< Psaumes 66 >
1 Au chef des chantres. Cantique. Psaume. Que toute la terre acclame Dieu!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
2 Chantez la gloire de son nom, faites de ses louanges un tribut d’honneur.
Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
3 Dites à Dieu: "Que tes œuvres sont prodigieuses! A cause de ta toute-puissance tes ennemis rampent devant toi;
Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
4 la terre entière se prosterne à tes pieds, entonne tes louanges, célèbre ton nom." (Sélah)
Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
5 Venez et contemplez les hauts faits de Dieu! Merveilleuse est son action sur les fils de l’homme.
Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
6 Il change la mer en terre ferme, à travers le fleuve on marche à pied sec; dès lors nous mîmes notre joie en lui.
Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
7 Il règne éternellement dans sa force, ses regards observent les nations: que les rebelles ne portent pas le front haut! (Sélah)
Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
8 Nations, bénissez notre Dieu, faites retentir le bruit de ses louanges!
Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
9 Il nous a gratifiés de la vie, et n’a pas laissé nos pieds chanceler.
Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
10 Car tu nous as éprouvés, ô notre Dieu, jetés au creuset comme on fait de l’argent.
Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
11 Tu nous avais amenés dans un filet, tu avais chargé nos reins d’un pesant fardeau,
Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
12 courbé notre tête sous le joug des gens. Nous avions passé par le feu et par l’eau; mais tu nous as remis dans l’abondance.
Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
13 Je me présenterai dans ta maison avec des holocaustes, pour m’acquitter envers toi de tous mes vœux,
Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
14 que mes lèvres ont exprimés, qu’au cours de ma détresse ma bouche a formulés.
Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
15 Je t’offrirai des brebis grasses comme holocaustes, avec la fumée des béliers; j’immolerai des taureaux ainsi que des boucs. (Sélah)
Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
16 Venez et écoutez: Je veux raconter, ô vous tous qui craignez Dieu, ce qu’il a fait en ma faveur!
Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
17 A pleine bouche je l’avais invoqué, il se trouvait exalté par mes lèvres.
Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
18 Si, dans mon cœur, j’avais eu en vue l’iniquité, Dieu ne m’eût pas entendu.
Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
19 Eh bien! Dieu a entendu; il a été attentif aux accents de ma prière.
koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
20 Loué soit Dieu qui n’a pas repoussé ma prière, et ne m’a pas retiré sa grâce!
Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!