< 1 Rois 16 >

1 Et la parole du Seigneur vint à Jéhu, fils d'Anani; celui-ci dit à Baasa:
Ndipo Yehova anayankhula kudzera mwa Yehu mwana wa Hanani, mawu odzudzula Baasa kuti,
2 En punition de ce qu'après avoir été, par moi, tiré de la poussière et élevé sur le trône d'Israël, tu as marché dans la voie de Jéroboam, tu as fait tomber dans le péché tout mon peuple d'Israël, qui, par ses vanités, a excité ma colère,
“Ine ndinakukuza kuchokera pa fumbi ndipo ndinakupanga kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli, koma iwe wakhala ukuyenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchimwitsa anthu anga Aisraeli naputa mkwiyo wanga chifukwa cha machimo awo.
3 Je susciterai des ennemis contre toi Baasa et contre toute ta maison, et je leur livrerai ta maison comme je t'ai livré la maison de Jéroboam, fils de Nabat.
Taonani, Ine ndatsala pangʼono kuwononga Baasa pamodzi ndi nyumba yake, ndipo ndidzachitira nyumba yake zimene ndinachita pa nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati.
4 Les chiens dévoreront celui du sang de Baasa qui mourra dans la ville; et les oiseaux du ciel dévoreront celui qui mourra dans les champs.
Agalu adzadya aliyense wa banja la Baasa amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya iwo amene adzafere kuthengo.”
5 Quant au reste de l'histoire de Baasa, n'est-il pas écrit au livre des Faits et gestes des rois d'Israël?
Tsono ntchito zina za Baasa ndi zamphamvu zake zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
6 Et Baasa s'endormit avec ses pères; il fut enseveli à Thersa, et son fils régna à sa place.
Baasa anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Tiriza. Ndipo Ela mwana wake anakhala mfumu mʼmalo mwake.
7 Or, le Seigneur avait parlé par la voix de Jéhu, fils d'Anani, contre Baasa et sa maison, à cause de tout le mal qu'il avait fait devant le Seigneur, pour irriter le Seigneur par les œuvres de ses mains, et pour que sa maison devînt comme celle de Jéroboam; et Baasa avait tué Jéhu.
Komatu Yehova anayankhula kwa Baasa pamodzi ndi banja lake lonse kudzera mwa mneneri Yehu mwana wa Hanani, chifukwa cha zoyipa zonse zimene iye anachita pamaso pa Yehova, kukwiyitsa Yehovayo nakhala ngati nyumba ya Yeroboamu ndiponso chifukwa anawonongeratu banja la Yeroboamu.
8 Et Ela, fils de Baasa, régna deux ans sur Israël, à Thersa.
Mʼchaka cha 26 cha ufumu wa Asa mfumu ya Yuda, Ela mwana wa Baasa anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira ku Tiriza zaka ziwiri.
9 Et Zambri, chef de la moitié de sa cavalerie, se révolta contre lui; comme il était à boire, et déjà ivre, dans la maison d'Osa, son économe, à Thersa,
Zimuri, mmodzi mwa akuluakulu ake, amene ankalamulira theka la magaleta ake, anamuchitira chiwembu. Nthawi imeneyi Ela anali ku Tiriza, akumwa koledzera nako mʼnyumba ya Ariza, munthu amene ankayangʼanira nyumba yaufumu ku Tiriza.
10 Zambri entra, le frappa, le tua, et régna à sa place.
Zimuri anadzalowa, namukantha ndi kumupha mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda. Ndipo Zimuriyo anakhala mfumu mʼmalo mwake.
11 Et, aussitôt qu'il fut proclamé roi, et qu'il se fut assis sur le trône,
Zimuri atangoyamba kulamulira, anapha banja lonse la Baasa. Sanasiyepo munthu wamwamuna ndi mmodzi yemwe, wachibale kapena bwenzi lake.
12 Il extermina toute la famille de Baasa, selon la parole qu'avait dite le Seigneur sur la maison de Baasa, par la voix de Jéhu le prophète,
Choncho Zimuri anawononga banja lonse la Baasa, molingana ndi mawu amene Yehova anayankhula motsutsa Baasa kudzera mwa mneneri Yehu,
13 Concernant les péchés de Baasa et de son fils Ela, et le péché où ils avaient fait tomber Israël, qui, par ses vanités, avait irrité le Seigneur.
chifukwa cha machimo onse amene Baasa ndi mwana wake Ela anachita nachimwitsa Israeli, anakwiyitsa Yehova, Mulungu wa Israeli ndi mafano awo osapindulitsa.
14 Quant au reste de l'histoire d'Ela, n'est-il pas écrit au livre des faits et gestes des rois d'Israël?
Tsono ntchito zina za Ela ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
15 Zambri régna sept jours à Thersa; alors, Israël était campé devant Gabathon, ville des Philistins.
Mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda, Zimuri analamulira ku Tiriza masiku asanu ndi awiri. Gulu la ankhondo linali litamanga misasa pafupi ndi Gibetoni, mzinda wa Afilisti.
16 Et le peuple mût dans le camp que l'on disait: Zambri s'est révolté et il a tué le roi; aussitôt, le peuple d'Israël proclama roi Ambri, qui, ce jour-là, commandait l'armée et le camp.
Ankhondo amene anali ku misasa atamva kuti Zimuri wachita chiwembu ndi kupha mfumu, tsiku lomwelo ku misasako anasankha Omuri, mkulu wa ankhondo kukhala mfumu ya Israeli.
17 Et Ambri, avec tout Israël, partit de Gabathon, et il assiégea Thersa.
Tsono Omuri ndi Aisraeli onse amene anali naye anachoka ku Gibetoni ndi kukazinga Mzinda wa Tiriza.
18 Quand Zambri vit que sa ville était prise, il se réfugia dans un souterrain de son palais; puis, il brûla sur lui le palais, et il mourut,
Zimuri ataona kuti mzinda walandidwa, anathawira ku nsanja ya nyumba ya mfumu ndipo anatentha nyumbayo iye ali momwemo. Kotero iyeyo anafa,
19 A cause des péchés qu'il avait commis en faisant le mal devant le Seigneur, en faisait tomber Israël dans le péché, et en marchant dans la voie de Jéroboam.
chifukwa cha machimo amene iye anachita, kuchita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuyenda mʼnjira za Yeroboamu, nachimwitsa nazo Aisraeli.
20 Pour le reste de l'histoire de Zambri, n'est-il pas écrit au livre des Faits et gestes des rois d'Israël?
Tsono ntchito zina za Zimuri ndi chiwembu chake chimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
21 Alors, le peuple d'Israël se divisa: la moitié voulut pour roi Thamni, fils de Gonath; l'autre moitié, Ambri.
Pambuyo pake Aisraeli anagawikana pakati: theka linatsatira Tibini mwana wa Ginati kuti limulonge ufumu, ndipo theka lina linatsatira Omuri.
22 Le peuple qui suivait Ambri l'emporta sur le peuple qui suivait Thamni, fils de Gonath; Thamni mourut, en ce temps-là, ainsi que Joram, son frère, et Ambri régna après Thamni.
Koma anthu otsatira Omuri anali amphamvu kupambana amene ankatsatira Tibini mwana wa Ginati. Choncho Tibini anafa ndipo Omuri anakhala mfumu.
23 En la trente et unième année du règne d'Asa en Juda, Ambri fut reconnu roi d'Israël; il régna douze ans, dont six à Thersa.
Mʼchaka cha 31 cha Asa mfumu ya Yuda, Omuri anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira zaka 12 ndi miyezi isanu ndi umodzi ku Tiriza.
24 Et Ambri acheta la montagne de Samarie, de Samar, qui était maître de cette montagne, au prix de deux talents d'argent; il bâtit sur la montagne une ville qu'il appela Samarie, du nom de celui qui la lui avait vendue.
Iye anagula phiri la Samariya kwa Semeri pa mtengo wa ndalama 6,000 za siliva ndipo pa phiripo anamangapo mzinda, nawutcha Samariya, potsata dzina la Semeri, dzina la mwini wakale wa phirilo.
25 Et Ambri fit le mal devant le Seigneur; il fit le mal plus que tous ceux qui avaient régné avant lui.
Koma Omuri anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo anachimwa kuposa mafumu ena onse amene analipo iye asanakhale mfumu.
26 Il marcha dans toutes les voies de Jéroboam, fils de Nabat, et dans les péchés où il avait fait tomber tout Israël qui, par ses vanités, avait irrité le Seigneur.
Pakuti iye anayenda mʼnjira zonse za Yeroboamu mwana wa Nebati, ndipo tchimo lake anachimwitsa nalo Aisraeli, nakwiyitsa Yehova Mulungu wa Israeli ndi mafano awo opandapake.
27 Quant au reste de l'histoire d'Ambri, aux actions qu'il fit dans sa puissance, ne sont-ils pas écrits au livre des Faits et gestes des rois d'Israël?
Tsono ntchito zina za Omuri ndi zamphamvu zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
28 Et Ambri s'endormit avec ses pères; il fut inhumé à Samarie, et; son fils Achab régna à sa place.
Choncho Omuri anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Samariya. Ndipo Ahabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
29 La seconde année du règne de Josaphat en Juda, Achab commença, dans Samarie, un règne de vingt-deux ans.
Mʼchaka cha 38 cha ufumu wa Asa, mfumu ya Yuda, Ahabu mwana wa Omuri anakhala mfumu ya Israeli nalamulira Israeli ku Samariya zaka 22.
30 Et Achab fit le mal devant le Seigneur; il fit le mal plus que tous ceux qui avaient régné avant lui.
Ahabu mwana wa Omuri anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova kupambana mafumu onse akale.
31 Il ne lui suffit pas de marcher dans les péchés de Jéroboam, fils de Nabat; il prit pour femme Jézabel, fille d'Ethbaal, roi des Sidoniens; il l'imita, il servit Baal, et l'adora.
Iye sanachiyese ngati chinthu chochepa chabe kuchita machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, koma anakwatiranso Yezebeli, mwana wa Etibaala mfumu ya Asidoni, nayamba kutumikira Baala ndi kumupembedza.
32 Et il éleva un autel à Baal dans le temple d'abomination qu'il avait bâti à Samarie.
Iye anapangira Baala guwa lansembe mʼnyumba ya Baala imene anamanga ku Samariya.
33 Il planta un bois sacré, et il continua ses abominations pour irriter le Seigneur et perdre son âme. Il fit le mal plus que tous ceux qui, avant lui, avaient régné sur Israël.
Ahabu anapanganso fano la Asera ndi kukwiyitsa kwambiri Yehova Mulungu wa Israeli, kupambana mafumu onse a Israeli amene analipo iye asanakhale mfumu.
34 En ces jours-là, Achiel le Béthélite rebâtit Jéricho en sacrifiant son premier-né, Abiron, qui mourut comme il jetait les fondations; et Segub, le plus jeune de ses fils, qui mourut quand il posa les portes, selon la parole que le Seigneur avait dite par la voix de Josué, fils de Nau.
Pa nthawi ya Ahabu, Hiyeli wa ku Beteli anamanganso mzinda wa Yeriko. Pa nthawi yomanga maziko ake, mwana wake woyamba wa mwamuna, Abiramu anamwalira, ndipo pa nthawi yomanga zipata zake, mwana wa mngʼono wa mwamuna Segubu, anamwaliranso. Izi zinachitika monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa Yoswa mwana wa Nuni.

< 1 Rois 16 >