< Zacharie 10 >

1 Demandez de la pluie à l’Eternel dans la saison des dernières pluies: c’est l’Eternel qui produit les éclairs. Il vous donnera des ondées abondantes, à chacun l’herbe des champs.
Pemphani mvula kwa Yehova pa nthawi yamphukira; ndi Yehova amene amapanga mitambo ya mvula. Iye amagwetsa mivumbi ya mvula kwa anthu, ndi kumeretsa mbewu za mʼmunda kwa aliyense.
2 C’Est que les Terafim débitent de vains discours, les augures des visions mensongères, les songes disent des faussetés, apportent des consolations illusoires; c’est pourquoi ils vaguent comme des brebis, ils sont dans la misère, faute de pasteurs.
Mafano amayankhula zachinyengo, owombeza mawula amaona masomphenya abodza; amafotokoza maloto onama, amapereka chitonthozo chopandapake. Choncho anthu amangoyendayenda ngati nkhosa zozunzika chifukwa chosowa mʼbusa.
3 Contre les pasteurs ma colère s’est allumée, je sévirai contre les boucs conducteurs du troupeau, car l’Eternel-Cebaot a passé en revue son troupeau, la maison de Juda, et la considère comme son coursier d’honneur dans la bataille.
“Ine ndawakwiyira kwambiri abusa, ndipo ndidzalanga atsogoleri; pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzasamalira nkhosa zake, nyumba ya Yuda, ndi kuwasandutsa ngati akavalo aulemerero ankhondo.
4 C’Est de là que provient la pierre d’angle, de là la cheville ouvrière, de là l’arc de combat; de là sortent les vainqueurs tous ensemble.
Mu Yuda mudzachokera mwala wapangodya, mudzachokera chikhomo cha tenti, mudzachokera uta wankhondo, mudzachokera mtsogoleri aliyense.
5 Ils seront comme des héros piétinant, dans la mêlée, la boue des chemins; ils soutiendront la lutte, car l’Eternel est avec eux: ceux qui montent des chevaux seront couverts de confusion.
Onse pamodzi adzakhala ngati ngwazi zankhondo zoponda mʼmatope a mʼmisewu nthawi yankhondo. Chifukwa Yehova adzakhala nawo, adzachita nkhondo ndi kugonjetsa okwera pa akavalo.
6 Je donnerai la victoire à la maison de Juda, je prêterai main-forte à la maison de Joseph; je les rétablirai après les avoir pris en pitié: ils seront comme si jamais je ne les avais délaissés, car je suis l’Eternel, leur Dieu, et je les exaucerai.
“Ndidzalimbitsa nyumba ya Yuda ndi kupulumutsa nyumba ya Yosefe. Ndidzawabwezeretsa chifukwa ndawamvera chisoni. Adzakhala ngati kuti sindinawakane, chifukwa ndine Yehova Mulungu wawo ndipo ndidzawayankha.
7 Ephraïm sera tel qu’un vaillant guerrier, son cœur sera joyeux comme sous l’action du vin. Ses fils le verront et se réjouiront, leur cœur exultera en l’Eternel.
Aefereimu adzakhala ngati ankhondo amphamvu adzasangalala ngati anthu amene amwa vinyo. Ana awo adzaziona zimenezi ndipo adzasangalala; mʼmitima mwawo adzakondwa mwa Ambuye.
8 Je leur ferai entendre le signal et les rassemblerai, parce que je les aurai rachetés. Ils seront nombreux comme jadis ils furent nombreux.
Ndidzaliza mluzu ndi kuwasonkhanitsa pamodzi. Ndithu ndawawombola; adzachulukana ngati poyamba paja.
9 Quand je les aurai semés parmi les nations, dans les pays lointains, ils se souviendront de moi; ils y vivront avec leurs enfants, puis ils reviendront.
Ndinawamwaza pakati pa mitundu ina ya anthu, koma ku mayiko akutaliwo adzandikumbukira. Iwo pamodzi ndi ana awo adzapulumuka, ndipo adzabwerera.
10 Je les ramènerai du pays d’Egypte, je les rassemblerai du pays d’Achour; je les ferai rentrer au pays de Galaad et au Liban, et ils s’y trouveront à l’étroit.
Ndidzawabweretsa kuchokera ku Igupto ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku Asiriya. Ndidzawabwezera ku Giliyadi ndi ku Lebanoni, mpaka malo woti nʼkukhalamo adzatheratu.
11 Alors la détresse franchira la mer et frappera les flots au sein de l’Océan, toutes les sources profondes du Nil tariront. Ainsi sera abaissé l’orgueil d’Achour, et le sceptre disparaîtra de l’Egypte.
Adzawoloka nyanja ya masautso; nyanja yokokoma idzagonja ndipo madzi onse a mu Nailo adzaphwa. Kudzikuza kwa Asiriya kudzatha ndipo ndodo yaufumu ya Igupto idzathyoka.
12 Quant à eux je les rendrai puissants par l’Eternel, et ils marcheront fièrement en son nom, dit l’Eternel.
Ndidzalimbitsa iwo mwa Yehova ndipo adzayenda mʼdzina lake,” akutero Yehova.

< Zacharie 10 >