< 1 Samuel 2 >
1 Mon cœur s'est affermi dans le Seigneur, ma force s'est relevée en mon Dieu, ma bouche s'est dilatée contre mes ennemis; je me suis réjouie, parce que vous m'avez sauvée.
Ndipo Hana anapemphera nati, “Moyo wanga ukukondwera mwa Yehova; Ndiyenda mwa tukumutukumu chifukwa cha Yehova. Pakamwa panga pakula ndi kuseka adani anga mowanyogodola. Ndikukondwa chifukwa mwandipulumutsa.
2 Car nul n'est saint comme le Seigneur, nul n'est juste comme mon Dieu, nul n'est saint, hormis vous.
“Palibe wina woyera ngati Yehova, palibe wina koma inu nokha, palibe thanthwe lofanana ndi Mulungu wathu.
3 Ne vous glorifiez pas, ne dites point de paroles superbes; que nul mot résonnant ne sorte de votre bouche, parce que le Seigneur est le Dieu des sciences, et que Dieu prépare ses desseins.
“Musandiyankhulenso modzitama, pakamwa panu pasatuluke zonyada, pakuti Yehova ndi Mulungu wanzeru, ndipo ndiye amene amayesa ntchito za anthu onse.
4 L'arc des puissants a été énervé, et les faibles se sont revêtus de force.
“Mauta a anthu ankhondo athyoka koma anthu ofowoka avala dzilimbe.
5 Ceux qui regorgeaient de biens ont été humiliés, et les pauvres n'ont pas eu de regards pour la terre, parce que la stérile a enfanté sept fois, et que celle qui avait beaucoup d'enfants a perdu sa fécondité.
Amene kale anali okhuta tsopano akukagula chakudya, koma iwo amene anali ndi njala sakumvanso njala. Amene anali wosabereka, wabereka ana aamuna asanu ndi awiri, koma iye wobereka ana ambiri watsala yekha.
6 Le Seigneur distribue la mort et la vie; il conduit aux enfers et il en ramène. (Sheol )
“Yehova amabweretsa imfa ndipo amaperekanso moyo, amatsitsira ku manda ndipo amawatulutsakonso. (Sheol )
7 Le Seigneur appauvrit et il enrichit; il abaisse et il élève;
Yehova amasaukitsa ndipo amalemeretsa, amatsitsa ndipo amakweza.
8 Il tire l'indigent de la poussière et le mendiant de la fange, pour les faire asseoir parmi les puissants du peuple, et leur donner en héritage un trône de gloire;
Iye amakweza osauka kuwachotsa pa fumbi, ndipo amachotsa anthu osowa pa dzala. Iye amawakhazika pamodzi ndi ana a mafumu, amawapatsa mpando waulemu. “Pakuti nsanamira za dziko lapansi ndi za Yehova, anakhazika dziko lapansi pa nsanamirazo.
9 Il accomplit les vœux des suppliants; il bénit les années du juste, tandis que l'homme, par sa propre force, ne peut rien.
Iye adzateteza moyo wa anthu okhulupirika koma anthu oyipa adzawonongedwa mu mdima. “Pakuti munthu sapambana ndi mphamvu zake.
10 Le Seigneur réduit à la faiblesse son adversaire; Le Seigneur est remonté aux cieux; il a fait retentir son tonnerre, il jugera jusqu'aux extrémités de la terre. Il donne à nos rois leur puissance, et il élèvera la force de son Christ.
Yehova adzaphwanya omutsutsa. Adzawaopsa ndi bingu kuchokera kumwamba; Yehova adzaweruza mathero a dziko lapansi. “Koma adzapereka mphamvu kwa mfumu yake, adzakuza mphamvu za odzozedwa wake.”
11 Après cela, elle laissa l'enfant devant le Seigneur, et elle retourna en Armathaïm. Cependant, l'enfant était employé au service du Seigneur, devant le prêtre Héli.
Tsono Elikana anapita ku mudzi kwawo ku Rama, koma mnyamatayo amatumikira Yehova pansi pa ulamuliro wa wansembe Eli.
12 Et les fils d'Héli le prêtre étaient des enfants de pestilence, ne connaissant pas le Seigneur.
Ana a Eli anali ana achabechabe pakuti samasamala za Yehova.
13 Or, tel était le droit du prêtre: quand quelqu'un du peuple venait sacrifier, le serviteur du prêtre arrivait aussitôt que les chairs étaient cuites, tenant à la main une fourchette.
Ndipo chizolowezi cha ansembe pakati pa anthu chinali motere kuti pamene munthu aliyense ankapereka nsembe ndipo nyama ija ikuwira pa moto, mtumiki wa wansembe ankabwera ndi chifoloko cha mano atatu mʼdzanja lake.
14 Il la plongeait dans la grande marmite, de terre ou d'airain, et tout ce que saisissait la fourchette était pour le prêtre. Voilà ce qui se faisait à l'égard de tous ceux d'Israël qui venaient en Silo sacrifier au Seigneur.
Iye ankachipisa mu mʼphikamo, ndipo wansembeyo amatenga chilichonse chimene folokoyo yabaya. Umu ndi mmene ansembewo amachitira ndi Aisraeli onse amene amabwera ku Silo.
15 Et avant que l'on brûlât la graisse, en odeur de suavité pour le Seigneur, le serviteur du prêtre accourait, et disait à l'homme qui offrait le sacrifice Donne-nous de la chair pour que le prêtre la fasse rôtir, et nous ne te prendrons pas de chair bouillie dans la marmite.
Ndipo ngakhale mafuta asanatenthedwe, mtumiki wansembe amabwera ndi kunena kwa munthu amene akupereka nsembeyo kuti, “Ndipatse nyama kuti ndiwotche, pakuti Yehova salandira nyama yophika koma yayiwisi.”
16 A quoi l'homme venu pour sacrifier répondait: Laisse-nous d'abord brûler la graisse, comme il convient, et tu prendras pour toi tous les morceaux que ton âme désire. Mais il disait: Non, donne-les-moi tout de suite, ou je les prendrai de force.
Ngati munthuyo anena kuti, “Apseretu mafuta poyamba, ndipo kenaka mutenge mmene mufunira,” mtumikiyo amayankha kuti, “Ayi ndipatse tsopano lino. Ngati sutero, ine nditenga molanda.”
17 Le péché des fils du prêtre était très grand devant le Seigneur, parce qu'ils méprisaient le sacrifice du Seigneur.
Tchimo la ana a Eli linali lalikulu kwambiri pamaso pa Yehova pakuti iwo amanyoza nsembe za Yehova.
18 Cependant, Samuel était employé au service du Seigneur, et l'enfant était revêtu d'un éphod de lin.
Koma Samueli amatumikira pamaso pa Yehova atavala efodi ya nsalu yofewa yosalala.
19 Sa mère lui fit en outre un petit manteau double, et elle le lui apporta le jour de la fête, lorsqu'elle monta avec son mari pour faire le sacrifice de la saison.
Chaka chilichonse amayi ake ankamusokera kamkanjo ndi kukamupatsa akamapita ndi mwamuna wake kukapereka nsembe za pa chaka.
20 Et Héli bénit Elcana et sa femme, disant: Que le Seigneur, en te donnant des enfants de cette femme, te récompense du serviteur que tu lui as consacré. Et l'homme retourna à sa maison.
Tsono Eli amadalitsa Elikana ndi mkazi wake ndi mawu akuti “Yehova akupatseni ana mwa mkazi uyu kulowa mʼmalo mwa amene anapempha ndi kumupereka kwa Yehova.”
21 Et le Seigneur visita Anne; elle enfanta encore trois fils et deux filles; et Samuel avait grandi devant le Seigneur.
Ndipo Yehova anamukomera mtima Hana. Anakhala ndi pathupi ndi kubereka ana aamuna atatu ndi ana aakazi awiri. Ndipo Samueli ankakula pamaso pa Yehova.
22 Or, Héli était très avancé en âge; il apprit ce que faisaient ses fils aux fils d'Israël.
Tsono Eli anakalamba kwambiri. Iye ankamva zonse zimene ana ake aamuna ankachitira Aisraeli onse, ndiponso kuti ankagona ndi akazi pa chipata cha tenti ya msonkhano.
23 Et il leur dit: Pourquoi faites-vous les choses que j'ai ouïes de la bouche de tout le peuple du Seigneur?
Choncho anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukuchita zinthu zotere? Ine ndikumva kuchokera kwa anthu onse za zoyipa zanuzo.
24 Ne les faites plus, enfants, car la nouvelle que j'ai entendue n'est pas une bonne nouvelle; ne vous conduisez plus ainsi; car ce ne sont pas de bonnes nouvelles quand on me rapporte que vous empêchez le peuple de servir Dieu.
Ayi, ana anga si mbiri yabwino imene ndikumva anthu a Mulungu akufalitsa.
25 Si un homme pèche contre un homme, on adressera pour lui des prières au Seigneur; mais s'il a péché contre le Seigneur, qui priera pour lui? Mais ils n'écoutèrent pas la voix de leur père, parce que le Seigneur voulait les détruire.
Ngati munthu alakwira munthu mnzake, mwina Mulungu adzamupepesera, koma ngati munthu achimwira Yehova adzamupepesera ndani?” Koma ana ake sanamvere kudzudzula kwa abambo awo, pakuti chinali cholinga cha Yehova kuti awaphe.
26 Et le jeune Samuel marchait; il était bon avec le Seigneur et avec les hommes.
Ndipo mnyamata Samueli anapitirira kukula mu msinkhu, ndipo ankapeza kuyanja pamaso pa Yehova ndi anthu.
27 Alors, un homme de Dieu vint auprès d'Héli, et dit: Voici ce que dit le Seigneur: Je me suis révélé à la famille de ton père quand elle était encore en Égypte, esclave dans la maison du Pharaon.
Tsiku lina munthu wa Mulungu anabwera kwa Eli ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti, ‘Kodi Ine sindinadziwulule ndekha kwa banja la kholo lako pamene iwo anali akapolo a Farao ku Igupto?
28 J'ai choisi la famille de ton père, parmi les puissants d'Israël, pour me servir, monter à l'autel, brûler de l'encens et porter l'éphod. J'ai donné à la famille de ton père, pour sa nourriture, une part de tout ce que les fils d'Israël offrent en sacrifice.
Ndipo ndinamusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti akhale wansembe wanga ndi kuti azipita pa guwa langa la nsembe, kufukiza Lubani ndi kuvala efodi pamaso panga. Ndinapatsa banja la abambo ako gawo la nsembe zonse zopsereza zimene Aisraeli amapereka.
29 Pourquoi donc as-tu regardé d'un œil avide mes victimes et mon encens? Pourquoi donc as-tu donné plus de gloire à tes fils qu'à moi, au point qu'ils consomment avant moi les prémices de toutes les victimes d'Israël?
Nʼchifukwa chiyani ukunyoza nsembe ndi zopereka zanga zimene ndinalamula? Nʼchifukwa chiyani ukupereka ulemu kwa ana ako kuposa Ine podzinenepetsa nokha ndi zopereka zabwino kwambiri za nsembe zimene Aisraeli amapereka?’”
30 A cause de cela, voici ce que dit le Seigneur Dieu d'Israël: J'avais dit: Ta famille, la famille de ton père se tiendra près de moi à toujours. Et maintenant, le Seigneur dit: Non, parce que je glorifierai ceux qui me glorifient, et que celui qui me méprise sera méprisé.
“Paja Ine Yehova Mulungu wa Israeli ‘Ndinalonjeza kuti anthu a pa banja lako ndi a pa banja la abambo ako azidzanditumikira nthawi zonse.’ Koma tsopano ndikuti, ‘Zonsezi zithe!’ Tsopano anthu amene amandilemekeza Inenso ndidzawalemekeza koma iwo amene amandinyoza Ine ndidzawanyoza.
31 Voilà que les temps approchent où j'exterminerai ta race, la postérité de ton père.
Nthawi ikubwera imene ndidzachotsa anyamata ako ndi anyamata a pa banja la abambo ako, kotero kuti sipadzakhala munthu wokalamba pa banja lako.
32 Il n'y aura plus jamais en ma maison un seul vieillard de ta race.
Pa mavuto ako udzayangʼana ndi maso ansanje zabwino zimene ndidzachitira Aisraeli ena. Mʼbanja lako simudzapezeka munthu wokalamba.
33 Et celui des tiens que je n'exterminerai pas en l'éloignant de mon autel, ses yeux s'éteindront, sa vie se consumera; et tout le reste périra par le glaive des hommes.
Komabe pa banja lako mmodzi yekha ndidzamuleka wosamuchotsa kuti azidzanditumikira. Iyeyu azidzakuliritsa ndi kukumvetsa chisoni. Koma ena onse pa banja lako adzafa akanali aangʼono.”
34 Or, voilà pour toi le signe, et il viendra sur tes deux fils, Ophni et Phinéès: ils mourront tous les deux le même jour.
“‘Ndipo chimene chidzachitike kwa ana ako awiriwa, Hofini ndi Finehasi, chidzakhala chizindikiro kwa iwe. Onse awiri adzafa pa tsiku limodzi.
35 Je susciterai alors pour moi un prêtre fidèle, qui pratiquera tout ce qui est en mon cœur et en mon âme; j'édifierai pour lui une maison fidèle, et il passera devant mon Christ, à jamais.
Pambuyo pake ndidzasankha wansembe wokhulupirika, amene adzachita zimene zili mu mtima ndi mʼmaganizo mwanga. Ndidzakhazikitsa banja lako kolimba ndipo adzatumikira pamaso pa wodzozedwa wanga nthawi zonse.
36 Celui de ta famille qui survivra, viendra se prosterner devant lui pour une obole, et dira: Admets-moi à l'une de tes distributions sacerdotales, afin que je mange du pain.
Ndipo aliyense wotsala wa banja lako adzabwera ndi kugwada pamaso pake kupempha ndalama kapena chakudya.’ Adzati, ‘Chonde ndiloleni kuti ndizithandizako pa ntchito iliyonse ya unsembe kuti ndipeze chakudya.’”