< Psaumes 57 >
1 Au chef des chantres. Al tachhêt. Mikhtam de David, lorsqu’il se fut réfugié, à cause de Saül, dans la caverne. Sois-moi propice, ô Dieu, sois-moi propice, car en toi s’abrite mon âme; je me mets à couvert à l’ombre de tes ailes, jusqu’à ce que le malheur ait passé.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide, pamene anathawa Sauli kupita ku phanga. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu mundichitire chifundo, pakuti mwa Inu moyo wanga umathawiramo. Ndidzathawira mu mthunzi wa mapiko anu mpaka chiwonongeko chitapita.
2 Je crie vers le Dieu suprême, vers le Tout-Puissant qui prendra ma cause en main.
Ine ndikufuwulira kwa Mulungu Wammwambamwamba, kwa Mulungu amene amakwaniritsa cholinga chake pa ine.
3 Que du haut du ciel il m’envoie son secours, celui qui m’opprime aura beau m’insulter, (Sélah) Que Dieu envoie sa grâce et sa bienveillance!
Mulungu amanditumizira kuchokera kumwamba ndi kundipulumutsa, kudzudzula iwo amene akundithamangitsa kwambiri. Mulungu amatumiza chikondi chake ndi kukhulupirika kwake.
4 Je pourrai me coucher parmi des lions aux regards flamboyants, parmi des hommes dont les dents sont des lances et des flèches, et la langue un glaive tranchant.
Ine ndili pakati pa mikango, ndagona pakati pa zirombo zolusa; anthu amene mano awo ndi milomo yawo ndi mivi, malilime awo ndi malupanga akuthwa.
5 Montre, ô Dieu, ta grandeur qui dépasse les cieux; que ta gloire brille sur toute la terre!
Mukwezekedwe Inu Mulungu, kuposa mayiko onse akumwamba; mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
6 On avait dressé des filets sous mes pas pour me faire ployer, on avait creusé une fosse devant moi: ils y sont tombés eux-mêmes. (Sélah)
Iwo anatchera mapazi anga ukonde ndipo ndinawerama pansi mosautsidwa. Anakumba dzenje mʼnjira yanga koma agweramo okha mʼmenemo.
7 Mon cœur reste ferme, ô Dieu, mon cœur reste ferme: je puis chanter, célébrer tes louanges.
Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu mtima wanga ndi wokhazikika. Ndidzayimba nyimbo, nyimbo yake yamatamando.
8 Réveille-toi, ô mon âme, réveillez-vous, ô luth et harpe: je veux réveiller l’aurore.
Dzuka moyo wanga! Dzukani zeze ndi pangwe! Ndidzadzuka mʼbandakucha.
9 Je te louerai parmi les nations, ô Seigneur, je te chanterai parmi les peuples.
Ndidzakutamandani Ambuye, pakati pa mitundu ya anthu, ndidzayimba za Inu pakati pa mayiko.
10 Car ta grâce s’élève jusqu’aux cieux, et ta bonté atteint jusqu’au firmament.
Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kufikira ku mayiko akumwamba; kukhulupirika kwanu kwafika ku mitambo.
11 Montre, ô Dieu, ta grandeur qui dépasse les cieux; que ta gloire brille sur toute la terre!
Mukwezekedwe Inu Mulungu kuposa mayiko akumwamba, mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.