< Psaumes 50 >

1 Psaume d’Assaph. Le Dieu tout-puissant, l’Eternel parle; il adresse un appel à la terre, du soleil levant jusqu’à son couchant.
Salimo la Asafu. Wamphamvuyo, Yehova Mulungu, akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.
2 De Sion, ce centre de beauté, l’Eternel rayonne.
Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri Mulungu akuwala.
3 Il s’avance, notre Dieu, et ce n’est pas en silence: devant lui, un feu qui dévore, autour de lui gronde la tempête.
Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete; moto ukunyeketsa patsogolo pake, ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho
4 Il adresse son appel aux cieux d’en haut ainsi qu’à la terre, en vue de juger son peuple:
Iye akuyitanitsa zamumlengalenga ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.
5 "Rassemblez-moi mes pieux serviteurs, qui ont sanctionné mon alliance par un sacrifice!"
Mundisonkhanitsire okhulupirika anga, amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.
6 Et les cieux proclament sa justice, car c’est Dieu qui est le juge. (Sélah)
Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake, pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.
7 Ecoute, mon peuple, je veux parler; Israël, je veux t’adjurer solennellement: Je suis Dieu, ton Dieu!
Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula, iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa; ndine Mulungu, Mulungu wako.
8 Ce n’est pas pour tes sacrifices que je te reprends: tes holocaustes sont constamment sous mes yeux.
Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako, kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.
9 Je ne réclame pas de taureau de ta maison, ni des béliers de tes parcs.
Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako kapena mbuzi za mʼkhola lako,
10 Car à moi sont tous les fauves de la forêt, les bêtes qui peuplent par milliers les montagnes.
pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.
11 Je connais tous les oiseaux des hauteurs, tout ce qui se meut dans les champs est à ma portée.
Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.
12 Dussé-je avoir faim, je ne te le dirais pas, car l’univers, avec ce qu’il renferme, m’appartient.
Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani, pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.
13 Est-ce donc que je mange la chair des taureaux? Est-ce que je bois le sang des béliers?
Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna kapena kumwa magazi a mbuzi?
14 En guise de sacrifice, offre à Dieu des actions de grâce, ainsi tu acquitteras tes vœux envers le Très-Haut.
“Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu, kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.
15 Alors tu pourras m’appeler au jour de la détresse, je te tirerai du danger, et tu m’honoreras!
Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso; Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza.”
16 Quant au méchant, Dieu lui dit: "Qu’as-tu à proclamer mes statuts et à porter mon alliance sur tes lèvres?
Koma kwa woyipa, Mulungu akuti, “Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?
17 Tu détestes pourtant la loi morale, et rejettes avec dédain mes paroles.
Iwe umadana ndi malangizo anga ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.
18 Vois-tu un voleur? Tu fais cause commune avec lui, tu t’associes avec des gens dissolus.
Ukaona wakuba umamutsatira, umachita maere ako pamodzi ndi achigololo
19 Tu donnes libre carrière à ta bouche pour le mal, et ta langue enfile des discours astucieux.
Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.
20 Tu t’installes pour déblatérer contre ton frère; sur le fils de ta mère tu jettes le déshonneur.
Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.
21 Voilà ce que tu fais, et je me tairais! T’Imagines-tu que je puisse être comme toi? Je te reprendrai et te mettrai mes griefs sous les yeux."
Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete; umaganiza kuti ndine wofanana nawe koma ndidzakudzudzula ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.
22 Faites-y donc attention, vous qui oubliez Dieu, de peur que je ne sévisse, sans que personne puisse détourner mes coups.
“Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:
23 Quiconque offre comme sacrifice des actions de grâce m’honore; quiconque dirige avec soin sa conduite, je le ferai jouir de l’aide divine.
Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza, ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse chipulumutso cha Mulungu.”

< Psaumes 50 >