< Ruth 3 >
1 Cependant Noémi, sa belle-mère, lui dit: "Ma fille, je désire te procurer un foyer qui fasse ton bonheur.
Tsiku lina Naomi anafunsa mpongozi wake Rute kuti, “Mwana wanga, kodi si kwabwino kuti ndikupezere kokhala kuti zinthu zizikuyendera bwino?
2 Or Booz, avec les servantes duquel tu t’es trouvée, n’est-il pas notre parent? Eh bien! Cette nuit même il doit vanner les orges dans son aire.
Bowazi amene adzakazi ake wakhala nawo nthawi yonseyi, si wachibale wathu kodi? Usiku uno akhala akupeta barele ku malo opunthira.
3 Tu auras soin de te laver, de te parfumer et de revêtir tes plus beaux habits; puis tu descendras à l’aire, mais tu ne te feras pas remarquer de cet homme, avant qu’il ait fini de manger et de boire.
Samba ndi kudzola mafuta onunkhira, ndipo uvale zovala zako zabwino kwambiri. Kenaka upite ku malo opunthirako tirigu ndi barele koma munthuyo asakakuzindikire kufikira atamaliza kudya ndi kumwa.
4 Puis, quand il se sera couché, tu observeras l’endroit où il repose; tu iras découvrir le bas de sa couche et t’y étendras: lui-même, il t’indiquera alors ce que tu devras faire."
Akamakagona, iwe ukaonetsetse malo amene wagonawo. Kenaka upite ndi kuvundukula chofunda ku mapazi ake ndi kugona. Iyeyo akakuwuza zoti uchite.”
5 Elle lui répondit: "Tout ce que tu me recommandes, je l’exécuterai."
Rute anayankha kuti, “Ndichita zonse zimene mwanena.”
6 Elle descendit à l’aire et fit ce que sa belle-mère lui avait recommandé.
Choncho Rute anapita ku malo opunthirawo ndipo anachita monga momwe apongozi ake anamuwuza.
7 Booz mangea et but et fut d’humeur joyeuse; puis il alla se coucher au pied du monceau de blé. Et Ruth se glissa furtivement, découvrit le bas de sa couche et s’y étendit.
Atamaliza kudya ndi kumwa, Bowazi anakhala wosangalala, ndipo anakagona pa mbali pa mulu wa barele. Tsono Rute anapita mwa kachetechete, navundukula chofunda ku mapazi ake ndi kugona.
8 Il arriva qu’au milieu de la nuit cet homme eut un mouvement de frayeur et se réveilla en sursaut, et voilà qu’une femme était couchée à ses pieds.
Tsono pakati pa usiku Bowazi anadzidzimuka, natembenuka, ndipo anangoona mkazi akugona ku mapazi ake.
9 "Qui es-tu?" s’écria-t-il. Elle répondit: "Je suis Ruth, ta servante; daigne étendre le pan de ton manteau sur ta servante, car tu es un proche parent."
Iye anafunsa kuti, “Ndiwe yani?” Ndipo anayankha kuti, “Ndine mdzakazi wanu Rute. Popeza ndinu wachibale amene muyenera kundiwombola, ndiye mundilowe chokolo.”
10 Il répliqua: "Que l’Eternel te bénisse, ma fille! Ce trait de générosité est encore plus méritoire de ta part que le précédent, puisque tu n’as pas voulu courir après les jeunes gens, riches ou pauvres.
Ndipo Bowazi anati, “Mwana wanga, Yehova akudalitse popeza kukoma mtima kumene wasonyeza panoku kwaposa koyamba kaja. Iwe sunathamangire anyamata olemera kapena osauka.
11 Maintenant, ma fille, sois sans crainte; tout ce que tu me demanderas, je le ferai pour toi, car tous les habitants de notre ville savent que tu es une vaillante femme.
Ndipo tsopano mwana wanga usaope. Ine ndidzakuchitira chilichonse udzapemphe popeza anzanga onse amʼmudzi muno akudziwa kuti ndiwe mkazi wa khalidwe labwino.
12 Toutefois, s’il est vrai que je suis ton parent, il existe un parent plus direct que moi.
Ngakhale kuti ndinedi wachibale woyenera kukusamala, koma alipo wachibale weniweni kuposa ine.
13 Passe donc la nuit ici; demain matin, s’il consent à t’épouser, c’est bien, qu’il le fasse! Mais s’il s’y refuse, c’est moi qui t’épouserai, par le Dieu vivant! Reste couchée jusqu’au matin."
Gona konkuno usiku uno mpaka mmawa. Tsono ngati iyeyu adzakulowa chokolo, chabwino alowe. Koma ngati safuna kutero, ine ndikulumbira pamaso pa Yehova Wamoyo kuti ndidzakulowa chokolo. Ugone kuno mpaka mmawa.”
14 Elle demeura étendue au bas de sa couche jusqu’au lendemain matin; puis elle se releva avant l’heure où on peut se reconnaître les uns les autres "Car, disait-il, il ne faut pas qu’on sache que cette femme a pénétré dans l’aire."
Choncho Rute anagona ku mapazi ake mpaka mmawa, koma anadzuka mmamawa kusanayere chifukwa Bowazi anati, “Aliyense asadziwe kuti kopondera barele kunabwera mkazi.”
15 Booz dit encore: "Déploie le châle qui te couvre et tiens-le bien."; elle le lui tendit, et il y mit six mesures d’orge, l’en chargea et rentra en ville.
Bowazi anati kwa Rute, “Bwera nacho kuno chofunda wavalacho ndipo uchiyale pansi.” Ndipo atayala, Bowazi anathira makilogalamu makumi awiri a barele ndi kumusenzetsa Rute. Rute anapita nakalowa mu mzinda.
16 Quant à Ruth, elle alla retrouver sa belle-mère, qui lui demanda: "Est-ce toi, ma fille?" Ruth lui raconta tout ce que l’homme avait fait pour elle.
Rute atafika kwa apongozi ake anamufunsa kuti, “Zinayenda bwanji mwana wanga?” Kenaka iye anafotokoza zonse zimene Bowazi anamuchitira.
17 "Voici, ajouta-t-elle, six mesures d’orge qu’il m’a données en me disant: Tu ne dois pas revenir les mains vides auprès de ta belle-mère."
Ndipo anati, “Munthuyo anandipatsa makilogalamu makumi awiri awa a barele, nandiwuza kuti usapite kwa apongozi ako wopanda kanthu.”
18 Noémi répondit: "Demeure tranquille, ma fille, jusqu’à ce que tu saches quel sera le dénouement de l’affaire; assurément, cet homme ne se tiendra pour satisfait qu’il ne l’ait menée à bonne fin aujourd’hui même."
Kenaka Naomi anati, “Mwana wanga, dikira mpaka titaona mmene zinthu zikhalire chifukwa munthuyu salekera pomwepo, mpaka zinthuzi zitakonzeka lero.”