< 1 Chroniques 9 >
1 Voilà tout Israël et son dénombrement, et ceux qui furent inscrits au livre des Rois d'Israël et de Juda, après qu'ils eurent été transportés à Babylone à cause de tous leurs péchés,
Aisraeli onse analembedwa potsata mibado yawo mʼbuku la mafumu a Aisraeli. Anthu a ku Yuda anatengedwa kunka ku ukapolo ku Babuloni chifukwa cha kusakhulupirika kwawo.
2 Et ceux qui les premiers revinrent en leurs possessions et dans les villes d'Israël, prêtres, lévites et autres à qui cela fut permis.
Tsono anthu oyamba kukhala mʼmadera awo anali Aisraeli wamba, ansembe, Alevi ndi otumikira ku Nyumba ya Yehova.
3 Jérusalem fut repeuplée par des fils de Juda, des fils de Benjamin, des fils d'Ephraïm et des fils de Manassé.
Anthu a ku Yuda, Benjamini ndi Efereimu ndiponso Manase amene anakhala mu Yerusalemu anali awa:
4 Il y eut parmi eux: Nothi, fils de Samiud, fils d'Amri, fils d'Ambraïm, fils de Buni, issus des fils de Pharès, fils de Juda,
Utai mwana wa Amihudi, mwana wa Omuri, mwana wa Imuri, mwana wa Bani, chidzukulu cha Perezi mwana wa Yuda.
5 Et de la famille de Seléni Asaie premier-né, et ses fils,
A banja la Siloni: Asaya mwana wake woyamba pamodzi ndi ana ake.
6 Issus de Zara; puis, Jehel et leurs frères au nombre de six cent quatre- vingt-dix.
A banja la Zera: Yeueli. Anthu ochokera ku Yuda analipo 690.
7 Et des fils de Benjamin: Salem, fils de Mosollam, fils d'Odes, fils d'Asinu.
A fuko la Benjamini: Salu mwana wa Mesulamu, mwana wa Hodaviya, mwana wa Hasenuya;
8 Et Jemnaa, fils de Jéroboam et Elo ceux-ci étaient issus d'Ozi, fils de Machir), et Mosollam, fils de Saphatia, fils de Raguel, fils de Jemnaï,
Ibineya mwana wa Yerohamu; Ela mwana wa Uzi, mwana wa Mikiri; ndi Mesulamu mwana wa Sefatiya, mwana wa Reueli mwana wa Ibiniya.
9 Et leurs frères, selon leur naissance, au nombre de neuf cent cinquante- six, tous chefs de familles dans leur tribu.
Anthu ochokera ku Benjamini monga analembedwera mwa mibado yawo, analipo 956. Anthu onsewa anali atsogoleri a mabanja awo.
10 Et parmi les prêtres: Jodaé, et Joarim, et Jachin;
Ansembe: Yedaya, Yehoyaribu; Yakini;
11 Et Azarias, fils d'Helcias, fils de Mosollam, fils de Sadoc, fils de Maraïoth, fils d'Achitob, grand prêtre du temple du Seigneur.
Azariya mwana wa Hilikiya, mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki mwana wa Merayoti, mwana wa Ahitubi, wamkulu woyangʼanira Nyumba ya Mulungu;
12 Et Adaie, fils d'Ira, fils de Phaschor, fils de Melchia, et Maasaïa, fils d'Adiel, fils d'Ezira, fils de Mosollam, fils de Maselmoth, fils d'Emmer;
Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pasi-Huri, mwana wa Malikiya; ndi Maasai mwana wa Adieli, mwana wa Yahizera, mwana wa Mesulamu, mwana wa Mesilemoti, mwana wa Imeri.
13 Et leurs frères, chefs de familles dans leur tribu, au nombre de dix-sept cent soixante, hommes vaillants et forts employés au temple de Dieu.
Ansembe amene anali atsogoleri a mabanja awo analipo 1,760. Anali anthu amphamvu ndi odziwa kutumikira mʼnyumba ya Mulungu.
14 Et des lévites: Saulaie, fils d'Asob, fils d'Ezricam, fils d'Asahia, des fils de Mérari.
Alevi: Semaya mwana wa Hasubu, mwana wa Azirikamu, mwana wa Hasabiya, wa mʼbanja la Merari;
15 Et Bacbacar, Arès, Galaal et Matthanias, fils de Micha, fils de Zéchri, fils d'Asaph.
Bakibakara, Heresi, Galali ndi Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zikiri, mwana wa Asafu;
16 Et Abdias, fils de Samias, fils de Galaal, fils d'Idithun, et Barachie, fils d'Ossa, fils d'Elcana, qui demeurait dans les bourgs de Notephati.
Obadiya mwana wa Semaya mwana wa Galali, mwana wa Yedutuni ndi Berekiya mwana wa Asa, mwana wa Elikana, amene ankakhala ku midzi ya Anetofati.
17 Les portiers étaient: Salom, Acum, Telmon et Diman, et ses frères; Salom était leur chef.
Alonda a pa makomo: Salumu, Akubu, Talimoni, Ahimani ndi abale awo. Mtsogoleri wawo anali Salumu.
18 Et jusqu'à ce jour, le chef est attaché à la porte royale du côté de l'orient; les portes sont les mêmes que celles des camps des fils de Lévi.
Amenewa amakhala pa chipata cha mfumu kummawa mpaka lero lino. Alonda a gulu la Alevi anali awa:
19 Or, Sellum était fils de Coré, fils d'Abiasaph, fils de Coré, et ses frères les Coréites, entre autres services dans le temple, gardaient le tabernacle; et leurs pères dans les camps du Seigneur en avaient gardé l'entrée.
Salumu mwana wa Kore, mwana wa Ebiyasafu, mwana wa Kora, pamodzi ndi abale ake a ku banja la makolo ake, Akora aja ankanyangʼanira khomo la Tenti monga ankachitira abambo awo polondera khomo la malo okhalapo Yehova.
20 Et Phinéès, fils d'Eléazar, avait été leur chef devant le Seigneur, et après lui ceux ci-dessus nommés.
Masiku oyamba Finehasi mwana wa Eliezara anali woyangʼanira alonda apakhomo ndipo Yehova anali naye.
21 Zacharie, fils de Mosollam, gardait la porte du tabernacle du témoignage.
Zekariya mwana wa Meselemiya anali mlonda woyangʼanira pa chipata cha tenti ya msonkhano.
22 Tous ceux qu'on avait choisis pour garder les portes du temple étaient au nombre de deux cent douze; ils étaient dénombrés selon leurs résidences; David et Samuel le voyant les avaient institués, s'en remettant à leur foi.
Onse amene anasankhidwa kukhala alonda pa khonde analipo 212. Iwo analembedwa mwa mibado yawo ku midzi yawo. Davide ndi mneneri Samueli ndiwo anawayika mʼmalo awo antchito chifukwa cha kukhulupirika kwawo.
23 Et eux et leurs fils gardaient les portes du temple, et, dans le temple, le tabernacle.
Iwo ndi zidzukulu zawo anali oyangʼanira zipata za nyumba ya Yehova imene imatchedwa Tenti.
24 Les portes regardaient les quatre vents du côté de l'orient, de la mer, de Borée et de Notos.
Alonda apakhomowa anali mbali zonse zinayi: kummawa, kumadzulo, kumpoto ndi kummwera.
25 Et leurs frères demeuraient dans leurs résidences, et en partaient pour qu'ils fussent relevés de sept en sept jours, à partir du jour du sabbat.
Abale awo a ku midzi yawo amabwera nthawi ndi nthawi kudzagwira ntchito yawo kwa masiku asanu ndi awiri.
26 A quatre chefs étaient confiés les gardiens des portes, et les lévites veillaient à ce quel nul ne s'introduisît furtivement dans les chambres, ni dans le trésor du temple du Seigneur.
Koma atsogoleri akuluakulu anayi a alonda, amene anali Alevi, anapatsidwa udindo woyangʼanira zipinda ndi chuma cha nyumba ya Mulungu.
27 Car la garde leur en était remise, et ils en avaient les clefs, et chaque matin dès l'aurore ils ouvraient les portes du lieu saint;
Iwo amakhala usiku wonse atayima mozungulira Nyumba ya Mulungu, chifukwa anayenera kuyilondera. Ndipo anali ndi kiyi wotsekulira mmawa uliwonse.
28 Et quelques-uns des leurs étaient chargés du service des vases, qu'on ne déplaçait pas sans qu'ils les eussent comptés.
Ena amayangʼanira zipangizo zimene amagwiritsa ntchito pa ntchito mʼNyumba ya Mulungu. Iwo amaziwerenga zikamalowetsedwa ndi potulutsidwa.
29 Et d'autres avaient la surveillance des provisions destinées aux choses saintes: de la fleur de farine, du vin, de l'huile, de, l'encens, des aromates.
Ena anapatsidwa udindo wosamalira zipangizo ndi zinthu zina zonse za ku malo opatulika, pamodzi ndi ufa, vinyo, mafuta, lubani ndi zonunkhira.
30 Et ceux qui préparaient les parfums et les aromates étaient pris parmi les fils des prêtres.
Koma ansembe ena amasakaniza zonunkhirazo.
31 Et Matthathias, issu de Lévi, fils premier-né de Salom le Coréite, avait la surveillance de tout ce qui se préparait après les sacrifices dans la poêle à frire du grand prêtre.
Mlevi wotchedwa Matitiya mwana woyamba wa Salumu wa mʼbanja la Kora, anapatsidwa udindo woyangʼanira zophikidwa mʼziwaya.
32 Et Banaïas, issu de ses frères, de la maison de Caath, était chargé des pains de proposition que l'on consacrait de sabbat en sabbat.
Abale ake ena a mʼbanja la Akohati amaphika buledi wa pa Sabata lililonse amene amayikidwa pa tebulo.
33 Et les chefs des chantres-harpistes, de la famille des lévites, étaient désignés chaque jour, car jour et nuit ils étaient employés;
Atsogoleri a mabanja a Alevi, amene anali ndi luso loyimba, amakhala mʼzipinda za Nyumba ya Mulungu ndipo samagwira ntchito zina chifukwa ankatumikira usana ndi usiku.
34 Et les chefs distribués par familles demeuraient à Jérusalem.
Onsewa anali atsogoleri a mabanja a Alevi, akuluakulu monga analembedwera pa mibado yawo, ndipo ankakhala mu Yerusalemu.
35 Or, Jehel avait habité Gabaon, qu'il avait fondée; et sa femme se nommait Moocha.
Yeiyeli abambo a Gibiyoni ankakhala ku Gibiyoni. Dzina la akazi awo linali Maaka,
36 Noms de ses fils: Abdon, premier-né; puis, Sur, Cis, Baal, Ner et Nadab,
ndipo mwana wawo woyamba kubadwa anali Abidoni, motsatana ndi Zuri, Kisi, Baala, Neri, Nadabu,
37 Gedur et son frère, et Zachur et Maceloth.
Gedori, Ahiyo, Zekariya ndi Mikiloti.
38 Et Maceloth engendra Samaa, et ceux-ci demeurèrent à Jérusalem au milieu de leurs frères.
Mikiloti anabereka Simeamu. Iwonso ankakhala ndi abale awo ku Yerusalemu.
39 Et Ner engendra Cis, et Cis engendra Saül, et Saül engendra Jonathas, et Melchisué, et Aminadab et Asabal.
Neri anabereka Kisi, Kisi anabereka Sauli, ndipo Sauli anabereka Yonatani, Maliki-Suwa, Abinadabu ndi Esibaala.
40 Et Jonathas engendra Meribaal, et Meribaal engendra Micha.
Mwana wa Yonatani anali Meri-Baala, amene anabereka Mika.
41 Fils de Micha: Phithon, Malach et Tharach.
Ana a Mika anali: Pitoni, Meleki, Tahireya ndi Ahazi.
42 Et Achaz engendra Juda, et Juda engendra Galemeth, Gazmoth et Zambri, et Zambri engendra Massa;
Ahazi anabereka Yara, Yara anabereka Alemeti, Azimaveti ndi Zimuri, ndipo Zimiri anabereka Moza.
43 Et Massa engendra Baana, et Raphaïe son fils, et Elasa son fils, et Esel son fils.
Moza anabereka Bineya. Ana ake anali Refaya, Eleasa ndi Azeli.
44 Et Esel eut six fils, et voici leurs noms: Ezricam, le premier-né; puis, Ismaël, Saraïa, Abdias, Anan et Asa; voilà les fils d'Esel.
Azeli anali ndi ana asanu ndi mmodzi ndipo mayina awo anali awa: Azirikamu, Bokeru, Ismaeli, Seariya, Obadiya ndi Hanani. Awa anali ana a Azeli.