< 1 Chroniques 17 >

1 Et quand David eut pris possession de son palais, il dit à Nathan le prophète: Voilà que j'habite une maison de cèdre, tandis que l'arche de l'alliance du Seigneur repose sous des courtines de peaux.
Davide atakhazikika mʼnyumba yake yaufumu, anawuza mneneri Natani kuti, “Ine pano ndikukhala mʼnyumba yaufumu yomanga ndi mitengo ya mkungudza, pomwe Bokosi la Chipangano la Yehova lili mu tenti.”
2 Et Nathan dit à David: Tout ce qui est en ton cœur, fais-le, car Dieu est avec toi.
Natani anayankha Davide kuti, “Chitani chilichonse chimene chili mu mtima mwanu, chifukwa Mulungu ali nanu.”
3 Mais, cette nuit même, la parole du Seigneur vint à Nathan, et lui dit:
Usiku umenewo mawu a Mulungu anafika kwa Natani, ndipo anati,
4 Va, et dis à mon serviteur David; Voici ce que dit le Seigneur: Tu ne me bâtiras pas un temple pour que je l'habite,
“Pita kamuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova akunena kuti, sudzandimangira ndiwe nyumba yokhalamo.’
5 Parce que je n'ai point résidé dans un temple depuis que j'ai tiré de l'Égypte les fils d'Israël jusqu'à ce jour, et que je me suis tenu dans un tabernacle et sous un voile.
Ine sindinakhalepo mʼnyumba kuyambira tsiku limene ndinatulutsa Israeli mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ndakhala ndikuyenda kuchoka mʼtenti ina kupita mʼtenti ina, kuchoka malo ena kupita malo ena.
6 En quelque lieu que j'aie passé avec tout Israël, ai-je jamais dit à celle des tribus que j'avais chargée de prendre soin de tout le peuple: Pourquoi ne m'avez-vous point bâti une maison de cèdre?
Konse ndakhala ndikuyenda ndi Aisraeli onse, kodi ndinanenapo kwa wina aliyense wa atsogoleri awo amene ndinamulamula kuweta anthu anga kuti, ‘Kodi nʼchifukwa chiyani simunandimangire nyumba ya mitengo ya mkungudza?’”
7 Dis encore à mon serviteur David: Voici ce que dit le Seigneur tout- puissant: Je t'ai tiré de la bergerie quand tu marchais derrière les troupeaux, pour que tu sois roi de mon peuple Israël.
Ndipo tsopano umuwuze mtumiki wanga Davide kuti, “Yehova Wamphamvuzonse akuti, Ine ndinakutenga ku busa ukuweta nkhosa, kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga, Aisraeli.
8 Je t'ai accompagné partout où tu as marché, j'ai exterminé devant toi tous tes ennemis, et je t'ai rendu célèbre autant que les plus renommés des grands de la terre.
Ineyo ndinali nawe kulikonse kumene unkapita, ndipo ndachotsa adani ako onse pamaso pako. Tsopano ndidzakuza dzina lako kuti likhale mʼgulu la mayina a anthu otchuka kwambiri pa dziko lapansi.
9 Et j'adopterai un lieu pour mon peuple Israël; je l'y fixerai et il s'y abritera, chacun aura sa demeure, et il ne sentira plus d'inquiétudes, et le fils de l'iniquité ne l'affligera plus comme il a fait dès le commencement,
Ndipo ndidzawapatsa malo anthu anga, Aisraeli ndipo ndidzawadzala pamalo awoawo kuti asadzavutitsidwenso. Anthu oyipa sadzawazunzanso monga ankachitira poyamba paja;
10 Depuis les temps où j'ai donné des juges à mon peuple; j'ai humilié tous tes ennemis, et je t'augmenterai, et le Seigneur te fera une maison.
monga akhala akuchitira kuchokera nthawi imene ndinasankha atsogoleri a anthu anga Aisraeli. Ine ndidzagonjetsanso adani anu onse. “‘Ine ndikulengeza kwa iwe kuti Yehova adzakhazikitsa banja lako.
11 Et, quand tes jours seront remplis, quand tu te seras endormi avec tes pères, j'élèverai après toi ta race et celui qui sera issu de ton sang; et je préparerai son règne.
Masiku ako akadzatha ndipo ukadzatsatira makolo ako, Ine ndidzawutsa mphukira yako imene idzalowa mʼmalo mwako, mmodzi mwa ana ako, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake.
12 Celui-là me bâtira un temple, et je dresserai son trône pour toujours.
Iye ndiye amene adzandimangira nyumba, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya.
13 Je serai pour lui un père, et il sera pour moi un fils, et je ne lui retirerai point ma miséricorde, comme je l'ai retirée à ceux qui t'ont précédé.
Ine ndidzakhala abambo ake, ndipo iye adzakhala mwana wanga. Ine sindidzasiya kumukonda monga ndinachitira ndi amene unalowa mʼmalo mwawo.
14 Et je l'établirai en mon temple, et en son royaume pour toujours; et son trône sera toujours debout.
Ndidzamuyika kukhala wolamulira nyumba yanga ndi ufumu wanga kwamuyaya. Mpando wake waufumu udzakhazikika kwamuyaya.’”
15 Ainsi, Nathan répéta à David toutes ces paroles, que lui-même avait ouïes en sa vision.
Natani anafotokozera Davide mawu onse avumbulutso limene analandira.
16 Alors, le roi David s'en alla; et il se plaça devant le Seigneur, et il dit: Qui suis-je, Seigneur mon Dieu, et qu'est ma maison pour que vous m'aimiez à jamais?
Choncho Mfumu Davide analowa mu tenti nakhala pamaso pa Yehova, ndipo anati, “Ine ndine yani, Inu Yehova Mulungu, ndipo banja langa nʼchiyani kuti mundifikitse pamene ndafikapa?
17 Ce que vous en avez fait c'était à vos yeux peu de chose, ô mon Dieu, et vous avez parlé de la maison de votre serviteur pour un avenir lointain, et vous m'avez regardé comme on regarde un ami, et vous m'avez élevé, Seigneur mon Dieu.
Inu Mulungu, kukhala ngati izi ndi zosakwanira pamaso panu, Inuyo mwayankhula zatsogolo la banja la mtumiki wanu. Mwandiyangʼana ndipo mwandiyesa ngati munthu wolemekezeka kwambiri pakati pa anthu, Inu Yehova Mulungu.”
18 Que pourra faire encore David devant vous pour vous glorifier? Vous connaissez maintenant votre serviteur.
“Kodi Davide anenenso chiyani kwa Inu, pakuti mwachitira ulemu wotere mtumiki wanu? Pakuti Inu mukumudziwa mtumiki wanu.
19 Vous avez opéré ces grandes choses au gré de votre cœur.
Inu Yehova, chifukwa cha mtumiki wanu komanso mwa chifuniro chanu, mwachita chinthu chachikulu ichi ndipo mwawulula malonjezo anu aakulu onse.
20 Seigneur, nul ne vous ressemble, nul n'est Dieu que vous, et vous vous êtes révélé par toutes les merveilles que nous avons oui redire.
“Palibe wina wofanana nanu, Inu Yehova, ndipo palibe Mulungu wina koma Inu nokha monga tamvera ndi makutu athu.
21 Et il n'est point sur la terre de peuple qui ressemble à Israël votre peuple. Il n'en est point que Dieu. ait guidé pour le racheter et s'en faire un peuple pour lui-même, pour se faire à lui-même un grand et glorieux nom, et pour expulser les nations devant votre peuple que vous avez délivré de l'Égypte.
Ndipo ndi ndani wofanana ndi anthu anu Aisraeli, mtundu wokhawo pa dziko lapansi umene Mulungu wake anapita kukawuwombola, monga anthu akeake ndi kukadzitchukitsa yekha pochita zinthu zodabwitsa zazikulu, pothamangitsa mitundu ina pamaso pa anthu ake, amene Inu munawawombola ku Igupto?
22 Vous vous êtes donné, en Israël, un peuple qui sera votre peuple à jamais; et vous, Seigneur, vous êtes son Dieu.
Inu munawapanga anthu anu Aisraeli kukhala anuanu kwamuyaya, ndipo Inu, Inu Yehova ndinu Mulungu wawo.
23 Maintenant donc, Seigneur, que la promesse que vous avez faite à votre serviteur, concernant sa maison, soit à jamais confirmée; faites comme vous avez dit.
“Ndipo tsopano Yehova, sungani kwamuyaya lonjezo limene mwachita ndi mtumiki wanu ndi banja lake, likhazikitseni kwamuyaya. Chitani monga mwalonjezera,
24 Et que votre nom soit glorifié à jamais, et que l'on y ait foi, et que l'on dise: Seigneur, Seigneur tout-puissant, Dieu d'Israël, la maison de David votre serviteur est érigée devant vous.
kotero dzina lanu likhazikike ndi kukhala lotchuka mpaka muyaya. Ndipo anthu adzanena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa woyangʼanira Israeli, ndi Mulungu wa Israeli!’ Ndipo banja la mtumiki wanu Davide lidzakhazikika pamaso panu.
25 Car, Seigneur Dieu, vous avez révélé vos desseins à votre serviteur, disant: Je te bâtirai une maison; c'est à ce sujet que votre serviteur a pensé à vous prier face à face.
“Inu Mulungu wanga, mwaululira mtumiki wanu kuti mudzamumangira nyumba. Nʼchifukwa chake ine mtumiki wanu ndalimba mtima kupemphera motere.
26 Et maintenant, Seigneur, vous seul êtes Dieu, et c'est vous qui avez fait à votre serviteur ces magnifiques promesses.
Inu Yehova, ndinu Mulungu! Mwalonjeza zinthu zabwinozi kwa mtumiki wanu.
27 Commencez donc et bénissez la maison de votre serviteur, pour qu'elle subsiste toujours devant vous; car, Seigneur, vous l'avez déjà bénie, bénissez-la donc à jamais.
Ndipo chakukomerani kudalitsa banja la mtumiki wanu kuti likhale pamaso panu mpaka muyaya. Pakuti Inu Yehova mwalidalitsa, lidzakhala lodalitsika mpaka muyaya.”

< 1 Chroniques 17 >