< Psaumes 81 >
1 Au chef des chantres. Sur la Ghitit. D’Assaph. Célébrez Dieu, notre force, acclamez le Dieu de Jacob!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu. Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu; Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!
2 Chantez des hymnes, faites retentir le tambourin, la harpe suave ainsi que le luth,
Yambani nyimbo, imbani tambolini imbani pangwe wolira bwino ndi zeze.
3 sonnez le Chofar à la nouvelle lune, au jour fixé pour notre solennité.
Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano, ndi pamene mwezi waoneka wonse, pa tsiku la phwando;
4 Car c’est une loi en Israël, une coutume en l’honneur du Dieu de Jacob;
ili ndi lamulo kwa Israeli, langizo la Mulungu wa Yakobo.
5 c’est un témoignage qu’il établit dans Joseph, quand il marcha contre l’Egypte. J’Entendis alors des accents inconnus pour moi…
Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe pamene anatuluka kulimbana ndi Igupto, kumene tinamva chiyankhulo chimene sitinachidziwe.
6 J’Ai déchargé du fardeau son épaule, ses mains sont affranchies du lourd panier.
Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo; Manja awo anamasulidwa mʼdengu.
7 Dans la détresse tu as appelé, et je t’ai délivré, je t’ai exaucé du sein mystérieux de la foudre, je t’ai éprouvé auprès des eaux de Meriba. (Sélah)
Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani, ndinakuyankhani kuchokera mʼmitambo ya mabingu; ndinakuyesani pa madzi a ku Meriba. (Sela)
8 "Ecoute, mon peuple, je veux t’adjurer; ô Israël, puisses-tu m’écouter!
“Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani ngati mungathe kumvetsera, Inu Israeli!
9 Qu’il n’y ait pas chez toi de divinité étrangère, ne te prosterne pas devant un dieu du dehors.
Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu; musadzagwadire mulungu wina.
10 Je suis, moi, l’Eternel, ton Dieu qui t’ai tiré du pays d’Egypte. Ouvre largement ta bouche et je la remplirai."
Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto. Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.
11 Mais mon peuple n’a pas écouté ma voix, Israël a refusé de m’obéir.
“Koma anthu anga sanandimvere; Israeli sanandigonjere.
12 Je les ai donc abandonnés à l’entraînement de leur cœur, ils suivirent leurs propres inspirations.
Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo kuti atsate zimene ankafuna.
13 Ah! si mon peuple voulait m’écouter, Israël marcher dans mes voies,
“Anthu anga akanangondimvera, Israeli akanatsatira njira zanga,
14 bien vite, je dompterais leurs ennemis, je ferais peser ma main sur leurs adversaires.
nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
15 Ceux qui haïssent l’Eternel ramperaient devant lui, mais leur bonheur, à eux, durerait toujours.
Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake, ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
16 Il les nourrirait de la mœlle du froment, et les rassasierait avec le miel des rochers.
Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri; ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”