< 1 Rois 21 >

1 Et Achab passa en revue les jeunes fils des chefs des provinces; ils étaient deux cent trente; après cela, il passa en revue l'armée, toute formée d'hommes vaillants; il y en avait sept mille.
Zitatha izi, panachitika nkhani yokhudza Naboti wa ku Yezireeli amene anali ndi munda wamphesa ku Yezireeli, pafupi ndi nyumba ya mfumu Ahabu, mfumu ya ku Samariya.
2 Puis, il sortit au milieu du jour, comme Ben-Ader était à boire et à s'enivrer en Socchoth, lui et les trente-deux rois ses alliés.
Ahabu anawuza Naboti kuti, “Patse munda wako wa mpesa kuti ukhale munda wanga wa ndiwo zamasamba, popeza uli pafupi ndi nyumba yanga yaufumu. Mosinthana ndi mundawu ndidzakupatsa wina wabwino, kapena ngati ungafune, ndidzakupatsa ndalama pa mtengo wake wa mundawu.”
3 Et les jeunes fils des chefs des provinces sortirent d'abord; on l'alla rapporter au roi de Syrie, disant: Des hommes sont arrivés de Samarie.
Koma Naboti anayankha Ahabu kuti, “Pali Yehova, sindingakupatseni cholowa cha makolo anga.”
4 Et il répondit: S'ils viennent en paix, prenez-les vivants; s'ils viennent en guerre, prenez-les vivants.
Pamenepo Ahabu anapita ku nyumba yake, wachisoni ndi wokwiya chifukwa Naboti wa ku Yezireeli anamuwuza kuti, “Sindidzakupatsani cholowa cha makolo anga.” Ahabu anakagona pa bedi lake atayangʼana kumbali ndipo anakana chakudya.
5 Et les jeunes fils des chefs des provinces sortirent de la ville; cependant l'armée les suivait.
Yezebeli mkazi wake analowa ndipo anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukuoneka achisoni? Chifukwa chiyani simukufuna chakudya?”
6 Et chacun frappa l'homme le plus près de lui; puis, une seconde fois, chacun frappa l'homme le plus près de lui; aussitôt, la Syrie prit la fuite, Israël la poursuivit, et Ben-Ader s'échappa sur le cheval d'un simple cavalier.
Ahabu anayankha mkazi wake kuti, “Chifukwa chake nʼchakuti ine ndinamuwuza Naboti wa ku Yezireeli kuti, ‘Gulitse munda wako wa mpesa kapena ngati ungakonde ine ndidzakupatsa munda wina wabwino mʼmalo mwake.’ Koma iye anandiyankha kuti, ‘Sindidzakupatsani munda wanga wa mpesa.’”
7 Et le roi d'Israël sortit; il prit tous les chevaux avec les chars, et il fit des Syriens un grand carnage.
Ndipo Yezebeli mkazi wake anati, “Kodi umu ndi mmene mumachitira ngati mfumu ya Israeli? Dzukani, idyani! Sangalalani. Ine ndidzakutengerani munda wamphesa wa Naboti wa ku Yezireeli.”
8 Ensuite, le prophète alla trouver le roi d'Israël, à qui il dit: Fortifie-toi, observe, et vois ce que tu as à faire; car, l'année révolue, Ben-Ader, roi de Syrie, reviendra contre toi.
Choncho Yezebeli analemba makalata mʼdzina la Ahabu, nawadinda chidindo cha mfumu, nawatumiza makalatawo kwa akuluakulu ndi kwa anthu olemekezeka amene ankakhala ndi Naboti mu mzinda mwake.
9 Et les serviteurs du roi de Syrie lui dirent: Le Dieu d'Israël est le Dieu des montagnes, et non le Dieu des vallées; voilà pourquoi ils nous ont vaincus; si nous leur faisons la guerre dans la plaine, nous l'emporterons sur eux.
Mʼmakalatamo Yezebeli analemba kuti: “Lengezani kuti anthu asale chakudya ndipo muyike Naboti pa malo aulemu pakati pa anthu.
10 Fais ceci: renvoie les rois chacun en leur demeure, remplace-les par les princes des Philistins.
Koma muyike anthu awiri oyipa mtima moyangʼanana naye ndipo iwo achitire umboni kuti watemberera Mulungu ndiponso mfumu. Ndipo mumutulutse ndi kumuponya miyala ndi kumupha.”
11 Et nous te donnerons une autre armée aussi nombreuse que celle qui a été détruite; un cheval remplacera un cheval, des chars remplaceront les chars; nous les combattrons dans la plaine, et nous l'emporterons sur eux. Et le roi les écouta, et il fit ainsi.
Choncho akuluakulu ndi anthu olemekezeka amene ankakhala ndi Naboti mu mzinda mwake anachita monga analamulira Yezebeli mʼmakalata amene anawalembera.
12 L'année révolue, Ben-Ader passa en revue les forces de la Syrie, et il se porta en Aphèca pour combattre Israël.
Iwo analengeza kuti anthu asale chakudya ndipo anayika Naboti pa malo aulemu pakati pa anthu.
13 Les fils d'Israël aussi passèrent en revue leur armée, et ils marchèrent contre eux. Et Israël campa vis-à-vis leur camp; ils étaient comme deux troupeaux de chèvres, et les Syriens remplissaient la terre.
Ndipo anthu awiri oyipa anabwera nakhala moyangʼanana naye ndipo anamunenera zoyipa Naboti pamaso pa anthu, ponena kuti, “Naboti watemberera Mulungu ndiponso mfumu.” Choncho anamutulutsira kunja kwa mzinda ndi kumuponya miyala ndi kumupha.
14 Alors, l'homme de Dieu revint, et il dit au roi d'Israël: Voici ce que dit le Seigneur: En punition de ce que la Syrie a dit: Le Dieu d'Israël est le Dieu des montagnes et non le Dieu des vallées, je te livrerai cette armée innombrable, et tu reconnaîtras que je suis le Seigneur.
Atatero anatumiza mawu kwa Yezebeli akuti, “Naboti amuponya miyala ndipo wafa.”
15 Et les deux camps restèrent sept jours l'un vis-à-vis de l'autre; le septième jour la bataille s'engagea, et Israël tua aux Syriens cent mille piétons en une seule journée.
Yezebeli atangomva kuti Naboti amuponya miyala ndipo wafa, iye anakamuwuza Ahabu kuti, “Dzukani, katengeni munda wamphesa wa Naboti wa ku Yezireeli umene anawukaniza kukugulitsani. Naboti sali moyonso, koma wafa.”
16 Et les survivants se réfugièrent dans Aphèca, dont les murs s'écroulèrent sur vingt-sept mille de ceux qui s'étaient échappés; Ben-Ader se cacha dans l'alcôve d'une chambre à coucher;
Ahabu atamva kuti Naboti wafa, ananyamuka kukatenga munda wamphesa wa Naboti.
17 Et il dit à ses serviteurs: Je sais que les rois d'Israël sont des rois miséricordieux; couvrons nos reins de cilices: , passons-nous des cordes autour du cou, et sortons au-devant du roi d'Israël; peut-être il nous renverra la vie sauve.
Ndipo Yehova anayankhula ndi Eliya wa ku Tisibe kuti,
18 Et ils se couvrirent les reins de cilices; ils se passèrent des cordes autour du cou, et ils dirent au roi d'Israël: Ton serviteur Ben-Ader dit: Que j'aie la vie sauve. Achab répondit: Vit-il encore? Il est mon frère.
“Nyamuka, pita ukakumane ndi Ahabu, mfumu ya Israeli amene amalamulira ku Samariya. Pano ali ku munda wamphesa wa Naboti kumene wapita kuti akatenge mundawo kuti ukhale wake.
19 Les serviteurs en tirèrent bon présage; ils firent des libations, et ils s'emparèrent de la parole qui était sortie de la bouche d'Achab, et ils dirent: Ben-Ader est ton frère. Il reprit: Allez le chercher et amenez-le. Ben-Ader sortit de sa retraite pour aller près d'Achab, et ses serviteurs le firent monter auprès de lui sur un char.
Ukamuwuze kuti: ‘Yehova akuti, Kodi siwapha munthu ndi kumulandanso munda wake?’ Ndipo ukamuwuzenso kuti, ‘Yehova akuti, Pamalo pamene agalu ananyambita magazi a Naboti, pamalo pomwepo agalu adzanyambita magazi ako, inde, akonso!’”
20 Et Achab dit: Je te rendrai les villes que mon père a prises au tien; tu pourras te faire des issues à Damas, comme mon père en a fait à Samarie, et je te renverrai après avoir conclu alliance avec toi. Et ils firent alliance, et il le renvoya.
Ahabu anati kwa Eliya, “Tsono wandipeza, iwe mdani wanga!” Eliya anayankha kuti, “Inde ndakupezani chifukwa mwadzigulitsa kuti muchite zoyipa pamaso pa Yehova.
21 Mais un homme, l'un des fils des prophètes, dit, d'après la parole du Seigneur, à son voisin: Frappe-moi. Mais l'autre ne voulut pas le frapper.
Iye akuti ‘Taonani, ine ndidzabweretsa mavuto pa iwe. Ndidzawononga kotheratu zidzukulu zako ndi kuchotsa mu Israeli munthu aliyense wamwamuna wa banja la Ahabu, kapolo kapena mfulu.
22 Et le prophète lui dit: En punition de ce que tu n'as point obéi à la voix du Seigneur, quand tu seras loin de moi un lion te tuera. En effet, l'homme s'éloigna, un lion le rencontra et le tua.
Ndidzawononga nyumba yako monga momwe ndinawonongera nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati ndiponso ngati nyumba ya Baasa mwana wa Ahiya, chifukwa wandikwiyitsa Ine ndi kuchimwitsa Israeli.’
23 Et le prophète alla trouver un autre homme, et il lui dit: Frappe-moi. L'homme le frappa, le frappa encore, et l'accabla de coups.
“Ndipo kunena za Yezebeli, Yehova akuti, ‘Agalu adzadya Yezebeli mʼmbali mwa khoma la Yezireeli.’
24 Ensuite, le prophète partit, et il se tint sur le chemin qu'avait pris le roi; or, il s'était bandé les yeux.
“Agalu adzadya munthu aliyense wa nyumba ya Ahabu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya aliyense wofera ku thengo.”
25 Quand le roi vint à passer, il cria après lui, disant: Ton serviteur est allé à la guerre, et voilà qu'un homme m'a amené un homme, et m'a dit: Garde cet homme; s'il s'échappe, tu me donneras ta vie pour sa vie, ou tu paieras un talent d'argent.
(Kunalibe munthu ngati Ahabu, amene anadzigulitsa kuchita zoyipa pamaso pa Yehova, amene anakopedwa ndi mkazi wake Yezebeli.
26 Mais ton serviteur a eu beau regarder tout alentour çà et là, l'homme s'est évadé. A ces mots, le roi d'Israël s'écria: Tu me tends un piège; tu l'as tué.
Iye anachita zonyansa kwambiri popembedza mafano, monga mmene ankachitira Aamori amene Yehova anawachotsa pamene Aisraeli ankafika).
27 Et le prophète se hâta d'ôter le bandeau qui couvrait ses yeux. Alors, le roi reconnut que c'était l'un des prophètes.
Ahabu atamva mawu amenewa, anangʼamba zovala zake, navala ziguduli ndi kusala chakudya. Anagona pa ziguduli, nayenda pangʼonopangʼono.
28 Et le prophète lui dit: Voici ce que dit le Seigneur: Parce que tu as laissé échapper un méchant homme, ta vie pour sa vie, ton peuple pour son peuple.
Pamenepo Yehova anayankhula ndi Eliya wa ku Tisibe kuti,
29 Le roi d'Israël s'en alla donc confondu et attristé; puis, il rentra dans Samarie.
“Kodi waona mmene Ahabu wadzichepetsera pamaso panga? Chifukwa wadzichepetsa, sindidzabweretsa mavuto amenewa pa nthawi ya moyo wake, koma ndidzawabweretsa pa nyumba yake pa nthawi ya mwana wake.”

< 1 Rois 21 >