< 1 Chroniques 29 >

1 Et le roi David dit à toute l'Église: Mon fils Salomon, en qui le Seigneur s'est complu, est jeune et délicat, et l'œuvre est grande, car elle n'est point pour l'homme, mais pour le Seigneur Dieu.
Kenaka, mfumu Davide inati kwa gulu lonse: “Mwana wanga Solomoni amene Mulungu wamusankha ndi wamngʼono ndipo sadziwa zambiri. Ntchitoyi ndi yayikulu chifukwa nyumba yaufumuyi si ya munthu, koma ndi ya Yehova Mulungu.
2 Autant que je l'ai pu, j'ai préparé pour le temple de mon Dieu: de l'or, de l'argent, de l'airain, du fer, des bois, des pierres d'onyx, quantité de pierres chères et variées, toutes sortes de pierres précieuses, et beaucoup de marbre.
Ine ndapereka ku ntchito ya Nyumba ya Mulungu zinthu zanga zonse, golide wopangira zinthu zagolide, siliva wopangira zinthu zasiliva ndi zitsulo zopangira zinthu zazitsulo, mkuwa wopangira zinthu zamkuwa ndi matabwa opangira zinthu zamatabwa komanso miyala yokongola ya onikisi yokongoletsera, miyala ya maonekedwe osiyanasiyana, ndi miyala yonse yosalala ndi miyala ya marabulo, zonsezi ndapereka zochuluka.
3 De plus, comme je mets ma joie en la demeure de mon Dieu, j'ai conservé l'or et l'argent que je me suis procuré pour moi-même; je le donne entièrement au temple de mon Dieu, outre ce que j'ai amassé pour la maison des choses saintes, savoir:
Kupatulapo izi, ine modzipereka ku Nyumba ya Mulungu wanga, tsopano ndikupereka chuma changachanga cha golide ndi siliva ku Nyumba ya Mulungu wanga, kuwonjezera pa zimene ndapereka ku ntchito ya Nyumba ya Mulungu woyerayu:
4 Trois mille talents d'or d'Ophir, et sept mille talents d'argent pur, pour que l'on en recouvre les murs du lieu saint.
Matani 100 agolide (golide wa ku Ofiri) ndi matani 240 a siliva woyengeka bwino wokutira makoma a nyumba,
5 Il y aura ce qu'il faut à la main de l'artisan. Mais est-il quelqu'un qui désire aujourd'hui remplir ses mains pour le Seigneur?
zinthu zagolide ndi zinthu zasiliva, ndiponso zinthu zonse zimene anthu aluso adzagwiritse ntchito. Tsopano ndani amene akufuna kudzipatulira yekha kwa Yehova lero?”
6 Et les princes des familles le désirèrent, les princes des fils d'Israël ainsi que les commandants de mille hommes, et les centeniers, et les intendants des travaux, et les architectes du roi.
Tsono atsogoleri a mabanja, akuluakulu a mafuko a Israeli, olamulira asilikali 1,000, ndi olamulira asilikali 100, ndiponso akuluakulu onse amene amayangʼanira ntchito ya mfumu anapereka mwaufulu.
7 Et ils donnèrent pour les travaux du temple du Seigneur: cinq mille talents et dix mille sicles d'or; dix mille talents d'argent; dix-huit mille talents d'airain et cent mille talents de fer.
Iwo anapereka ku ntchito ya Nyumba ya Mulungu matani 170 a golide, matani 340 a siliva, matani 620 a mkuwa ndi matani 3,400 a chitsulo.
8 Et celui chez qui il se trouva quelque pierre précieuse, la donna pour le trésor du temple par les mains de Dehiel, de la famille de Gerson.
Aliyense amene anali ndi miyala yokongola anayipereka ku nyumba yosungiramo chuma cha Nyumba ya Yehova ndipo amene ankayangʼanira anali Yehieli Mgeresoni.
9 Et le peuple eut une grande joie à cause de ce zèle, car chacun eut ce zèle pour Dieu de plein cœur. Et le roi David fut comblé de joie.
Anthu anakondwa chifukwa cha kupereka mwaufulu kwa atsogoleri awo, pakuti anapereka kwa Yehova mwaufulu ndiponso ndi mtima wonse. Nayenso mfumu Davide anakondwera kwambiri.
10 Et le roi David bénit le Seigneur devant toute l'Église, disant: Béni soyez-vous, Seigneur Dieu d'Israël, ô notre Père, dans tous les siècles des siècles!
Davide anatamanda Yehova pamaso pa gulu lonse, ponena kuti, “Mutamandidwe Inu Yehova Mulungu wa kholo lathu Israeli kuchokera muyaya mpaka muyaya.
11 A vous, Seigneur, la magnificence, la force, la gloire, la victoire et la puissance; car vous êtes le maître de toutes les choses qui sont sur la terre et dans les cieux. Tous les rois des nations sont troublés devant vous.
Wanu, Inu Yehova ndi ukulu ndi mphamvu, ulemerero ndiponso ufumu ndi kukongola. Pakuti zinthu zonse zakumwamba ndi pa dziko lapansi ndi zanu. Wanu, Inu Yehova ndi ufumu; Inu ndinu wokwezeka ndipo ndinu mtsogoleri wa zonse.
12 De vous viennent gloire et richesse; vous régnez sur toutes choses, ô Seigneur, prince de toutes les dominations; la force et le pouvoir résident en vos mains, et il dépend de vous, ô Tout-Puissant, de grandir et de fortifier toutes choses.
Chuma ndi ulemu zimachokera kwa Inu; Inu ndinu wolamulira zinthu zonse. Mʼdzanja lanu muli nyonga ndi mphamvu, kukweza ndi kupereka nyonga kwa onse.
13 Et maintenant, Seigneur, nous vous rendons hommage, nous louons votre nom et votre gloire.
Tsopano Mulungu wathu, ife tikukuthokozani ndi kutamanda dzina lanu laulemerero.
14 Et qui suis-je, moi, et qui est mon peuple, pour que nous ayons pu vous faire ces offrandes avec tant de zèle? Tout est à vous, et nous vous avons donné de ce qui vous appartient.
“Koma ine ndine yani, ndipo anthu anga ndani, kuti tikupatsani mowolowamanja motere? Zinthu zonse zimachokera kwa Inu, ndipo ife takupatsani zomwe zimachokera mʼdzanja lanu.
15 Car nous sommes des passagers devant vous, et Nous passons comme tous nos pères; nos jours sur la terre sont comme l'ombre, et rien n'a de la durée.
Ife ndife anthu osadziwika ndiponso alendo pamaso panu, monga analili makolo athu. Masiku anthu pa dziko lapansi ali ngati chithunzithunzi, wopanda chiyembekezo.
16 Seigneur notre Dieu, toutes les richesses que j'ai préparées pour bâtir un temple à votre saint nom, viennent de vous; tout cela vous appartient.
Inu Yehova Mulungu wathu, zinthu zonse zimene tapereka kumangira Nyumba yanu zachokera mʼdzanja lanu ndipo zonsezi ndi zanu.
17 Et j'ai reconnu, ô mon Dieu, que c'est vous qui sondez les cœurs et que vous aimez la justice; et je vous ai fait mes offrandes dans la simplicité de mon cœur, et je viens de voir ici avec joie ce peuple mettre tant de zèle à vous faire ses offrandes.
Mulungu wanga, ine ndikudziwa kuti mumayesa mtima ndipo mumakondwera ndi anthu angwiro. Zinthu zonsezi ndapereka mwaufulu ndi cholinga chabwino. Ndipo tsopano ndaona ndi chimwemwe momwe anthu anu amene ali pano akuperekera mwaufulu kwa Inu.
18 Seigneur Dieu d'Abraham, d'Isaac et d'Israël nos pères, faites que votre peuple conserve toujours en son cœur le même amour, et dirigez son cœur vers vous.
Inu Yehova Mulungu wa makolo athu Abrahamu, Isake ndi Israeli, mukhazikitse chofuna ichi mʼmitima ya anthu anu kwamuyaya, ndipo mukhazikitse mtima wokhulupirika kwa Inu.
19 Et donnez à mon fils Salomon un bon cœur pour exécuter vos commandements, pour être attentif à vos ordres et à vos témoignages, et pour conduire jusqu'à la fin la construction de votre temple.
Ndipo mumupatse mwana wanga Solomoni mtima wodzipereka kwathunthu kwa Inu kuti asunge malamulo anu, zofuna ndi malangizo anu. Achite chilichonse pomanga nyumba yaufumu imene ine ndayipezera zofunika zonse.”
20 Et David dit à toute l'Église: Bénissez le Seigneur notre Dieu. Et toute l'Église bénit le Seigneur Dieu de leurs pères; ils plièrent les genoux et ils adorèrent le Seigneur et le roi.
Kenaka mfumu Davide inati kwa gulu lonse, “Tamandani Yehova Mulungu wanu.” Kotero onse anatamanda Yehova, Mulungu wa makolo awo ndipo anawerama pansi ndi kugona chafufumimba pamaso pa Yehova ndi mfumu.
21 Et David sacrifia au Seigneur; il offrit en holocauste à Dieu, dès le matin du jour suivant: mille bœufs, mille béliers, mille agneaux; il fit leurs libations, et il distribua des victimes en abondance à tout Israël.
Mmawa mwake anthu anapereka nsembe zosiyanasiyana ndi nsembe zopsereza kwa Yehova; ngʼombe zamphongo 1,000, nkhosa zamphongo 1,000 ndi ana ankhosa 1,000, pamodzi ndi nsembe yachakumwa ndi nsembe zina zambiri zoperekera Aisraeli onse.
22 Et ils mangèrent, et ils burent avec joie devant le Seigneur toute la journée, et, pour la seconde fois, ils proclamèrent roi Salomon, fils de David; ils le sacrèrent roi devant le Seigneur, et ils sacrèrent Sadoc comme pontife.
Tsiku limeneli, iwo anadya ndi kumwa mosangalala pamaso pa Yehova ndipo anavomereza Solomoni mwana wa Davide kukhala mfumu yawo kachiwiri. Anamudzoza pamaso pa Yehova kukhala wolamulira wawo ndipo Zadoki anadzozedwa kukhala wansembe.
23 Et Salomon s'assit sur le trône de David son père; il fut honoré, et tout Israël lui obéit.
Ndipo Solomoni ankakhala pa mpando waufumu wa Yehova monga mfumu mʼmalo mwa Davide abambo ake. Iye analemera ndipo Aisraeli onse ankamumvera.
24 Les princes, les vaillants, et tous les fils du roi David son père, se soumirent à sa puissance.
Akuluakulu onse a ankhondo ndi anthu amphamvu, pamodzinso ndi ana onse aamuna a mfumu Davide, analonjeza kumvera mfumu Solomoni.
25 Et le Seigneur éleva Salomon au-dessus de tout Israël, il lui donna plus de gloire qu'à nul des rois qui l'avaient devancé.
Yehova anamukweza kwambiri Solomoni pamaso pa Aisraeli onse ndi kumupatsa ulemerero waufumu umene sunapatsidwepo kwa mfumu ina iliyonse ya Israeli.
26 Or, David, fils de Jessé, avait régné sur Israël
Davide mwana wa Yese anali mfumu ya Aisraeli onse.
27 Quarante ans: sept à Hébron, trente-trois à Jérusalem.
Iye analamulira Israeli kwa zaka makumi anayi; zaka zisanu ndi ziwiri ali ku Hebroni ndi zaka 33 ali ku Yerusalemu.
28 Et il finit en une heureuse vieillesse, plein de jours, de richesses et de gloire, et son fils Salomon régna à sa place.
Iye anamwalira atakalamba kwambiri, atakhala ndi moyo wautali, chuma ndi ulemu. Solomoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
29 Le reste des discours du roi David, ses premières et ses dernières paroles, sont écrits parmi les Récits de Samuel le voyant, de Nathan le prophète, et de Gad le voyant,
Tsono zonse zimene mfumu Davide anachita, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mneneri Samueli, mʼbuku la mneneri Natani ndi mʼbuku la mneneri Gadi,
30 Concernant tout son règne, ses guerres et les événements arrivés tant à lui qu'à Israël, et en tous les royaumes de la terre.
pamodzi ndi tsatanetsatane wa mbiri ya ulamuliro wake ndi mphamvu zake, ndi zonse zomwe zinamuzungulira iye ndi Israeli ndiponso mafumu a mayiko ena onse.

< 1 Chroniques 29 >