< 1 Chroniques 28 >

1 Et David rassembla en Jérusalem tous les chefs d'Israël, les chefs des juges, tous les chefs des gardes qui tour à tour veillaient à la personne du roi, les commandants de mille hommes, les centeniers, les trésoriers, les intendants de ses domaines, ceux des troupeaux du roi, les gouverneurs de ses fils, les eunuques, les vaillants et les guerriers de l'armée.
Davide anayitana akuluakulu onse a Israeli kuti asonkhane ku Yerusalemu: akuluakulu a mafuko, olamulira magulu a ntchito ya mfumu, olamulira ankhondo 1,000, ndi olamulira ankhondo 100, ndiponso akuluakulu onse osunga katundu ndi ziweto za mfumu ndi ana ake, pamodzinso ndi akuluakulu a ku nyumba yaufumu, anthu amphamvu ndi asilikali onse olimba mtima.
2 Et David se plaça au milieu de l'assemblée, et il dit: Écoutez-moi, mes frères et mon peuple: J'ai eu le dessein de bâtir une maison de repos, pour l'arche de l'alliance un lieu du Seigneur, où notre Seigneur arrête ses pas; j'ai préparé ce qui convient pour cette construction.
Mfumu Davide inayimirira ndipo inati: “Tamverani abale anga ndi anthu anga. Ine ndinali ndi maganizo omanga nyumba monga malo okhalamo Bokosi la Chipangano la Yehova, malo oyikapo mapazi a Mulungu wathu, ndipo ndinakonza ndondomeko yomangira nyumbayo.”
3 Mais Dieu a dit: Tu ne bâtiras pas un temple où mon nom soit invoqué, parce que tu es un homme de guerre, et que tu as versé le sang.
Koma Mulungu anati kwa ine, “Usandimangire nyumba chifukwa ndiwe munthu wankhondo ndipo wakhala ukukhetsa magazi.”
4 Le Seigneur Dieu d'Israël m'a choisi dans la maison de mon père pour être à jamais roi d'Israël, et il a choisi Juda pour sa tribu royale; dans Juda il a choisi la maison de mon père; et, parmi les fils de mon père, il a voulu que je fusse roi de tout Israël.
“Komabe Yehova Mulungu wa Israeli anasankha ine pakati pa onse a banja langa kukhala mfumu ya Israeli kwamuyaya. Iye anasankha Yuda kukhala mtsogoleri, ndipo pa banja la Yuda anasankha banja langa. Pakati pa ana aamuna a abambo anga, kunamukomera Iye kundikhazika mfumu ya Aisraeli onse.
5 Et, parmi tous mes fils, car le Seigneur m'en a accordé un grand nombre, il a choisi Salomon, mon fils, pour l'asseoir sur le trône du royaume du Seigneur, et pour qu'il soit roi d'Israël.
Pa ana anga ambiri onse amene Yehova wandipatsa, Iye wasankha mwana wanga Solomoni kuti akhale pa mpando waufumu wa ufumu wa Yehova kuti alamulire Israeli.”
6 Et Dieu m'a dit: Salomon, ton fils, bâtira mon parvis et mon temple; car je l'ai choisi pour qu'il soit mon fils, et je serai pour lui un père.
Yehova anati kwa ine, “Solomoni mwana wako ndiye amene adzamanga nyumba yanga ndi mabwalo anga, pakuti Ine ndamusankha kuti akhale mwana wanga ndipo Ine ndidzakhala abambo ake.
7 Et je maintiendrai, dans tous les siècles, son royaume, s'il observe sans faiblir, comme il les observe maintenant, mes commandements et mes préceptes.
Ine ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya ngati iye saleka kutsatira malamulo ndi malangizo anga, monga momwe zikuchitikira leromu.”
8 Je vous recommande donc en présence de toute l'Église du Seigneur, et devant notre Dieu qui nous entend, d'observer et d'aimer tous les commandements du Seigneur notre Dieu, afin que vous possédiez cette terre féconde, et que vous en transmettiez l'héritage à vos fils pour toujours.
“Tsono lero ine ndikulamula inu pamaso pa Aisraeli onse ndi pa msonkhano wa Yehova, ndipo Mulungu wathu akumva: Mutsatire mosamala malamulo a Yehova Mulungu wathu, kuti dziko labwinoli likhale lanu ndi kuti mudzalipereke kwa zidzukulu zanu kukhala cholowa chawo kwamuyaya.”
9 Et toi, Salomon, mon fils, reconnais le Dieu de tes pères, sers-le d'un cœur pur et d'une âme ferme, car le Seigneur sonde tous les cœurs et il connaît toutes les pensées. Si tu le cherches tu le trouveras, et si tu l'abandonnes il t'abandonnera pour toujours.
“Ndipo iwe mwana wanga Solomoni, umvere Mulungu wa abambo ako, umutumikire ndi mtima wodzipereka kwathunthu ndi mtima wako wonse, pakuti Yehova amasanthula mtima wa aliyense, ndipo amadziwa maganizo aliwonse a munthu. Ngati ufunafuna Yehova, Iye adzapezeka; koma ngati umutaya, Iye adzakukana kwamuyaya.
10 Vois aujourd'hui que le Seigneur t'a choisi pour que tu lui bâtisses une maison où sera son sanctuaire; sois fort et agis.
Tsopano ganizira bwino, pakuti Yehova wakusankha iwe kuti umange Nyumba ya Mulungu monga malo ake opatulika. Khala wamphamvu ndipo ugwire ntchito.”
11 Ensuite, David donna à Salomon, son fils, le modèle du temple, de ses constructions, de ses trésors, de ses chambres hautes, des logements intérieurs et du propitiatoire,
Kotero Davide anapatsa Solomoni mwana wake mapulani a khonde la Nyumba ya Mulungu, nyumba zake, mosungiramo katundu, zipinda zake zamʼmwamba, zipinda zamʼkati ndi malo a nsembe zopepesera machimo.
12 Et le plan, qu'il avait eu en l'esprit, du parvis du temple du Seigneur, de tous les vestibules d'alentour communiquant aux trésors, des trésors, des choses saintes et des chambres secrètes,
Iye anapatsa Solomoni mapulani a zonse zimene ankaziganizira za bwalo la Nyumba ya Yehova ndi zipinda zonse zozungulira, zipinda zosungiramo chuma cha Nyumba ya Mulungu ndi zinthu zoperekedwa kwa Yehova.
13 Et le règlement du service journalier des prêtres et des lévites, pour toutes leurs œuvres liturgiques dans le temple du Seigneur, et des trésors où seraient déposés les vases liturgiques employés aux cérémonies du culte dans le temple du Seigneur.
Davide anamulangiza za magulu a ansembe ndi Alevi ndi ntchito yonse yotumikira mʼNyumba ya Yehova, komanso za zinthu zonse zogwirira ntchito potumikira.
14 Et il donna le poids des vases d'or et d'argent,
Iye anakonzeratu za kulemera kwa golide wopangira zida zonse zagolide zogwirira ntchito zosiyanasiyana, ndiponso kulemera kwa siliva wopangira zida zonse zasiliva zogwirira ntchito zosiyanasiyana:
15 Des lampes et des chandeliers,
kulemera kwa golide wopangira choyikapo nyale chagolide ndi nyale zake; ndiponso kulemera kwa siliva wa choyikapo nyale chilichonse ndi nyale zake, molingana ndi kagwiritsidwe ka choyikapo nyale chilichonse;
16 Il donna pareillement le poids des tables de proposition, de chaque table d'or, et de chaque table d'argent,
kulemera kwa golide wa tebulo iliyonse yoyikapo buledi wopatulika; kulemera kwa siliva wopangira matebulo asiliva;
17 Et des fourchettes, et des coupes à libations, et des fioles d'or, et des encensoirs, et d'autres objets d'or et d'argent.
muyeso wa golide woyengeka bwino wopangira mafoloko, mbale ndi zotungira; muyeso wa golide wa beseni lililonse la siliva;
18 Il lui montra aussi le poids, en or pur, de toutes les parties de l'autel des parfums, et le modèle du char des deux chérubins aux ailes déployées, qui devaient ombrager l'arche de l'alliance du Seigneur.
ndiponso muyeso wa golide wabwino wopangira guwa la zofukiza. Davide anamupatsanso ndondomeko ya mapangidwe a galeta, akerubi agolide atatambasula mapiko awo kuphimba Bokosi la Chipangano la Yehova.
19 David donna tout cela à Salomon en écriture de la main du Seigneur, avec la sagesse dont il fut assisté pour réaliser le modèle.
Davide anati, “Zonsezi ndalemba kuchokera kwa Yehova, ndipo Iye wachita kuti ndimvetsetse zonse za mapulaniwa.”
20 Et David dit à Salomon, son fils: Sois fort, agis en homme, exécute, n'aie ni crainte, ni faiblesse; car le Seigneur Dieu est avec toi; il ne te négligera pas, il ne t'abandonnera point que tu n'aies terminé toute l'œuvre destinée au service de son temple. Voici le modèle de sa nef et de son temple, de son trésor, des chambres hautes, des logements intérieurs et du propitiatoire; voici le plan du temple du Seigneur.
Davide anatinso kwa mwana wake Solomoni, “Khala wamphamvu ndi wolimba mtima ndipo uchite ntchitoyi. Usachite mantha kapena kutaya mtima pakuti Yehova Mulungu wanga ali nawe. Iye sadzakukhumudwitsa kapena kukusiya mpaka ntchito yonse ya Nyumba ya Mulungu itatha.
21 Voici encore l'ordre des fonctions journalières des prêtres et des lévites, dans tout le service du temple du Seigneur; et tu seras assisté en ton œuvre par chaque homme zélé et habile en quelque art, et les princes et tout le peuple exécuteront tous tes commandements.
Magulu a ansembe ndi Alevi ndi okonzeka kugwira ntchito ya Nyumba ya Mulungu, ndipo munthu waluso aliyense wodzipereka adzakuthandiza pa ntchito yonse. Akuluakulu ndi anthu onse adzamvera chilichonse chomwe udzalamula.”

< 1 Chroniques 28 >