibe lina lofanana nalo. Ndipatseni lomwelo.”
10 Le prêtre la lui donna, et David partit. Ce jour-là, il s'enfuit loin de Saül, et il alla chez Achis, roi de Geth.
Tsiku lomwelo Davide ananyamuka kuthawa Sauli ndipo anapita kwa Akisi, mfumu wa ku Gati.
11 Et les serviteurs d'Achis dirent à leur maître: N'est-ce point là David, le roi de la terre? N'est-ce pas celui dont les danseuses, en chantant, disaient: Saül les a tués par milliers, David les a tués par myriades?
Koma nduna za Akisi zinafunsa mfumuyo kuti, “Kodi uyu si Davide mfumu ya dzikoli? Kodi iyeyu si uja pomuvinira ankayimba kuti, “Sauli wapha 1,000, koma Davide wapha miyandamiyanda?”
12 Et David pesa ces paroles en son cœur, et il eut grande crainte en présence du roi Achis.
Mawu amenewa anamulowa kwambiri Davide mu mtima ndipo anayamba kuopa kwambiri Akisi mfumu ya ku Gati.
13 Aussitôt, devant lui, il se donna un nouvel aspect, et, ce jour-là, il usa de feinte; il tambourina sur les portes de la ville; il fit de ses mains des gestes insensés; il tomba contre les battants des portes, et l'écume ruisselait sur sa barbe.
Choncho anasintha makhalidwe ake pamaso pawo, nʼkudzisandutsa ngati wamisala. Iye ankangolembalemba pa zitseko za chipata ndi kumangotuluka dovi, nʼkumayenderera mʼndevu zake.
14 Et Achis dit à ses serviteurs: Voyez, cet homme est épileptique. Pourquoi me l'avez-vous amené?
Akisi anawuza nduna zake kuti, “Mukumuona munthu uyu kuti ndi wamisala! Nʼchifukwa chiyani mukubwera naye kwa ine?
15 Ai-je besoin d'épileptiques? A quoi bon l'avoir amené pour qu'il tombe en épilepsie devant moi? Il n'entrera pas dans ma maison.
Kodi ine ndikusowa anthu amisala kuti muzibwera naye munthuyu kwa ine kuti azidzachita zamisala zake pamaso panga? Kodi munthu ameneyu nʼkulowa mʼnyumba mwanga?”