< Psaumes 45 >
1 Au chef des chantres. Sur les Chochanim. Par les fils de Coré. Maskîl. Chant d’amour. Mon cœur agite un beau dessein; je veux consacrer mon poème au roi! Ma langue est le burin d’un scribe expert.
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati. Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu; lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.
2 Tu es beau entre tous les fils de l’homme, la grâce est répandue sur tes lèvres; aussi Dieu t’a-t-il béni pour toujours.
Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika, popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.
3 Ceins ton glaive sur ton flanc, ô héros, c’est ta parure et ton honneur;
Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu; mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.
4 oui, ton honneur! Bon courage et en selle, pour défendre la vérité, la modestie, la justice! Que ta droite t’enseigne de beaux exploits!
Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo; dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.
5 Tes flèches sont aiguës, des peuples succombent sous tes coups elles percent le cœur des ennemis du roi.
Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu, mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.
6 Ton trône, fondé par Dieu, durera à jamais; le sceptre de ta royauté est un sceptre de droiture.
Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi; ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.
7 Tu aimes la justice, tu hais l’iniquité; voilà pourquoi Dieu ton Dieu t’a consacré par une huile d’allégresse, de préférence à tes compagnons.
Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa; choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.
8 Myrrhe, aloès et casse parfument tes vêtements; du fond des palais d’ivoire les concerts te ravissent.
Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya; kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.
9 Des filles de rois figurent parmi tes favorites; la reine se tient à ta droite, parée de l’or d’Ophir.
Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka; ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.
10 Ecoute ma fille, ouvre les yeux, tends l’oreille: oublie ton peuple et la maison de ton père!
Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu; iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.
11 Que le roi s’éprenne de ta beauté, car il est ton maître incline-toi devant lui.
Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako; mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.
12 La fille de Tyr… Chargés de présents, les gens les plus opulents recherchent ta bienveillance.
Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso, amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.
13 Toute resplendissante est la fille du roi dans son intérieur, sa robe est faite d’un tissu d’or.
Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake, chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.
14 Couverte de broderies, elle est introduite auprès du roi, suivie d’un cortège de jeunes filles, ses compagnes, qui sont amenées pour toi;
Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu; anamwali okhala naye akumutsatira ndipo abweretsedwa kwa inu.
15 amenées avec des cris de joie et d’allégresse, elles pénètrent dans le palais du roi.
Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo; akulowa mʼnyumba yaufumu.
16 Que la place de tes pères soit occupée par tes fils! Puisses-tu les établir comme princes sur tout le pays!
Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako; udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.
17 Je ferai en sorte que ton nom vive de siècle en siècle; aussi les nations te rendront-elles hommage à tout jamais!
Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse; choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.