< 1 Rois 13 >

1 Or, voilà qu'un homme de Dieu vint de Juda à Béthel avec la parole du Seigneur, et Jéroboam était devant l'autel pour y sacrifier.
Ndipo taonani, munthu wa Mulungu wochokera ku Yuda anapita ku Beteli molamulidwa ndi Yehova. Nthawi imeneyo nʼkuti Yeroboamu atayimirira pambali pa guwa akufukiza lubani.
2 Et l'homme cria contre l'autel avec la parole du Seigneur, et il dit: Autel! autel! Voici ce que dit le Seigneur: Il naîtra de la maison de David un fils, son nom sera Josias; il immolera sur toi les prêtres des hauts lieux qui font pour toi des sacrifices, et il brûlera sur toi des ossements humains.
Mneneriyo anatemberera guwalo mofuwula potsata mawu a Yehova nati: “Guwa iwe, guwa iwe! Yehova akuti, ‘Taonani mʼbanja la Davide mudzabadwa mwana dzina lake Yosiya. Pa iwe, iyeyo adzaperekapo ngati nsembe, ansembe otumikira ku malo achipembedzo amene tsopano akufukiza lubani pa iwe, ndipo pa iwe adzatenthapo mafupa a anthu.’”
3 Et, ce jour même, l'homme donna un signe, et dit: Voici la parole qu'a dite le Seigneur; il a dit: Voilà que l'autel est fendu; la graisse qu'on y a déposée va se répandre à terre.
Tsiku lomwelo munthu wa Mulungu uja anapereka chizindikiro ichi: “Chizindikiro chimene Yehova wanena ndi ichi: Taonani guwali lidzangʼambika pakati ndipo phulusa lili pamenepo lidzamwazika.”
4 Lorsque le roi Jéroboam eut ouï les paroles de l'homme de Dieu et ses imprécations contre l'autel, il étendit sur lui la main, et il dit: Saisissez- le. Aussitôt la main que de l'autel il avait étendue vers l'homme, se dessécha, et il ne put la ramener à lui.
Mfumu Yeroboamu atamva zimene munthu wa Mulungu ananena motemberera guwa lansembe ku Beteli, anatambasula dzanja lake ali ku guwako ndipo anati, “Mugwireni!” Koma dzanja limene anatambasula kuloza munthu wa Mulunguyo linawuma kuti gwaa, kotero kuti sanathenso kulibweza.
5 Et l'autel se fendit, et la graisse qu'on y avait déposée se répandit à terre, selon le signe que l'homme de Dieu avait donné avec la parole du Seigneur.
Nthawi yomweyo guwa lija linangʼambika pakati ndipo phulusa lake linamwazika molingana ndi chizindikiro chimene munthu wa Mulungu anapereka potsata mawu a Yehova.
6 Alors, le roi Jéroboam dit à l'homme de Dieu: Prie devant le Seigneur ton Dieu, que je puisse ramener ma main. L'homme de Dieu pria devant le Seigneur, et il rendit au roi l'usage de sa main, qui redevint comme auparavant.
Pamenepo mfumu inati kwa munthu wa Mulunguyo, “Undipempherere kwa Yehova Mulungu wako kuti andikomere mtima ndipo undipempherere kuti dzanja langa lichire.” Choncho munthu wa Mulungu anapempha kwa Yehova, ndipo dzanja la mfumu linachiritsidwa nʼkukhala ngati momwe linalili kale.
7 Après cela, le roi dit à l'homme de Dieu: Entre avec moi dans ma demeure, déjeune, et je te ferai des présents.
Mfumu inati kwa munthu wa Mulunguyo, “Tiye kwathu kuti ukadye chakudya, ndipo ndidzakupatsa mphatso.”
8 Mais l'homme de Dieu dit au roi: Tu me donnerais la moitié de ta maison que je n'y entrerais pas avec toi; je ne mangerai pas de pain, je ne boirai point d'eau en ce lieu.
Koma munthu wa Mulunguyo anayankha mfumu kuti, “Ngakhale mutandipatsa theka la chuma chanu, sindingapite nanu, kapena kudya chakudya, kapenanso kumwa madzi kuno.
9 Car le Seigneur, avec sa parole, m'a fait un ordre, il a dit: Ne mange pas de pain, ne bois point d'eau, et, en t'en allant, ne prends pas le chemin par où tu es venu.
Pakuti Yehova anandilamula kuti, ‘Usakadye chakudya kapena kumwa madzi kapena kubwerera podzera njira imene unayendamo kale.’”
10 Et il s'en retourna par un autre chemin, et il ne prit point celui par où il était venu à Béthel.
Choncho munthu wa Mulunguyo anadzera njira ina ndipo sanatsate njira imene anayendamo pobwera ku Beteliko.
11 Or, il y avait à Béthel un prophète avancé en âge, et ses fils allèrent lui raconter les œuvres que, ce jour-là, l'homme de Dieu avait faites en Béthel, et les paroles qu'il avait dites au roi. Et leur père changea de visage.
Tsono ku Beteli kunkakhala mneneri wina wokalamba. Mmodzi mwa ana ake anamufotokozera zonse zomwe munthu wa Mulungu anachita kumeneko tsiku limenelo. Anawuzanso abambo ake zimene ananena kwa mfumu.
12 Et leur père dit: Par où s'en va-t-il? Ses fils lui montrèrent le chemin que venait de prendre l'homme de Dieu venu de Juda.
Abambo awo aja anawafunsa kuti, “Kodi wadzera njira iti?” Ana akewo anamufotokozera njira imene munthu wa Mulungu wochokera ku Yudayo anadzera.
13 Et il dit à ses fils: Bâtez-moi l'âne; ils lui bâtèrent son âne, et il courut après l'homme.
Ndipo abambo aja anati kwa ana akewo, “Mangireni chishalo pa bulu.” Anawo atamangirira chishalo pa bulu, nkhalambayo inakwera buluyo
14 Il prit le même chemin que l'homme de Dieu; et il le trouva assis sous un chêne, et il lui dit: Es-tu l'homme de Dieu venu de Juda? L'autre répliqua: Je le suis.
ndipo inalondola munthu wa Mulunguyo. Inamupeza atakhala pansi pa mtengo wa thundu ndipo inamufunsa kuti, “Kodi ndiwe munthu wa Mulungu amene anabwera kuchokera ku Yuda?” Munthuyo anayankha kuti, “Inde, ndineyo.”
15 Et il lui dit: Viens avec moi, et mange du pain.
Choncho mneneri wokalambayo anati kwa iye, “Tiye kwathu kuti ukadye chakudya.”
16 Je ne puis te suivre, reprit l'autre, ni manger du pain ni boire de l'eau en ce lieu.
Munthu wa Mulungu uja anati, “Sindingabwerere nanu kapena kudya chakudya kapenanso kumwa madzi kuno.
17 Car le Seigneur m'a donné ses ordres de sa propre bouche; il a dit: Ne mange pas là de pain, n'y bois point d'eau, et, en t'en allant, ne prends pas le chemin par où tu es venu.
Pakuti ndawuzidwa ndi Yehova kuti, ‘Usadye chakudya kapena kumwa madzi kumeneko kapenanso kubwerera poyenda njira imene unayendamo popita.’”
18 Mais le vieillard lui dit: Moi aussi je suis comme toi prophète; un ange du Seigneur m'a parlé avec la parole du Seigneur, disant: Ramène-le avec toi en ta maison; qu'il mange du pain, qu'il boive de l'eau. Or, le vieillard le trompait.
Mneneri wokalambayo anayankha kuti, “Inenso ndine mneneri ngati iwe. Ndipo mngelo wa Yehova anayankhula nane mawu a Yehova kuti, ‘Kamubweze abwere ku nyumba yako kuti akadye chakudya ndi kumwa madzi.’” Koma anamunamiza.
19 Il revint donc, il mangea du pain, il but de l'eau en sa maison.
Choncho munthu wa Mulungu uja anabwerera naye ndipo anakadya ndi kumwa madzi mʼnyumba mwake.
20 Et ceci advint: Comme ils étaient assis à table, la parole du Seigneur vint au prophète qui l'avait ramené.
Ali pa tebulo, Yehova anayankhula ndi mneneri wokalambayo amene anamubweza munthu wa Mulunguyo.
21 Et il dit à l'homme de Dieu qui était venu de Juda: Voici ce que dit le Seigneur: En punition de ce que tu as irrité la parole du Seigneur, de ce que tu n'as point gardé le commandement que t'avait fait le Seigneur ton Dieu,
Iye anafuwulira munthu wa Mulungu wochokera ku Yudayo kuti, “Yehova akuti, ‘Iwe wanyoza mawu a Yehova ndipo sunasunge lamulo limene Yehova Mulungu wako anakupatsa.
22 De ce que tu es revenu, de ce que tu as bu et mangé dans ce lieu, après qu'il t'avait dit: «Tu n'y mangeras pas de pain, tu n'y boiras point d'eau, » ton corps n'entrera pas dans le sépulcre de tes pères.
Iwe wabwerera ndi kudya chakudya ndiponso kumwa madzi ku malo amene Iye anakuwuza kuti usadye chakudya kapena kumwa madzi. Choncho mtembo wako sadzawuyika mʼmanda a makolo ako.’”
23 Or, quand l'homme de Dieu eut mangé du pain et bu de l'eau, il bâta son âne, et s'en alla.
Munthu wa Mulungu atatha kudya ndi kumwa, mneneri amene anamubweza uja anamangirira chishalo pa bulu wa munthu wa Mulunguyo.
24 Mais un lion le trouva en route, et le tua; son corps resta étendu sur le chemin; l'âne ne bougea pas, et le lion se tint auprès du corps.
Akupita, anakumana ndi mkango pa msewu ndipo unamupha, mtembo wake unagwera pansi pa msewu, bulu uja anayima pambali pake ndipo mkango unayima pafupi ndi mtembowo.
25 Et des hommes vinrent à passer; ils virent le cadavre gisant sur le chemin, et le lion se tenant auprès du cadavre; puis, ils entrèrent dans la ville où demeurait le vieux prophète, et ils racontèrent ce qu'ils avaient vu.
Ndipo taonani, anthu ena amene ankapita mu msewumo anaona mtembowo uli pansi potero, mkango utayima pa mbali pa mtembo uja ndipo anapita nakafotokozera anthu mu mzinda umene mumakhala mneneri wokalamba uja.
26 Le vieillard l'apprit, et il s'écria: Ce doit être l'homme de Dieu qui a irrité la parole du Seigneur.
Mneneri amene anamubweza mnzake ku njira uja atamva zimenezi, anati, “Ameneyo ndi munthu wa Mulungu amene wanyoza mawu a Yehova. Yehova wamupereka kwa mkango umene wamukhadzula ndi kumupha, monga momwe Yehova anamuchenjezera.”
27 Et il sortit, et il trouva le cadavre gisant sur le chemin, l'âne et le lion se tenant auprès du corps; et le lion n'avait point mangé le mort, et il n'avait point déchiré l'âne.
Mneneri wokalambayo anati kwa ana ake, “Mundimangire chishalo pa bulu,” ndipo anaterodi.
28 Et il sortit, et il trouva le cadavre gisant sur le chemin, l'âne et le lion se tenant auprès du corps; et le lion n'avait point mangé le mort, et il n'avait point déchiré l'âne.
Ndipo anapita, nakapezadi mtembo utagwera pansi mu msewu, bulu pamodzi ndi mkango atayima pambali pake. Koma mkangowo sunadye mtembowo kapena kukhadzula buluyo.
29 Le prophète souleva le corps de l'homme de Dieu, le plaça sur son âne, et le ramena à la ville, afin de l'ensevelir
Choncho mneneri wokalambayo anatenga mtembo wa munthu wa Mulunguyo, nawuyika pa bulu, ndipo anabwera nawo ku mzinda kuti alire maliro ndi kuyika mtembowo mʼmanda.
30 Dans son propre sépulcre; et ils pleurèrent sur lui, disant: Hélas! frère.
Tsono anayika mtembowo mʼmanda amene mneneri wokalamba uja anadzikonzera, ndipo anamulira pomanena kuti, “Mʼbale wanga ine! Mʼbale wanga ine!”
31 Après qu'ils eurent pleuré sur lui, le vieillard dit à ses fils: Quand je mourrai, ensevelissez-moi dans le sépulcre où l'homme de Dieu a été enseveli; placez-moi auprès de ses ossements, afin que mes ossements soient sauvés avec les siens.
Atamuyika mʼmanda, iye anati kwa ana ake, “Ine ndikafa, mudzandiyike mʼmanda amene munthu wa Mulungu wayikidwa. Mudzayike mafupa anga pambali pa mafupa ake.
32 Car la chose qu'il a dite d'après la parole du Seigneur, concernant l'autel de Béthel et les temples des hauts lieux en Samarie, s'accomplira.
Pakuti uthenga umene Yehova anamuyankhulitsa, wotsutsana ndi guwa lansembe la ku Beteli ndi nyumba zonse za chipembedzo za mʼmizinda ya ku Samariya, zidzachitika ndithu.”
33 Après ces choses, Jéroboam ne se repentit point de sa méchanceté; il continua de prendre, parmi tout le peuple, des prêtres des hauts lieux. Le premier venu put avoir la main pleine, et devenir prêtre sur les hauts lieux.
Ngakhale izi zinachitika, Yeroboamu sanasiye njira zake zoyipa, koma anasankhanso anthu wamba kukhala ansembe pa malo ake achipembedzo. Aliyense amene ankafuna kukhala wansembe iye anamupatula kukhala wansembe.
34 Ce fut le péché de la maison de Jéroboam, cause de sa perte et de sa disparition de la face de la terre.
Limeneli ndiye linali tchimo la nyumba ya Yeroboamu limene linabweretsa kugwa kwake ndiponso chiwonongeko mʼdzikomo.

< 1 Rois 13 >